< Ezekieli 45 >

1 “‘Mukamadzagawa dziko kuti fuko lililonse lilandire cholowa chake, mudzapatuleko chigawo chimodzi kuti chikhale cha Yehova. Mulitali mwake mudzakhale makilomita khumi ndi awiri ndi theka ndipo mulifupi mwake makilomita khumi. Malo onsewo adzakhale opatulika.
«و چون زمین را به جهت ملکیت به قرعه تقسیم نمایید، حصه مقدس را که طولش بیست و پنج هزار (نی ) و عرضش ده هزار(نی ) باشد هدیه‌ای برای خداوند بگذرانید و این به تمامی حدودش از هر طرف مقدس خواهدبود.۱
2 Mʼkati mwa chigawo chimenechi, malo a mamita 250 mbali iliyonse adzakhala malo a Nyumba ya Mulungu. Pozungulira pake ponse padzakhala malo a mamita 25.
و از این پانصد در پانصد (نی ) از هر طرف مربع برای قدس خواهد بود و نواحی آن از هرطرفش پنجاه ذراع.۲
3 Mʼchigawo chopatulikacho muyeze malo a makilomita 12 ndi theka mulitali mwake, makilomita asanu mulifupi mwake. Pamenepo padzakhala malo opatulika kwambiri.
و از این پیمایش طول بیست و پنج هزار و عرض ده هزار (نی ) خواهی پیمود تا در آن جای مقدس قدس‌الاقداس باشد.۳
4 Malo opatulika amenewa adzakhalanso a ansembe amene amatumikira ku malo opatulika, amene amayandikira Yehova kuti amutumikire. Pamenepo padzakhala malo omangapo nyumba zawo ndi malo omangapo Nyumba ya Mulungu.
و این برای کاهنانی که خادمان مقدس باشند و به جهت خدمت خداوند نزدیک می‌آیند، حصه مقدس از زمین خواهد بود تا جای خانه‌ها به جهت ایشان و جای مقدس به جهت قدس باشد.۴
5 Alevi otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzakhala ndi malo a makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake ndi makilomita asanu mulifupi mwake. Kumeneko ndiko kudzakhale midzi yawo.
و طول بیست و پنج هزار و عرض ده هزار (نی )به جهت لاویانی که خادمان خانه باشند خواهدبود تا ملک ایشان برای بیست خانه باشد.۵
6 “‘Moyandikana ndi malo opatulika, padzakhale malo a makilomita awiri ndi theka mulifupi mwake ndi makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake; kuti akhale malo a mzinda. Malo amenewa adzakhala a Aisraeli onse.
و ملک شهر را که عرضش پنجهزار و طولش بیست وپنجهزار (نی ) باشد موازی آن هدیه مقدس قرار خواهید داد و این از آن تمامی خاندان اسرائیل خواهد بود.۶
7 “‘Mfumu idzakhale ndi malo okhudzana ndi chigawo cha malo opatulika ndi cha mzinda. Malowo ayandikane ndi zigawozo chakummawa ndi chakumadzulo. Malowo atalike ngati chigawo chimodzi cha fuko la Israeli kuyambira ku malire akummawa mpaka ku malire akumadzulo.
و از اینطرف و از آنطرف هدیه مقدس و ملک شهر مقابل هدیه مقدس و مقابل ملک شهر از جانب غربی به سمت مغرب و ازجانب شرقی به سمت مشرق حصه رئیس خواهدبود و طولش موازی یکی از قسمت‌ها از حدمغرب تا حد مشرق خواهد بود.۷
8 Malowa adzakhala chigawo cha mfumu mu Israeli. Choncho mafumu anga sadzazunzanso anthu anga, koma adzidzalola Aisraeli kuti akhale ndi zigawo zawozawo.
و این در آن زمین در اسرائیل ملک او خواهد بود تا روسای من بر قوم من دیگر ستم ننمایند و ایشان زمین را به خاندان اسرائیل بر‌حسب اسباط ایشان خواهندداد.۸
9 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsono pakwana, inu akalonga a Israeli. Lekani nkhanza zanu ndi kupondereza anthu anga. Muzitsata chilungamo ndi kuchita zokomera anthu. Musapirikitse anthu anga mʼdzikomo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
«خداوند یهوه چنین می‌گوید: ای سروران اسرائیل باز ایستید و جور و ستم را دور کنید وانصاف و عدالت را بجا آورید و ظلم خود را ازقوم من رفع نمایید. قول خداوند یهوه این است:۹
10 Miyeso yanu yoyezera zinthu monga efa ndi bati zizikhala zokhulupirika.
میزان راست و ایفای راست و بت راست برای شما باشد۱۰
11 Efa ndi bati ikhale miyeso yolingana kukula kwake. Muyeso wa homeri ukhale wokwanira mabati khumi, ukhalenso wokwanira maefa khumi. Ndiye kuti kukula kwa miyeso iwiriyo kuzidzatsata kukula kwa homeriyo.
و ایفا و بت یکمقدار باشد به نوعی که بت به عشر حومر و ایفا به عشر حومر مساوی باشد. مقدار آنها بر‌حسب حومر باشد.۱۱
12 Muyeso wa sekeli ukhale wokwanira magera makumi awiri. Muyeso wa mina ukhale wolemera masekeli 60.
و مثقال بیست جیره باشد. و منای شما بیست مثقال وبیست و پنج مثقال و پانزده مثقال باشد.۱۲
13 “‘Zopereka zomwe mudzidzapereka ndi izi: chimodzi mwa zigawo 60 za tirigu, barelenso chimodzimodzi ndiponso gawo limodzi la magawo asanu ndi limodzi la efa, kulitapa pa barele wa homeri.
«و هدیه‌ای که بگذرانید این است: یک سدس ایفا از هر حومر گندم و یک سدس ایفا ازهر حومر جو بدهید.۱۳
14 Gawo loyenera la mafuta, loyezedwa ndi bati, ndiponso chigawo mwa zigawo 100 za mafuta. Miyeso yake ili motere: mabati khumi afanana ndi homeri imodzi kapena kori imodzi.
و قسمت معین روغن برحسب بت روغن یک عشر بت از هر کر یا حومرده بت باشد زیرا که ده بت یک حومر می‌باشد.۱۴
15 Muperekenso nkhosa imodzi pa gulu lankhosa 200 za pa msipu wabwino wa mu Israeli. Izi zidzagwiritsidwa ntchito monga nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano ndi nsembe zopepesera milandu ya anthu. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
و یک گوسفند از دویست گوسفند از مرتع های سیراب اسرائیل برای هدیه آردی و قربانی سوختنی و ذبایح سلامتی بدهند تا برای ایشان کفاره بشود. قول خداوند یهوه این است.۱۵
16 Anthu onse a mʼdzikomo azidzapereka zimenezi kwa mfumu ya Israeli.
وتمامی قوم زمین این هدیه را برای رئیس دراسرائیل بدهند.۱۶
17 Udzakhala udindo wa mfumu kupereka zofunikira ku nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, ndi nsembe za zakumwa pa nthawi ya zikondwerero, chikondwerero cha mwezi watsopano ndi cha masabata, nthawi yonse ya zikondwerero zoyikika za Aisraeli. Mfumuyo idzapereka nsembe zopepesera machimo, nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano kuti zikhale nsembe zopepesera machimo a Aisraeli.
و رئیس قربانی های سوختنی و هدایای آردی و هدایای ریختنی را در عیدها وهلال‌ها و سبت‌ها و همه مواسم خاندان اسرائیل بدهد واو قربانی گناه و هدیه آردی و قربانی سوختنی و ذبایح سلامتی را به جهت کفاره برای خاندان اسرائیل بگذراند.»۱۷
18 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba muzitenga mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndi kuchita mwambo woyeretsa malo opatulika.
خداوند یهوه چنین می‌گوید: «در غره ماه اول، گاوی جوان بی‌عیب گرفته، مقدس را طاهرخواهی نمود.۱۸
19 Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera machimoyo ndipo awapake pa mphuthu za Nyumba ya Mulungu, pa ngodya zinayi za pamwamba pa guwa lansembe ndi pa mphuthu za pa chipata cha bwalo la mʼkati.
و کاهن قدری از خون قربانی گناه گرفته، آن را بر چهار چوب خانه و بر چهارگوشه خروج مذبح و بر چهار چوب دروازه صحن اندرونی خواهد پاشید.۱۹
20 Muzichita chimodzimodzi pa tsiku la chisanu ndi chiwiri la mwezi, kuchitira aliyense amene wachimwa mosafuna kapena mosadziwa. Motero Nyumba ya Mulungu idzakhala yoyera.
و همچنین درروز هفتم ماه برای هر‌که سهو یا غفلت خطا ورزدخواهی کرد و شما برای خانه کفاره خواهیدنمود.۲۰
21 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita chikondwerero cha Paska, chikondwerero chake cha masiku asanu ndi awiri. Pa masiku amenewo muzidzadya buledi wopanda yisiti.
و در روز چهاردهم ماه اول برای شماهفت روز عید فصح خواهد بود که در آنها نان فطیر خورده شود.۲۱
22 Pa tsiku loyamba la chikondwererocho, mfumu ipereke nsembe ya ngʼombe yayimuna monga nsembe yopepesera machimo ake ndi machimo a anthu onse a mʼdziko.
و در آن روز رئیس، گاوقربانی گناه را برای خود و برای تمامی اهل زمین بگذراند.۲۲
23 Pa masiku asanu ndi awiri a chikondwererocho, mfumu ipereke kwa Yehova nsembe zopsereza izi: ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, zonsezi zopanda chilema. Pa masikuwa mfumu iziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
و در هفت روز عید، یعنی در هر روزاز آن هفت روز، هفت گاو و هفت قوچ بی‌عیب به جهت قربانی سوختنی برای خداوند و هر روزیک بز نر به جهت قربانی گناه بگذارند.۲۳
24 Pamodzi ndi ngʼombe iliyonse yayimuna ndi nkhosa iliyonse yayimuna, mfumu ipereke chopereka cha chakudya chokwanira efa imodzi ndiponso mafuta okwanira hini imodzi pa efa iliyonse.
و هدیه آردیش را یک ایفا برای هر گاو و یک ایفا برای هرقوچ و یک هین روغن برای هر ایفا بگذراند.۲۴
25 “‘Pa nthawi ya chikondwerero cha masiku asanu ndi awiri, chimene chimayamba pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mfumuyo iziperekanso nsembe za mtundu womwewo: nsembe zopepesera machimo, nsembe zopsereza, nsembe za chakudya ndi za mafuta.’”
واز روز پانزدهم ماه هفتم، در وقت عید موافق اینهایعنی موافق قربانی گناه و قربانی سوختنی و هدیه آردی و روغن تا هفت روز خواهد گذرانید.»۲۵

< Ezekieli 45 >