< Ezekieli 45 >

1 “‘Mukamadzagawa dziko kuti fuko lililonse lilandire cholowa chake, mudzapatuleko chigawo chimodzi kuti chikhale cha Yehova. Mulitali mwake mudzakhale makilomita khumi ndi awiri ndi theka ndipo mulifupi mwake makilomita khumi. Malo onsewo adzakhale opatulika.
Kuzakuthi-ke lapho lisaba ilizwe ngenkatho ukuthi libe yilifa, lizanikela umnikelo eNkosini, indawo engcwele yelizwe; ubude buzakuba yibude bezinkulungwane ezingamatshumi amabili lanhlanu, lobubanzi buzakuba zinkulungwane ezilitshumi. Leyo izakuba ngcwele kuyo yonke imingcele yayo inhlangothi zonke.
2 Mʼkati mwa chigawo chimenechi, malo a mamita 250 mbali iliyonse adzakhala malo a Nyumba ya Mulungu. Pozungulira pake ponse padzakhala malo a mamita 25.
Kuleyo kuzakuba lokwendawo engcwele engamakhulu amahlanu, lamakhulu amahlanu, ilingana inhlangothi zone ezizingelezeleyo; ibe legceke ngengalo ezingamatshumi amahlanu inhlangothi zonke.
3 Mʼchigawo chopatulikacho muyeze malo a makilomita 12 ndi theka mulitali mwake, makilomita asanu mulifupi mwake. Pamenepo padzakhala malo opatulika kwambiri.
Langalesisilinganiso lizalinganisa; ubude bube zingalo ezizinkulungwane ezingamatshumi amabili lanhlanu, lobubanzi bube zinkulungwane ezilitshumi, laphakathi kwayo kuzakuba khona indawo engcwele, lengcwele yezingcwele.
4 Malo opatulika amenewa adzakhalanso a ansembe amene amatumikira ku malo opatulika, amene amayandikira Yehova kuti amutumikire. Pamenepo padzakhala malo omangapo nyumba zawo ndi malo omangapo Nyumba ya Mulungu.
Kuzakuba yindawo engcwele yelizwe; izakuba ngeyabapristi, abakhonzi bendawo engcwele, abasondela ukuze bakhonze iNkosi; njalo izakuba kubo yindawo yezindlu, lendawo engcwele yendlu engcwele.
5 Alevi otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzakhala ndi malo a makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake ndi makilomita asanu mulifupi mwake. Kumeneko ndiko kudzakhale midzi yawo.
Lobude bezinkulungwane ezingamatshumi amabili lanhlanu, lobubanzi bezinkulungwane ezilitshumi, amaLevi, abakhonzi bendlu, azakuba labo, bube yimfuyo, amakamelo angamatshumi amabili.
6 “‘Moyandikana ndi malo opatulika, padzakhale malo a makilomita awiri ndi theka mulifupi mwake ndi makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake; kuti akhale malo a mzinda. Malo amenewa adzakhala a Aisraeli onse.
Njalo lizanika imfuyo yomuzi, ububanzi bezinkulungwane ezinhlanu, lobude bamatshumi amabili lanhlanu, maqondana lomnikelo ongcwele; izakuba ngeyendlu yonke kaIsrayeli.
7 “‘Mfumu idzakhale ndi malo okhudzana ndi chigawo cha malo opatulika ndi cha mzinda. Malowo ayandikane ndi zigawozo chakummawa ndi chakumadzulo. Malowo atalike ngati chigawo chimodzi cha fuko la Israeli kuyambira ku malire akummawa mpaka ku malire akumadzulo.
Njalo isiphathamandla sizakuba lesabelo ngapha langapha komnikelo wesabelo esingcwele lakwemfuyo yomuzi, phambi komnikelo wesabelo ongcwele, laphambi kwemfuyo yomuzi, kusukela ngentshonalanga kuqonda entshonalanga, lakusukela ngempumalanga kuqonda empumalanga. Lobude buzaqondana lesinye sezabelo, kusukela emngceleni wentshonalanga kuze kube semngceleni wempumalanga.
8 Malowa adzakhala chigawo cha mfumu mu Israeli. Choncho mafumu anga sadzazunzanso anthu anga, koma adzidzalola Aisraeli kuti akhale ndi zigawo zawozawo.
Mayelana lelizwe, uzakuba lalo libe yimfuyo koIsrayeli. Njalo iziphathamandla zami kazisayikubacindezela abantu bami, kodwa zizanika ilizwe kuyo indlu kaIsrayeli njengokwezizwe zabo.
9 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsono pakwana, inu akalonga a Israeli. Lekani nkhanza zanu ndi kupondereza anthu anga. Muzitsata chilungamo ndi kuchita zokomera anthu. Musapirikitse anthu anga mʼdzikomo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Itsho njalo iNkosi uJehova: Sekwanele kini, lina ziphathamandla zakoIsrayeli! Susani udlakela lokuchitha, lenze isahlulelo lokulunga, lisuse ukuxotsha kwenu kubo abantu bami, itsho iNkosi uJehova.
10 Miyeso yanu yoyezera zinthu monga efa ndi bati zizikhala zokhulupirika.
Lizakuba lesikali esilungileyo, le-efa elilungileyo, lebhathi elilungileyo.
11 Efa ndi bati ikhale miyeso yolingana kukula kwake. Muyeso wa homeri ukhale wokwanira mabati khumi, ukhalenso wokwanira maefa khumi. Ndiye kuti kukula kwa miyeso iwiriyo kuzidzatsata kukula kwa homeriyo.
I-efa lebhathi kuzakuba yisilinganiso sinye, ukuthi ibhathi limumethe ingxenye eyodwa etshumini yehomeri, le-efa ingxenye eyodwa etshumini yehomeri; isilinganiso sakho sizakuba ngokwehomeri.
12 Muyeso wa sekeli ukhale wokwanira magera makumi awiri. Muyeso wa mina ukhale wolemera masekeli 60.
Leshekeli lizakuba ngamagera angamatshumi amabili; amashekeli angamatshumi amabili, amashekeli angamatshumi amabili lanhlanu, lamashekeli alitshumi lanhlanu, azakuba yimane kini.
13 “‘Zopereka zomwe mudzidzapereka ndi izi: chimodzi mwa zigawo 60 za tirigu, barelenso chimodzimodzi ndiponso gawo limodzi la magawo asanu ndi limodzi la efa, kulitapa pa barele wa homeri.
Lokhu kungumnikelo elizawunikela: Ingxenye eyodwa kweziyisithupha ye-efa yehomeri yengqoloyi, futhi lizakupha ingxenye eyodwa kweziyisithupha ye-efa yehomeri yebhali.
14 Gawo loyenera la mafuta, loyezedwa ndi bati, ndiponso chigawo mwa zigawo 100 za mafuta. Miyeso yake ili motere: mabati khumi afanana ndi homeri imodzi kapena kori imodzi.
Mayelana lesimiso samafutha, ibhathi lamafutha, lizanikela ingxenye eyodwa etshumini yebhathi kulo ikhori, eliyihomeri yamabhathi alitshumi; ngoba amabathi alitshumi alihomeri.
15 Muperekenso nkhosa imodzi pa gulu lankhosa 200 za pa msipu wabwino wa mu Israeli. Izi zidzagwiritsidwa ntchito monga nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano ndi nsembe zopepesera milandu ya anthu. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Lewundlu elilodwa emhlanjini, kuwo amakhulu amabili, endaweni elamanzi kaIsrayeli, libe ngumnikelo wokudla, libe ngumnikelo wokutshiswa, libe yiminikelo yokuthula, yokubenzela ukubuyisana, itsho iNkosi uJehova.
16 Anthu onse a mʼdzikomo azidzapereka zimenezi kwa mfumu ya Israeli.
Bonke abantu belizwe bazakuba kulowomnikelo kusenzelwa isiphathamandla koIsrayeli.
17 Udzakhala udindo wa mfumu kupereka zofunikira ku nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, ndi nsembe za zakumwa pa nthawi ya zikondwerero, chikondwerero cha mwezi watsopano ndi cha masabata, nthawi yonse ya zikondwerero zoyikika za Aisraeli. Mfumuyo idzapereka nsembe zopepesera machimo, nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano kuti zikhale nsembe zopepesera machimo a Aisraeli.
Kuzakuba phezu kwesiphathamandla ukunikela iminikelo yokutshisa, lomnikelo wempuphu, lomnikelo wokunathwayo, emikhosini, lekuthwaseni kwezinyanga, lemasabatheni, kuyo yonke imikhosi emisiweyo yendlu yakoIsrayeli. Sona sizalungisa umnikelo wesono, lomnikelo wempuphu, lomnikelo wokutshiswa, leminikelo yokuthula, ukwenzela indlu yakoIsrayeli ukubuyisana.
18 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba muzitenga mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndi kuchita mwambo woyeretsa malo opatulika.
Itsho njalo iNkosi uJehova: Ngenyanga yokuqala, ngolokuqala lwenyanga, uzathatha ijongosi elilithole lenkomo elingelasici, uhlambulule indawo engcwele.
19 Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera machimoyo ndipo awapake pa mphuthu za Nyumba ya Mulungu, pa ngodya zinayi za pamwamba pa guwa lansembe ndi pa mphuthu za pa chipata cha bwalo la mʼkati.
Njalo umpristi uzathatha okwegazi lomnikelo wesono, alifake emigubazini yendlu, lezingonsini ezine zomngcele welathi, lemigubazini yesango leguma langaphakathi.
20 Muzichita chimodzimodzi pa tsiku la chisanu ndi chiwiri la mwezi, kuchitira aliyense amene wachimwa mosafuna kapena mosadziwa. Motero Nyumba ya Mulungu idzakhala yoyera.
Futhi uzakwenza njalo ngolwesikhombisa lwenyanga ngenxa yomuntu oduhayo, langenxa yongelalwazi; ngokunjalo uzakwenzela indlu inhlawulo yokuthula.
21 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita chikondwerero cha Paska, chikondwerero chake cha masiku asanu ndi awiri. Pa masiku amenewo muzidzadya buledi wopanda yisiti.
Ngenyanga yokuqala, ngosuku lwetshumi lane lwenyanga, lizakuba lephasika, umkhosi wensuku eziyisikhombisa; isinkwa esingelamvubelo sizadliwa.
22 Pa tsiku loyamba la chikondwererocho, mfumu ipereke nsembe ya ngʼombe yayimuna monga nsembe yopepesera machimo ake ndi machimo a anthu onse a mʼdziko.
Langalolosuku isiphathamandla sizazilungisela sona kanye labo bonke abantu belizwe ijongosi lomnikelo wesono.
23 Pa masiku asanu ndi awiri a chikondwererocho, mfumu ipereke kwa Yehova nsembe zopsereza izi: ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, zonsezi zopanda chilema. Pa masikuwa mfumu iziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
Ngensuku eziyisikhombisa zomkhosi uzalungisa umnikelo wokutshiswa eNkosini, amajongosi ayisikhombisa lenqama eziyisikhombisa ezingelasici ngosuku, okwensuku eziyisikhombisa, lomnikelo wesono wezinyane lezimbuzi ngosuku.
24 Pamodzi ndi ngʼombe iliyonse yayimuna ndi nkhosa iliyonse yayimuna, mfumu ipereke chopereka cha chakudya chokwanira efa imodzi ndiponso mafuta okwanira hini imodzi pa efa iliyonse.
Uzalungisa-ke umnikelo wokudla, i-efa ngejongosi, le-efa ngenqama, lehini yamafutha nge-efa.
25 “‘Pa nthawi ya chikondwerero cha masiku asanu ndi awiri, chimene chimayamba pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mfumuyo iziperekanso nsembe za mtundu womwewo: nsembe zopepesera machimo, nsembe zopsereza, nsembe za chakudya ndi za mafuta.’”
Ngenyanga yesikhombisa, ngosuku lwetshumi lanhlanu lwenyanga, uzakwenza njengalokhu emkhosini, insuku eziyisikhombisa, njengomnikelo wesono, njengomnikelo wokutshiswa, lanjengomnikelo wokudla, lanjengamafutha.

< Ezekieli 45 >