< Ezekieli 45 >
1 “‘Mukamadzagawa dziko kuti fuko lililonse lilandire cholowa chake, mudzapatuleko chigawo chimodzi kuti chikhale cha Yehova. Mulitali mwake mudzakhale makilomita khumi ndi awiri ndi theka ndipo mulifupi mwake makilomita khumi. Malo onsewo adzakhale opatulika.
“And in your causing the land to fall into inheritance, you lift up a raised-offering to YHWH, a holy [portion] of the land: the length—twenty-five thousand [is] the length, and the breadth—ten thousand; it [is] holy in all its surrounding border.
2 Mʼkati mwa chigawo chimenechi, malo a mamita 250 mbali iliyonse adzakhala malo a Nyumba ya Mulungu. Pozungulira pake ponse padzakhala malo a mamita 25.
There is of this for the sanctuary five hundred by five hundred, square, around; and fifty cubits of outskirt [is] around it.
3 Mʼchigawo chopatulikacho muyeze malo a makilomita 12 ndi theka mulitali mwake, makilomita asanu mulifupi mwake. Pamenepo padzakhala malo opatulika kwambiri.
And by this measure you measure: the length—twenty-five thousand, and the breadth—ten thousand: and the sanctuary is in it, the Holy of Holies.
4 Malo opatulika amenewa adzakhalanso a ansembe amene amatumikira ku malo opatulika, amene amayandikira Yehova kuti amutumikire. Pamenepo padzakhala malo omangapo nyumba zawo ndi malo omangapo Nyumba ya Mulungu.
It [is] the holy [portion] of the land; it is for priests, servants of the sanctuary, who are drawing near to serve YHWH; and it has been a place for their houses, and a holy place for the sanctuary.
5 Alevi otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzakhala ndi malo a makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake ndi makilomita asanu mulifupi mwake. Kumeneko ndiko kudzakhale midzi yawo.
And of the twenty-five thousand of length, and of the ten thousand of breadth, there is to the Levites, servants of the house, for them—for a possession—twenty chambers.
6 “‘Moyandikana ndi malo opatulika, padzakhale malo a makilomita awiri ndi theka mulifupi mwake ndi makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake; kuti akhale malo a mzinda. Malo amenewa adzakhala a Aisraeli onse.
And of the possession of the city you set [an area] of five thousand breadth, and twenty-five thousand length, alongside the raised-offering of the holy [portion]; it is for all the house of Israel.
7 “‘Mfumu idzakhale ndi malo okhudzana ndi chigawo cha malo opatulika ndi cha mzinda. Malowo ayandikane ndi zigawozo chakummawa ndi chakumadzulo. Malowo atalike ngati chigawo chimodzi cha fuko la Israeli kuyambira ku malire akummawa mpaka ku malire akumadzulo.
And for the prince: on this side and on that side of the raised-offering of the holy place, and of the possession of the city, at the front of the raised-offering of the holy place, and at the front of the possession of the city, from the west corner westward, and from the east corner eastward—and the length [is] corresponding to one of the portions from the west border to the east border—
8 Malowa adzakhala chigawo cha mfumu mu Israeli. Choncho mafumu anga sadzazunzanso anthu anga, koma adzidzalola Aisraeli kuti akhale ndi zigawo zawozawo.
of the land there is for a possession to him in Israel, and My princes do not oppress My people anymore, and they give the land to the house of Israel according to their tribes.”
9 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsono pakwana, inu akalonga a Israeli. Lekani nkhanza zanu ndi kupondereza anthu anga. Muzitsata chilungamo ndi kuchita zokomera anthu. Musapirikitse anthu anga mʼdzikomo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Thus said Lord YHWH: “Enough from you—princes of Israel; turn violence and spoil aside, and do judgment and righteousness; lift up your exactions from off My people—a declaration of Lord YHWH.
10 Miyeso yanu yoyezera zinthu monga efa ndi bati zizikhala zokhulupirika.
You must have just balances, and a just ephah, and a just bath.
11 Efa ndi bati ikhale miyeso yolingana kukula kwake. Muyeso wa homeri ukhale wokwanira mabati khumi, ukhalenso wokwanira maefa khumi. Ndiye kuti kukula kwa miyeso iwiriyo kuzidzatsata kukula kwa homeriyo.
The ephah and the bath is of one measure, for the bath to carry a tenth of the homer, and the ephah a tenth of the homer: its measurement is according to the homer.
12 Muyeso wa sekeli ukhale wokwanira magera makumi awiri. Muyeso wa mina ukhale wolemera masekeli 60.
And the shekel [is] twenty gerah: twenty shekels, twenty-five shekels, fifteen shekels—is your maneh.
13 “‘Zopereka zomwe mudzidzapereka ndi izi: chimodzi mwa zigawo 60 za tirigu, barelenso chimodzimodzi ndiponso gawo limodzi la magawo asanu ndi limodzi la efa, kulitapa pa barele wa homeri.
This [is] the raised-offering that you lift up; a sixth part of the ephah of a homer of wheat, also you have given a sixth part of the ephah of a homer of barley,
14 Gawo loyenera la mafuta, loyezedwa ndi bati, ndiponso chigawo mwa zigawo 100 za mafuta. Miyeso yake ili motere: mabati khumi afanana ndi homeri imodzi kapena kori imodzi.
and the portion of oil, the bath of oil, a tenth part of the bath out of the cor, a homer of ten baths—for ten baths [are] a homer;
15 Muperekenso nkhosa imodzi pa gulu lankhosa 200 za pa msipu wabwino wa mu Israeli. Izi zidzagwiritsidwa ntchito monga nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano ndi nsembe zopepesera milandu ya anthu. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
and one lamb out of the flock, out of two hundred, out of the watered country of Israel, for a present, and for a burnt-offering, and for peace-offerings, to make atonement by them—a declaration of Lord YHWH.
16 Anthu onse a mʼdzikomo azidzapereka zimenezi kwa mfumu ya Israeli.
All the people of the land are at this raised-offering for the prince in Israel.
17 Udzakhala udindo wa mfumu kupereka zofunikira ku nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, ndi nsembe za zakumwa pa nthawi ya zikondwerero, chikondwerero cha mwezi watsopano ndi cha masabata, nthawi yonse ya zikondwerero zoyikika za Aisraeli. Mfumuyo idzapereka nsembe zopepesera machimo, nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano kuti zikhale nsembe zopepesera machimo a Aisraeli.
And on the prince are the burnt-offerings, and the present, and the drink-offering, in celebrations, and in new moons, and in Sabbaths, in all appointed times of the house of Israel: he makes the sin-offering, and the present, and the burnt-offering, and the peace-offerings, to make atonement for the house of Israel.”
18 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba muzitenga mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndi kuchita mwambo woyeretsa malo opatulika.
Thus said Lord YHWH: “In the first [month], on the first of the month, you take a bullock, a son of the herd, a perfect one, and have cleansed the sanctuary:
19 Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera machimoyo ndipo awapake pa mphuthu za Nyumba ya Mulungu, pa ngodya zinayi za pamwamba pa guwa lansembe ndi pa mphuthu za pa chipata cha bwalo la mʼkati.
and the priest has taken from the blood of the sin offering, and has put [it] on the doorpost of the house, and on the four corners of the border of the altar, and on the post of the gate of the inner court.
20 Muzichita chimodzimodzi pa tsiku la chisanu ndi chiwiri la mwezi, kuchitira aliyense amene wachimwa mosafuna kapena mosadziwa. Motero Nyumba ya Mulungu idzakhala yoyera.
And so you do on the seventh of the month, because of each erring one, and because of the simple one—and you have purified the house.
21 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita chikondwerero cha Paska, chikondwerero chake cha masiku asanu ndi awiri. Pa masiku amenewo muzidzadya buledi wopanda yisiti.
In the first [month], on the fourteenth day of the month, you have the Passover, a celebration of seven days, unleavened bread is eaten.
22 Pa tsiku loyamba la chikondwererocho, mfumu ipereke nsembe ya ngʼombe yayimuna monga nsembe yopepesera machimo ake ndi machimo a anthu onse a mʼdziko.
And the prince has prepared on that day, for himself, and for all the people of the land, a bullock, a sin-offering.
23 Pa masiku asanu ndi awiri a chikondwererocho, mfumu ipereke kwa Yehova nsembe zopsereza izi: ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, zonsezi zopanda chilema. Pa masikuwa mfumu iziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
And [on] the seven days of the celebration he prepares a burnt-offering to YHWH, seven bullocks, and seven rams, perfect ones, daily [for] seven days, and a sin-offering, a kid of the goats, daily.
24 Pamodzi ndi ngʼombe iliyonse yayimuna ndi nkhosa iliyonse yayimuna, mfumu ipereke chopereka cha chakudya chokwanira efa imodzi ndiponso mafuta okwanira hini imodzi pa efa iliyonse.
And he prepares a present of an ephah for a bullock, and an ephah for a ram, and a hin of oil for an ephah.
25 “‘Pa nthawi ya chikondwerero cha masiku asanu ndi awiri, chimene chimayamba pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mfumuyo iziperekanso nsembe za mtundu womwewo: nsembe zopepesera machimo, nsembe zopsereza, nsembe za chakudya ndi za mafuta.’”
In the seventh [month], on the fifteenth day of the month, in the celebration, he does according to these things [for] seven days; as the sin-offering so the burnt-offering, and as the present so also the oil.”