< Ezekieli 45 >

1 “‘Mukamadzagawa dziko kuti fuko lililonse lilandire cholowa chake, mudzapatuleko chigawo chimodzi kuti chikhale cha Yehova. Mulitali mwake mudzakhale makilomita khumi ndi awiri ndi theka ndipo mulifupi mwake makilomita khumi. Malo onsewo adzakhale opatulika.
Moreover, when ye shall divide the land by lot for inheritance, ye shall offer an oblation to Jehovah, a holy portion of the land. The length shall be the length of twenty-five thousand measures, and the breadth shall be ten thousand. It shall be holy in all the border of it round about.
2 Mʼkati mwa chigawo chimenechi, malo a mamita 250 mbali iliyonse adzakhala malo a Nyumba ya Mulungu. Pozungulira pake ponse padzakhala malo a mamita 25.
Of this there shall be for the holy place five hundred by five hundred square round about, and fifty cubits for the suburbs of it round about.
3 Mʼchigawo chopatulikacho muyeze malo a makilomita 12 ndi theka mulitali mwake, makilomita asanu mulifupi mwake. Pamenepo padzakhala malo opatulika kwambiri.
And of this measure thou shall measure a length of twenty-five thousand, and a breadth of ten thousand. And the sanctuary shall be in it, which is most holy.
4 Malo opatulika amenewa adzakhalanso a ansembe amene amatumikira ku malo opatulika, amene amayandikira Yehova kuti amutumikire. Pamenepo padzakhala malo omangapo nyumba zawo ndi malo omangapo Nyumba ya Mulungu.
It is a holy portion of the land. It shall be for the priests, the ministers of the sanctuary, who come near to minister to Jehovah, and it shall be a place for their houses, and a holy place for the sanctuary.
5 Alevi otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzakhala ndi malo a makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake ndi makilomita asanu mulifupi mwake. Kumeneko ndiko kudzakhale midzi yawo.
And twenty-five thousand in length, and ten thousand in breadth, shall be to the Levites, the ministers of the house, for a possession to themselves, for twenty chambers.
6 “‘Moyandikana ndi malo opatulika, padzakhale malo a makilomita awiri ndi theka mulifupi mwake ndi makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake; kuti akhale malo a mzinda. Malo amenewa adzakhala a Aisraeli onse.
And ye shall appoint the possession of the city five thousand broad, and twenty-five thousand long, side by side with the oblation of the holy portion. It shall be for the whole house of Israel.
7 “‘Mfumu idzakhale ndi malo okhudzana ndi chigawo cha malo opatulika ndi cha mzinda. Malowo ayandikane ndi zigawozo chakummawa ndi chakumadzulo. Malowo atalike ngati chigawo chimodzi cha fuko la Israeli kuyambira ku malire akummawa mpaka ku malire akumadzulo.
And whatever is for the ruler shall be on the one side and on the other side of the holy oblation and of the possession of the city, in front of the holy oblation and in front of the possession of the city, on the west side westward, and on the east side eastward, and in length answerable to one of the portions, from the west border to the east border.
8 Malowa adzakhala chigawo cha mfumu mu Israeli. Choncho mafumu anga sadzazunzanso anthu anga, koma adzidzalola Aisraeli kuti akhale ndi zigawo zawozawo.
It shall be to him for a possession in the land in Israel. And my rulers shall no more oppress my people, but they shall give the land to the house of Israel according to their tribes.
9 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsono pakwana, inu akalonga a Israeli. Lekani nkhanza zanu ndi kupondereza anthu anga. Muzitsata chilungamo ndi kuchita zokomera anthu. Musapirikitse anthu anga mʼdzikomo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Thus says the lord Jehovah: Let it suffice you, O rulers of Israel. Remove violence and spoil, and execute justice and righteousness. Take away your exactions from my people, says the lord Jehovah.
10 Miyeso yanu yoyezera zinthu monga efa ndi bati zizikhala zokhulupirika.
Ye shall have just balances, and a just ephah, and a just bath.
11 Efa ndi bati ikhale miyeso yolingana kukula kwake. Muyeso wa homeri ukhale wokwanira mabati khumi, ukhalenso wokwanira maefa khumi. Ndiye kuti kukula kwa miyeso iwiriyo kuzidzatsata kukula kwa homeriyo.
The ephah and the bath shall be of one measure, that the bath may contain the tenth part of a homer, and the ephah the tenth part of a homer. The measure of it shall be according to the homer.
12 Muyeso wa sekeli ukhale wokwanira magera makumi awiri. Muyeso wa mina ukhale wolemera masekeli 60.
And the shekel shall be twenty gerahs. Twenty shekels, twenty-five shekels, fifteen shekels, shall be your maneh.
13 “‘Zopereka zomwe mudzidzapereka ndi izi: chimodzi mwa zigawo 60 za tirigu, barelenso chimodzimodzi ndiponso gawo limodzi la magawo asanu ndi limodzi la efa, kulitapa pa barele wa homeri.
This is the oblation that ye shall offer: The sixth part of an ephah from a homer of wheat, and ye shall give the sixth part of an ephah from a homer of barley,
14 Gawo loyenera la mafuta, loyezedwa ndi bati, ndiponso chigawo mwa zigawo 100 za mafuta. Miyeso yake ili motere: mabati khumi afanana ndi homeri imodzi kapena kori imodzi.
and the set portion of oil, of the bath of oil, the tenth part of a bath out of the cor, which is ten baths, even a homer, (for ten baths are a homer),
15 Muperekenso nkhosa imodzi pa gulu lankhosa 200 za pa msipu wabwino wa mu Israeli. Izi zidzagwiritsidwa ntchito monga nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano ndi nsembe zopepesera milandu ya anthu. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
and one lamb of the flock, out of two hundred, from the well-watered pastures of Israel, for a meal offering, and for a burnt offering, and for peace offerings, to make atonement for them, says the lord Jehovah.
16 Anthu onse a mʼdzikomo azidzapereka zimenezi kwa mfumu ya Israeli.
All the people of the land shall give to this oblation for the ruler in Israel.
17 Udzakhala udindo wa mfumu kupereka zofunikira ku nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, ndi nsembe za zakumwa pa nthawi ya zikondwerero, chikondwerero cha mwezi watsopano ndi cha masabata, nthawi yonse ya zikondwerero zoyikika za Aisraeli. Mfumuyo idzapereka nsembe zopepesera machimo, nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano kuti zikhale nsembe zopepesera machimo a Aisraeli.
And it shall be the ruler's part to give the burnt offerings, and the meal offerings, and the drink offerings, in the feasts, and on the new moons, and on the sabbaths, in all the appointed feasts of the house of Israel. He shall prepare the sin offering, and the meal offering, and the burnt offering, and the peace offerings, to make atonement for the house of Israel.
18 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba muzitenga mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndi kuchita mwambo woyeretsa malo opatulika.
Thus says the lord Jehovah: In the first month, in the first day of the month, thou shall take a young bullock without blemish, and thou shall cleanse the sanctuary.
19 Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera machimoyo ndipo awapake pa mphuthu za Nyumba ya Mulungu, pa ngodya zinayi za pamwamba pa guwa lansembe ndi pa mphuthu za pa chipata cha bwalo la mʼkati.
And the priest shall take of the blood of the sin offering, and put it upon the door-posts of the house, and upon the four corners of the ledge of the altar, and upon the posts of the gate of the inner court.
20 Muzichita chimodzimodzi pa tsiku la chisanu ndi chiwiri la mwezi, kuchitira aliyense amene wachimwa mosafuna kapena mosadziwa. Motero Nyumba ya Mulungu idzakhala yoyera.
And so thou shall do on the seventh day of the month for each one who errs, and for him who is simple. So shall ye make atonement for the house.
21 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita chikondwerero cha Paska, chikondwerero chake cha masiku asanu ndi awiri. Pa masiku amenewo muzidzadya buledi wopanda yisiti.
In the first month, in the fourteenth day of the month, ye shall have the Passover, a feast of seven days. Unleavened bread shall be eaten.
22 Pa tsiku loyamba la chikondwererocho, mfumu ipereke nsembe ya ngʼombe yayimuna monga nsembe yopepesera machimo ake ndi machimo a anthu onse a mʼdziko.
And upon that day the ruler shall prepare for himself and for all the people of the land a bullock for a sin offering.
23 Pa masiku asanu ndi awiri a chikondwererocho, mfumu ipereke kwa Yehova nsembe zopsereza izi: ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, zonsezi zopanda chilema. Pa masikuwa mfumu iziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
And the seven days of the feast he shall prepare a burnt offering to Jehovah, seven bullocks and seven rams without blemish daily the seven days, and a he-goat daily for a sin offering.
24 Pamodzi ndi ngʼombe iliyonse yayimuna ndi nkhosa iliyonse yayimuna, mfumu ipereke chopereka cha chakudya chokwanira efa imodzi ndiponso mafuta okwanira hini imodzi pa efa iliyonse.
And he shall prepare a meal offering, an ephah for a bullock, and an ephah for a ram, and a hin of oil to an ephah.
25 “‘Pa nthawi ya chikondwerero cha masiku asanu ndi awiri, chimene chimayamba pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mfumuyo iziperekanso nsembe za mtundu womwewo: nsembe zopepesera machimo, nsembe zopsereza, nsembe za chakudya ndi za mafuta.’”
In the seventh month, in the fifteenth day of the month, in the feast, he shall do the like the seven days, according to the sin offering, according to the burnt offering, and according to the meal offering, and according to the oil.

< Ezekieli 45 >