< Ezekieli 45 >
1 “‘Mukamadzagawa dziko kuti fuko lililonse lilandire cholowa chake, mudzapatuleko chigawo chimodzi kuti chikhale cha Yehova. Mulitali mwake mudzakhale makilomita khumi ndi awiri ndi theka ndipo mulifupi mwake makilomita khumi. Malo onsewo adzakhale opatulika.
Kad budete zemlju ždrijebom dijelili u baštinu, prinesite kao prinos pridržan Jahvi jedan sveti dio zemlje, dugačak dvadeset i pet tisuća lakata, širok deset tisuća; to neka bude sveto područje uzduž i poprijeko.
2 Mʼkati mwa chigawo chimenechi, malo a mamita 250 mbali iliyonse adzakhala malo a Nyumba ya Mulungu. Pozungulira pake ponse padzakhala malo a mamita 25.
Od toga neka bude za Svetište četvorina od pet stotina lakata i čistina od deset lakata uokolo.
3 Mʼchigawo chopatulikacho muyeze malo a makilomita 12 ndi theka mulitali mwake, makilomita asanu mulifupi mwake. Pamenepo padzakhala malo opatulika kwambiri.
Od toga područja izmjeri u dužinu dvadeset i pet tisuća lakata, a u širinu deset tisuća: tu neka bude Svetište - Svetinja nad svetinjama.
4 Malo opatulika amenewa adzakhalanso a ansembe amene amatumikira ku malo opatulika, amene amayandikira Yehova kuti amutumikire. Pamenepo padzakhala malo omangapo nyumba zawo ndi malo omangapo Nyumba ya Mulungu.
Taj sveti dio zemlje pripada svećenicima koji služe u Svetištu i koji pristupaju k Jahvi da mu služe: tu neka im bude mjesto za kuće; i to neka je sveto mjesto koje pripada Svetištu.
5 Alevi otumikira ku Nyumba ya Mulungu adzakhala ndi malo a makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake ndi makilomita asanu mulifupi mwake. Kumeneko ndiko kudzakhale midzi yawo.
Dvadeset i pet tisuća u dužinu i deset tisuća u širinu neka bude levitima koji služe Domu: neka ondje sagrade gradove u kojima će stanovati.
6 “‘Moyandikana ndi malo opatulika, padzakhale malo a makilomita awiri ndi theka mulifupi mwake ndi makilomita khumi ndi awiri ndi theka mulitali mwake; kuti akhale malo a mzinda. Malo amenewa adzakhala a Aisraeli onse.
Za posjed gradu dodijelite pet tisuća lakata u širinu i dvadeset i pet tisuća lakata u dužinu usporedo sa svetim područjem: to će pripadati svemu domu Izraelovu.
7 “‘Mfumu idzakhale ndi malo okhudzana ndi chigawo cha malo opatulika ndi cha mzinda. Malowo ayandikane ndi zigawozo chakummawa ndi chakumadzulo. Malowo atalike ngati chigawo chimodzi cha fuko la Israeli kuyambira ku malire akummawa mpaka ku malire akumadzulo.
Knezu pripada dio s obje strane svetoga područja i gradskoga posjeda - duž svetoga područja i duž gradskoga posjeda - od zapadne strane prema zapadu i od istočne strane prema istoku, a dužina neka bude jednaka svakom tom dijelu, od zapadne do istočne granice.
8 Malowa adzakhala chigawo cha mfumu mu Israeli. Choncho mafumu anga sadzazunzanso anthu anga, koma adzidzalola Aisraeli kuti akhale ndi zigawo zawozawo.
To neka bude njegova zemlja, posjed u Izraelu, da knezovi više ne tlače narod moj i da zemlju dadu domu Izraelovu po plemenima.'
9 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsono pakwana, inu akalonga a Israeli. Lekani nkhanza zanu ndi kupondereza anthu anga. Muzitsata chilungamo ndi kuchita zokomera anthu. Musapirikitse anthu anga mʼdzikomo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Ovako govori Jahve Gospod: 'Dosta je, knezovi Izraelovi! Okanite se nasilja i pljačke i vršite zakon i pravdu; izbavite narod moj od svojih tražbina - riječ je Jahve Gospoda.
10 Miyeso yanu yoyezera zinthu monga efa ndi bati zizikhala zokhulupirika.
Mjerite pravom mjerom: pravom efom i pravim batom.
11 Efa ndi bati ikhale miyeso yolingana kukula kwake. Muyeso wa homeri ukhale wokwanira mabati khumi, ukhalenso wokwanira maefa khumi. Ndiye kuti kukula kwa miyeso iwiriyo kuzidzatsata kukula kwa homeriyo.
Efa i bat neka jednako hvataju: bat neka iznosi desetinu homera i efa desetinu homera - neka im mjera bude prema homeru.
12 Muyeso wa sekeli ukhale wokwanira magera makumi awiri. Muyeso wa mina ukhale wolemera masekeli 60.
Šekel neka bude dvadeset gera; mina neka vam bude dvadeset šekela, dvadeset i pet šekela i petnaest šekela.
13 “‘Zopereka zomwe mudzidzapereka ndi izi: chimodzi mwa zigawo 60 za tirigu, barelenso chimodzimodzi ndiponso gawo limodzi la magawo asanu ndi limodzi la efa, kulitapa pa barele wa homeri.
Ovo je prinos koji ćete prinositi: šestinu efe od svakoga homera pšenice i šestinu efe od svakoga homera ječma.
14 Gawo loyenera la mafuta, loyezedwa ndi bati, ndiponso chigawo mwa zigawo 100 za mafuta. Miyeso yake ili motere: mabati khumi afanana ndi homeri imodzi kapena kori imodzi.
A za ulje ova je uredba: desetina bata od svakoga kora - deset bata jedan je kor.
15 Muperekenso nkhosa imodzi pa gulu lankhosa 200 za pa msipu wabwino wa mu Israeli. Izi zidzagwiritsidwa ntchito monga nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano ndi nsembe zopepesera milandu ya anthu. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Od svakoga stada od dvije stotine ovaca sa sočnih izraelskih pašnjaka po jednu ovcu za žrtvu prinosnicu, paljenicu i pričesnicu - vama za pomirenje - riječ je Jahve Gospoda.
16 Anthu onse a mʼdzikomo azidzapereka zimenezi kwa mfumu ya Israeli.
Sav narod zemlje duguje ovaj prinos knezu Izraelovu.
17 Udzakhala udindo wa mfumu kupereka zofunikira ku nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, ndi nsembe za zakumwa pa nthawi ya zikondwerero, chikondwerero cha mwezi watsopano ndi cha masabata, nthawi yonse ya zikondwerero zoyikika za Aisraeli. Mfumuyo idzapereka nsembe zopepesera machimo, nsembe za chakudya, nsembe zopsereza, ndi nsembe zachiyanjano kuti zikhale nsembe zopepesera machimo a Aisraeli.
A knez je dužan davati žrtve paljenice, prinosnice i ljevanice za svetkovine i za mlađake, za subote i blagdane doma Izraelova: on neka se postara za okajnicu, za pomirnicu, prinosnicu, paljenicu i pričesnicu za pomirenje doma Izraelova.'
18 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku loyamba la mwezi woyamba muzitenga mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndi kuchita mwambo woyeretsa malo opatulika.
Ovako govori Jahve Gospod: 'Prvoga mjeseca, prvoga dana u mjesecu, uzmi june bez mane i okaj njime Svetište.
19 Wansembe atengeko magazi a nsembe yopepesera machimoyo ndipo awapake pa mphuthu za Nyumba ya Mulungu, pa ngodya zinayi za pamwamba pa guwa lansembe ndi pa mphuthu za pa chipata cha bwalo la mʼkati.
Svećenik neka uzme krvi te žrtve okajnice i neka njome pomaže dovratnike Doma i sva četiri ugla pojasa žrtveničkoga i dovratnike vrata unutrašnjega predvorja.
20 Muzichita chimodzimodzi pa tsiku la chisanu ndi chiwiri la mwezi, kuchitira aliyense amene wachimwa mosafuna kapena mosadziwa. Motero Nyumba ya Mulungu idzakhala yoyera.
Tako neka učini i sedmoga dana istoga mjeseca za svakoga koji je sagriješio iz slabosti i neznanja. Tako ćete dovršiti pomirenje Doma.
21 “‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita chikondwerero cha Paska, chikondwerero chake cha masiku asanu ndi awiri. Pa masiku amenewo muzidzadya buledi wopanda yisiti.
Prvoga mjeseca, četrnaestoga dana u mjesecu, svetkujte Pashu, sedmodnevni blagdan, kad se blaguju beskvasni hljebovi.
22 Pa tsiku loyamba la chikondwererocho, mfumu ipereke nsembe ya ngʼombe yayimuna monga nsembe yopepesera machimo ake ndi machimo a anthu onse a mʼdziko.
Toga dana neka knez za se i za sav puk zemlje prinese june za okajnicu.
23 Pa masiku asanu ndi awiri a chikondwererocho, mfumu ipereke kwa Yehova nsembe zopsereza izi: ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri, nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri, zonsezi zopanda chilema. Pa masikuwa mfumu iziperekanso mbuzi imodzi yayimuna ngati nsembe yopepesera machimo.
Sedam dana blagdana neka prinosi za paljenicu Jahvi sedam junčića i sedam ovnova bez mane - svaki dan tih sedam dana - i svaki dan jarca kao okajnicu.
24 Pamodzi ndi ngʼombe iliyonse yayimuna ndi nkhosa iliyonse yayimuna, mfumu ipereke chopereka cha chakudya chokwanira efa imodzi ndiponso mafuta okwanira hini imodzi pa efa iliyonse.
A kao prinosnicu neka prinese efu po svakom juncu i efu po ovnu i hin ulja na svaku efu.
25 “‘Pa nthawi ya chikondwerero cha masiku asanu ndi awiri, chimene chimayamba pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mfumuyo iziperekanso nsembe za mtundu womwewo: nsembe zopepesera machimo, nsembe zopsereza, nsembe za chakudya ndi za mafuta.’”
Sedmoga mjeseca, petnaestoga dana u mjesecu, neka o blagdanu isto toliko prinosi sedam dana: isto toliko okajnica, paljenica, prinosnica i ulja.'