< Ezekieli 44 >
1 Munthu uja anabwerera nane ku chipata chakunja kwa malo opatulika, chomwe chimayangʼana kummawa. Chipatacho chinali chotseka.
І вернув мене в напрямі брами зо́внішньої святині, що обе́рнена на схід, а вона за́мкнена.
2 Yehova anandiwuza kuti, “Chipata ichi chikhale chotseka, chisatsekulidwe. Wina asalowerepo chifukwa Yehova, Mulungu wa Israeli walowera pomwepa.
І сказав мені Господь: „Брама ця буде за́мкнена, не буде відчи́нена, і ніхто не вві́йде в неї, бо в неї ввійшов Господь, Бог Ізраїлів, і вона буде за́мкнена.
3 Kalonga yekha angathe kukhala mʼmenemo ndi kumadya chakudya pamaso pa Yehova. Iye adzalowere pa njira ya ku khonde lamʼkati ndi kutulukiranso njira yomweyo.”
Князь, сам князь буде сидіти в ній, щоб їсти хліб перед Господнім лицем; сі́ньми брами він уві́йде, і сі́ньми ви́йде“.
4 Kenaka munthuyo anandidzeretsa pa chipata chakumpoto ndipo tinafika kumaso kwa Nyumba ya Mulungu. Nditapenyetsetsa ndinangoona ulemerero wa Yehova utadzaza mʼNyumba ya Mulungu, ndipo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba.
І ви́провадив мене в напрямі півні́чної брами до пе́реду храму, і побачив я, аж ось слава Господня напо́внила Госпо́дній дім! І впав я на обличчя своє.
5 Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, samala bwino ndipo uyangʼanitsitse ndi kumvetsa bwino zonse zimene ndikuwuze zokhudza malamulo ndi malangizo a Nyumbayi. Usamalitse za amene angalowe ndi kutuluka mʼNyumbayi.
І сказав мені Господь: „Сину лю́дський, зверни́ своє серце, і побач своїми очима, а своїми ву́хами послухай усе, що́ Я говоритиму з тобою щодо всіх постанов Господнього дому, і щодо всяких зако́нів його, і зве́рнеш своє серце до входу того храму в усіх ви́ходах святині.
6 Uwuze mtundu wopanduka wa Israeli kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu Aisraeli, andikwana machitidwe anu onyansawo!
І скажеш до ворохо́бників, до Ізраїлевого дому: Так говорить Господь Бог: До́сить вам усіх ваших гидот, Ізраїлів доме,
7 Munalowetsa alendo osachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi momwe mʼNyumba yanga ndipotu anayipitsa Nyumba yanga. Pamene inu munkandipatsa chakudya changa ndi magazi omwe kuwonjezera pa zonyansa zanu zonse ndiye kuti munaphwanya pangano langa.
що ви вво́дили чужи́нців, необрізаносе́рдих та необрізаноті́лих, щоб були в Моїй святині, щоб знева́жити його, Мій храм, коли прино́сили Мій хліб, лій та кров, і, крім усіх ваших гидот, зламали Мого заповіта.
8 Mʼmalo moti muzisamalira zinthu zanga zopatulika, mwayika alendo kuti aziyangʼanira malo anga opatulika.
І ви не не́сли сторо́жі святощів Моїх, але поставили їх собі за сторожі́в Моєї ва́рти в Моїй святині.
9 Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Palibe mlendo wosachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi ngakhalenso mlendo amene amakhala pakati pa Aisraeli amene adzalowe mʼmalo anga opatulika.
Так говорить Господь Бог: Кожен чужи́нець, необрізаносе́рдий та необрізанотілий, не вві́йде до Моєї святині; це і про всякого чужи́нця, що живе́ серед Ізраїлевих синів.
10 “Ndiponso Alevi amene anandisiya kutali pa nthawi imene Israeli anasochera potsata mafano, adzalangidwa chifukwa cha tchimo lawo.
І на́віть Левити, що були віддали́лися від Мене, коли блукав Ізраїль, що були зблудили від Мене за своїми божка́ми, і вони понесу́ть кару за свою вину, —
11 Adzangokhala atumiki chabe mʼmalo anga opatulika. Azidzayangʼanira zipata za Nyumba ya Mulungu ndi kugwira ntchito kumeneko. Azidzapha nyama za nsembe zopsereza ndi za nsembe zina za anthu. Choncho azidzayimirira pamaso pa anthu nʼkumawatumikira.
і будуть вони в святині Моїй служити сторожа́ми при брамах храму, і обслуговувати храм, вони будуть прино́сити цілопа́лення й жертву наро́дові, і вони будуть ставати перед ними, щоб служити їм.
12 Iwowa ankatumikira anthu popembedza mafano awo, ndipo anachititsa Aisraeli kugwa mu uchimo. Nʼchifukwa chake Ine ndikulumbira kuti iwowa ayenera kulangidwa chifukwa cha machimo awo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
За те, що вони служили їм перед їхніми бовва́нами, і стали для Ізраїлевого дому за спотика́ння на прови́ну, тому підняв Я Свою руку на них, — говорить Господь Бог, — і вони понесу́ть прови́ну свою!
13 Iwo sayenera kufika pafupi ndi Ine ndi kunditumikira ngati ansembe, kapena kuyandikira chilichonse cha zinthu zanga zopatulika, kapenanso zopereka zanga zopatulika kwambiri. Iwo adzachititsidwa manyazi chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
І вони не піді́йдуть до Мене, щоб бути священиками Мені, і щоб підхо́дити до всіх святощів Моїх, до Святого Святих, і будуть носити га́ньбу свою та гидо́ти свої, які наробили.
14 Komabe ndidzawayika kuti aziyangʼanira Nyumba yanga ndi kutumikira pa ntchito zake zonse zoyenera kuti zigwiridwe mʼmenemo.
І дам Я їх сторожами ва́рти храму щодо всієї його праці, і щодо всього, що робиться в ньому.
15 “Koma ansembe, a fuko la Levi, a banja la Zadoki amene ankatumikira mokhulupirika ku malo anga opatulika pa nthawi imene Aisraeli anasochera ndi kundisiya Ine; iwowa adzasendera kwa Ine kudzanditumikira. Adzafika pamaso panga kuti apereke nsembe za mafuta ndi magazi. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
А священики-Левити, Садокові сини, що несли сторо́жу Моєї святині, коли Ізраїлеві сини зблуди́ли були від Мене, вони набли́зяться до Мене на службу Мені, і будуть стояти перед Моїм лицем, щоб прино́сити Мені лій та кров, говорить Господь Бог.
16 Okhawa ndiwo adzalowe ku malo anga opatulika ndi kudzayandikira tebulo langa kuti adzanditumikire. Amenewa okha ndiwo adzasamalire zinthu zanga.
Вони вві́йдуть до Моєї святині, і вони набли́зяться до Мого сто́лу на службу Мені, і будуть нести Мої сторо́жі.
17 “Pamene alowa ku zipata za bwalo lamʼkati azivala zovala zabafuta. Asamavale chovala china chilichonse cha ubweya wankhosa pamene akutumikira pa zipata za bwalo la mʼkati kapena kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
I станеться, коли вони вхо́дитимуть до брами внутрішнього подві́р'я, то зодяга́тимуть льняну́ одіж, і не вві́йде на них вовна, коли вони служитимуть у брамах внутрішнього подві́р'я та назо́вні.
18 Azivala nduwira za bafuta ndi kabudula wabafuta mʼkati. Asavale chilichonse chowachititsa thukuta.
Льняні́ заво́ї будуть на їхній голові, а льняна́ спідня одежа буде на їхніх сте́гнах; не будуть опері́зуватися тим, що виклика́є піт.
19 Pamene atuluka ndi kupita ku bwalo lakunja kumene kuli anthu, azivula zovala zimene amatumikira nazo, ndipo azisiye zovalazo mu zipinda zopatulika. Pambuyo pake avale zovala zina, kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu enawo ndi zovala zawozo.
А коли вони будуть вихо́дити до зовнішнього подві́р'я, до наро́ду, здійма́тимуть ша́ти свої, в яких служили, і поскладають їх у священних кімна́тах, і зодягнуть іншу одежу, щоб своїми священними ша́тами не торкатися наро́ду.
20 “‘Ansembe asamamete mpala kapena kusunga tsitsi lalitali kwambiri, koma azingoliyepula.
А голови́ своєї вони не будуть голи́ти, і воло́сся не запу́стять, — конче будуть стри́гти волосся своє.
21 Wansembe asamwe vinyo pamene ali pafupi kulowa mʼbwalo la mʼkati.
І вина не будуть пити кожен із священиків, коли ма́ють вхо́дити до вну́трішнього подві́р'я.
22 Iwo asakwatire akazi amasiye kapena osudzulidwa; koma azikwatira anamwali osadziwa mwamuna a fuko la Israeli kapena akazi amasiye a ansembe anzawo.
А вдів та ро́звідок не братимуть собі за жінок, а братимуть тільки дівчат із насіння Ізраїлевого дому, та вдову, що буде вдовою по священикові.
23 Ansembe aziphunzitsa anthu anga kusiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, ndiponso pakati pa zinthu zoyenera ndi zosayenera kuperekedwa nsembe.
А наро́д Мій будуть вони навчати розрізняти між святим та звичайним, і зроблять їх знаю́чими різницю між нечистим та чистим.
24 “‘Pakakhala milandu, ansembe azikhala oweruza ndipo agamule milanduyo potsata malamulo anga. Atsate malamulo anga ndi malangizo anga pa za masiku anga onse a chikondwerero. Asamalirenso kuti masiku anga a Sabata akhale oyera.
А в супере́чці вони стануть, щоб судити, — правосу́ддям Моїм розсудять її, і будуть стерегти́ Зако́ни Мої, і устави Мої при всіх святах Моїх, і суботи Мої будуть святити!
25 “‘Wansembe asadziyipitse pokhudza munthu wakufa, pokhapokha ngati wakufayo ndi abambo ake kapena amayi ake, mwana wake wamwamuna kapena wamkazi, mʼbale wake kapena mlongo wake wosakwatiwa.
І до мертвої люди́ни не піді́йдуть, щоб не занечи́стити себе, а тільки ради батька й матері, і ради сина, і дочки́, і ради брата й сестри, що не належала чоловікові, занечи́стяться.
26 Atatha kuyeretsedwa adikirebe masiku asanu ndi awiri kuti ayere ndithu.
А по його очи́щенні прирахують йому ще сім день.
27 Pa tsiku lomwe akukalowa mʼbwalo la mʼkati la malo opatulika kuti akatumikire, apereke nsembe yopepesera machimo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
А того дня, коли він входить до святині, до вну́трішнього подвір'я, щоб служити в святині, він принесе свою жертву за гріх, говорить Госпо́дь Бог.
28 “‘Ansembe asadzakhale ndi cholowa chilichonse ayi. Cholowa chawo ndi Ine. Musadzawapatse chuma mu Israeli; Ine ndidzakhala chuma chawo.
І оце буде їм за спа́дщину: Я їхня спа́дщина, а володі́ння не дасте́ їм в Ізраїлі, — Я їхнє володі́ння!
29 Iwo azidzadya nsembe ya chakudya, nsembe yopereka chifukwa cha tchimo ndi nsembe yopepesera machimo. Zinthu zonse zoperekedwa kwa Yehova mu Israeli zidzakhala zawo.
Жертву хлі́бну, і жертву за гріх, і жертву за провину, — оце будуть вони їсти, і все закляте в Ізраїлі буде їхнє.
30 Zabwino za zipatso zanu zoyambirira kucha ndiponso mphatso zanu zonse zapadera zidzakhala za ansembe. Inu muziwapatsa chigawo choyamba cha ufa wanu kuti pa nyumba panu pakhale madalitso.
І перше з усяких первонаро́джених зо всього, і всякі прино́шення всього зо всіх ваших прино́шень буде священикам, і поча́ток ваших діж дасте священикові, щоб він поклав благослове́ння на вашому домі.
31 Ansembe sayenera kudya kalikonse kofa kokha, kaya mbalame, kapena nyama. Kapena yochita kujiwa.’”
Усякого па́дла та пошмато́ваного з птаства та скоти́ни священики не будуть їсти.