< Ezekieli 44 >

1 Munthu uja anabwerera nane ku chipata chakunja kwa malo opatulika, chomwe chimayangʼana kummawa. Chipatacho chinali chotseka.
И одведе ме опет к вратима спољашњим од светиње, која гледају на исток, а она беху затворена.
2 Yehova anandiwuza kuti, “Chipata ichi chikhale chotseka, chisatsekulidwe. Wina asalowerepo chifukwa Yehova, Mulungu wa Israeli walowera pomwepa.
И рече ми Господ: Ова врата нека буду затворена и да се не отварају, и нико да не улази на њих, јер је Господ Бог Израиљев ушао на њих; зато нека буду затворена.
3 Kalonga yekha angathe kukhala mʼmenemo ndi kumadya chakudya pamaso pa Yehova. Iye adzalowere pa njira ya ku khonde lamʼkati ndi kutulukiranso njira yomweyo.”
За кнеза су; сам кнез нека седа на њима да једе хлеб пред Господом; кроз трем од ових врата нека улази и истим путем нека излази.
4 Kenaka munthuyo anandidzeretsa pa chipata chakumpoto ndipo tinafika kumaso kwa Nyumba ya Mulungu. Nditapenyetsetsa ndinangoona ulemerero wa Yehova utadzaza mʼNyumba ya Mulungu, ndipo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba.
И одведе ме к северним вратима пред дом; и видех, и гле, дом Господњи беше пун славе Господње, и падох на лице своје.
5 Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, samala bwino ndipo uyangʼanitsitse ndi kumvetsa bwino zonse zimene ndikuwuze zokhudza malamulo ndi malangizo a Nyumbayi. Usamalitse za amene angalowe ndi kutuluka mʼNyumbayi.
И рече ми Господ: Сине човечји, пази срцем својим и види очима својим и слушај ушима својим шта ћу ти казати за све уредбе дома Господњег и за све законе Његове; пази срцем својим на све улазе у дом и на све излазе из светиње.
6 Uwuze mtundu wopanduka wa Israeli kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu Aisraeli, andikwana machitidwe anu onyansawo!
И реци одметничком дому Израиљевом: Овако вели Господ Господ: Доста је гадова ваших, доме Израиљев,
7 Munalowetsa alendo osachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi momwe mʼNyumba yanga ndipotu anayipitsa Nyumba yanga. Pamene inu munkandipatsa chakudya changa ndi magazi omwe kuwonjezera pa zonyansa zanu zonse ndiye kuti munaphwanya pangano langa.
Што уводисте туђинце необрезаног срца и необрезаног тела да буду у мојој светињи да скврне дом мој, и приносисте мој хлеб, претилину и крв, и тамо преступаше мој завет осим свих гадова ваших;
8 Mʼmalo moti muzisamalira zinthu zanga zopatulika, mwayika alendo kuti aziyangʼanira malo anga opatulika.
И не извршавасте шта треба за моју светињу, него постависте људе по својој вољи да извршују шта треба у мојој светињи.
9 Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Palibe mlendo wosachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi ngakhalenso mlendo amene amakhala pakati pa Aisraeli amene adzalowe mʼmalo anga opatulika.
Овако вели Господ Господ: Ни један туђин необрезаног срца и необрезаног тела да не долази у моју светињу, ни један од свих туђинаца који су међу синовима Израиљевим.
10 “Ndiponso Alevi amene anandisiya kutali pa nthawi imene Israeli anasochera potsata mafano, adzalangidwa chifukwa cha tchimo lawo.
А Левити који одступаше од мене кад зађе Израиљ, који зађоше од мене за гадним боговима својим, носиће безакоње своје.
11 Adzangokhala atumiki chabe mʼmalo anga opatulika. Azidzayangʼanira zipata za Nyumba ya Mulungu ndi kugwira ntchito kumeneko. Azidzapha nyama za nsembe zopsereza ndi za nsembe zina za anthu. Choncho azidzayimirira pamaso pa anthu nʼkumawatumikira.
И биће слуге у мојој светињи у служби на вратима од дома служећи дому; они ће клати жртве паљенице и друге жртве народу, и стајаће пред њима служиће им.
12 Iwowa ankatumikira anthu popembedza mafano awo, ndipo anachititsa Aisraeli kugwa mu uchimo. Nʼchifukwa chake Ine ndikulumbira kuti iwowa ayenera kulangidwa chifukwa cha machimo awo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Што им служише пред гадним боговима њиховим и бише дому Израиљевом спотицање на безакоње, зато подигох руку своју на њих, говори Господ Господ, да ће носити безакоње своје,
13 Iwo sayenera kufika pafupi ndi Ine ndi kunditumikira ngati ansembe, kapena kuyandikira chilichonse cha zinthu zanga zopatulika, kapenanso zopereka zanga zopatulika kwambiri. Iwo adzachititsidwa manyazi chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
И неће приступати к мени да ми врше свештеничку службу, нити којој светињи мојој, ни светињи над светињама неће приступати, него ће носити срамоту своју и гадове своје, које чинише.
14 Komabe ndidzawayika kuti aziyangʼanira Nyumba yanga ndi kutumikira pa ntchito zake zonse zoyenera kuti zigwiridwe mʼmenemo.
Него ћу их поставити за чуваре дому на сваку службу његову и на све што бива у њему.
15 “Koma ansembe, a fuko la Levi, a banja la Zadoki amene ankatumikira mokhulupirika ku malo anga opatulika pa nthawi imene Aisraeli anasochera ndi kundisiya Ine; iwowa adzasendera kwa Ine kudzanditumikira. Adzafika pamaso panga kuti apereke nsembe za mafuta ndi magazi. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
А свештеници Левити синови Садокови, који извршаваху шта треба у мојој светињи, кад синови Израиљеви зађоше од мене, они ће приступати к мени да ми служе, и стајаће преда мном приносећи ми претилину и крв, говори Господ Господ.
16 Okhawa ndiwo adzalowe ku malo anga opatulika ndi kudzayandikira tebulo langa kuti adzanditumikire. Amenewa okha ndiwo adzasamalire zinthu zanga.
Они нека улазе у моју светињу и они нека приступају к столу мом да ми служе и нека извршују шта сам заповедио да се извршује.
17 “Pamene alowa ku zipata za bwalo lamʼkati azivala zovala zabafuta. Asamavale chovala china chilichonse cha ubweya wankhosa pamene akutumikira pa zipata za bwalo la mʼkati kapena kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
И кад улазе на врата унутрашњег трема, нека обуку ланене хаљине, и ништа да не буде на њима вунено кад служе на вратима унутрашњег трема и у њему.
18 Azivala nduwira za bafuta ndi kabudula wabafuta mʼkati. Asavale chilichonse chowachititsa thukuta.
На главама нека им буду капе ланене и гаће ланене по бедрима, и да се не пашу ничим ода шта би се знојили.
19 Pamene atuluka ndi kupita ku bwalo lakunja kumene kuli anthu, azivula zovala zimene amatumikira nazo, ndipo azisiye zovalazo mu zipinda zopatulika. Pambuyo pake avale zovala zina, kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu enawo ndi zovala zawozo.
А кад излазе у трем спољашњи, у спољашњи трем к народу, нека свуку са себе хаљине у којима служе, и оставе их у клетима светим, па нека обуку друге хаљине, да не освећују народ хаљинама својим.
20 “‘Ansembe asamamete mpala kapena kusunga tsitsi lalitali kwambiri, koma azingoliyepula.
И главе своје да не брију, а ни косе да не остављају, него нека стрижу главе своје.
21 Wansembe asamwe vinyo pamene ali pafupi kulowa mʼbwalo la mʼkati.
И вино да не пије ниједан свештеник кад хоће да уђе у унутрашњи трем.
22 Iwo asakwatire akazi amasiye kapena osudzulidwa; koma azikwatira anamwali osadziwa mwamuna a fuko la Israeli kapena akazi amasiye a ansembe anzawo.
И удовицом ни пуштеницом да се не жене, него девојком од семена дома Израиљевог или удовицом свештеничком нека се жене.
23 Ansembe aziphunzitsa anthu anga kusiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, ndiponso pakati pa zinthu zoyenera ndi zosayenera kuperekedwa nsembe.
И народ мој нека уче шта је свето шта ли није свето, и нека их уче распознавати нечисто од чистог.
24 “‘Pakakhala milandu, ansembe azikhala oweruza ndipo agamule milanduyo potsata malamulo anga. Atsate malamulo anga ndi malangizo anga pa za masiku anga onse a chikondwerero. Asamalirenso kuti masiku anga a Sabata akhale oyera.
А у распри нека стану да суде, по мојим законима нека суде, и законе моје и уредбе моје нека држе о свим празницима мојим, и суботе моје нека светкују.
25 “‘Wansembe asadziyipitse pokhudza munthu wakufa, pokhapokha ngati wakufayo ndi abambo ake kapena amayi ake, mwana wake wamwamuna kapena wamkazi, mʼbale wake kapena mlongo wake wosakwatiwa.
И к мртвацу да не иду да се не оскврне; само за оцем и за матером и за сином и за кћерју, за братом и за сестром неудатом могу се оскврнити.
26 Atatha kuyeretsedwa adikirebe masiku asanu ndi awiri kuti ayere ndithu.
А кад се очисти, нека му се броји седам дана.
27 Pa tsiku lomwe akukalowa mʼbwalo la mʼkati la malo opatulika kuti akatumikire, apereke nsembe yopepesera machimo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
И у који би дан ушао у светињу, у трем унутрашњи, да служи у светињи, нека принесе жртву за грех свој, говори Господ Господ.
28 “‘Ansembe asadzakhale ndi cholowa chilichonse ayi. Cholowa chawo ndi Ine. Musadzawapatse chuma mu Israeli; Ine ndidzakhala chuma chawo.
А наследство што ће имати, ја сам њихово наследство; и ви им не дајте достојања у Израиљу, ја сам њихово достојање.
29 Iwo azidzadya nsembe ya chakudya, nsembe yopereka chifukwa cha tchimo ndi nsembe yopepesera machimo. Zinthu zonse zoperekedwa kwa Yehova mu Israeli zidzakhala zawo.
Дар и жртву за грех и жртву за кривицу они ће јести; и све заветовано у Израиљу њихово ће бити.
30 Zabwino za zipatso zanu zoyambirira kucha ndiponso mphatso zanu zonse zapadera zidzakhala za ansembe. Inu muziwapatsa chigawo choyamba cha ufa wanu kuti pa nyumba panu pakhale madalitso.
И првине од сваког првог рода и сви приноси подизани од свега између свих приноса ваших биће свештеницима; и првине од теста свог даваћете свештенику да би почивао благослов на домовима вашим.
31 Ansembe sayenera kudya kalikonse kofa kokha, kaya mbalame, kapena nyama. Kapena yochita kujiwa.’”
Свештеници да не једу мрцино ни шта зверка раскине, било птица или шта од стоке.

< Ezekieli 44 >