< Ezekieli 44 >

1 Munthu uja anabwerera nane ku chipata chakunja kwa malo opatulika, chomwe chimayangʼana kummawa. Chipatacho chinali chotseka.
Puis, il me ramena du côté de la porte extérieure du Sanctuaire, qui est tournée vers l’Est; mais elle était fermée.
2 Yehova anandiwuza kuti, “Chipata ichi chikhale chotseka, chisatsekulidwe. Wina asalowerepo chifukwa Yehova, Mulungu wa Israeli walowera pomwepa.
Et l’Eternel me dit: "Cette porte restera fermée, on ne l’ouvrira point, et personne n’entrera par elle, car l’Eternel Dieu d’Israël, est entré par elle: elle restera donc fermée.
3 Kalonga yekha angathe kukhala mʼmenemo ndi kumadya chakudya pamaso pa Yehova. Iye adzalowere pa njira ya ku khonde lamʼkati ndi kutulukiranso njira yomweyo.”
C’Est le prince, en sa qualité de prince, qui s’y asseoira pour manger le pain devant l’Eternel; c’est par la voie du vestibule de la porte qu’il entrera et par cette voie qu’il sortira."
4 Kenaka munthuyo anandidzeretsa pa chipata chakumpoto ndipo tinafika kumaso kwa Nyumba ya Mulungu. Nditapenyetsetsa ndinangoona ulemerero wa Yehova utadzaza mʼNyumba ya Mulungu, ndipo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba.
Puis, il me conduisit par la porte du Nord jusqu’au front de l’édifice, et je vis soudain la gloire de l’Eternel remplir le temple de l’Eternel, et je tombai sur ma face.
5 Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, samala bwino ndipo uyangʼanitsitse ndi kumvetsa bwino zonse zimene ndikuwuze zokhudza malamulo ndi malangizo a Nyumbayi. Usamalitse za amene angalowe ndi kutuluka mʼNyumbayi.
L’Eternel me dit: "Fils de l’homme, applique ton attention, vois de tes yeux, et écoute de tes oreilles tout ce que je vais te dire touchant les ordonnances de la maison de l’Eternel et toutes ses lois; dirige ton attention sur l’accès de l’édifice ainsi que sur toutes les issues du Sanctuaire.
6 Uwuze mtundu wopanduka wa Israeli kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu Aisraeli, andikwana machitidwe anu onyansawo!
Et tu diras à la rébellion, à la maison d’Israël: Ainsi parle le Seigneur Dieu: C’En est assez de toutes vos turpitudes, maison d’Israël!
7 Munalowetsa alendo osachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi momwe mʼNyumba yanga ndipotu anayipitsa Nyumba yanga. Pamene inu munkandipatsa chakudya changa ndi magazi omwe kuwonjezera pa zonyansa zanu zonse ndiye kuti munaphwanya pangano langa.
Car vous avez introduit des enfants de l’étranger, incirconcis de coeur et incirconcis de chair, dans mon sanctuaire, pour profaner ma maison, quand vous me présentiez mon pain, graisse et sang et portiez atteinte à mon alliance à côté de toutes vos autres turpitudes.
8 Mʼmalo moti muzisamalira zinthu zanga zopatulika, mwayika alendo kuti aziyangʼanira malo anga opatulika.
Et vous n’avez pas veillé à la garde de mes choses saintes, mais vous les avez chargés, eux, d’assurer le service de mon sanctuaire à votre intention."
9 Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Palibe mlendo wosachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi ngakhalenso mlendo amene amakhala pakati pa Aisraeli amene adzalowe mʼmalo anga opatulika.
Ainsi parle le Seigneur Dieu: "Aucun fils d’étranger, incirconcis de coeur et incirconcis de chair, n’entrera dans mon sanctuaire, aucun fils d’étranger se trouvant parmi les enfants d’Israël.
10 “Ndiponso Alevi amene anandisiya kutali pa nthawi imene Israeli anasochera potsata mafano, adzalangidwa chifukwa cha tchimo lawo.
Mais les Lévites eux-mêmes, qui s’étaient éloignés de moi quand Israël faisait fausse route, qui m’avaient abandonné pour suivre leurs idoles, ils porteront la peine de leur faute.
11 Adzangokhala atumiki chabe mʼmalo anga opatulika. Azidzayangʼanira zipata za Nyumba ya Mulungu ndi kugwira ntchito kumeneko. Azidzapha nyama za nsembe zopsereza ndi za nsembe zina za anthu. Choncho azidzayimirira pamaso pa anthu nʼkumawatumikira.
Ils seront dans mon sanctuaire des serviteurs, des surveillants préposés aux portes de l’édifice, et feront la corvée de la maison; ce sont eux qui immoleront l’holocauste et les sacrifices pour le peuple et qui se tiendront devant eux pour les servir.
12 Iwowa ankatumikira anthu popembedza mafano awo, ndipo anachititsa Aisraeli kugwa mu uchimo. Nʼchifukwa chake Ine ndikulumbira kuti iwowa ayenera kulangidwa chifukwa cha machimo awo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Parce qu’ils les ont servis devant leurs idoles et ont été pour la maison d’Israël une cause de péché, c’est pourquoi j’ai levé ma main contre eux, dit le Seigneur Dieu, et ils porteront la peine de leur faute.
13 Iwo sayenera kufika pafupi ndi Ine ndi kunditumikira ngati ansembe, kapena kuyandikira chilichonse cha zinthu zanga zopatulika, kapenanso zopereka zanga zopatulika kwambiri. Iwo adzachititsidwa manyazi chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
Ils ne s’approcheront pas de moi pour exercer mon sacerdoce, ils ne s’approcheront d’aucune de mes saintetés, des objets tout à fait saints: ainsi ils porteront leur opprobre et la peine de leurs abominations, qu’ils ont commises.
14 Komabe ndidzawayika kuti aziyangʼanira Nyumba yanga ndi kutumikira pa ntchito zake zonse zoyenera kuti zigwiridwe mʼmenemo.
Je ferai d’eux des préposés à la surveillance de la maison, en ce qui en concerne la corvée et tout ce qui s’y fait.
15 “Koma ansembe, a fuko la Levi, a banja la Zadoki amene ankatumikira mokhulupirika ku malo anga opatulika pa nthawi imene Aisraeli anasochera ndi kundisiya Ine; iwowa adzasendera kwa Ine kudzanditumikira. Adzafika pamaso panga kuti apereke nsembe za mafuta ndi magazi. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Quant aux pontifes Lévites, descendants de Çadok, qui ont veillé à la garde de mon sanctuaire, tandis que les enfants d’Israël s’égaraient loin de moi, ce sont eux qui s’approcheront de moi pour me servir et se tiendront en ma présence pour m’offrir la graisse et le sang, dit le Seigneur Dieu.
16 Okhawa ndiwo adzalowe ku malo anga opatulika ndi kudzayandikira tebulo langa kuti adzanditumikire. Amenewa okha ndiwo adzasamalire zinthu zanga.
Ce sont eux qui auront accès dans mon sanctuaire, eux qui s’approcheront de ma table pour me servir et veilleront à mon observance.
17 “Pamene alowa ku zipata za bwalo lamʼkati azivala zovala zabafuta. Asamavale chovala china chilichonse cha ubweya wankhosa pamene akutumikira pa zipata za bwalo la mʼkati kapena kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
Lorsqu’ils franchiront les portes du parvis intérieur, ils se vêtiront d’habillements de lin; ils ne porteront pas de laine pendant qu’ils fonctionneront aux portes du parvis intérieur et dans le temple.
18 Azivala nduwira za bafuta ndi kabudula wabafuta mʼkati. Asavale chilichonse chowachititsa thukuta.
Des turbans de lin entoureront leur tête, des caleçons de lin leurs reins: ils ne se ceindront d’aucune étoffe échauffante.
19 Pamene atuluka ndi kupita ku bwalo lakunja kumene kuli anthu, azivula zovala zimene amatumikira nazo, ndipo azisiye zovalazo mu zipinda zopatulika. Pambuyo pake avale zovala zina, kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu enawo ndi zovala zawozo.
Et quand ils passeront dans le parvis extérieur, dans le parvis extérieur où se tient le peuple, ils ôteront les vêtements dans lesquels ils fonctionnent, les déposeront dans les salles consacrées et en mettront d’autres, pour ne pas sanctifier le peuple par leurs vêtements.
20 “‘Ansembe asamamete mpala kapena kusunga tsitsi lalitali kwambiri, koma azingoliyepula.
Ils ne devront ni raser leur chevelure, ni la laisser croître inculte, ils devront la tailler.
21 Wansembe asamwe vinyo pamene ali pafupi kulowa mʼbwalo la mʼkati.
Le vin, aucun prêtre n’en boira, quand il aura à pénétrer au parvis intérieur.
22 Iwo asakwatire akazi amasiye kapena osudzulidwa; koma azikwatira anamwali osadziwa mwamuna a fuko la Israeli kapena akazi amasiye a ansembe anzawo.
Ils ne prendront pour épouse ni veuve ni femme répudiée; ils n’épouseront que des vierges issues de la maison d’Israël, ou une veuve, si c’est la veuve d’un pontife.
23 Ansembe aziphunzitsa anthu anga kusiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, ndiponso pakati pa zinthu zoyenera ndi zosayenera kuperekedwa nsembe.
Ils enseigneront à mon peuple à discerner le sacré du profane, ils lui feront connaître la distinction de l’impur et du pur.
24 “‘Pakakhala milandu, ansembe azikhala oweruza ndipo agamule milanduyo potsata malamulo anga. Atsate malamulo anga ndi malangizo anga pa za masiku anga onse a chikondwerero. Asamalirenso kuti masiku anga a Sabata akhale oyera.
Dans les litiges, ce sont eux qui exerceront la justice, et ils prononceront d’après mes lois; ils observeront mes doctrines et mes statuts pour toutes mes solennités et ils sanctifieront mes sabbats.
25 “‘Wansembe asadziyipitse pokhudza munthu wakufa, pokhapokha ngati wakufayo ndi abambo ake kapena amayi ake, mwana wake wamwamuna kapena wamkazi, mʼbale wake kapena mlongo wake wosakwatiwa.
Ils ne s’approcheront pas d’un cadavre humain, qui les souillerait; c’est seulement pour un père ou une mère, un fils ou une fille, un frère ou une sœur non mariée qu’ils pourront se souiller.
26 Atatha kuyeretsedwa adikirebe masiku asanu ndi awiri kuti ayere ndithu.
Après sa purification, l’on comptera au pontife sept jours.
27 Pa tsiku lomwe akukalowa mʼbwalo la mʼkati la malo opatulika kuti akatumikire, apereke nsembe yopepesera machimo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Et le jour où il entrera au saint lieu, dans le parvis intérieur, pour le ministère sacré, il offrira son expiatoire, dit le Seigneur Dieu.
28 “‘Ansembe asadzakhale ndi cholowa chilichonse ayi. Cholowa chawo ndi Ine. Musadzawapatse chuma mu Israeli; Ine ndidzakhala chuma chawo.
Quant à ce qui doit être leur héritage, c’est moi qui serai leur héritage; de possession, vous ne leur en donnerez point en Israël: moi, je serai leur possession.
29 Iwo azidzadya nsembe ya chakudya, nsembe yopereka chifukwa cha tchimo ndi nsembe yopepesera machimo. Zinthu zonse zoperekedwa kwa Yehova mu Israeli zidzakhala zawo.
L’Oblation, l’expiatoire et le délictif, eux seuls pourront les consommer; toute chose vouée en Israël leur appartiendra.
30 Zabwino za zipatso zanu zoyambirira kucha ndiponso mphatso zanu zonse zapadera zidzakhala za ansembe. Inu muziwapatsa chigawo choyamba cha ufa wanu kuti pa nyumba panu pakhale madalitso.
Les prémices de toute primeur quelle qu’elle soit, tout prélèvement quelconque que vous aurez à faire, appartiendront aux pontifes; de même la première part de vos pâtes, vous la donnerez au pontife, pour que la bénédiction repose sur votre maison.
31 Ansembe sayenera kudya kalikonse kofa kokha, kaya mbalame, kapena nyama. Kapena yochita kujiwa.’”
D’Aucun animal mort ou déchiré, soit volatile, soit quadrupède, les pontifes ne pourront manger.

< Ezekieli 44 >