< Ezekieli 44 >

1 Munthu uja anabwerera nane ku chipata chakunja kwa malo opatulika, chomwe chimayangʼana kummawa. Chipatacho chinali chotseka.
Il me ramena par le chemin de la porte extérieure du sanctuaire, qui donne sur l'orient, et elle était fermée.
2 Yehova anandiwuza kuti, “Chipata ichi chikhale chotseka, chisatsekulidwe. Wina asalowerepo chifukwa Yehova, Mulungu wa Israeli walowera pomwepa.
Yahvé me dit: « Cette porte sera fermée. On ne l'ouvrira pas, personne n'entrera par elle, car c'est par elle qu'est entré Yahvé, le Dieu d'Israël. C`est pourquoi elle sera fermée.
3 Kalonga yekha angathe kukhala mʼmenemo ndi kumadya chakudya pamaso pa Yehova. Iye adzalowere pa njira ya ku khonde lamʼkati ndi kutulukiranso njira yomweyo.”
Le prince s'y assiéra comme prince pour manger le pain devant Yahvé. Il entrera par le chemin du porche de la porte, et il sortira par le même chemin. »
4 Kenaka munthuyo anandidzeretsa pa chipata chakumpoto ndipo tinafika kumaso kwa Nyumba ya Mulungu. Nditapenyetsetsa ndinangoona ulemerero wa Yehova utadzaza mʼNyumba ya Mulungu, ndipo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba.
Et il me conduisit par le chemin de la porte nord, devant la maison; et je regardai, et voici, la gloire de Yahvé remplissait la maison de Yahvé; et je tombai sur ma face.
5 Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, samala bwino ndipo uyangʼanitsitse ndi kumvetsa bwino zonse zimene ndikuwuze zokhudza malamulo ndi malangizo a Nyumbayi. Usamalitse za amene angalowe ndi kutuluka mʼNyumbayi.
Yahvé me dit: « Fils d'homme, observe bien, vois de tes yeux et écoute de tes oreilles tout ce que je te dirai au sujet de toutes les ordonnances de la maison de Yahvé et de toutes ses lois; et marque bien l'entrée de la maison, ainsi que toute sortie du sanctuaire.
6 Uwuze mtundu wopanduka wa Israeli kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu Aisraeli, andikwana machitidwe anu onyansawo!
Tu diras aux rebelles, à la maison d'Israël: « Le Seigneur Yahvé dit: « Maison d'Israël, c'en est assez de toutes vos abominations,
7 Munalowetsa alendo osachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi momwe mʼNyumba yanga ndipotu anayipitsa Nyumba yanga. Pamene inu munkandipatsa chakudya changa ndi magazi omwe kuwonjezera pa zonyansa zanu zonse ndiye kuti munaphwanya pangano langa.
car vous avez introduit des étrangers, incirconcis de cœur et incirconcis de chair, dans mon sanctuaire, pour le profaner, ma maison, quand vous offrez mon pain, la graisse et le sang, et ils ont rompu mon alliance, pour ajouter à toutes vos abominations.
8 Mʼmalo moti muzisamalira zinthu zanga zopatulika, mwayika alendo kuti aziyangʼanira malo anga opatulika.
Vous n'avez pas accompli le devoir de mes choses saintes; mais vous avez établi pour vous-mêmes des interprètes de mon devoir dans mon sanctuaire. »
9 Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Palibe mlendo wosachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi ngakhalenso mlendo amene amakhala pakati pa Aisraeli amene adzalowe mʼmalo anga opatulika.
Le Seigneur Yahvé dit: « Aucun étranger, incirconcis de cœur et incirconcis de chair, n'entrera dans mon sanctuaire, parmi les étrangers qui sont parmi les enfants d'Israël.
10 “Ndiponso Alevi amene anandisiya kutali pa nthawi imene Israeli anasochera potsata mafano, adzalangidwa chifukwa cha tchimo lawo.
"''Mais les Lévites qui se sont éloignés de moi quand Israël s'est égaré, qui se sont éloignés de moi après leurs idoles, ils porteront leur iniquité.
11 Adzangokhala atumiki chabe mʼmalo anga opatulika. Azidzayangʼanira zipata za Nyumba ya Mulungu ndi kugwira ntchito kumeneko. Azidzapha nyama za nsembe zopsereza ndi za nsembe zina za anthu. Choncho azidzayimirira pamaso pa anthu nʼkumawatumikira.
Mais ils seront ministres dans mon sanctuaire, ils surveilleront les portes de la maison et feront le service dans la maison. Ils égorgeront l'holocauste et le sacrifice pour le peuple, et ils se tiendront devant lui pour le servir.
12 Iwowa ankatumikira anthu popembedza mafano awo, ndipo anachititsa Aisraeli kugwa mu uchimo. Nʼchifukwa chake Ine ndikulumbira kuti iwowa ayenera kulangidwa chifukwa cha machimo awo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Parce qu'ils les ont servis devant leurs idoles et qu'ils ont été une pierre d'achoppement et d'iniquité pour la maison d'Israël, j'ai levé ma main sur eux, dit le Seigneur Yahvé, et ils porteront la peine de leur iniquité.
13 Iwo sayenera kufika pafupi ndi Ine ndi kunditumikira ngati ansembe, kapena kuyandikira chilichonse cha zinthu zanga zopatulika, kapenanso zopereka zanga zopatulika kwambiri. Iwo adzachititsidwa manyazi chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
Ils ne s'approcheront pas de moi, pour exercer la fonction de prêtre à mon égard, ni pour s'approcher d'aucune de mes choses saintes, des choses les plus saintes; mais ils porteront leur honte et leurs abominations qu'ils ont commises.
14 Komabe ndidzawayika kuti aziyangʼanira Nyumba yanga ndi kutumikira pa ntchito zake zonse zoyenera kuti zigwiridwe mʼmenemo.
Pourtant, je les rendrai exécutants de la fonction de la maison, pour tout son service et pour tout ce qui s'y fera.
15 “Koma ansembe, a fuko la Levi, a banja la Zadoki amene ankatumikira mokhulupirika ku malo anga opatulika pa nthawi imene Aisraeli anasochera ndi kundisiya Ine; iwowa adzasendera kwa Ine kudzanditumikira. Adzafika pamaso panga kuti apereke nsembe za mafuta ndi magazi. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
"''Mais les prêtres lévitiques, fils de Tsadok, qui ont accompli le service de mon sanctuaire lorsque les enfants d'Israël s'éloignaient de moi, s'approcheront de moi pour me servir. Ils se tiendront devant moi pour m'offrir la graisse et le sang, dit le Seigneur Yahvé.
16 Okhawa ndiwo adzalowe ku malo anga opatulika ndi kudzayandikira tebulo langa kuti adzanditumikire. Amenewa okha ndiwo adzasamalire zinthu zanga.
« Ils entreront dans mon sanctuaire, ils s'approcheront de ma table, pour me servir, et ils garderont mes instructions.
17 “Pamene alowa ku zipata za bwalo lamʼkati azivala zovala zabafuta. Asamavale chovala china chilichonse cha ubweya wankhosa pamene akutumikira pa zipata za bwalo la mʼkati kapena kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
"''Lorsqu'ils entreront par les portes du parvis intérieur, ils seront revêtus de vêtements de lin. Aucune laine ne viendra sur eux pendant qu'ils feront leur service aux portes du tribunal intérieur et à l'intérieur.
18 Azivala nduwira za bafuta ndi kabudula wabafuta mʼkati. Asavale chilichonse chowachititsa thukuta.
Ils auront sur la tête des turbans de lin, et à la taille des pantalons de lin. Ils ne se vêtiront d'aucun vêtement qui les fasse transpirer.
19 Pamene atuluka ndi kupita ku bwalo lakunja kumene kuli anthu, azivula zovala zimene amatumikira nazo, ndipo azisiye zovalazo mu zipinda zopatulika. Pambuyo pake avale zovala zina, kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu enawo ndi zovala zawozo.
Lorsqu'ils iront dans le parvis extérieur, vers le peuple, ils ôteront les vêtements dans lesquels ils font le service et les déposeront dans les pièces saintes. Ils revêtiront d'autres vêtements, afin de ne pas sanctifier le peuple avec leurs vêtements.
20 “‘Ansembe asamamete mpala kapena kusunga tsitsi lalitali kwambiri, koma azingoliyepula.
"''Ils ne se raseront pas la tête et ne laisseront pas pousser leurs cheveux. Ils ne couperont que les cheveux de leur tête.
21 Wansembe asamwe vinyo pamene ali pafupi kulowa mʼbwalo la mʼkati.
Aucun des prêtres ne boira de vin lorsqu'il entrera dans le parvis intérieur.
22 Iwo asakwatire akazi amasiye kapena osudzulidwa; koma azikwatira anamwali osadziwa mwamuna a fuko la Israeli kapena akazi amasiye a ansembe anzawo.
Ils ne prendront pas pour femme une veuve ou une répudiée, mais ils prendront des vierges de la descendance de la maison d'Israël ou une veuve de prêtre.
23 Ansembe aziphunzitsa anthu anga kusiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, ndiponso pakati pa zinthu zoyenera ndi zosayenera kuperekedwa nsembe.
Ils enseigneront à mon peuple la différence entre ce qui est saint et ce qui est commun, et ils lui feront discerner ce qui est impur et ce qui est pur.
24 “‘Pakakhala milandu, ansembe azikhala oweruza ndipo agamule milanduyo potsata malamulo anga. Atsate malamulo anga ndi malangizo anga pa za masiku anga onse a chikondwerero. Asamalirenso kuti masiku anga a Sabata akhale oyera.
"''Dans une controverse, ils se tiendront debout pour juger. Ils la jugeront selon mes ordonnances. Ils observeront mes lois et mes statuts dans toutes les fêtes que j'ai fixées. Ils sanctifieront mes sabbats.
25 “‘Wansembe asadziyipitse pokhudza munthu wakufa, pokhapokha ngati wakufayo ndi abambo ake kapena amayi ake, mwana wake wamwamuna kapena wamkazi, mʼbale wake kapena mlongo wake wosakwatiwa.
"''Ils n'entreront chez aucun mort pour se souiller; mais pour le père, ou pour la mère, ou pour le fils, ou pour la fille, pour le frère, ou pour la sœur qui n'a pas eu de mari, ils pourront se souiller.
26 Atatha kuyeretsedwa adikirebe masiku asanu ndi awiri kuti ayere ndithu.
Après qu'il se sera purifié, on lui comptera sept jours.
27 Pa tsiku lomwe akukalowa mʼbwalo la mʼkati la malo opatulika kuti akatumikire, apereke nsembe yopepesera machimo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Le jour où il entrera dans le sanctuaire, dans le parvis intérieur, pour faire le service dans le sanctuaire, il offrira son sacrifice pour le péché, dit le Seigneur Yahvé.
28 “‘Ansembe asadzakhale ndi cholowa chilichonse ayi. Cholowa chawo ndi Ine. Musadzawapatse chuma mu Israeli; Ine ndidzakhala chuma chawo.
"'Ils auront un héritage: Je suis leur héritage; et vous ne leur donnerez aucune possession en Israël. Je suis leur propriété.
29 Iwo azidzadya nsembe ya chakudya, nsembe yopereka chifukwa cha tchimo ndi nsembe yopepesera machimo. Zinthu zonse zoperekedwa kwa Yehova mu Israeli zidzakhala zawo.
Ils mangeront l'offrande de gâteau, le sacrifice pour le péché et le sacrifice de culpabilité, et tout ce qui est consacré en Israël leur appartiendra.
30 Zabwino za zipatso zanu zoyambirira kucha ndiponso mphatso zanu zonse zapadera zidzakhala za ansembe. Inu muziwapatsa chigawo choyamba cha ufa wanu kuti pa nyumba panu pakhale madalitso.
Le premier de tous les prémices de chaque chose, et de chaque offrande de chaque chose, de toutes vos offrandes, sera pour le prêtre. Tu donneras aussi aux prêtres les prémices de ta pâte, afin que la bénédiction repose sur ta maison.
31 Ansembe sayenera kudya kalikonse kofa kokha, kaya mbalame, kapena nyama. Kapena yochita kujiwa.’”
Les prêtres ne mangeront pas de ce qui meurt de lui-même ou qui est déchiré, que ce soit un oiseau ou un animal.

< Ezekieli 44 >