< Ezekieli 44 >

1 Munthu uja anabwerera nane ku chipata chakunja kwa malo opatulika, chomwe chimayangʼana kummawa. Chipatacho chinali chotseka.
The man took me back to the outside gate of the sanctuary that faced to the east, but it was shut.
2 Yehova anandiwuza kuti, “Chipata ichi chikhale chotseka, chisatsekulidwe. Wina asalowerepo chifukwa Yehova, Mulungu wa Israeli walowera pomwepa.
The Lord told me, “This gate will stay shut. It is not be opened. No one is allowed to come in through it, because the Lord, the God of Israel, has passed through it. So it will stay shut.
3 Kalonga yekha angathe kukhala mʼmenemo ndi kumadya chakudya pamaso pa Yehova. Iye adzalowere pa njira ya ku khonde lamʼkati ndi kutulukiranso njira yomweyo.”
The prince himself is permitted to come and sit inside the gateway to eat in the presence of the Lord. He is to come in through the gateway's porch and leave the same way.”
4 Kenaka munthuyo anandidzeretsa pa chipata chakumpoto ndipo tinafika kumaso kwa Nyumba ya Mulungu. Nditapenyetsetsa ndinangoona ulemerero wa Yehova utadzaza mʼNyumba ya Mulungu, ndipo ndinadzigwetsa pansi chafufumimba.
The man took me to the front of the Temple through the north gate. As I looked, I saw the glory of the Lord filling his Temple, and I fell with my face to the ground.
5 Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, samala bwino ndipo uyangʼanitsitse ndi kumvetsa bwino zonse zimene ndikuwuze zokhudza malamulo ndi malangizo a Nyumbayi. Usamalitse za amene angalowe ndi kutuluka mʼNyumbayi.
The Lord told me, “Son of man, concentrate! Keep your eyes open! Listen carefully to everything I tell you about all the regulations and laws of the Lord's Temple. Pay close attention to the Temple entrance and all the exits of the sanctuary.
6 Uwuze mtundu wopanduka wa Israeli kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu Aisraeli, andikwana machitidwe anu onyansawo!
Tell those rebels, the people of Israel, that this is what the Lord God says: I've had more than enough of all your disgusting sins, people of Israel!
7 Munalowetsa alendo osachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi momwe mʼNyumba yanga ndipotu anayipitsa Nyumba yanga. Pamene inu munkandipatsa chakudya changa ndi magazi omwe kuwonjezera pa zonyansa zanu zonse ndiye kuti munaphwanya pangano langa.
As well as all your other offensive practices, you invited unconverted, pagan foreigners to come into my sanctuary. You made my Temple unclean even while you offered food to me, the fat and the blood. You broke my agreement.
8 Mʼmalo moti muzisamalira zinthu zanga zopatulika, mwayika alendo kuti aziyangʼanira malo anga opatulika.
In addition you have not taken care of my sanctuary as you were required to, but instead you employed others to look after my sanctuary for you.
9 Ambuye Wamphamvuzonse akuti: Palibe mlendo wosachita mdulidwe mu mtima ndi mʼthupi ngakhalenso mlendo amene amakhala pakati pa Aisraeli amene adzalowe mʼmalo anga opatulika.
This is what the Lord God says: No unconverted, pagan foreigners are allowed to enter my sanctuary—not even a foreigner who lives with the Israelites.
10 “Ndiponso Alevi amene anandisiya kutali pa nthawi imene Israeli anasochera potsata mafano, adzalangidwa chifukwa cha tchimo lawo.
The Levites who abandoned me when Israel turned from worshiping me and went off to follow their idols will experience the consequences of their sins.
11 Adzangokhala atumiki chabe mʼmalo anga opatulika. Azidzayangʼanira zipata za Nyumba ya Mulungu ndi kugwira ntchito kumeneko. Azidzapha nyama za nsembe zopsereza ndi za nsembe zina za anthu. Choncho azidzayimirira pamaso pa anthu nʼkumawatumikira.
However, they will serve in my sanctuary, supervising the Temple gates and working in the Temple. They will slaughter the burnt offerings and sacrifices brought by the people and be there to serve them.
12 Iwowa ankatumikira anthu popembedza mafano awo, ndipo anachititsa Aisraeli kugwa mu uchimo. Nʼchifukwa chake Ine ndikulumbira kuti iwowa ayenera kulangidwa chifukwa cha machimo awo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
But because they served the people in front of their idols and encouraged the people of Israel to sin, I held up my hand to promise on oath that they would experience the consequences of their sin, declares the Lord God.
13 Iwo sayenera kufika pafupi ndi Ine ndi kunditumikira ngati ansembe, kapena kuyandikira chilichonse cha zinthu zanga zopatulika, kapenanso zopereka zanga zopatulika kwambiri. Iwo adzachititsidwa manyazi chifukwa cha machitidwe awo onyansa.
They are not allowed to come near me to serve me as priests, and they are not to touch anything I regard as holy or most holy. They will have to experience the shame of the disgusting sins they committed.
14 Komabe ndidzawayika kuti aziyangʼanira Nyumba yanga ndi kutumikira pa ntchito zake zonse zoyenera kuti zigwiridwe mʼmenemo.
However, I will put them in charge of all Temple work and everything that needs to be done there.
15 “Koma ansembe, a fuko la Levi, a banja la Zadoki amene ankatumikira mokhulupirika ku malo anga opatulika pa nthawi imene Aisraeli anasochera ndi kundisiya Ine; iwowa adzasendera kwa Ine kudzanditumikira. Adzafika pamaso panga kuti apereke nsembe za mafuta ndi magazi. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
It is the Levitical priests, descended from Zadok and who took care of my sanctuary when the Israelites abandoned me, are the ones to come near to me and minister before me. They will stand in my presence to offer me fat and blood, declares the Lord God.
16 Okhawa ndiwo adzalowe ku malo anga opatulika ndi kudzayandikira tebulo langa kuti adzanditumikire. Amenewa okha ndiwo adzasamalire zinthu zanga.
Only they are allowed to enter my sanctuary and approach my table to minister before me. They will do what I say.
17 “Pamene alowa ku zipata za bwalo lamʼkati azivala zovala zabafuta. Asamavale chovala china chilichonse cha ubweya wankhosa pamene akutumikira pa zipata za bwalo la mʼkati kapena kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
When they come in through the entrances of the inner courtyard, they shall wear linen garments. They must not wear any woolen clothes when they serve at the entrances of the inner courtyard or inside the Temple.
18 Azivala nduwira za bafuta ndi kabudula wabafuta mʼkati. Asavale chilichonse chowachititsa thukuta.
They shall wear linen turbans on their heads and linen underwear. They are not to wear anything that makes them sweat.
19 Pamene atuluka ndi kupita ku bwalo lakunja kumene kuli anthu, azivula zovala zimene amatumikira nazo, ndipo azisiye zovalazo mu zipinda zopatulika. Pambuyo pake avale zovala zina, kuopa kuti angapatsireko kuyera anthu enawo ndi zovala zawozo.
When they go to the outer court where the people are, they must take off their priestly clothes they wore when they were serving, and leave them in the holy rooms. They are to put on other clothes so that they don't carry holiness to the people with their clothing.
20 “‘Ansembe asamamete mpala kapena kusunga tsitsi lalitali kwambiri, koma azingoliyepula.
They are not permitted to shave their heads or let their hair grow long; they must have a proper haircut.
21 Wansembe asamwe vinyo pamene ali pafupi kulowa mʼbwalo la mʼkati.
No priest shall drink wine before he enters the inner courtyard.
22 Iwo asakwatire akazi amasiye kapena osudzulidwa; koma azikwatira anamwali osadziwa mwamuna a fuko la Israeli kapena akazi amasiye a ansembe anzawo.
They are not to marry a woman who is a widow or divorced; they can only marry a virgin of Israelite descent, or a widow of a priest.
23 Ansembe aziphunzitsa anthu anga kusiyanitsa pakati pa zinthu zopatulika ndi zinthu wamba, ndiponso pakati pa zinthu zoyenera ndi zosayenera kuperekedwa nsembe.
They are to teach my people the difference between what is holy and what is common, and explain to them how to distinguish between what is clean and what is unclean.
24 “‘Pakakhala milandu, ansembe azikhala oweruza ndipo agamule milanduyo potsata malamulo anga. Atsate malamulo anga ndi malangizo anga pa za masiku anga onse a chikondwerero. Asamalirenso kuti masiku anga a Sabata akhale oyera.
They are to serve as judges in legal cases, and base their decisions on my laws. They are to follow my instructions and regulations regarding all my regular religious festivals, and they are to keep my Sabbaths holy.
25 “‘Wansembe asadziyipitse pokhudza munthu wakufa, pokhapokha ngati wakufayo ndi abambo ake kapena amayi ake, mwana wake wamwamuna kapena wamkazi, mʼbale wake kapena mlongo wake wosakwatiwa.
A priest must not make himself unclean by going near a dead body. However, if it's his father, mother, son, daughter, brother, or a sister that's not married, then he may do so.
26 Atatha kuyeretsedwa adikirebe masiku asanu ndi awiri kuti ayere ndithu.
Afterwards, once he is purified, he must wait for seven days.
27 Pa tsiku lomwe akukalowa mʼbwalo la mʼkati la malo opatulika kuti akatumikire, apereke nsembe yopepesera machimo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Then when he enters the sanctuary, going into the inner courtyard and ministering there in the sanctuary, he has to present his sin offering, declares the Lord God.
28 “‘Ansembe asadzakhale ndi cholowa chilichonse ayi. Cholowa chawo ndi Ine. Musadzawapatse chuma mu Israeli; Ine ndidzakhala chuma chawo.
Regarding their share of the land, I will take care of them. You are not to give them any property in Israel, because I will provide for them.
29 Iwo azidzadya nsembe ya chakudya, nsembe yopereka chifukwa cha tchimo ndi nsembe yopepesera machimo. Zinthu zonse zoperekedwa kwa Yehova mu Israeli zidzakhala zawo.
They are to eat the grain offerings, sin offerings, and guilt offerings. Everything brought by the people of Israel and dedicated to the Lord will be theirs.
30 Zabwino za zipatso zanu zoyambirira kucha ndiponso mphatso zanu zonse zapadera zidzakhala za ansembe. Inu muziwapatsa chigawo choyamba cha ufa wanu kuti pa nyumba panu pakhale madalitso.
The best of all the firstfruits and all your offerings are for the priests. You shall give the first loaf you bake to the priest, so that your home may be blessed.
31 Ansembe sayenera kudya kalikonse kofa kokha, kaya mbalame, kapena nyama. Kapena yochita kujiwa.’”
The priests are not permitted to eat any bird or animal found dead or killed by wild beasts.”

< Ezekieli 44 >