< Ezekieli 43 >

1 Pambuyo pake munthuyo anapita nane ku chipinda choyangʼana kummawa,
Potem zaprowadził mnie do bramy, do bramy, która była zwrócona w kierunku wschodnim.
2 ndipo ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ukubwera kuchokera kummawa. Liwu lake linali ngati mkokomo wamadzi, ndipo dziko linawala ndi ulemerero wake.
A oto chwała Boga Izraela przybyła od wschodu i jego głos [był] jak szum wielkich wód, a ziemia jaśniała od jego chwały.
3 Masomphenya amene ndinawaonawa anali ngati masomphenya amene ndinawaona pamene Yehova anabwera kudzawononga mzinda ndiponso ngati masomphenya amene ndinawaona ku mtsinje wa Kebara. Ndipo ndinadzigwetsa chafufumimba.
A to widzenie, które miałem, było podobne do tego widzenia, które miałem, gdy przybyłem, aby zniszczyć miasto; widzenie, podobne do tego widzenia, które miałem nad rzeką Kebar. I upadłem na twarz.
4 Ulemerero wa Yehova unalowa mʼNyumba ya Mulungu kudzera pa chipata choyangʼana kummawa.
Gdy chwała PANA weszła do domu przez bramę wschodnią;
5 Tsono Mzimu unandinyamula nundilowetsa mʼbwalo lamʼkati, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.
Wtedy uniósł mnie duch i wprowadził na dziedziniec wewnętrzny, a oto dom był pełen chwały PANA.
6 Munthuyo ali chiyimire pambali panga, ndinamva wina akundiyankhula kuchokera mʼNyumba ya Mulungu.
I usłyszałem, jak ktoś mówił do mnie z domu, a jakiś mąż stał obok mnie.
7 Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, awa ndi malo a mpando wanga waufumu, ndi malo opondapo mapazi anga. Pano ndiye pamene ndidzakhala pakati pa Aisraeli mpaka muyaya. Aisraeliwa kapena mafumu awo sadzayipitsa dzina langa popembedza milungu ina kapena poyika mitembo ya mafumu awo ku zitunda zachipembedzo.
I powiedział do mnie: Synu człowieczy, [oto] miejsce mojego tronu i miejsce dla moich stóp, gdzie będę mieszkać pośród synów Izraela na wieki. Dom Izraela już nie zbezcześci mojego świętego imienia, ani on, [ani] jego królowie, przez swój nierząd i przez zwłoki swych królów na wyżynach.
8 Ankamanga chiwundo chawo pafupi ndi chiwundo changa, ndiponso mphuthu zawo pafupi ndi mphuthu zanga, nʼkungokhala khoma chabe pakati pa iwowo ndi Ine. Motero anayipitsa dzina langa loyera ndi machitidwe awo onyansa. Choncho Ine ndinawawononga ndili wokwiya.
Gdy kładli swój próg obok mojego progu, swoje odrzwia obok moich odrzwi i ścianę między mną a sobą, zbezcześcili bardzo moje święte imię przez swoje obrzydliwości, które popełniali. Dlatego zniszczyłem ich w swoim gniewie.
9 Tsopano alekeretu kupembedza milungu ina ndipo achotseretu mitembo ya mafumu awo, isakhale pafupi ndi Ine, ndipo Ine ndidzakhala pakati pawo mpaka muyaya.
[Ale] teraz niech oddalą ode mnie swój nierząd i zwłoki swoich królów, a zamieszkam wśród nich na wieki.
10 “Iwe mwana wa munthu, awuze Aisraeliwa za Nyumba ya Mulunguyi, mamangidwe ake ndipo achite manyazi ndi machimo awo,
Ty, synu człowieczy, powiedz domowi Izraela o tym domu, aby się wstydzili swoich nieprawości. Niech [sobie] wymierzą [jego] plan.
11 akachita manyazi ndi zoyipa zonse anachita, uwafotokozera za Nyumba ya Mulungu, mamangidwe ake, makomo ake otulukira ndi makomo olowera, ndiye kuti, mamangidwe ake onse. Uwafotokozerenso malangizo ndi malamulo ake. Uwalembe akuona kuti athe kuwasunga ndi kuwachita.
A jeśli się zawstydzą wszystkiego, co uczynili, wtedy opisz im wygląd tego domu, jego układ, jego wyjście i wejścia, cały jego kształt i wszystkie jego ustawy, cały kształt i wszystkie jego prawa. Zapisz to przed ich oczami, aby przestrzegali całego jego kształtu i wszystkich jego ustaw i czynili je.
12 “Limeneli ndi lamulo la Nyumba ya Mulungu imene idzamangidwe pamwamba pa phiri. Malo ake onse ozungulira adzakhala oyera kwambiri. Limeneli ndilo lamulo la Nyumba ya Mulungu.
A takie [jest] prawo tego domu: Na szczycie góry cały jego obszar wszędzie dokoła [ma być] bardzo święty. Oto takie [jest] prawo tego domu.
13 “Miyeso ya guwa lansembe ndi iyi: Pa tsinde pake padzakhala ngalande ya masentimita makumi asanu kuzama kwake ndi mulifupi mwake. Mʼphepete mwa ngalandeyo kuzungulira guwa lonse, mudzakhala mkombero wa masentimita 25.
I takie [są] wymiary ołtarza w łokciach [liczonych] na łokieć i cztery palce: jego podstawa [wysoka] na łokieć i szeroka na łokieć, a obramowanie na jego brzegu wokoło ma wynosić jedną piędź. Taka będzie górna część ołtarza:
14 Kuchokera mʼngalande ya pansi padzakhala mpaka pa phaka lapansi mita imodzi, mulifupi mwake theka la mita. Kuchokera pa phaka lalingʼono mpaka pa phaka lalikulu, msinkhu wake ndi mamita awiri, mulifupi mwake ndi masentimita makumi asanu.
Od podstawy na ziemi aż do dolnego odstępu dwa łokcie, a jeden łokieć szerokości; od mniejszego odstępu do większego odstępu cztery łokcie, a [jeden] łokieć szerokości.
15 Malo osonkhapo moto pa guwa, msinkhu wake udzakhala mamita awiri. Pa ngodya iliyonse ya malo osonkhapo motowo panatuluka nyanga imodzi.
Ale sam ołtarz ma mieć cztery łokcie [wysokości], a z ołtarza w górę – cztery rogi.
16 Malo osankhalapo moto pa guwa lansembe miyeso yake ndi yofanana mbali zonse. Mulitali mwake mudzakhala mamita asanu ndi limodzi ndipo mulifupi mwake mudzakhalanso mamita asanu ndi limodzi.
A ołtarz ma mieć dwanaście łokci długości i dwanaście szerokości, [ma być] czworokątny po czterech swoich bokach.
17 Phaka lapamwamba muyeso wake udzakhala wofanana mbali zonse. Mulitali mudzakhala mamita asanu ndi awiri ndiponso mulifupi mwake mudzakhalanso mamita asanu ndi awiri. Mkombero wake udzakhala wa masentimita 25 ndiponso ngalande yake yozungulira idzakhala ya masentimita 25. Makwerero a guwa lansembe adzayangʼana kummawa.”
Górny odstęp ma mieć czternaście łokci długości i czternaście szerokości, po czterech bokach, a obramowanie wokół niego [ma być] na pół łokcia, jego podstawa – na łokieć wokoło i jego stopnie skierowane ku wschodowi.
18 Kenaka munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, Ambuye Yehova akuti: Guwalo litamangidwa, tsono malamulo awa azidzatsatidwa popereka nsembe zopsereza ndiponso powaza magazi pa guwapo.
I powiedział do mnie: Synu człowieczy, tak mówi Pan BÓG: To są ustawy ołtarza na dzień, w którym zostanie zbudowany, aby na nim składać całopalenia i skrapiać go krwią.
19 Udzawapatse ansembe, omwe ndi Alevi, a banja la Zadoki, amene amabwera pafupi nane kudzanditumikira, mwana wangʼombe wamwamuna kuti aperekere nsembe yopepesera machimo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
A kapłanom, Lewitom, którzy są z potomstwa Sadoka i zbliżają się do mnie, aby mi służyć, mówi Pan BÓG, dasz młodego cielca na ofiarę za grzech.
20 Udzatengeko magazi ake ena ndi kuwapaka pa nyanga zinayi za pa guwa lansembe, pa ngodya zinayi za phaka ndiponso mozungulira mkombero wonse. Motero udzaliyeretsa ndi kulipatula.
Wtedy weźmiesz z jego krwi i nałożysz na cztery rogi, na cztery narożniki odstępu i na obramowanie wokoło. W ten sposób oczyścisz go i poświęcisz.
21 Udzatenge ngʼombe yayimuna yomwe yaperekedwa ngati nsembe yopepesera machimo, ndipo udzayiwotche pa malo ake enieni mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, kunja kwa malo opatulika.
Potem weźmiesz tego cielca za grzech i spalisz go w oznaczonym miejscu domu poza świątynią.
22 “Mmawa mwake udzatenge mbuzi yopanda chilema kuti nayonso iperekedwe ngati nsembe yopepesera machimo. Pambuyo pake idzayeretse guwa lansembe monga unachitira ndi ngʼombe yayimuna ija.
A drugiego dnia złożysz kozła bez skazy na ofiarę za grzech i oczyszczą ołtarz, tak jak oczyścili go cielcem.
23 Utatha kuyeretsa guwa lansembelo, udzatenge mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndiponso nkhosa yayimuna yopanda chilema.
A gdy dokonasz oczyszczenia, będziesz ofiarowywać młodego cielca bez skazy i barana z trzody bez skazy.
24 Udzapereke zonsezi pamaso pa Yehova, ndipo ansembe adzazithire mchere ndi kuzipereka kuti zikhale nsembe zopsereza kwa Yehova.
Gdy je ofiarujesz przed PANEM, kapłani rzucą na nie sól i złożą je na całopalenie dla PANA.
25 “Kwa masiku asanu ndi awiri, uzidzapereka tsiku ndi tsiku mbuzi yayimuna, mwana wangʼombe, ndiponso nkhosa kuti zikhale nsembe zopepesera machimo. Zonsezi zidzakhale zopanda chilema.
Przez siedem dni codziennie będziesz składał kozła [na ofiarę] za grzech. Ma być przygotowany także młody cielec i baran z trzody bez skazy.
26 Kwa masiku asanu ndi awiriwo ansembe adzachite mwambo woyeretsa ndi kupatula guwa lansembelo.
Przez siedem dni będą oczyszczać ołtarz i poświęcać go. I poświęcą się.
27 Masiku amenewa atatha, kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu, ansembe azipereka nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pa guwa lansembe. Apo ndidzakulandirani. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
A po upływie tych dni, dnia ósmego i w następne kapłani będą składali na ołtarzu wasze całopalenia i ofiary pojednawcze i przyjmę was łaskawie, mówi Pan BÓG.

< Ezekieli 43 >