< Ezekieli 43 >

1 Pambuyo pake munthuyo anapita nane ku chipinda choyangʼana kummawa,
Wiódł mię potem ku bramie, która brama patrzyła ku drodze na wschód słońca.
2 ndipo ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ukubwera kuchokera kummawa. Liwu lake linali ngati mkokomo wamadzi, ndipo dziko linawala ndi ulemerero wake.
A oto chwała Boga Izraelskiego przychodziła drogą od wschodu, a szum jej był jako szum wód wielkich, a ziemia się lśniła od chwały jego.
3 Masomphenya amene ndinawaonawa anali ngati masomphenya amene ndinawaona pamene Yehova anabwera kudzawononga mzinda ndiponso ngati masomphenya amene ndinawaona ku mtsinje wa Kebara. Ndipo ndinadzigwetsa chafufumimba.
A podobne było ono widzenie, którem widział, cale onemu widzeniu, którem widział, gdym przychodził, abym psuł miasto; widzenie, mówię, podobne onemu widzeniu, którem widział u rzeki Chebar, i upadłem na twarz moję.
4 Ulemerero wa Yehova unalowa mʼNyumba ya Mulungu kudzera pa chipata choyangʼana kummawa.
A gdy chwała Pańska wchodziła do domu drogą bramy, która patrzała ku drodze na wschód słońca,
5 Tsono Mzimu unandinyamula nundilowetsa mʼbwalo lamʼkati, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.
Tedy mię podniósł duch, i wwiódł mię do sieni wewnętrznej, a oto dom pełen był chwały Pańskiej.
6 Munthuyo ali chiyimire pambali panga, ndinamva wina akundiyankhula kuchokera mʼNyumba ya Mulungu.
I usłyszałem, a oto mówiono do mnie z domu, a on mąż stał podle mnie,
7 Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, awa ndi malo a mpando wanga waufumu, ndi malo opondapo mapazi anga. Pano ndiye pamene ndidzakhala pakati pa Aisraeli mpaka muyaya. Aisraeliwa kapena mafumu awo sadzayipitsa dzina langa popembedza milungu ina kapena poyika mitembo ya mafumu awo ku zitunda zachipembedzo.
I mówił do mnie: Synu człowieczy! miejsce stolicy mojej, i miejsce stóp nóg moich, na którem mieszkać będę w pośród synów Izraelskich na wieki; nie splugawi więcej dom Izraelski imienia świętobliwości mojej, ani oni, ani królowie ich w szeteczeńs twy swemi i trupami królów swych, ani wyżynami swemi.
8 Ankamanga chiwundo chawo pafupi ndi chiwundo changa, ndiponso mphuthu zawo pafupi ndi mphuthu zanga, nʼkungokhala khoma chabe pakati pa iwowo ndi Ine. Motero anayipitsa dzina langa loyera ndi machitidwe awo onyansa. Choncho Ine ndinawawononga ndili wokwiya.
Gdy kładli próg swój podle progu mego, a podwoje swoje podle podwoi moich, a ścianę między mną i między sobą; a tak splugawiali imię świętobliwości mojej obrzydliwościami swemi, które czynili, przetożem ich zniszczył w popędliwości mojej.
9 Tsopano alekeretu kupembedza milungu ina ndipo achotseretu mitembo ya mafumu awo, isakhale pafupi ndi Ine, ndipo Ine ndidzakhala pakati pawo mpaka muyaya.
Ale teraz niech odrzucą wszeteczeństwo swoje, i trupy królów swoich odemnie, a będę mieszkał w pośrodku ich na wieki.
10 “Iwe mwana wa munthu, awuze Aisraeliwa za Nyumba ya Mulunguyi, mamangidwe ake ndipo achite manyazi ndi machimo awo,
Ty, synu człowieczy! powiedz domowi Izraelskiemu o tym domu, a niech się wstydzą za nieprawości swoje, i niech sobie rozmierzą wizerunek jego.
11 akachita manyazi ndi zoyipa zonse anachita, uwafotokozera za Nyumba ya Mulungu, mamangidwe ake, makomo ake otulukira ndi makomo olowera, ndiye kuti, mamangidwe ake onse. Uwafotokozerenso malangizo ndi malamulo ake. Uwalembe akuona kuti athe kuwasunga ndi kuwachita.
A jeźliby się zawstydzili za wszystko, co czynili, tydy im oznajmij wizerunek domu tego, i wymiar jego, wyjście jego, i wejście jego, i wszystkie kształty jego, i wszystkie ustawy jego, wszystkie, mówię, kształty, i wszystkie prawa jego, a napisz przed oczyma ich, aby przestrzegali wszystkiego kształtu jego, i wszystkich ustaw jego, i czynili je.
12 “Limeneli ndi lamulo la Nyumba ya Mulungu imene idzamangidwe pamwamba pa phiri. Malo ake onse ozungulira adzakhala oyera kwambiri. Limeneli ndilo lamulo la Nyumba ya Mulungu.
A tenci jest zakon domu tego: Na wierzchu góry wszystko ogrodzenie jego wszędzie w około najświętsze jest; oto tenci jest zakon domu tego.
13 “Miyeso ya guwa lansembe ndi iyi: Pa tsinde pake padzakhala ngalande ya masentimita makumi asanu kuzama kwake ndi mulifupi mwake. Mʼphepete mwa ngalandeyo kuzungulira guwa lonse, mudzakhala mkombero wa masentimita 25.
A teć są pomiary ołtarza według tychże łokci, a miara łokcia na łokieć i na dłoń; podstawek jego na łokieć wzwyż, a wszerz także na łokieć, a kraniec jego aż do kraju jego w około był na piędź jedną; a tać była wystawa ołtarza;
14 Kuchokera mʼngalande ya pansi padzakhala mpaka pa phaka lapansi mita imodzi, mulifupi mwake theka la mita. Kuchokera pa phaka lalingʼono mpaka pa phaka lalikulu, msinkhu wake ndi mamita awiri, mulifupi mwake ndi masentimita makumi asanu.
To jest od podstawku, który był przy ziemi, aż do przepasania niższego, dwa łokcie, a szerokość na jeden łokieć; a od mniejszego przepasania aż do przepasania większego cztery łokcie, a szerokość na łokieć;
15 Malo osonkhapo moto pa guwa, msinkhu wake udzakhala mamita awiri. Pa ngodya iliyonse ya malo osonkhapo motowo panatuluka nyanga imodzi.
Ale sam ołtarz niech będzie na cztery łokcie, a z ołtarza w górę cztery rogi.
16 Malo osankhalapo moto pa guwa lansembe miyeso yake ndi yofanana mbali zonse. Mulitali mwake mudzakhala mamita asanu ndi limodzi ndipo mulifupi mwake mudzakhalanso mamita asanu ndi limodzi.
A ołtarz na dwanaście łokci wdłuż, a na dwanaście wszerz czworograniasty po czterech stronach swoich;
17 Phaka lapamwamba muyeso wake udzakhala wofanana mbali zonse. Mulitali mudzakhala mamita asanu ndi awiri ndiponso mulifupi mwake mudzakhalanso mamita asanu ndi awiri. Mkombero wake udzakhala wa masentimita 25 ndiponso ngalande yake yozungulira idzakhala ya masentimita 25. Makwerero a guwa lansembe adzayangʼana kummawa.”
A przepasanie jego na czternaście łokci wdłuż, a na czternaście wszerz, po czterech stronach jego, a kraniec około niego na pół łokcia, a podstawek jego na łokieć w około, a wschód jego na wschód słońca.
18 Kenaka munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, Ambuye Yehova akuti: Guwalo litamangidwa, tsono malamulo awa azidzatsatidwa popereka nsembe zopsereza ndiponso powaza magazi pa guwapo.
I rzekł do mnie: Synu człowieczy! tak mówi panujący Pan: Teć są ustawy około ołtarza w dzień, w który zbudowany będzie, aby na nim ofiarowano całopalenia, i krwią na nim kropiono.
19 Udzawapatse ansembe, omwe ndi Alevi, a banja la Zadoki, amene amabwera pafupi nane kudzanditumikira, mwana wangʼombe wamwamuna kuti aperekere nsembe yopepesera machimo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
A kapłanom Lewitom, którzy są z nasienia Sadokowego, a przystępują do mnie, mówi panujący Pan, aby mi służyli, dasz cielca młodego na ofiarę za grzech;
20 Udzatengeko magazi ake ena ndi kuwapaka pa nyanga zinayi za pa guwa lansembe, pa ngodya zinayi za phaka ndiponso mozungulira mkombero wonse. Motero udzaliyeretsa ndi kulipatula.
Weźmiesz tedy ze krwi jego, a włożysz na cztery rogi jego, i na cztery węgły przepasania, i na kraniec w około; a tak go oczyścisz, i poświęcisz go.
21 Udzatenge ngʼombe yayimuna yomwe yaperekedwa ngati nsembe yopepesera machimo, ndipo udzayiwotche pa malo ake enieni mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, kunja kwa malo opatulika.
Potem weźmiesz onego cielca za grzech, a spalisz go na miejscu postanowionem w onym domu zewnątrz przed świątnicą.
22 “Mmawa mwake udzatenge mbuzi yopanda chilema kuti nayonso iperekedwe ngati nsembe yopepesera machimo. Pambuyo pake idzayeretse guwa lansembe monga unachitira ndi ngʼombe yayimuna ija.
A wtórego dnia będziesz ofiarował kozła z kóz bez wady za grzech, i oczyszczą ołtarz, tak jako go cielcem oczyścili.
23 Utatha kuyeretsa guwa lansembelo, udzatenge mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndiponso nkhosa yayimuna yopanda chilema.
A gdy dokończysz oczyszczania, będziesz ofiarował cielca młodego bez wady, i barana z trzody bez wady.
24 Udzapereke zonsezi pamaso pa Yehova, ndipo ansembe adzazithire mchere ndi kuzipereka kuti zikhale nsembe zopsereza kwa Yehova.
Które gdy ofiarować będziesz przed Panem, wrzucą kapłani na nie soli, i uczynią z nich ofiarę całopalenia Panu.
25 “Kwa masiku asanu ndi awiri, uzidzapereka tsiku ndi tsiku mbuzi yayimuna, mwana wangʼombe, ndiponso nkhosa kuti zikhale nsembe zopepesera machimo. Zonsezi zidzakhale zopanda chilema.
Przez siedm dni będziesz ofiarował kozła za grzech na każdy dzień, także i cielca młodego, i barana z trzody bez wady ofiarować będą,
26 Kwa masiku asanu ndi awiriwo ansembe adzachite mwambo woyeretsa ndi kupatula guwa lansembelo.
Przez siedm dni oczyszczać będą ołtarz, i oczyszczą go, a poświęcą ręce swoje.
27 Masiku amenewa atatha, kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu, ansembe azipereka nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pa guwa lansembe. Apo ndidzakulandirani. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
A wypełniwszy te dni, ósmego dnia napotem sprawować będą kapłani na ołtarzu całopalenia wasze, i spokojne ofiary wasze, i przyjmę was łaskawie, mówi panujący Pan.

< Ezekieli 43 >