< Ezekieli 43 >

1 Pambuyo pake munthuyo anapita nane ku chipinda choyangʼana kummawa,
Et il me conduisit vers la porte qui regarde l'orient et il me fit entrer.
2 ndipo ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ukubwera kuchokera kummawa. Liwu lake linali ngati mkokomo wamadzi, ndipo dziko linawala ndi ulemerero wake.
Et voilà que la gloire du Dieu d'Israël vint par la voie de l'orient, et le bruit qu'elle fit à son entrée était comme le bruit d'une grande multitude qui redouble ses clameurs; et à l'entour de cette gloire la terre resplendit comme une flamme.
3 Masomphenya amene ndinawaonawa anali ngati masomphenya amene ndinawaona pamene Yehova anabwera kudzawononga mzinda ndiponso ngati masomphenya amene ndinawaona ku mtsinje wa Kebara. Ndipo ndinadzigwetsa chafufumimba.
Et la vision que j'eus fut comme la vision que j'avais eue lorsque je vins pour marquer la ville. Et j'eus la vision d'un char, comme dans la vision que j'avais eue sur le fleuve Chobar. Et je tombai la face contre terre.
4 Ulemerero wa Yehova unalowa mʼNyumba ya Mulungu kudzera pa chipata choyangʼana kummawa.
Et la gloire du Seigneur entra dans le temple par la voie de la porte qui regarde l'orient.
5 Tsono Mzimu unandinyamula nundilowetsa mʼbwalo lamʼkati, ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza Nyumba ya Mulungu.
Et l'Esprit me ravit, et il m'introduisit dans le parvis intérieur, et voilà que le temple était plein de la gloire de Dieu.
6 Munthuyo ali chiyimire pambali panga, ndinamva wina akundiyankhula kuchokera mʼNyumba ya Mulungu.
Et je me tins immobile; et voilà qu'une voix me parla du temple, et l'homme se tenait auprès de moi.
7 Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, awa ndi malo a mpando wanga waufumu, ndi malo opondapo mapazi anga. Pano ndiye pamene ndidzakhala pakati pa Aisraeli mpaka muyaya. Aisraeliwa kapena mafumu awo sadzayipitsa dzina langa popembedza milungu ina kapena poyika mitembo ya mafumu awo ku zitunda zachipembedzo.
Et la voix me dit: Fils de l'homme, tu vois la place de mon trône et la trace de mes pieds; c'est ici que mon nom s'abritera pour tous les siècles au milieu de la maison d'Israël. Et la maison d'Israël, ses enfants et leurs rois ne profaneront plus mon saint nom, soit par leurs prostitutions, soit par les meurtres qu'au milieu d'eux commettaient leurs rois,
8 Ankamanga chiwundo chawo pafupi ndi chiwundo changa, ndiponso mphuthu zawo pafupi ndi mphuthu zanga, nʼkungokhala khoma chabe pakati pa iwowo ndi Ine. Motero anayipitsa dzina langa loyera ndi machitidwe awo onyansa. Choncho Ine ndinawawononga ndili wokwiya.
Lorsqu'ils avaient mon portique près de leurs portiques, et mes portes auprès de leurs portes. Et ils avaient fait de mon mur comme un lien entre eux et moi; mais ils ont profané mon saint nom par leurs iniquités. Et je les ai broyés en ma colère, et ils ont péri.
9 Tsopano alekeretu kupembedza milungu ina ndipo achotseretu mitembo ya mafumu awo, isakhale pafupi ndi Ine, ndipo Ine ndidzakhala pakati pawo mpaka muyaya.
Et maintenant, qu'ils répudient loin de moi leurs prostitutions, et je m'abriterai au milieu d'eux dans tous les siècles.
10 “Iwe mwana wa munthu, awuze Aisraeliwa za Nyumba ya Mulunguyi, mamangidwe ake ndipo achite manyazi ndi machimo awo,
Et toi, fils de l'homme, montre ce temple à la maison d'Israël, et ils cesseront de pécher; montre-leur son plan et sa distribution.
11 akachita manyazi ndi zoyipa zonse anachita, uwafotokozera za Nyumba ya Mulungu, mamangidwe ake, makomo ake otulukira ndi makomo olowera, ndiye kuti, mamangidwe ake onse. Uwafotokozerenso malangizo ndi malamulo ake. Uwalembe akuona kuti athe kuwasunga ndi kuwachita.
Et eux-mêmes accepteront les châtiments de toutes les choses qu'ils ont faites. Décris-leur le temple, ses issues, toute sa structure; fais-leur connaître ses règlements et toutes ses lois; décris-les devant eux, et ils garderont mes ordonnances et mes commandements, et ilsles mettront en pratique.
12 “Limeneli ndi lamulo la Nyumba ya Mulungu imene idzamangidwe pamwamba pa phiri. Malo ake onse ozungulira adzakhala oyera kwambiri. Limeneli ndilo lamulo la Nyumba ya Mulungu.
Et tu leur montreras le plan du temple sur le sommet de la montagne, et toute son étendue sera sainte et sacrée.
13 “Miyeso ya guwa lansembe ndi iyi: Pa tsinde pake padzakhala ngalande ya masentimita makumi asanu kuzama kwake ndi mulifupi mwake. Mʼphepete mwa ngalandeyo kuzungulira guwa lonse, mudzakhala mkombero wa masentimita 25.
Et voici les mesures de l'autel: il sera d'une grande coudée, c'est-à-dire d'une coudée et un palme; sa cavité aura une coudée; il aura une coudée de large, et un palme pour la corniche du rebord tout alentour. Et voici la hauteur de l'autel:
14 Kuchokera mʼngalande ya pansi padzakhala mpaka pa phaka lapansi mita imodzi, mulifupi mwake theka la mita. Kuchokera pa phaka lalingʼono mpaka pa phaka lalikulu, msinkhu wake ndi mamita awiri, mulifupi mwake ndi masentimita makumi asanu.
À partir du commencement de la cavité jusqu'au grand propitiatoire, deux coudées de haut sur une de large; et du petit propitiatoire an grand propitiatoire, quatre coudées de haut et une de large.
15 Malo osonkhapo moto pa guwa, msinkhu wake udzakhala mamita awiri. Pa ngodya iliyonse ya malo osonkhapo motowo panatuluka nyanga imodzi.
Et l'Ariel sera de quatre coudées, et à partir de l'Ariel, au-dessous des cornes, il y aura une coudée.
16 Malo osankhalapo moto pa guwa lansembe miyeso yake ndi yofanana mbali zonse. Mulitali mwake mudzakhala mamita asanu ndi limodzi ndipo mulifupi mwake mudzakhalanso mamita asanu ndi limodzi.
Et l'Ariel sera long de douze coudées sur douze de large; c'est un tétragone aux côtés égaux.
17 Phaka lapamwamba muyeso wake udzakhala wofanana mbali zonse. Mulitali mudzakhala mamita asanu ndi awiri ndiponso mulifupi mwake mudzakhalanso mamita asanu ndi awiri. Mkombero wake udzakhala wa masentimita 25 ndiponso ngalande yake yozungulira idzakhala ya masentimita 25. Makwerero a guwa lansembe adzayangʼana kummawa.”
Et le propitiatoire sera long de quatorze coudées sur quatorze de large; ses quatre côtéssont égaux. Et il a tout alentour une corniche d'une demi-coudée en saillie d'une coudée de hauteur; et ses degrés regardent l'orient.
18 Kenaka munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, Ambuye Yehova akuti: Guwalo litamangidwa, tsono malamulo awa azidzatsatidwa popereka nsembe zopsereza ndiponso powaza magazi pa guwapo.
Et la voix me dit: Fils de l'homme, ainsi parle le Seigneur Dieu d'Israël: Voici la règle pour l'autel: du jour où il aura été fait, on y offrira des holocaustes, et on y versera le sang des victimes:
19 Udzawapatse ansembe, omwe ndi Alevi, a banja la Zadoki, amene amabwera pafupi nane kudzanditumikira, mwana wangʼombe wamwamuna kuti aperekere nsembe yopepesera machimo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Et tu donneras aux prêtres lévites, à. ceux de la famille de Sadduc, qui s'approchent de moi, dit le Seigneur Dieu, un veau choisi parmi le troupeau, afin de me le sacrifier pour le péché.
20 Udzatengeko magazi ake ena ndi kuwapaka pa nyanga zinayi za pa guwa lansembe, pa ngodya zinayi za phaka ndiponso mozungulira mkombero wonse. Motero udzaliyeretsa ndi kulipatula.
Et ils prendront de son sang, et ils le mettront sur les quatre cornes de l'autel et sur les quatre angles du propitiatoire, et sur la base tout alentour, et ainsi ils le purifieront.
21 Udzatenge ngʼombe yayimuna yomwe yaperekedwa ngati nsembe yopepesera machimo, ndipo udzayiwotche pa malo ake enieni mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu, kunja kwa malo opatulika.
Et ils prendront le veau offert pour le péché, et il sera brûlé par le feu, dans le lieu séparé du temple, hors du sanctuaire.
22 “Mmawa mwake udzatenge mbuzi yopanda chilema kuti nayonso iperekedwe ngati nsembe yopepesera machimo. Pambuyo pake idzayeretse guwa lansembe monga unachitira ndi ngʼombe yayimuna ija.
Et le second jour ils prendront deux chevreaux sans tache pour le péché, et ils purifieront l'autel, comme ils l'auront purifié avec le veau.
23 Utatha kuyeretsa guwa lansembelo, udzatenge mwana wangʼombe wamwamuna wopanda chilema ndiponso nkhosa yayimuna yopanda chilema.
Et lorsqu'ils auront achevé la purification, ils offriront un veau sans tache et un bélier sans tache.
24 Udzapereke zonsezi pamaso pa Yehova, ndipo ansembe adzazithire mchere ndi kuzipereka kuti zikhale nsembe zopsereza kwa Yehova.
Et vous les offrirez devant le Seigneur; et les prêtres les saupoudreront de sel, et ils les offriront en holocauste au Seigneur.
25 “Kwa masiku asanu ndi awiri, uzidzapereka tsiku ndi tsiku mbuzi yayimuna, mwana wangʼombe, ndiponso nkhosa kuti zikhale nsembe zopepesera machimo. Zonsezi zidzakhale zopanda chilema.
Pendant sept jours, tu offriras chaque jour pour le péché un chevreau, un veau et un bélier choisis parmi les bœufs et les brebis; et on sacrifiera ces victimes, toutes sans tache,
26 Kwa masiku asanu ndi awiriwo ansembe adzachite mwambo woyeretsa ndi kupatula guwa lansembelo.
Durant sept jours. Et ils purifieront l'autel, ils le sanctifieront, et ils consacreront leurs mains.
27 Masiku amenewa atatha, kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu, ansembe azipereka nsembe zanu zopsereza ndi nsembe zachiyanjano pa guwa lansembe. Apo ndidzakulandirani. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
Et à partir du huitième jour et dans la suite les prêtres sacrifieront sur l'autel vos holocaustes et vos victimes pour le salut; et je vous agréerai, dit le Seigneur.

< Ezekieli 43 >