< Ezekieli 42 >

1 Pambuyo pake munthuyo anapita nane ku bwalo lakunja chakumpoto ndipo anafika nane ku zipinda zoyangʼanana ndi bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi nyumba ina yakumpoto.
Umuntu lowo wangikhokhelela enyakatho egumeni langaphandle wangisa ezindlini eziqondane leguma lethempeli maqondana lomduli waphandle eceleni lasenyakatho.
2 Nyumba yakumpotoyi mulitali mwake munali mamita makumi asanu, mulifupi mwake munali mamita 25.
Indlu elomnyango owawukhangele enyakatho yayizingalo ezilikhulu ubude lezingalo ezingamatshumi amahlanu ububanzi.
3 Panali midadada iwiri, umodzi umayangʼanana ndi bwalo lamʼkati la mamita khumi, winawo umayangʼanana ndi bwalo lakunja. Midadada iwiriyi inali ya nyumba zitatu zosanjikana ndipo imayangʼanana.
Kokubili ehlangothini izingalo ezingamatshumi amabili kusukela egumeni langaphakathi lasehlangothini oluqondane lendawo egandelweyo yeguma langaphandle, umduli wawukhangele umduli ezigabeni ezintathu.
4 Kumaso kwa zipindazo kunali njira yamʼkati, mulifupi mwake munali mamita asanu, mulitali mwake munali mamita makumi asanu. Makomo ake analoza chakumpoto.
Phambi kwezindlu kwakulendawo yokuhamba izingalo ezilitshumi ububanzi lezingalo ezilikhulu ubude. Iminyango yazo yayingenyakatho.
5 Zipinda zammwamba zinali zazifupi mʼmimbamu kupambana zipinda zamʼmunsi ndi zipinda zapakati chifukwa njira zake zinatenga malo ambiri.
Izindlu zangaphezulu zazincane ngoba imikhandlu yayithethe indawo enengi kuzo kulezindlini ezingaphansi leziphakathi zesakhiwo.
6 Popeza zipinda zinali zosanjikizana katatu ndipo zinalibe nsanamira monga za mabwalo, motero zipinda zamʼmwamba zinali zochepa kuyerekeza ndi zipinda zapansi ndi zipinda zapakati.
Izindlu zaphezulu zazingelansika, njengamaguma ayelazo, ngakho iphansi lazo lalilincane kulalezo ezazisesitezi esingaphansi lesiphakathi.
7 Panali khoma lakunja lomwe limatsatana ndi zipindazo kutsogolo kwake pambali pabwalo lakunja, kutalika kwake kunali mamita 25.
Kwakulomduli wangaphandle owawusekelene lezindlu kanye leguma langaphandle; wawuquma ngaphambi kwezindlu okwezingalo ezingamatshumi amahlanu.
8 Zipinda za mʼmbali mwa bwalo lakunja mulitali mwake munali mamita 25. Koma zomwe zinali mʼmbali mwa Nyumba ya Mulungu, mulitali mwake munali mamita makumi asanu.
Lanxa udwendwe lwezindlu eceleni elaliseduze leguma langaphandle lwaluzingalo ezingamatshumi amahlanu ubude, udwendwe olwaluseceleni eliseduze lendlu engcwele lwaluzingalo ezilikhulu ubude.
9 Pansi pa zipinda zimenezi panali khomo chakummawa kuchokera ku bwalo lakunja kumene khoma lake linkayambira.
Izindlu zangaphansi zazilentuba ngasempumalanga lapho umuntu angena lakhona evela egumeni langaphandle.
10 Mbali yakummwera kuyangʼanana ndi bwalo ndi nyumbayo kunali zipinda zina.
Eceleni langaseningizimu kulandela ubude bomduli weguma langaphandle, kuxhume iguma lethempeli maqondana lomduli wangaphandle, kwakulezindlu
11 Kumaso kwa zipindazi kunali njira. Zipindazi mulitali mwake, mulifupi mwake ndiponso maonekedwe ake onse zinali zofanana ndi zipinda zoyangʼana zakumpoto zija. Makomo ndi zitseko zake zinalinso zofanana
ezilendawo yokuhamba phambi kwazo. Lezi zazinjengezindlu ezingenyakatho; ubude lobubanzi bazo babulingana, zileminyango yokuphuma efananayo kanye lobukhulu. Njengeminyango yangenyakatho,
12 ndi makomo a zipinda zakummwera. Kunali khomo mʼmbali ya kummawa kumene ankalowerako. Kunalinso khoma logawa zipinda.
iminyango yezindlu zangaseningizimu layo yayinjalo. Kwakulomnyango ekuqaliseni kwendawo yokuhamba eyayisekelane lomduli owawuhambelana layo usiya empumalanga, okuyiwo umuntu owayengena ngawo ezindlini.
13 Ndipo munthuyo anandiwuza kuti, “Zipinda zakumpoto ndi zakummwera zoyangʼanana ndi bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi zoyera. Mʼmenemo ansembe amene amakhala pafupi ndi Yehova amadyeramo zopereka zopatulika kwambiri. Mʼmenemo adzayikamo zopereka zopatulika kwambiri, zopereka za chakudya, nsembe zopepesera machimo ndi nsembe zopepesera kupalamula, poti malowo ndi opatulika.
Wasesithi kimi, “Izindlu ezingenyakatho leziseningizimu ezikhangele iguma lethempeli yizindlu zabaphristi lapho abaphristi abasondela kuThixo abazadlela khona iminikelo engcwele kakhulu. Bazayibeka khonapho iminikelo engcwele kakhulu, iminikelo yamabele, iminikelo yesono kanye leminikelo yecala ngoba indawo ingcwele.
14 Pamene ansembe alowa ku malo opatulikawa, asatuluke kupita ku bwalo lakunja popanda kusiya momwemo zovala zimene anavala potumikira zija, pakuti zovalazi ndi zopatulika. Avale kaye zovala zina ndipo akhoza kufika kwa anthu.”
Abaphristi bangavele bangene endaweni engcwele, akumelanga baye egumeni langaphandle baze batshiye ngemuva izembatho abakhonza bezigqokile, ngoba lezi zingcwele. Kumele bagqoke ezinye izigqoko bengakayi eduze lezindawo ezingezabantu.”
15 Munthuyo atamaliza kuyeza zimene zinali mʼkati mwa Nyumba ya Mulungu, anatuluka nane pa chipata chakummawa ndi kuyeza bwalo lonse.
Wathi eseqede ukulinganisa okwakuphakathi kwendawo yethempeli, wangisa phandle ngesango lasempumalanga walinganisa indawo yonke.
16 Anayeza mbali yakummawa ndi ndodo yake yoyezera; kutalika kwake kunali mamita 250.
Walinganisa icele lasempumalanga ngoluthi lokulinganisa; lalizingalo ezingamakhulu amahlanu.
17 Anayeza mbali ya kumpoto ndi ndodo yake; kutalika kwake kunali mamita 250.
Walinganisa icele lasenyakatho; lalizingalo ezingamakhulu amahlanu ngoluthi lokulinganisa.
18 Munthuyo anayeza mbali yakummwera; kutalika kwake kunali mamita 250 atayeza ndi ndodo yake.
Walinganisa icele laseningizimu; lalizingalo ezingamakhulu amahlanu ngoluthi lokulinganisa.
19 Kenaka anatembenukira ku mbali ya kumadzulo ndi kuyeza ndi ndodo yake; kutalika kwake kunali mamita 250 atayeza ndi ndodo yake.
Waphendukela eceleni langasentshonalanga walinganisa; lalizingalo ezingamakhulu amahlanu ngoluthi lokulinganisa.
20 Motero anayeza mbali zonse zinayi. Panali khoma lozungulira bwalolo mulitali mwake munali mamita 250 ndipo mulifupi mwake munalinso mamita 250. Khomalo linali lolekanitsa zinthu zoyera ndi zinthu wamba.
Ngakho walinganisa indawo yamacele wonke amane. Yayilomduli owawuyizingelezele, izingalo ezingamakhulu amahlanu ubude lezingalo ezingamakhulu amahlanu ububanzi, ukwehlukanisa okungcwele kokwabantu bonke.

< Ezekieli 42 >