< Ezekieli 40 >

1 Kumayambiriro a chaka cha 25, cha ukapolo wathu, tsiku la khumi lamwezi, patapita zaka khumi ndi zinayi mzinda wa Yerusalemu utawonongedwa, pa tsiku lomwelo dzanja la Yehova linali pa ine ndipo Iye anapita nane ku Yerusalemu.
Dwudziestego i piątego roku zaprowadzenia naszego, na początku roku, dziesiątego dnia miesiąca, czternastego roku po zburzeniu miasta, tegoż prawie dnia była nademną ręka Pańska, a przywiódł mię tam.
2 Mʼmasomphenyawo Yehova ananditenga ndi kupita nane ku dziko la Israeli ndipo anandiyika pa phiri lalitali kwambiri, moti ndinaona ngati mzinda.
W widzeniach Bożych przywiódł mię do ziemi Izraelskiej, a postawił mię na górze bardzo wysokiej, na której było jakoby budowanie miasta na południe.
3 Atandifikitsa kumeneko ndinaona munthu wonyezimira ngati mkuwa. Iye anali atayima pa chipata ndipo mʼdzanja lake munali chingwe cha nsalu yabafuta ndi ndodo yoyezera.
I przywiódł mię tam, a oto mąż, który był na wejrzeniu jako kształt miedzi, mając sznur lniany w ręce swej i laskę ku rozmierzaniu, a ten stał w bramie.
4 Munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, penyetsetsa ndipo umvetse bwinobwino. Uyikepo mtima wako pa zonse zimene ndikukuonetsa pakuti anakubweretsa kuno kuti uwone zimenezi. Tsono ukawawuze Aisraeli zonse zimene uzione.”
I mówił do mnie ten mąż: Synu człowieczy! patrz oczyma swemi, a uszyma swemi słuchaj, i przyłóż serce swoje do wszystkiego, coć okażę; boś tu na to przywiedziony, abyć to ukazano, a ty oznajmisz wszystko, co widzisz, domowi Izraelskiemu.
5 Ine ndinaona khoma litazungulira mbali zonse za Nyumba ya Mulungu. Mʼdzanja la munthuyo munali bango lopimira limene kutalika kwake kunali kwa mamita atatu. Atayeza chipupacho anapeza kuti kuchindikira kwake kunali mamita atatu, ndiponso kutalika kwake kunalinso mamita atatu.
A oto mur zewnątrz przy domu zewsząd w około; a w ręce onego męża była laska ku rozmierzaniu na sześć łokci, (a każdy łokieć na dłoń był nad zwyczajny dłuższy.) i wymierzył szerokość onego budowania na laskę jednę, i wysokość na laskę jednę,
6 Anapita ku chipata chakummawa. Anakwera pa makwerero a nyumbayo, nayeza chiwundo choyamba cha chipatacho; kutalika kwake kunali mamita atatu.
Potem wszedłszy do bramy, która była na drodze wschodniej, wstąpił po schodach jej, i wymierzył próg bramy na laskę jednę wszerz, a próg drugiej na jednę laskę wszerz;
7 Kudutsa chiwundo choyambachi, panali zipinda za alonda zisanu ndi chimodzi, zitatu kudzanja lamanja, zitatu kudzanja lamanzere. Chilichonse chinali cha mamita atatu mulitali mwake, chimodzimodzinso mulifupi mwake. Mipata ya pakati pa zipindazo inali ya mamita awiri ndi theka. Ndipo chiwundo cha pa chipata pafupi ndi khonde lapachipata, chinali mamita atatu.
Każdą też komorę na jednę laskę wdłuż, a na jednę laskę wszerz; a między komorami był plac na pięć łokci, próg też bramy podle przysionku bramy wewnątrz był na jednę laskę.
8 Ndipo iye anayeza khonde la chipata ndipo chinali cha mamita atatu.
I wymierzył przysionek bramy wewnątrz na jednę laskę.
9 Anayeza khonde ndipo linali mamita anayi. Mphuthu zake zinali mita imodzi kuchindikira kwake. Khonde lamʼkati lapachipata linali kumapeto kwenikweni pafupi ndi Nyumba ya Mulungu.
Wymierzył też przysionek bramy na ośm łokci, a podwoje jej na dwa łokcie, a ten przysionek bramy był wewnątrz.
10 Mʼkati mwa chipata chakummawa munali zipinda za alonda zitatu mbali iliyonse. Zitatu zonsezo zinali zofanana, ndipo khonde la pakati pa zipindazo linali lofanana.
Komory też bramy ku drodze wschodniej były trzy z jednej a trzy z drugiej strony; jednaka miara była wszystkich trzech, jednaka też miara podwoi ich z obu stron.
11 Kenaka anayeza chipata cholowera; mulifupi mwake munali mamita asanu ndipo mulitali mwake munali mamita asanu ndi limodzi ndi theka.
Wymierzył też szerokość drzwi onej bramy na dziesięć łokci, a długość bramy na trzynaście łokci.
12 Kutsogolo kwa chipinda chilichonse cha alonda kunali khoma lalifupi lotalika theka la mita, ndipo mbali iliyonse ya zipinda za alondazo inali yotalika mamita atatu.
Była też wystawa przed komorami na jeden łokieć, także wystawa z drugiej strony na jeden łokieć, a każda też komora na sześć łokci z jednej, a na sześć łokci z drugiej strony.
13 Ndipo anayeza kutalika kwa mulifupi mwa chipata cholowera, kuchokera ku khoma lakumbuyo la chipinda chimodzi mpaka ku khoma la chipinda china; kuchokera ku chitseko mpaka ku chitseko china. Kutalika kwake kunali mamita khumi ndi awiri ndi theka.
Potem wymierzył bramę od dachu komory jednej aż do dachu drugiej, szerokość na dwadzieścia i pięć łokci, a drzwi były przeciwko drzwiom.
14 Anayezanso khonde lamʼkati ndipo linali la mamita makumi atatu. Ndipo mozungulira khondelo munali bwalo. Muyesowu sukuphatikiza khonde loyangʼanana ndi bwalo.
I uczynił podwoje na sześćdziesiąt łokci, a każdy podwój u sieni i u bramy zewsząd w około był pod jedną miarą.
15 Kuchokera pa chipata cholowera mpaka ku mapeto a khonde la chipata, kutalika kwake kunali mamita 27.
A od przodku bramy, gdzie się wchodzi do przodku przysionka bramy wnętrznej, było pięćdziesięt łokci.
16 Makoma a zipinda ndiponso makoma a pakati pa zipindazo anali ndi mazenera. Khonde lamʼkati linalinso ndi mazenera mʼkati mwake. Pa makoma onsewo anajambulapo zithunzi za kanjedza.
Okna też pochodziste były w komorach, i nad podwojami ich wewnątrz bramy zewsząd w około, także też i w przysionkach, a na oknach zewsząd w około wewnątrz, i na podwojach były palmy.
17 Kenaka munthuyo anandilowetsa mʼbwalo lakunja, ndipo ndinaona zipinda zina ndi msewu wa miyala wozungulira bwalo lonse. Zipinda zonse zinali makumi atatu ndipo zinkayangʼana msewuwo.
Potem mię przywiódł do sieni zewnętrznej, a oto komory i tło uczynione było w sieni wszędy w około, a trzydzieści komór było na onem tle.
18 Utali wa mulifupi mwa msewuwo unkayenda mamita 27 kufanana ndi utali wa chipata cholowera. Uwu unali msewu wa mʼmunsi.
A to tło było po stronach bram, jako długie były bramy, a toć było tło niższe.
19 Tsono, anayeza kutalika kwa bwalo kuyambira chipata cholowera choyamba mpaka polowera pa chipata chakunja cha bwalo la mʼkati. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Wymierzył także szerokość od przodku bramy niższej aż do przodku sieni wewnętrznej z dworu na sto łokci ku wschodowi i ku północy.
20 Kenaka munthuyo anayeza mulitali ndi mulifupi mwa chipata chimene chimayangʼana kumpoto, chotulukira kunja.
Bramę też, która była ku północy przy sieni zewnętrznej, wymierzy wdłuż i wszerz:
21 Zipinda za alonda zimene zinalipo zitatu mbali iliyonse, makoma ake ndi khonde zinali ndi muyeso wofanana ndi wachipata choyamba chija. Kutalika kwake kunali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
(A komory jej były trzy z jednej, a trzy z drugiej strony, a podwoje jej i przysionki jej były według pomiaru pierwszej bramy; ) na pięćdziesiąt łokci była długość jej, a szerokość na dwadzieścia i pięć łokci.
22 Mipata yake, khonde lake ndi zojambula za kanjedza zinali ndi miyeso yofanana ndi za chipata chakummawa. Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndipo kotsirizira kwa chipatacho kunali khonde.
Okna też jej, i przysionki jej, i palmy jej były według pomiaru bramy onej, która patrzyła na wschód, a po siedmiu stopniach wstępowano na nią, a przysionki jej były tuż przed schodami.
23 Panalinso chipata cholowera ku bwalo lamʼkati chofanana ndi chakummawa chimene chimayangʼanana ndi chipata chakumpoto, chofanana ndi cha mbali ya kummawa. Anachiyeza kuchokera ku chipata china mpaka ku chipata china. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Także brama sieni wewnętrznej była przeciw bramie ku północy i ku wschodowi, a wymierzył od bramy do bramy sto łokci.
24 Ndipo munthuyo anapita nane ku mbali yakummwera ndipo ndinaona chipata chakummwera. Iye anayeza mphuthu zake ndi khonde ndipo zinali ndi miyeso yofanana ndi ya zina zija.
Potem mię wywiódł na drogę południową, a oto brama była ku drodze południowej, i wymierzył podwoje jej, i przysionki jej według tejże miary.
25 Mʼzipinda za chipata cholowera chimenechi ndi mʼkhonde lake munali mipata yofanana ndi ya mʼzipinda zina. Mulitali mwake munali mamita 27, mulifupi mwake munali mamita 13.
(A okna jej, i przysionki jej wszędy w około były, także jako i drugie) na pięćdziesięt łokci wdłuż a wszerz na dwadzieścia i pięć łokci,
26 Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndi khonde kotsirizira kwake. Chipindacho chinali ndi zojambula za kanjedza ku mbali zonse za makoma.
Wschód też był do niej o siedmiu stopniach, a przysionki jej były przed nimi, także i palmy, jedna z jednej a druga z drugiej strony przy podwojach jej.
27 Bwalo lamʼkati linalinso ndi chipata kummwera. Munthuyo analiyeza kuchokera ku chipata chimenechi mpaka ku chipata chakunja. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Rozmierzył też bramę sieni wewnętrznej ku południu, od bramy do bramy ku południu sto łokci.
28 Ndipo munthu uja anandilowetsa mʼbwalo lamʼkati kudzera ku chipata chakummwera. Anayeza chipatachi ndipo chinali chofanana ndi zinzake zija.
Potem mię wwiódł do sieni wewnętrznej przez południową bramę, i rozmierzył onę bramę południową według tychże miar.
29 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake zinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi munali mamita 13.
A komory jej i podwoje jej i przysionki jej były według tychże miar, a okna jej i przysionki jej około niej zewsząd mające na pięćdziesiąt łokci wdłuż a wszerz na dwadzieścia i pięć łokci.
30 (Khonde lililonse la makonde atatu a zipata zolowera bwalo lamʼkati aja linali la mamita ozungulira mʼbwalo lamʼkati anali mamita 13 mulitali mwake, mamita awiri ndi theka mulifupi mwake).
A przysionki zewsząd w około na dwadzieścia i pięć łokci wdłuż, a wszerz na pięćdziesiąt łokci.
31 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
A przysionki jej były jako sień zewnętrzna, mając palmy na podwojach; wchód też był do niej o ośmiu stopniach.
32 Kenaka munthuyo anapita nane ku bwalo la mʼkati mbali ya kummawa, ndipo anayeza chipata cholowera; chinali chofanana ndi zinzake zina zija.
Wwiódł mię także do sieni wewnętrznej drogą wschodnią, i wymierzył onę bramę według onychże miar;
33 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake chinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
Taże komory jej i podwoje jej i przysionki jej według onychże miar, i okna jej i przysionki jej wszędy w około; wdłuż na pięćdziesiąt łokci, a wszerz na dwadzieścia i pięć łokci.
34 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
Taże przysionki jej przy sieni zewnętrznej, i palmy przy podwojach jej z obu stron; wchód też był do niej o ośmiu stopniach.
35 Kenaka anapita nane ku chipata chakumpoto ndipo anachiyeza. Chinali chofanana ndi zina zija.
Potem mię wwiódł do bramy północnej, i wymierzył ją według onychże miar.
36 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndiponso khonde lake zinali zofanana ndi zina zija, ndipo chinalinso ndi mipata mbali zonse ziwiri. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
Komory jej, podwoje jej, i przysionki jej i okna jej były wszędy w około wdłuż na pięćdziesiąt łokci, a wszerz na dwadzieścia i pięć łokci.
37 Khonde lake limayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu zake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
A podwoje jej przy sieni zewnętrznej, i palmy przy podwojach jej z obu stron, a wchód był do niej o ośmiu stopniach.
38 Panali chipinda ndipo khomo lake linali pafupi ndi khonde la chipata cholowera chamʼkati. Mʼchipinda mʼmenemo ankatsukira nyama ya nsembe yopsereza.
Były też komory i drzwi ich przy podwojach bram, a tam omywano całopalenia.
39 Pa khonde la chipatacho panali matebulo awiri, lina kuno lina uko. Ankapherapo nsembe zopsereza, nsembe zopepesera machimo ndi nsembe zopepesera kupalamula.
W przysionku też bramy były dwa stoły z jednej strony, a dwa stoły z drugiej strony, na których bito całopalenia, i ofiary za grzech, i ofiary za występek.
40 Panali matebulo anayi, awiri a iwo anali kunja kwa khoma la khonde pafupi ndi makwerero olowera pa chipata chakumpoto ndi awiri enawo anali mbali inayo ya makwerero.
Na stronie też przed wchodem przy drzwiach bramy północnej były dwa stoły, także i przy drugiej stronie, która jest u przysionku bramy, były dwa stoły.
41 Choncho ku mbali imodzi ya chipata kunali matebulo anayi, ndiponso ku mbali inayo kunali matebulo anayi. Onse pamodzi anali matebulo asanu ndi atatu. Pa matebulopo ankapherapo nyama za nsembe zopsereza.
Cztery stoły z jednej, a cztery stoły z drugiej strony były przy stronie bramy; ośm było wszystkich stołów, na których bito ofiary.
42 Matebulo anayiwa anali a miyala yosema. Lililonse mulitali mwake linali la masentimita 75, mulifupi mwake linali la masentimita 75, ndipo msinkhu wake unali wa masentimita makumi asanu. Pa matebulopo amayikapo zipangizo zophera nsembe zopsereza ndi nsembe zina.
A cztery stoły do całopalenia były z ciosanego kamienia, na półtora łokcia wdłuż, a wszerz na półtora łokcia, a wzwyż na jeden łokieć; na których kładziono naczynia, któremi bito całopalenia i inne ofiary.
43 Choncho pa matebulopo ankayikapo nyama za nsembe zopsereza. Mbedza zitatu zazitali ngati chikhatho amazikoleka pa makoma pozungulira ponse.
Haki też wmięsz na jednę dłoń w domu wszędy w około były zgotowane, a mięso na stołach dla ofiar.
44 Munthu uja anapita nane mʼkati mwa bwalo ndipo ndinaona zipinda ziwiri. Chimodzi chinali pafupi ndi chipata chakumpoto kuyangʼana kummwera ndi china chinali pafupi ndi chipata chakummwera kuyangʼana kumpoto.
Były też zewnątrz przed bramą wnętrzną komory śpiewaków w sieni wnętrznej, których rząd jeden był przy stronie bramy północnej, patrzący na południe; drugi rząd był przy stronie bramy wschodniej, patrzący na północ.
45 Munthuyo anandiwuza kuti, “Chipinda chimene chikuyangʼana kummwera ndi cha ansembe amene amayangʼanira Nyumba ya Mulungu,
I rzeł do mnie: Te komory, które patrzą ku drodze południowej, są dla kapłanów straż trzymających w domu.
46 ndipo chipinda chimene chikuyangʼana kumpoto ndi cha ansembe amene amayangʼanira guwa lansembe. Amenewa ndiwo ana a Zadoki, ndipo ndi okhawo mwa zidzukulu za Levi amene ayenera kutumikira pamaso pa Yehova mʼNyumba ya Mulungu.”
A te zaś komory, których przodek jest ku drodze północnej, są dla kapłanów straż trzymających koło ołtarza; ci są synowie Sadokowi, którzy się przybliżają z synów Lewiego do Pana, aby mu służyli.
47 Kenaka munthuyo anayeza bwalo; linali lofanana mbali zonse kutalika kwake, mulitali mwake munali mamita 53, ndipo mulifupi mwake munali mamita 53. Ndipo guwa lansembe linali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
I wymierzył tę sień na cztery granie, wdłuż na sto łokci, a wszerz na sto łokci, a ołtarz był przed domem.
48 Munthuyo anapita nane pa khonde la Nyumba ya Mulunguyo. Anayeza mphuthu za khondelo ndipo zinali mamita awiri ndi theka mbali zonse. Mulifupi mwa chipatacho munali mamita asanu ndi awiri ndipo mulifupi mwa makoma ake munali mamita awiri mbali zonse.
Wwiódł mię potem do przysionka domu, i rozmierzył podwoje przysionka na pięć łokci z jednej, a na pięć łokci z drugiej strony; szerz zasię bramy była na trzy łokcie z jednej, a na trzy łokcie z drugiej strony.
49 Mulitali mwa khonde munali mamita khumi, mulifupi mwake munali mamita asanu ndi limodzi kuchokera kutsogolo mpaka kumbuyo. Panali makwerero khumi, ndipo mbali zonse kunali nsanamira.
A długość przysionka była na dwadzieścia łokci, a szerokość na jedenaście łokci, a po stopniach wchodzono do niego; słupy też były przy podwojach, jeden z jednej, a drugi z drugiej strony.

< Ezekieli 40 >