< Ezekieli 40 >

1 Kumayambiriro a chaka cha 25, cha ukapolo wathu, tsiku la khumi lamwezi, patapita zaka khumi ndi zinayi mzinda wa Yerusalemu utawonongedwa, pa tsiku lomwelo dzanja la Yehova linali pa ine ndipo Iye anapita nane ku Yerusalemu.
I det fem og tyvende år efterat vi var bortført, i begynnelsen av året, på den tiende dag i måneden, i det fjortende år efterat staden var inntatt, nettop på den dag kom Herrens hånd over mig, og han førte mig dit.
2 Mʼmasomphenyawo Yehova ananditenga ndi kupita nane ku dziko la Israeli ndipo anandiyika pa phiri lalitali kwambiri, moti ndinaona ngati mzinda.
I syner fra Gud førte han mig til Israels land og satte mig ned på et meget høit fjell, og på det var det likesom en bygget stad i syd.
3 Atandifikitsa kumeneko ndinaona munthu wonyezimira ngati mkuwa. Iye anali atayima pa chipata ndipo mʼdzanja lake munali chingwe cha nsalu yabafuta ndi ndodo yoyezera.
Og han førte mig dit, og se, der var en mann hvis utseende var som kobber, og han hadde en linsnor og en målestang i hånden, og han stod i porten.
4 Munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, penyetsetsa ndipo umvetse bwinobwino. Uyikepo mtima wako pa zonse zimene ndikukuonetsa pakuti anakubweretsa kuno kuti uwone zimenezi. Tsono ukawawuze Aisraeli zonse zimene uzione.”
Og mannen talte til mig og sa: Menneskesønn! Se med dine øine og hør med dine ører og akt på alt det jeg vil la dig se! For du er ført hit, forat jeg skal la dig se det. Forkynn Israels hus alt det du ser!
5 Ine ndinaona khoma litazungulira mbali zonse za Nyumba ya Mulungu. Mʼdzanja la munthuyo munali bango lopimira limene kutalika kwake kunali kwa mamita atatu. Atayeza chipupacho anapeza kuti kuchindikira kwake kunali mamita atatu, ndiponso kutalika kwake kunalinso mamita atatu.
Og se, der var en mur utenom huset rundt omkring, og målestangen som mannen hadde i hånden, var seks alen lang, hver alen regnet til en almindelig alen og en håndsbredd, og han målte murens bredde: den var én stang, og dens høide: den var én stang.
6 Anapita ku chipata chakummawa. Anakwera pa makwerero a nyumbayo, nayeza chiwundo choyamba cha chipatacho; kutalika kwake kunali mamita atatu.
Så kom han til den port hvis forside vendte mot øst, og han steg op efter dens trin, og han målte portens treskel: den var én stang i bredden - det var den første treskel, og den var én stang i bredden.
7 Kudutsa chiwundo choyambachi, panali zipinda za alonda zisanu ndi chimodzi, zitatu kudzanja lamanja, zitatu kudzanja lamanzere. Chilichonse chinali cha mamita atatu mulitali mwake, chimodzimodzinso mulifupi mwake. Mipata ya pakati pa zipindazo inali ya mamita awiri ndi theka. Ndipo chiwundo cha pa chipata pafupi ndi khonde lapachipata, chinali mamita atatu.
Og hver vaktstue var én stang i lengden og én stang i bredden, og mellem vaktstuene var det fem alen, og portens treskel ved portens forhall på den indre side var én stang.
8 Ndipo iye anayeza khonde la chipata ndipo chinali cha mamita atatu.
Og han målte portens forhall på den indre side: den var én stang.
9 Anayeza khonde ndipo linali mamita anayi. Mphuthu zake zinali mita imodzi kuchindikira kwake. Khonde lamʼkati lapachipata linali kumapeto kwenikweni pafupi ndi Nyumba ya Mulungu.
Og han målte portens forhall: den var åtte alen, og dens pilarer: de var to alen, og portens forhall lå på innsiden.
10 Mʼkati mwa chipata chakummawa munali zipinda za alonda zitatu mbali iliyonse. Zitatu zonsezo zinali zofanana, ndipo khonde la pakati pa zipindazo linali lofanana.
Og vaktstuene i porten mot øst var tre på hver side; alle tre var like store, og pilarene på begge sider var også like store.
11 Kenaka anayeza chipata cholowera; mulifupi mwake munali mamita asanu ndipo mulitali mwake munali mamita asanu ndi limodzi ndi theka.
Og han målte bredden av portåpningen: den var ti alen, og portens lengde: den var tretten alen.
12 Kutsogolo kwa chipinda chilichonse cha alonda kunali khoma lalifupi lotalika theka la mita, ndipo mbali iliyonse ya zipinda za alondazo inali yotalika mamita atatu.
Foran vaktstuene var det et rum på én alen, og på den andre side likeledes et rum på én alen, og hver vaktstue var seks alen på den ene og seks alen på den andre side.
13 Ndipo anayeza kutalika kwa mulifupi mwa chipata cholowera, kuchokera ku khoma lakumbuyo la chipinda chimodzi mpaka ku khoma la chipinda china; kuchokera ku chitseko mpaka ku chitseko china. Kutalika kwake kunali mamita khumi ndi awiri ndi theka.
Og han målte porten fra den ene vaktstues tak til den andres tak; bredden var fem og tyve alen, dør midt imot dør.
14 Anayezanso khonde lamʼkati ndipo linali la mamita makumi atatu. Ndipo mozungulira khondelo munali bwalo. Muyesowu sukuphatikiza khonde loyangʼanana ndi bwalo.
Og han gjorde pilarene seksti alen høie, og tett inn til pilarene lå forgården, rundt omkring porten.
15 Kuchokera pa chipata cholowera mpaka ku mapeto a khonde la chipata, kutalika kwake kunali mamita 27.
Og fra forsiden av inngangsporten til forsiden av den indre ports forhall var det femti alen.
16 Makoma a zipinda ndiponso makoma a pakati pa zipindazo anali ndi mazenera. Khonde lamʼkati linalinso ndi mazenera mʼkati mwake. Pa makoma onsewo anajambulapo zithunzi za kanjedza.
Og det var vinduer med fast gitter på vaktstuene og på deres pilarer innentil mot porten rundt omkring, og likeså på hallene; og således var det vinduer rundt omkring innentil, og på pilarene var det palmer.
17 Kenaka munthuyo anandilowetsa mʼbwalo lakunja, ndipo ndinaona zipinda zina ndi msewu wa miyala wozungulira bwalo lonse. Zipinda zonse zinali makumi atatu ndipo zinkayangʼana msewuwo.
Så førte han mig til den ytre forgård, og se, der var kammere og et stenlagt gulv i forgården rundt omkring; det var tretti kammer på stengulvet.
18 Utali wa mulifupi mwa msewuwo unkayenda mamita 27 kufanana ndi utali wa chipata cholowera. Uwu unali msewu wa mʼmunsi.
Og stengulvet var ved siden av portene, svarende til portenes lengde; det var det nedre stengulv.
19 Tsono, anayeza kutalika kwa bwalo kuyambira chipata cholowera choyamba mpaka polowera pa chipata chakunja cha bwalo la mʼkati. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Og han målte bredden fra forsiden av den nedre port til den ytre forside av den indre forgård: den var hundre alen mot øst og mot nord.
20 Kenaka munthuyo anayeza mulitali ndi mulifupi mwa chipata chimene chimayangʼana kumpoto, chotulukira kunja.
Så målte han lengden og bredden av den port hvis forside vendte mot nord, og som hørte til den ytre forgård.
21 Zipinda za alonda zimene zinalipo zitatu mbali iliyonse, makoma ake ndi khonde zinali ndi muyeso wofanana ndi wachipata choyamba chija. Kutalika kwake kunali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
Den hadde tre vaktstuer på hver side, og dens pilarer og haller var like store som de i den første port; den var femti alen lang og fem og tyve alen bred.
22 Mipata yake, khonde lake ndi zojambula za kanjedza zinali ndi miyeso yofanana ndi za chipata chakummawa. Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndipo kotsirizira kwa chipatacho kunali khonde.
Og vinduene og hallene og palmene var like store som i den port hvis forside vendte mot øst, og på syv trin steg en op i den, og dens haller lå foran dem.
23 Panalinso chipata cholowera ku bwalo lamʼkati chofanana ndi chakummawa chimene chimayangʼanana ndi chipata chakumpoto, chofanana ndi cha mbali ya kummawa. Anachiyeza kuchokera ku chipata china mpaka ku chipata china. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Og porten til den indre forgård lå midt imot porten som vendte mot nord og mot øst, og han målte hundre alen fra port til port.
24 Ndipo munthuyo anapita nane ku mbali yakummwera ndipo ndinaona chipata chakummwera. Iye anayeza mphuthu zake ndi khonde ndipo zinali ndi miyeso yofanana ndi ya zina zija.
Så førte han mig mot syd, og se, der var en port som vendte mot syd; og han målte dens pilarer og haller: de var like store som de andre.
25 Mʼzipinda za chipata cholowera chimenechi ndi mʼkhonde lake munali mipata yofanana ndi ya mʼzipinda zina. Mulitali mwake munali mamita 27, mulifupi mwake munali mamita 13.
Og det var vinduer på den og på dens haller rundt omkring, likesom de andre vinduer; den var femti alen lang og fem og tyve alen bred.
26 Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndi khonde kotsirizira kwake. Chipindacho chinali ndi zojambula za kanjedza ku mbali zonse za makoma.
Dens trapper hadde syv trin, og dens haller lå foran dem, og på dens pilarer var det palmer, én på hver side.
27 Bwalo lamʼkati linalinso ndi chipata kummwera. Munthuyo analiyeza kuchokera ku chipata chimenechi mpaka ku chipata chakunja. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Og der var en port til den indre forgård mot syd, og fra denne port til porten mot syd målte han hundre alen.
28 Ndipo munthu uja anandilowetsa mʼbwalo lamʼkati kudzera ku chipata chakummwera. Anayeza chipatachi ndipo chinali chofanana ndi zinzake zija.
Så førte han mig til den indre forgård gjennem sydporten, og han målte sydporten: den var like stor som de andre.
29 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake zinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi munali mamita 13.
Og dens vaktstuer og pilarer og haller var like store som de andre, og det var vinduer på den og på dens haller rundt omkring; den var femti alen lang og fem og tyve alen bred.
30 (Khonde lililonse la makonde atatu a zipata zolowera bwalo lamʼkati aja linali la mamita ozungulira mʼbwalo lamʼkati anali mamita 13 mulitali mwake, mamita awiri ndi theka mulifupi mwake).
Og det var haller rundt omkring, fem og tyve alen lange og fem alen brede.
31 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
Hallene vendte ut mot den ytre forgård, og det var palmer på pilarene, og trappene hadde åtte trin.
32 Kenaka munthuyo anapita nane ku bwalo la mʼkati mbali ya kummawa, ndipo anayeza chipata cholowera; chinali chofanana ndi zinzake zina zija.
Så førte han mig til den indre forgård mot øst, og han målte porten: den var like stor som de andre.
33 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake chinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
Og dens vaktstuer og pilarer og haller var like store som de andre; og det var vinduer på den og på dens haller rundt omkring; den var femti alen lang og fem og tyve alen bred.
34 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
Hallene vendte ut mot den ytre forgård, og det var palmer på pilarene på begge sider, og trappene hadde åtte trin.
35 Kenaka anapita nane ku chipata chakumpoto ndipo anachiyeza. Chinali chofanana ndi zina zija.
Så førte han mig til nordporten, og han målte den: den var like stor som de andre;
36 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndiponso khonde lake zinali zofanana ndi zina zija, ndipo chinalinso ndi mipata mbali zonse ziwiri. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
likeså målte han dens vaktstuer, pilarer og haller, og det var vinduer på den rundt omkring; den var femti alen lang og fem og tyve alen bred.
37 Khonde lake limayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu zake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
Dens pilarer vendte mot den ytre forgård, og det var palmer på pilarene på begge sider, og trappene hadde åtte trin.
38 Panali chipinda ndipo khomo lake linali pafupi ndi khonde la chipata cholowera chamʼkati. Mʼchipinda mʼmenemo ankatsukira nyama ya nsembe yopsereza.
Og det var et kammer med dør i pilarene ved portene; der skulde de skylle brennofferet.
39 Pa khonde la chipatacho panali matebulo awiri, lina kuno lina uko. Ankapherapo nsembe zopsereza, nsembe zopepesera machimo ndi nsembe zopepesera kupalamula.
Og i portens forhall stod det to bord på hver side til å slakte brennofferet og syndofferet og skyldofferet på.
40 Panali matebulo anayi, awiri a iwo anali kunja kwa khoma la khonde pafupi ndi makwerero olowera pa chipata chakumpoto ndi awiri enawo anali mbali inayo ya makwerero.
Og ved den ytre sidevegg, når en steg op i inngangen til porten mot nord, stod det to bord, og ved deri andre sidevegg på portens forhall stod det også to bord -
41 Choncho ku mbali imodzi ya chipata kunali matebulo anayi, ndiponso ku mbali inayo kunali matebulo anayi. Onse pamodzi anali matebulo asanu ndi atatu. Pa matebulopo ankapherapo nyama za nsembe zopsereza.
fire bord ved hver sidevegg på porten, tilsammen åtte bord; på dem skulde de slakte.
42 Matebulo anayiwa anali a miyala yosema. Lililonse mulitali mwake linali la masentimita 75, mulifupi mwake linali la masentimita 75, ndipo msinkhu wake unali wa masentimita makumi asanu. Pa matebulopo amayikapo zipangizo zophera nsembe zopsereza ndi nsembe zina.
Og det var fire bord til brennofferet; de var av hugne stener, halvannen alen lange og halvannen alen brede og én alen høie; på dem skulde de legge de redskaper som de skulde slakte brennofferet og slaktofferet med.
43 Choncho pa matebulopo ankayikapo nyama za nsembe zopsereza. Mbedza zitatu zazitali ngati chikhatho amazikoleka pa makoma pozungulira ponse.
Og dobbelte knagger, en hånd brede, var festet på huset rundt omkring, og på bordene skulde offerkjøttet legges.
44 Munthu uja anapita nane mʼkati mwa bwalo ndipo ndinaona zipinda ziwiri. Chimodzi chinali pafupi ndi chipata chakumpoto kuyangʼana kummwera ndi china chinali pafupi ndi chipata chakummwera kuyangʼana kumpoto.
Og utenfor den indre port var det kammere for sangerne i den indre forgård, ved siden av nordporten, og deres forside vendte mot syd; og en annen rad kammer lå ved siden av østporten, med forsiden mot nord.
45 Munthuyo anandiwuza kuti, “Chipinda chimene chikuyangʼana kummwera ndi cha ansembe amene amayangʼanira Nyumba ya Mulungu,
Og han talte til mig og sa: Denne rad kammer, hvis forside vender mot syd, er for de prester som tar vare på det som er å vareta ved huset;
46 ndipo chipinda chimene chikuyangʼana kumpoto ndi cha ansembe amene amayangʼanira guwa lansembe. Amenewa ndiwo ana a Zadoki, ndipo ndi okhawo mwa zidzukulu za Levi amene ayenera kutumikira pamaso pa Yehova mʼNyumba ya Mulungu.”
men den rad kammer hvis forside vender mot nord, er for de prester som tar vare på det som er å vareta ved alteret; det er Sadoks sønner, de av Levis sønner som treder nær til Herren for å tjene ham.
47 Kenaka munthuyo anayeza bwalo; linali lofanana mbali zonse kutalika kwake, mulitali mwake munali mamita 53, ndipo mulifupi mwake munali mamita 53. Ndipo guwa lansembe linali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
Og han målte forgården: den var hundre alen lang og hundre alen bred i firkant, og alteret stod foran huset.
48 Munthuyo anapita nane pa khonde la Nyumba ya Mulunguyo. Anayeza mphuthu za khondelo ndipo zinali mamita awiri ndi theka mbali zonse. Mulifupi mwa chipatacho munali mamita asanu ndi awiri ndipo mulifupi mwa makoma ake munali mamita awiri mbali zonse.
Så førte han mig til husets forhall og målte forhallens pilarer: de var fem alen på den ene og fem alen på den andre side, og portens bredde: den var tre alen på hver side.
49 Mulitali mwa khonde munali mamita khumi, mulifupi mwake munali mamita asanu ndi limodzi kuchokera kutsogolo mpaka kumbuyo. Panali makwerero khumi, ndipo mbali zonse kunali nsanamira.
Forhallen var tyve alen lang og elleve alen bred, og den hadde trin som førte op til den, og ved pilarene stod der søiler, én på hver side.

< Ezekieli 40 >