< Ezekieli 40 >

1 Kumayambiriro a chaka cha 25, cha ukapolo wathu, tsiku la khumi lamwezi, patapita zaka khumi ndi zinayi mzinda wa Yerusalemu utawonongedwa, pa tsiku lomwelo dzanja la Yehova linali pa ine ndipo Iye anapita nane ku Yerusalemu.
Ngomnyaka wamatshumi amabili lanhlanu wokuthunjwa kwethu, ekuqaliseni komnyaka, ngolwetshumi lwenyanga, ngomnyaka wetshumi lane emva kokuthi umuzi usutshayiwe, ngalona lolosuku isandla seNkosi saba phezu kwami, wangiletha lapho.
2 Mʼmasomphenyawo Yehova ananditenga ndi kupita nane ku dziko la Israeli ndipo anandiyika pa phiri lalitali kwambiri, moti ndinaona ngati mzinda.
Ngemibono kaNkulunkulu wangisa elizweni lakoIsrayeli, wangibeka phezu kwentaba ende kakhulu; njalo eceleni kwayo kwakulokunjengesakhiwo somuzi ngaseningizimu.
3 Atandifikitsa kumeneko ndinaona munthu wonyezimira ngati mkuwa. Iye anali atayima pa chipata ndipo mʼdzanja lake munali chingwe cha nsalu yabafuta ndi ndodo yoyezera.
Wasengiletha khona, khangela-ke, kwakulomuntu osimo sakhe sasinjengesimo sethusi, elentambo yefilakisi esandleni sakhe, lomhlanga wokulinganisa; wema-ke esangweni.
4 Munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, penyetsetsa ndipo umvetse bwinobwino. Uyikepo mtima wako pa zonse zimene ndikukuonetsa pakuti anakubweretsa kuno kuti uwone zimenezi. Tsono ukawawuze Aisraeli zonse zimene uzione.”
Lowomuntu wasesithi kimi: Ndodana yomuntu, bona ngamehlo akho, uzwe ngendlebe zakho, ubeke inhliziyo yakho phezu kwakho konke engizakutshengisa khona; ngoba ulethwe lapha ukuze ngikutshengise khona. Landisa konke okubonayo kuyo indlu yakoIsrayeli.
5 Ine ndinaona khoma litazungulira mbali zonse za Nyumba ya Mulungu. Mʼdzanja la munthuyo munali bango lopimira limene kutalika kwake kunali kwa mamita atatu. Atayeza chipupacho anapeza kuti kuchindikira kwake kunali mamita atatu, ndiponso kutalika kwake kunalinso mamita atatu.
Khangela-ke, kwakulomduli ngaphandle kwendlu ozingelezeleyo inhlangothi zonke, lesandleni somuntu kwakulomhlanga wokulinganisa wezingalo eziyisithupha, ngengalo lobubanzi besandla. Waselinganisa ububanzi besakhiwo, baba ngumhlanga owodwa, lokuphakama, kwaba ngumhlanga owodwa.
6 Anapita ku chipata chakummawa. Anakwera pa makwerero a nyumbayo, nayeza chiwundo choyamba cha chipatacho; kutalika kwake kunali mamita atatu.
Wasesiza esangweni elikhangele indlela yempumalanga, wakhwela ngezinyathelo zalo, walinganisa umbundu wesango, ububanzi baba ngumhlanga owodwa, lomunye umbundu, ububanzi baba ngumhlanga owodwa.
7 Kudutsa chiwundo choyambachi, panali zipinda za alonda zisanu ndi chimodzi, zitatu kudzanja lamanja, zitatu kudzanja lamanzere. Chilichonse chinali cha mamita atatu mulitali mwake, chimodzimodzinso mulifupi mwake. Mipata ya pakati pa zipindazo inali ya mamita awiri ndi theka. Ndipo chiwundo cha pa chipata pafupi ndi khonde lapachipata, chinali mamita atatu.
Njalo yilelo lalelokamelo, ubude baba ngumhlanga owodwa, lobubanzi baba ngumhlanga owodwa; laphakathi kwamakamelo kwaba yizingalo ezinhlanu; lombundu wesango ngasekhulusini lesango ngaphakathi waba ngumhlanga owodwa.
8 Ndipo iye anayeza khonde la chipata ndipo chinali cha mamita atatu.
Walinganisa lekhulusi lesango ngaphakathi, laba ngumhlanga owodwa.
9 Anayeza khonde ndipo linali mamita anayi. Mphuthu zake zinali mita imodzi kuchindikira kwake. Khonde lamʼkati lapachipata linali kumapeto kwenikweni pafupi ndi Nyumba ya Mulungu.
Waselinganisa ikhulusi lesango, laba yizingalo eziyisificaminwembili; lemigubazi yawo, yaba zingalo ezimbili; lekhulusi lesango lalingaphakathi.
10 Mʼkati mwa chipata chakummawa munali zipinda za alonda zitatu mbali iliyonse. Zitatu zonsezo zinali zofanana, ndipo khonde la pakati pa zipindazo linali lofanana.
Lamakamelo esango ngendlela yempumalanga ayemathathu ngapha lamathathu ngapha; njalo womathathu ayelesilinganiso sinye; lemigubazi yayilesilinganiso sinye ngapha langapha.
11 Kenaka anayeza chipata cholowera; mulifupi mwake munali mamita asanu ndipo mulitali mwake munali mamita asanu ndi limodzi ndi theka.
Waselinganisa ububanzi bentuba yesango, baba yizingalo ezilitshumi; ubude besango, baba yizingalo ezilitshumi lantathu.
12 Kutsogolo kwa chipinda chilichonse cha alonda kunali khoma lalifupi lotalika theka la mita, ndipo mbali iliyonse ya zipinda za alondazo inali yotalika mamita atatu.
Lomkhawulo phambi kwamakamelo wawuyingalo eyodwa ngapha, lomkhawulo wengalo eyodwa ngapha; lekamelo laliyizingalo eziyisithupha ngapha, lezingalo eziyisithupha ngapha.
13 Ndipo anayeza kutalika kwa mulifupi mwa chipata cholowera, kuchokera ku khoma lakumbuyo la chipinda chimodzi mpaka ku khoma la chipinda china; kuchokera ku chitseko mpaka ku chitseko china. Kutalika kwake kunali mamita khumi ndi awiri ndi theka.
Waselinganisa isango kusukela ephahleni lwelinye ikamelo kusiya ephahleni lwelinye; ububanzi babuzingalo ezingamatshumi amabili lanhlanu, umnyango phambi komnyango.
14 Anayezanso khonde lamʼkati ndipo linali la mamita makumi atatu. Ndipo mozungulira khondelo munali bwalo. Muyesowu sukuphatikiza khonde loyangʼanana ndi bwalo.
Wenza futhi imigubazi yaba zingalo ezingamatshumi ayisithupha, ngitsho kuze kube semgubazini weguma inhlangothi zonke zesango zizingelezele.
15 Kuchokera pa chipata cholowera mpaka ku mapeto a khonde la chipata, kutalika kwake kunali mamita 27.
Njalo kusukela ebusweni besango lokungena kuze kube sebusweni bekhulusi lesango elingaphakathi kwaba zingalo ezingamatshumi amahlanu.
16 Makoma a zipinda ndiponso makoma a pakati pa zipindazo anali ndi mazenera. Khonde lamʼkati linalinso ndi mazenera mʼkati mwake. Pa makoma onsewo anajambulapo zithunzi za kanjedza.
Futhi kwakulamawindi avaliweyo emakamelweni, lasemigubazini yawo ngaphakathi kwesango inhlangothi zonke azingelezeleyo; langokunjalo amakhulusi; lamawindi inhlangothi zonke azingelezeleyo ngaphakathi; laphezu kwemigubazi kwakulezihlahla zelala.
17 Kenaka munthuyo anandilowetsa mʼbwalo lakunja, ndipo ndinaona zipinda zina ndi msewu wa miyala wozungulira bwalo lonse. Zipinda zonse zinali makumi atatu ndipo zinkayangʼana msewuwo.
Wasengingenisa egumeni elingaphandle, khangela-ke, kwakulamakamelo, lendawo egandelweyo eyenzelwe iguma inhlangothi zonke ezingelezeleyo; kwakulamakamelo angamatshumi amathathu phezu kwendawo egandelweyo.
18 Utali wa mulifupi mwa msewuwo unkayenda mamita 27 kufanana ndi utali wa chipata cholowera. Uwu unali msewu wa mʼmunsi.
Lendawo egandelweyo yayingasemasangweni maqondana lobude bamasango; kwakuyindawo egandelweyo engaphansi.
19 Tsono, anayeza kutalika kwa bwalo kuyambira chipata cholowera choyamba mpaka polowera pa chipata chakunja cha bwalo la mʼkati. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Waselinganisa ububanzi, kusukela ngaphambi kwesango elingaphansi kusiya ngaphambi kweguma elingaphakathi ngaphandle, kwaba yizingalo ezilikhulu, ngasempumalanga langasenyakatho.
20 Kenaka munthuyo anayeza mulitali ndi mulifupi mwa chipata chimene chimayangʼana kumpoto, chotulukira kunja.
Lesango elikhangele indlela yenyakatho, kulo iguma elingaphandle, walinganisa ubude balo lobubanzi balo.
21 Zipinda za alonda zimene zinalipo zitatu mbali iliyonse, makoma ake ndi khonde zinali ndi muyeso wofanana ndi wachipata choyamba chija. Kutalika kwake kunali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
Lamakamelo alo ayemathathu ngapha, njalo emathathu ngapha; lemigubazi yalo lamakhulusi alo kwakunjengesilinganiso sesango lokuqala. Ubude balo babuzingalo ezingamatshumi amahlanu, lobubanzi buzingalo ezingamatshumi amabili lanhlanu.
22 Mipata yake, khonde lake ndi zojambula za kanjedza zinali ndi miyeso yofanana ndi za chipata chakummawa. Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndipo kotsirizira kwa chipatacho kunali khonde.
Lamawindi alo lamakhulusi alo lezihlahla zalo zelala kwakunjengesilinganiso sesango elikhangele indlela yempumalanga. Njalo benyukela kilo ngezinyathelo eziyisikhombisa; lamakhulusi alo ayephambi kwakho.
23 Panalinso chipata cholowera ku bwalo lamʼkati chofanana ndi chakummawa chimene chimayangʼanana ndi chipata chakumpoto, chofanana ndi cha mbali ya kummawa. Anachiyeza kuchokera ku chipata china mpaka ku chipata china. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Lesango leguma elingaphakathi lalimaqondana lesango elingasenyakatho langasempumalanga. Waselinganisa kusukela esangweni kusiya esangweni, kwaba zingalo ezilikhulu.
24 Ndipo munthuyo anapita nane ku mbali yakummwera ndipo ndinaona chipata chakummwera. Iye anayeza mphuthu zake ndi khonde ndipo zinali ndi miyeso yofanana ndi ya zina zija.
Emva kwalokho wangiletha ngendlela yeningizimu, khangela-ke, kwakukhona isango ngasendleleni yeningizimu; waselinganisa imigubazi yalo lamakhulusi alo njengokwalezizilinganiso.
25 Mʼzipinda za chipata cholowera chimenechi ndi mʼkhonde lake munali mipata yofanana ndi ya mʼzipinda zina. Mulitali mwake munali mamita 27, mulifupi mwake munali mamita 13.
Kwakukhona amawindi kilo lakuwo amakhulusi alo azingelezeleyo inhlangothi zonke, njengalawomawindi. Ubude babuzingalo ezingamatshumi amahlanu, lobubanzi buzingalo ezingamatshumi amabili lanhlanu.
26 Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndi khonde kotsirizira kwake. Chipindacho chinali ndi zojambula za kanjedza ku mbali zonse za makoma.
Kwakukhona izinyathelo eziyisikhombisa zokwenyukela kilo, lamakhulusi alo ayephambi kwazo; njalo lalilezihlahla zelala, esinye ngapha, lesinye ngapha, phezu kwemigubazi yalo.
27 Bwalo lamʼkati linalinso ndi chipata kummwera. Munthuyo analiyeza kuchokera ku chipata chimenechi mpaka ku chipata chakunja. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Kwakukhona isango egumeni elingaphakathi ngendlela yeningizimu; waselinganisa kusukela esangweni kusiya esangweni ngendlela yeningizimu, kwaba zingalo ezilikhulu.
28 Ndipo munthu uja anandilowetsa mʼbwalo lamʼkati kudzera ku chipata chakummwera. Anayeza chipatachi ndipo chinali chofanana ndi zinzake zija.
Wasengiletha egumeni elingaphakathi ngesango leningizimu, walinganisa isango leningizimu njengokwezilinganiso lezi.
29 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake zinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi munali mamita 13.
Lamakamelo alo lemigubazi yalo lamakhulusi alo kwakunjengokwezilinganiso lezi. Njalo kwakukhona amawindi kilo lakuwo amakhulusi alo inhlangothi zonke azingelezeleyo. Lobude babuyizingalo ezingamatshumi amahlanu, lobubanzi babuzingalo ezingamatshumi amabili lanhlanu.
30 (Khonde lililonse la makonde atatu a zipata zolowera bwalo lamʼkati aja linali la mamita ozungulira mʼbwalo lamʼkati anali mamita 13 mulitali mwake, mamita awiri ndi theka mulifupi mwake).
Kwakulamakhulusi azingelezeleyo inhlangothi zonke; ubude babuzingalo ezingamatshumi amabili lanhlanu, lobubanzi babuzingalo ezinhlanu.
31 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
Lamakhulusi alo aba ngasegumeni elingaphandle, lezihlahla zelala zaziphezu kwemigubazi yalo, lokwenyukela kilo kwakulezinyathelo eziyisificaminwembili.
32 Kenaka munthuyo anapita nane ku bwalo la mʼkati mbali ya kummawa, ndipo anayeza chipata cholowera; chinali chofanana ndi zinzake zina zija.
Wasengiletha egumeni elingaphakathi ngasendleleni yempumalanga; walinganisa isango njengokwezilinganiso lezi.
33 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake chinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
Lamakamelo alo lemigubazi yalo lamakhulusi alo kwakunjengokwezilinganiso lezi; kwakukhona amawindi kilo lakuwo amakhulusi alo inhlangothi zonke kuzingelezele. Ubude babuzingalo ezingamatshumi amahlanu, lobubanzi babuzingalo ezingamatshumi amabili lanhlanu.
34 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
Lamakhulusi alo ayengasegumeni elingaphandle; lezihlahla zelala zazisemigubazini yalo, ngapha langapha; lokwenyukela kilo kwakulezinyathelo eziyisificaminwembili.
35 Kenaka anapita nane ku chipata chakumpoto ndipo anachiyeza. Chinali chofanana ndi zina zija.
Wasengisa esangweni elingenyakatho, walinganisa njengezilinganiso lezi.
36 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndiponso khonde lake zinali zofanana ndi zina zija, ndipo chinalinso ndi mipata mbali zonse ziwiri. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
Amakamelo alo, imigubazi yalo, lamakhulusi alo, lamawindi ayekulo inhlangothi zonke azingelezeleyo; ubude babuzingalo ezingamatshumi amahlanu, lobubanzi buzingalo ezingamatshumi amabili lanhlanu.
37 Khonde lake limayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu zake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
Lemigubazi yalo yayingasegumeni elingaphandle, lezihlahla zelala zazisemigubazini yalo, ngapha langapha; lokwenyukela kilo kwakulezinyathelo eziyisificaminwembili.
38 Panali chipinda ndipo khomo lake linali pafupi ndi khonde la chipata cholowera chamʼkati. Mʼchipinda mʼmenemo ankatsukira nyama ya nsembe yopsereza.
Njalo amakamelo leminyango yalo kwakungasemigubazini yamasango; lapho babegezisela umnikelo wokutshiswa.
39 Pa khonde la chipatacho panali matebulo awiri, lina kuno lina uko. Ankapherapo nsembe zopsereza, nsembe zopepesera machimo ndi nsembe zopepesera kupalamula.
Lekhulusini lesango kwakukhona amatafula amabili ngapha, lamatafula amabili ngapha, ukuhlabela phezu kwawo umnikelo wokutshiswa lomnikelo wesono lomnikelo wecala.
40 Panali matebulo anayi, awiri a iwo anali kunja kwa khoma la khonde pafupi ndi makwerero olowera pa chipata chakumpoto ndi awiri enawo anali mbali inayo ya makwerero.
Laseceleni ngaphandle ekwenyukeleni kuso isivalo sesango lenyakatho kwakulamatafula amabili, laseceleni elinye elingasekhulusini lesango kwakulamatafula amabili.
41 Choncho ku mbali imodzi ya chipata kunali matebulo anayi, ndiponso ku mbali inayo kunali matebulo anayi. Onse pamodzi anali matebulo asanu ndi atatu. Pa matebulopo ankapherapo nyama za nsembe zopsereza.
Amatafula amane ngapha, lamatafula amane ngapha, ngaseceleni kwesango; amatafula ayisificaminwembili, ababehlabela phezu kwawo.
42 Matebulo anayiwa anali a miyala yosema. Lililonse mulitali mwake linali la masentimita 75, mulifupi mwake linali la masentimita 75, ndipo msinkhu wake unali wa masentimita makumi asanu. Pa matebulopo amayikapo zipangizo zophera nsembe zopsereza ndi nsembe zina.
Lamatafula amane omnikelo wokutshiswa awamatshe abaziweyo; ubude babuyingalo eyodwa lengxenye, lobubanzi babuyingalo eyodwa lengxenye, lokuphakama kwakuyingalo eyodwa. Phezu kwawo babeka izikhali abahlaba ngazo umnikelo wokutshiswa lomhlatshelo.
43 Choncho pa matebulopo ankayikapo nyama za nsembe zopsereza. Mbedza zitatu zazitali ngati chikhatho amazikoleka pa makoma pozungulira ponse.
Kwakulezingwegwe, eziyibubanzi besandla sinye, zimisiwe ngaphakathi inhlangothi zonke ezizingelezeleyo; laphezu kwamatafula kwakulenyama yomnikelo.
44 Munthu uja anapita nane mʼkati mwa bwalo ndipo ndinaona zipinda ziwiri. Chimodzi chinali pafupi ndi chipata chakumpoto kuyangʼana kummwera ndi china chinali pafupi ndi chipata chakummwera kuyangʼana kumpoto.
Langaphandle kwesango elingaphakathi kwakulamakamelo abahlabeleli egumeni elingaphakathi, elaliseceleni kwesango elisenyakatho, lokukhangela kwalo kusendleleni yeningizimu; elilodwa liseceleni kwesango eliseningizimu, likhangele ngasendleleni yenyakatho.
45 Munthuyo anandiwuza kuti, “Chipinda chimene chikuyangʼana kummwera ndi cha ansembe amene amayangʼanira Nyumba ya Mulungu,
Wasesithi kimi: Lelikamelo okukhangela kwalo kusendleleni yeningizimu, lingelabapristi, abagcina umlindo wendlu.
46 ndipo chipinda chimene chikuyangʼana kumpoto ndi cha ansembe amene amayangʼanira guwa lansembe. Amenewa ndiwo ana a Zadoki, ndipo ndi okhawo mwa zidzukulu za Levi amene ayenera kutumikira pamaso pa Yehova mʼNyumba ya Mulungu.”
Lekamelo okukhangela kwalo kusendleleni yenyakatho lingelabapristi, abagcina umlindo welathi. La ngamadodana kaZadoki phakathi kwamadodana kaLevi, asondela eNkosini ukuyikhonza.
47 Kenaka munthuyo anayeza bwalo; linali lofanana mbali zonse kutalika kwake, mulitali mwake munali mamita 53, ndipo mulifupi mwake munali mamita 53. Ndipo guwa lansembe linali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
Waselinganisa iguma; ubude baba zingalo ezilikhulu, lobubanzi baba zingalo ezilikhulu, lilingene inhlangothi zozine; lelathi laliphambi kwendlu.
48 Munthuyo anapita nane pa khonde la Nyumba ya Mulunguyo. Anayeza mphuthu za khondelo ndipo zinali mamita awiri ndi theka mbali zonse. Mulifupi mwa chipatacho munali mamita asanu ndi awiri ndipo mulifupi mwa makoma ake munali mamita awiri mbali zonse.
Wasengiletha ekhulusini lendlu, walinganisa umgubazi wekhulusi, izingalo ezinhlanu ngapha lezingalo ezinhlanu ngapha, lobubanzi besango, izingalo ezintathu ngapha, lezingalo ezintathu ngapha.
49 Mulitali mwa khonde munali mamita khumi, mulifupi mwake munali mamita asanu ndi limodzi kuchokera kutsogolo mpaka kumbuyo. Panali makwerero khumi, ndipo mbali zonse kunali nsanamira.
Ubude bekhulusi babuzingalo ezingamatshumi amabili, lobubanzi buzingalo ezilitshumi lanye; wasengiletha ngezinyathelo abenyukela kulo ngazo; futhi kwakulezinsika ngasemigubazini, enye ngapha, lenye ngapha.

< Ezekieli 40 >