< Ezekieli 40 >

1 Kumayambiriro a chaka cha 25, cha ukapolo wathu, tsiku la khumi lamwezi, patapita zaka khumi ndi zinayi mzinda wa Yerusalemu utawonongedwa, pa tsiku lomwelo dzanja la Yehova linali pa ine ndipo Iye anapita nane ku Yerusalemu.
En la vingt-cinquième année de notre transmigration, au commencement de l’année, au dixième jour du mois, en la quatorzième année, après qu’eut été frappée la cité; en ce même jour, la main du Seigneur fut sur moi. et il m’amena là.
2 Mʼmasomphenyawo Yehova ananditenga ndi kupita nane ku dziko la Israeli ndipo anandiyika pa phiri lalitali kwambiri, moti ndinaona ngati mzinda.
Dans des visions divines, il m’amena dans la terre d’Israël, et me laissa sur une montagne très haute, sur laquelle était comme l’édifice d’une cité tournée vers le midi.
3 Atandifikitsa kumeneko ndinaona munthu wonyezimira ngati mkuwa. Iye anali atayima pa chipata ndipo mʼdzanja lake munali chingwe cha nsalu yabafuta ndi ndodo yoyezera.
Et il m’introduisit là, et voilà un homme dont l’apparence était comme l’apparence de l’airain; et un cordeau de lin était dans sa main, et une canne à mesurer dans son autre main; mais il se tenait à la porte.
4 Munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, penyetsetsa ndipo umvetse bwinobwino. Uyikepo mtima wako pa zonse zimene ndikukuonetsa pakuti anakubweretsa kuno kuti uwone zimenezi. Tsono ukawawuze Aisraeli zonse zimene uzione.”
Et ce même homme me dit: Fils d’un homme, vois de tes yeux, et écoute de tes oreilles, et applique ton cœur à toutes les choses que moi je te montrerai, parce que c’est pour qu’elles te soient montrées que tu as été amené ici; et annonce tout ce que tu vois à la maison d’Israël.
5 Ine ndinaona khoma litazungulira mbali zonse za Nyumba ya Mulungu. Mʼdzanja la munthuyo munali bango lopimira limene kutalika kwake kunali kwa mamita atatu. Atayeza chipupacho anapeza kuti kuchindikira kwake kunali mamita atatu, ndiponso kutalika kwake kunalinso mamita atatu.
Et voici au dehors un mur tout autour de la maison, et dans la main de l’homme une canne à mesurer de six coudées et d’un palme; et il mesura la largeur de l’édifice, qui était d’une canne; et la hauteur, qui était aussi d’une canne.
6 Anapita ku chipata chakummawa. Anakwera pa makwerero a nyumbayo, nayeza chiwundo choyamba cha chipatacho; kutalika kwake kunali mamita atatu.
Et il vint à la porte qui regardait la voie de l’orient, et il monta par ses degrés; et il mesura le seuil de la porte; il avait une canne en largeur, c’est-à-dire qu’un seuil avait une canne en largeur;
7 Kudutsa chiwundo choyambachi, panali zipinda za alonda zisanu ndi chimodzi, zitatu kudzanja lamanja, zitatu kudzanja lamanzere. Chilichonse chinali cha mamita atatu mulitali mwake, chimodzimodzinso mulifupi mwake. Mipata ya pakati pa zipindazo inali ya mamita awiri ndi theka. Ndipo chiwundo cha pa chipata pafupi ndi khonde lapachipata, chinali mamita atatu.
Il mesura aussi la chambre; elle avait une canne en longueur et une canne en largeur, et entre les chambres, cinq coudées;
8 Ndipo iye anayeza khonde la chipata ndipo chinali cha mamita atatu.
Et le seuil de la porte près du vestibule au-dedans de la porte, une canne.
9 Anayeza khonde ndipo linali mamita anayi. Mphuthu zake zinali mita imodzi kuchindikira kwake. Khonde lamʼkati lapachipata linali kumapeto kwenikweni pafupi ndi Nyumba ya Mulungu.
Et il mesura le vestibule de la porte; il avait huit coudées, et son frontispice, il avait deux coudées; or le vestibule de la porte était en dedans.
10 Mʼkati mwa chipata chakummawa munali zipinda za alonda zitatu mbali iliyonse. Zitatu zonsezo zinali zofanana, ndipo khonde la pakati pa zipindazo linali lofanana.
Mais à la porte qui regardait la voie de l’orient étaient trois chambres d’un côté et trois chambres de l’autre; les trois chambres et les frontispices des deux côtés étaient d’une même mesure.
11 Kenaka anayeza chipata cholowera; mulifupi mwake munali mamita asanu ndipo mulitali mwake munali mamita asanu ndi limodzi ndi theka.
Et il mesura la largeur du seuil de la porte; elle était de dix coudées; et la longueur de la porte, elle était de treize coudées;
12 Kutsogolo kwa chipinda chilichonse cha alonda kunali khoma lalifupi lotalika theka la mita, ndipo mbali iliyonse ya zipinda za alondazo inali yotalika mamita atatu.
Et un rebord qu’il y avait de van t les chambres; il était d’une coudée; une coudée finissait le rebord des deux côtés; et les chambres d’un côté et de l’autre étaient de six coudées.
13 Ndipo anayeza kutalika kwa mulifupi mwa chipata cholowera, kuchokera ku khoma lakumbuyo la chipinda chimodzi mpaka ku khoma la chipinda china; kuchokera ku chitseko mpaka ku chitseko china. Kutalika kwake kunali mamita khumi ndi awiri ndi theka.
Et il mesura la porte depuis le toit d’une chambre jusqu’au toit de l’autre, largeur de vingt-cinq coudées; une porte était vis-à-vis une autre porte.
14 Anayezanso khonde lamʼkati ndipo linali la mamita makumi atatu. Ndipo mozungulira khondelo munali bwalo. Muyesowu sukuphatikiza khonde loyangʼanana ndi bwalo.
Et il fit les frontispices de soixante coudées, et dans ses mesures il ajouta aux frontispices le vestibule de la porte qui régnait d’un côté et de l’autre tout autour.
15 Kuchokera pa chipata cholowera mpaka ku mapeto a khonde la chipata, kutalika kwake kunali mamita 27.
Et devant la face de la première porte qui s’étendait jusqu’à la face du vestibule de la porte intérieure, il mesura cinquante coudées;
16 Makoma a zipinda ndiponso makoma a pakati pa zipindazo anali ndi mazenera. Khonde lamʼkati linalinso ndi mazenera mʼkati mwake. Pa makoma onsewo anajambulapo zithunzi za kanjedza.
Il mesura aussi les fenêtres de biais aux chambres et aux frontispices qui étaient au-dedans de la porte, d’un côté et de l’autre tout autour; mais il y avait pareillement au dedans des vestibules, des fenêtres tout autour, et devant les frontispices des palmes peintes.
17 Kenaka munthuyo anandilowetsa mʼbwalo lakunja, ndipo ndinaona zipinda zina ndi msewu wa miyala wozungulira bwalo lonse. Zipinda zonse zinali makumi atatu ndipo zinkayangʼana msewuwo.
Et il me mena au parvis extérieur; et voici des chambres, et un pavé de pierres dans le parvis tout autour; et trente chambres autour du pavé.
18 Utali wa mulifupi mwa msewuwo unkayenda mamita 27 kufanana ndi utali wa chipata cholowera. Uwu unali msewu wa mʼmunsi.
Et le pavé au frontispice des portes était plus bas, selon la longueur des portes.
19 Tsono, anayeza kutalika kwa bwalo kuyambira chipata cholowera choyamba mpaka polowera pa chipata chakunja cha bwalo la mʼkati. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Et il mesura la largeur depuis la face de la porte d’en bas, jusqu’au frontispice du parvis intérieur par dehors; il y avait cent coudées vers l’orient et vers l’aquilon.
20 Kenaka munthuyo anayeza mulitali ndi mulifupi mwa chipata chimene chimayangʼana kumpoto, chotulukira kunja.
La porte aussi qui regardait la voie de l’aquilon du parvis extérieur, il la mesura tant en longueur qu’en largeur;
21 Zipinda za alonda zimene zinalipo zitatu mbali iliyonse, makoma ake ndi khonde zinali ndi muyeso wofanana ndi wachipata choyamba chija. Kutalika kwake kunali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
Et ses chambres, trois d’un côté et trois de l’autre, et son frontispice et son vestibule, selon la mesure de la première porte; il y avait cinquante coudées de long et vingt-cinq coudées de large.
22 Mipata yake, khonde lake ndi zojambula za kanjedza zinali ndi miyeso yofanana ndi za chipata chakummawa. Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndipo kotsirizira kwa chipatacho kunali khonde.
Mais ses fenêtres, son vestibule et ses sculptures étaient selon la mesure de la porte qui regardait vers l’orient; et on y montait par sept degrés, et il y avait au devant un vestibule.
23 Panalinso chipata cholowera ku bwalo lamʼkati chofanana ndi chakummawa chimene chimayangʼanana ndi chipata chakumpoto, chofanana ndi cha mbali ya kummawa. Anachiyeza kuchokera ku chipata china mpaka ku chipata china. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Et la porte du parvis intérieur était vis-à-vis de la porte de l’aquilon et de l’orient; et il mesura d’une porte à l’autre porte; il y avait cent coudées;
24 Ndipo munthuyo anapita nane ku mbali yakummwera ndipo ndinaona chipata chakummwera. Iye anayeza mphuthu zake ndi khonde ndipo zinali ndi miyeso yofanana ndi ya zina zija.
Il me mena aussi vers la voie du midi, et voici une porte qui regardait vers le midi, et il en mesura le frontispice et le vestibule; ils étaient selon les mesures des précédents.
25 Mʼzipinda za chipata cholowera chimenechi ndi mʼkhonde lake munali mipata yofanana ndi ya mʼzipinda zina. Mulitali mwake munali mamita 27, mulifupi mwake munali mamita 13.
Il mesura aussi ses fenêtres avec les vestibules autour comme les autres fenêtres; elles avaient cinquante coudées de long, et de large vingt-cinq coudées.
26 Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndi khonde kotsirizira kwake. Chipindacho chinali ndi zojambula za kanjedza ku mbali zonse za makoma.
Et on y montait par sept degrés; et le vestibule était devant la porte; et il y avait des palmes ciselées, une d’un côté et l’autre de l’autre au frontispice du vestibule.
27 Bwalo lamʼkati linalinso ndi chipata kummwera. Munthuyo analiyeza kuchokera ku chipata chimenechi mpaka ku chipata chakunja. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
Et il y avait une porte au parvis intérieur du côté du midi; et il mesura d’une porte jusqu’à l’autre porte, du côté du midi; il y avait cent coudées.
28 Ndipo munthu uja anandilowetsa mʼbwalo lamʼkati kudzera ku chipata chakummwera. Anayeza chipatachi ndipo chinali chofanana ndi zinzake zija.
Il m’introduisit aussi dans le parvis intérieur de la porte du midi, et il mesura la porte selon les mesures précédentes,
29 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake zinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi munali mamita 13.
La chambre du parvis, et son frontispice, et son vestibule, avec les mêmes mesures; et ses fenêtres et son vestibule tout autour; il y avait cinquante coudées de long, et de large vingt-cinq coudées;
30 (Khonde lililonse la makonde atatu a zipata zolowera bwalo lamʼkati aja linali la mamita ozungulira mʼbwalo lamʼkati anali mamita 13 mulitali mwake, mamita awiri ndi theka mulifupi mwake).
Il mesura aussi le vestibule tout autour; il avait vingt-cinq coudées de long, et de large cinq;
31 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
Et son vestibule allait au parvis extérieur; et ses palmes sur le frontispice; or il y avait huit degrés par lesquels on y montait.
32 Kenaka munthuyo anapita nane ku bwalo la mʼkati mbali ya kummawa, ndipo anayeza chipata cholowera; chinali chofanana ndi zinzake zina zija.
Et il m’introduisit dans le parvis intérieur par la voie de l’orient, et il mesura la porte selon les mesures précédentes,
33 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake chinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
Et sa chambre, et son frontispice, et son vestibule, comme il est dit plus haut; et ses fenêtres, et ses vestibules tout autour; ils avaient cinquante coudées de long, et de large vingt-cinq.
34 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
Il mesura aussi son vestibule, c’est-à-dire le vestibule du parvis extérieur; et il y avait des palmes ciselées sur le frontispice d’un côté et de l’autre; et c’est par huit degrés qu’on y montait.
35 Kenaka anapita nane ku chipata chakumpoto ndipo anachiyeza. Chinali chofanana ndi zina zija.
Il me mena ensuite vers la porte qui regardait l’aquilon, et il mesura selon les mesures précédentes,
36 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndiponso khonde lake zinali zofanana ndi zina zija, ndipo chinalinso ndi mipata mbali zonse ziwiri. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
Sa chambre, et son frontispice, et son vestibule, et ses fenêtres tout autour; il y avait cinquante coudées de long, et de large vingt-cinq coudées.
37 Khonde lake limayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu zake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
Et son vestibule regardait vers le parvis extérieur; et il y avait des palmes ciselées au frontispice d’un côté et de l’autre; et c’est par huit degrés qu’on y montait.
38 Panali chipinda ndipo khomo lake linali pafupi ndi khonde la chipata cholowera chamʼkati. Mʼchipinda mʼmenemo ankatsukira nyama ya nsembe yopsereza.
Et à chaque chambre du trésor, il y avait une entrée aux frontispices des portes; c’était là qu’on lavait l’holocauste.
39 Pa khonde la chipatacho panali matebulo awiri, lina kuno lina uko. Ankapherapo nsembe zopsereza, nsembe zopepesera machimo ndi nsembe zopepesera kupalamula.
Et dans le vestibule de la porte il y avait deux tables d’un côté, et deux tables de l’autre, afin que fût immolé dessus l’holocauste pour le péché et pour le délit.
40 Panali matebulo anayi, awiri a iwo anali kunja kwa khoma la khonde pafupi ndi makwerero olowera pa chipata chakumpoto ndi awiri enawo anali mbali inayo ya makwerero.
Et au côté extérieur qui monte vers l’entrée de la porte qui va vers l’aquilon, étaient deux tables; et à l’autre côté devant le vestibule de la porte, deux tables.
41 Choncho ku mbali imodzi ya chipata kunali matebulo anayi, ndiponso ku mbali inayo kunali matebulo anayi. Onse pamodzi anali matebulo asanu ndi atatu. Pa matebulopo ankapherapo nyama za nsembe zopsereza.
Quatre tables d’un côté, et quatre tables de l’autre; aux côtés de la porte, étaient en tout huit tables, sur lesquelles on immolait.
42 Matebulo anayiwa anali a miyala yosema. Lililonse mulitali mwake linali la masentimita 75, mulifupi mwake linali la masentimita 75, ndipo msinkhu wake unali wa masentimita makumi asanu. Pa matebulopo amayikapo zipangizo zophera nsembe zopsereza ndi nsembe zina.
Or, les quatre tables pour l’holocauste étaient construites de pierres carrées; elles avaient une coudée et demie de long, et de large une coudée et demie, et de haut une coudée; on mettait dessus les instruments avec lesquels on immolait l’holocauste et la victime.
43 Choncho pa matebulopo ankayikapo nyama za nsembe zopsereza. Mbedza zitatu zazitali ngati chikhatho amazikoleka pa makoma pozungulira ponse.
Et leurs rebords d’un palme se courbaient en dedans tout autour, et on mettait sur les tables les chairs de l’oblation.
44 Munthu uja anapita nane mʼkati mwa bwalo ndipo ndinaona zipinda ziwiri. Chimodzi chinali pafupi ndi chipata chakumpoto kuyangʼana kummwera ndi china chinali pafupi ndi chipata chakummwera kuyangʼana kumpoto.
Et en dehors de la porte intérieure, étaient les chambres des chantres dans le parvis intérieur, qui était à côte de la porte qui regarde vers l’aquilon; et leur face était tournée vers le midi; il y en avait une du côté de la porte orientale, qui regardait vers l’aquilon.
45 Munthuyo anandiwuza kuti, “Chipinda chimene chikuyangʼana kummwera ndi cha ansembe amene amayangʼanira Nyumba ya Mulungu,
Et il me dit: Voici la chambre qui regarde le midi; elle sera pour les prêtres qui veillent à la garde du temple.
46 ndipo chipinda chimene chikuyangʼana kumpoto ndi cha ansembe amene amayangʼanira guwa lansembe. Amenewa ndiwo ana a Zadoki, ndipo ndi okhawo mwa zidzukulu za Levi amene ayenera kutumikira pamaso pa Yehova mʼNyumba ya Mulungu.”
Mais la chambre qui regarde vers l’aquilon sera pour les prêtres qui veillent pour le ministère de l’autel; ceux-ci sont les fils de’ Sadoc, qui d’entre les fils de Lévi s’approchent du Seigneur, afin de le servir.
47 Kenaka munthuyo anayeza bwalo; linali lofanana mbali zonse kutalika kwake, mulitali mwake munali mamita 53, ndipo mulifupi mwake munali mamita 53. Ndipo guwa lansembe linali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
Il mesura aussi le parvis; il avait cent coudées de long, et de large cent coudées en carré; et l’autel devant la face du temple.
48 Munthuyo anapita nane pa khonde la Nyumba ya Mulunguyo. Anayeza mphuthu za khondelo ndipo zinali mamita awiri ndi theka mbali zonse. Mulifupi mwa chipatacho munali mamita asanu ndi awiri ndipo mulifupi mwa makoma ake munali mamita awiri mbali zonse.
Et il m’introduisit dans le vestibule du temple, et il mesura le vestibule, il avait cinq coudées d’un côté, et cinq coudées de l’autre; et la largeur de la porte, elle avait trois coudées d’un côté, et trois coudées de l’autre;
49 Mulitali mwa khonde munali mamita khumi, mulifupi mwake munali mamita asanu ndi limodzi kuchokera kutsogolo mpaka kumbuyo. Panali makwerero khumi, ndipo mbali zonse kunali nsanamira.
Mais il mesura la longueur du vestibule; elle était de vingt-cinq coudées; et la largeur, elle était de onze coudées; et c’était par huit degrés qu’on y montait. Et il y avait dans les frontispices deux colonnes, l’une d’un côté et l’autre de l’autre.

< Ezekieli 40 >