< Ezekieli 40 >

1 Kumayambiriro a chaka cha 25, cha ukapolo wathu, tsiku la khumi lamwezi, patapita zaka khumi ndi zinayi mzinda wa Yerusalemu utawonongedwa, pa tsiku lomwelo dzanja la Yehova linali pa ine ndipo Iye anapita nane ku Yerusalemu.
In the twenty-fifth year of our transmigration, at the beginning of the year, on the tenth of the month, in the fourteenth year after the city was struck, on this very day, the hand of the Lord was placed upon me, and he brought me to that place.
2 Mʼmasomphenyawo Yehova ananditenga ndi kupita nane ku dziko la Israeli ndipo anandiyika pa phiri lalitali kwambiri, moti ndinaona ngati mzinda.
In the visions of God, he brought me into the land of Israel, and he released me on an exceedingly high mountain, on which there was something like the edifice of a city, verging toward the south.
3 Atandifikitsa kumeneko ndinaona munthu wonyezimira ngati mkuwa. Iye anali atayima pa chipata ndipo mʼdzanja lake munali chingwe cha nsalu yabafuta ndi ndodo yoyezera.
And he led me into that place. And behold, there was a man, whose appearance was like the appearance of brass, with a linen rope in his hand, and a measuring reed in his hand. And he was standing at the gate.
4 Munthuyo anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, penyetsetsa ndipo umvetse bwinobwino. Uyikepo mtima wako pa zonse zimene ndikukuonetsa pakuti anakubweretsa kuno kuti uwone zimenezi. Tsono ukawawuze Aisraeli zonse zimene uzione.”
And the same man said to me: “Son of man, look with your eyes, and listen with your ears, and set your heart upon all that I will reveal to you. For you have been brought to this place, so that these things may be revealed to you. Announce all that you see to the house of Israel.”
5 Ine ndinaona khoma litazungulira mbali zonse za Nyumba ya Mulungu. Mʼdzanja la munthuyo munali bango lopimira limene kutalika kwake kunali kwa mamita atatu. Atayeza chipupacho anapeza kuti kuchindikira kwake kunali mamita atatu, ndiponso kutalika kwake kunalinso mamita atatu.
And behold, there was a wall outside of the house, encircling it all around, and in the man’s hand was a measuring reed of six cubits and a palm. And he measured the width of the edifice with one reed; likewise, the height with one reed.
6 Anapita ku chipata chakummawa. Anakwera pa makwerero a nyumbayo, nayeza chiwundo choyamba cha chipatacho; kutalika kwake kunali mamita atatu.
And he went to the gate which looked toward the east, and he ascended by its steps. And he measured the width of the threshold of the gate as one reed, that is, one threshold was one reed in width.
7 Kudutsa chiwundo choyambachi, panali zipinda za alonda zisanu ndi chimodzi, zitatu kudzanja lamanja, zitatu kudzanja lamanzere. Chilichonse chinali cha mamita atatu mulitali mwake, chimodzimodzinso mulifupi mwake. Mipata ya pakati pa zipindazo inali ya mamita awiri ndi theka. Ndipo chiwundo cha pa chipata pafupi ndi khonde lapachipata, chinali mamita atatu.
And a chamber was one reed in length and one reed in width. And between the chambers, there were five cubits.
8 Ndipo iye anayeza khonde la chipata ndipo chinali cha mamita atatu.
And the threshold of the gate, next to the inner vestibule of the gate, was one reed.
9 Anayeza khonde ndipo linali mamita anayi. Mphuthu zake zinali mita imodzi kuchindikira kwake. Khonde lamʼkati lapachipata linali kumapeto kwenikweni pafupi ndi Nyumba ya Mulungu.
And he measured the vestibule of the gate as eight cubits, and its front as two cubits. But the vestibule of the gate was inside.
10 Mʼkati mwa chipata chakummawa munali zipinda za alonda zitatu mbali iliyonse. Zitatu zonsezo zinali zofanana, ndipo khonde la pakati pa zipindazo linali lofanana.
Moreover, the chambers of the gate, toward the way of the east, were three from one side to the other. The three were of one measure, and the fronts were of one measure, on both sides.
11 Kenaka anayeza chipata cholowera; mulifupi mwake munali mamita asanu ndipo mulitali mwake munali mamita asanu ndi limodzi ndi theka.
And he measured the width of the threshold of the gate as ten cubits, and the length of the gate as thirteen cubits.
12 Kutsogolo kwa chipinda chilichonse cha alonda kunali khoma lalifupi lotalika theka la mita, ndipo mbali iliyonse ya zipinda za alondazo inali yotalika mamita atatu.
And before the chambers, the border was one cubit. And on both sides, the border was one cubit. But the chambers were six cubits, from one side to the other.
13 Ndipo anayeza kutalika kwa mulifupi mwa chipata cholowera, kuchokera ku khoma lakumbuyo la chipinda chimodzi mpaka ku khoma la chipinda china; kuchokera ku chitseko mpaka ku chitseko china. Kutalika kwake kunali mamita khumi ndi awiri ndi theka.
And he measured the gate, from the roof of one chamber to the roof of another, twenty-five cubits in width, from door to door.
14 Anayezanso khonde lamʼkati ndipo linali la mamita makumi atatu. Ndipo mozungulira khondelo munali bwalo. Muyesowu sukuphatikiza khonde loyangʼanana ndi bwalo.
And he found the fronts to be sixty cubits. And at the front, there was a court for the gate on every side all around.
15 Kuchokera pa chipata cholowera mpaka ku mapeto a khonde la chipata, kutalika kwake kunali mamita 27.
And before the face of the gate, which extended even to the face of the vestibule of the gate of the interior, there were fifty cubits.
16 Makoma a zipinda ndiponso makoma a pakati pa zipindazo anali ndi mazenera. Khonde lamʼkati linalinso ndi mazenera mʼkati mwake. Pa makoma onsewo anajambulapo zithunzi za kanjedza.
And there were slanting windows in the chambers and at their fronts, which were within the gate on every side all around. And similarly, there were also windows in the vestibules all around the interior, and there were images of palm trees before the fronts.
17 Kenaka munthuyo anandilowetsa mʼbwalo lakunja, ndipo ndinaona zipinda zina ndi msewu wa miyala wozungulira bwalo lonse. Zipinda zonse zinali makumi atatu ndipo zinkayangʼana msewuwo.
And he led me away to the outer court, and behold, there were storerooms and a layer of pavement stones throughout the court. Thirty storerooms encircled the pavement.
18 Utali wa mulifupi mwa msewuwo unkayenda mamita 27 kufanana ndi utali wa chipata cholowera. Uwu unali msewu wa mʼmunsi.
And the pavement in front of the gates, along the length of the gates, was lower.
19 Tsono, anayeza kutalika kwa bwalo kuyambira chipata cholowera choyamba mpaka polowera pa chipata chakunja cha bwalo la mʼkati. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
And he measured the width, from the face of the lower gate to the front of the outer part of the inner court, to be one hundred cubits, to the east and to the north.
20 Kenaka munthuyo anayeza mulitali ndi mulifupi mwa chipata chimene chimayangʼana kumpoto, chotulukira kunja.
Likewise, he measured the gate of the outer court, which looked to the way of the north, to be as much in length as in width.
21 Zipinda za alonda zimene zinalipo zitatu mbali iliyonse, makoma ake ndi khonde zinali ndi muyeso wofanana ndi wachipata choyamba chija. Kutalika kwake kunali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
And its chambers were three from one side to the other. And its front and its vestibule, in accord with the measure of the former gate, were fifty cubits in its length and twenty-five cubits in width.
22 Mipata yake, khonde lake ndi zojambula za kanjedza zinali ndi miyeso yofanana ndi za chipata chakummawa. Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndipo kotsirizira kwa chipatacho kunali khonde.
Now its windows, and the vestibule, and the engravings were in accord with the measure of the gate which looked to the east. And its ascent was by seven steps, and a vestibule was before it.
23 Panalinso chipata cholowera ku bwalo lamʼkati chofanana ndi chakummawa chimene chimayangʼanana ndi chipata chakumpoto, chofanana ndi cha mbali ya kummawa. Anachiyeza kuchokera ku chipata china mpaka ku chipata china. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
And the gate of the inner court was opposite the gate of the north, and that of the east. And he measured from gate to gate as one hundred cubits.
24 Ndipo munthuyo anapita nane ku mbali yakummwera ndipo ndinaona chipata chakummwera. Iye anayeza mphuthu zake ndi khonde ndipo zinali ndi miyeso yofanana ndi ya zina zija.
And he led me to the way of the south, and behold, there was a gate which looked toward the south. And he measured its front and its vestibule to be the same as the measures above.
25 Mʼzipinda za chipata cholowera chimenechi ndi mʼkhonde lake munali mipata yofanana ndi ya mʼzipinda zina. Mulitali mwake munali mamita 27, mulifupi mwake munali mamita 13.
And its windows and the vestibule all around were like the other windows: fifty cubits in length and twenty-five cubits in width.
26 Chipatacho chinali ndi makwerero asanu ndi awiri ndi khonde kotsirizira kwake. Chipindacho chinali ndi zojambula za kanjedza ku mbali zonse za makoma.
And there were seven steps to ascend to it, and a vestibule before its doors. And there were engraved palm trees, one on each side, at its front.
27 Bwalo lamʼkati linalinso ndi chipata kummwera. Munthuyo analiyeza kuchokera ku chipata chimenechi mpaka ku chipata chakunja. Kutalika kwake kunali mamita makumi asanu.
And there was a gate at the inner court, on the way to the south. And he measured from one gate to another, on the way to the south, to be one hundred cubits.
28 Ndipo munthu uja anandilowetsa mʼbwalo lamʼkati kudzera ku chipata chakummwera. Anayeza chipatachi ndipo chinali chofanana ndi zinzake zija.
And he led me into the inner court, to the south gate. And he measured the gate to be in accord with the measures above.
29 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake zinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi munali mamita 13.
Its chamber, and its front, and its vestibule had the same measures. And its windows and its vestibule all around were fifty cubits in length, and twenty-five cubits in width.
30 (Khonde lililonse la makonde atatu a zipata zolowera bwalo lamʼkati aja linali la mamita ozungulira mʼbwalo lamʼkati anali mamita 13 mulitali mwake, mamita awiri ndi theka mulifupi mwake).
And the vestibule all around was twenty-five cubits in length, and five cubits in width.
31 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
And its vestibule was toward the outer court, and its palm trees were at the front. And there were eight steps to ascend to it.
32 Kenaka munthuyo anapita nane ku bwalo la mʼkati mbali ya kummawa, ndipo anayeza chipata cholowera; chinali chofanana ndi zinzake zina zija.
And he led me into the inner court, along the way of the east. And he measured the gate to be in accord with the measures above.
33 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndi khonde lake zinali zofanana ndi zina zija. Chipata cholowera ndi khonde lake chinali ndi mipata mʼmbali zonse. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
Its chamber, and its front, and its vestibule were as above. And its windows and its vestibules all around were fifty cubits in length, and twenty-five cubits in width.
34 Khonde lake linayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu pake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
And it had a vestibule, that is, at the outer court. And the engraved palm trees at its front were on one side and the other. And its ascent was by eight steps.
35 Kenaka anapita nane ku chipata chakumpoto ndipo anachiyeza. Chinali chofanana ndi zina zija.
And he led me to the gate which looked toward the north. And he measured it to be in accord with the measures above.
36 Zipinda zake za alonda, makoma ake ndiponso khonde lake zinali zofanana ndi zina zija, ndipo chinalinso ndi mipata mbali zonse ziwiri. Mulitali mwake munali mamita 27 ndipo mulifupi mwake munali mamita 13.
Its chamber, and its front, and its vestibule, and its windows all around were fifty cubits in length, and twenty-five cubits in width.
37 Khonde lake limayangʼanana ndi bwalo lakunja. Pa mphuthu zake anajambulapo zithunzi za kanjedza mbali zonse ziwiri, ndipo linali ndi makwerero asanu ndi atatu.
And its vestibule looked toward the outer court. And an engraving of palm trees at its front was on one side and the other. And its ascent was by eight steps.
38 Panali chipinda ndipo khomo lake linali pafupi ndi khonde la chipata cholowera chamʼkati. Mʼchipinda mʼmenemo ankatsukira nyama ya nsembe yopsereza.
And at each one of the storerooms, there was a door at the front of the gates. There, they washed the holocaust.
39 Pa khonde la chipatacho panali matebulo awiri, lina kuno lina uko. Ankapherapo nsembe zopsereza, nsembe zopepesera machimo ndi nsembe zopepesera kupalamula.
And at the vestibule of the gate, there were two tables on one side, and two tables on the other side, so that the holocaust, and the offering for sin, and the offering for transgression could be immolated upon them.
40 Panali matebulo anayi, awiri a iwo anali kunja kwa khoma la khonde pafupi ndi makwerero olowera pa chipata chakumpoto ndi awiri enawo anali mbali inayo ya makwerero.
And at the outer side, which ascends to the door of the gate that goes toward the north, there were two tables. And at the other side, before the vestibule of the gate, there were two tables.
41 Choncho ku mbali imodzi ya chipata kunali matebulo anayi, ndiponso ku mbali inayo kunali matebulo anayi. Onse pamodzi anali matebulo asanu ndi atatu. Pa matebulopo ankapherapo nyama za nsembe zopsereza.
Four tables were on one side, and four tables were on the other side; along the sides of the gate, there were eight tables, upon which they immolated.
42 Matebulo anayiwa anali a miyala yosema. Lililonse mulitali mwake linali la masentimita 75, mulifupi mwake linali la masentimita 75, ndipo msinkhu wake unali wa masentimita makumi asanu. Pa matebulopo amayikapo zipangizo zophera nsembe zopsereza ndi nsembe zina.
Now the four tables for the holocausts were constructed of square stones: one and a half cubit in length, and one and a half cubits in width, and one cubit in height. Upon these, they placed the vessels, in which the holocaust and the victim were immolated.
43 Choncho pa matebulopo ankayikapo nyama za nsembe zopsereza. Mbedza zitatu zazitali ngati chikhatho amazikoleka pa makoma pozungulira ponse.
And their edges were one palm in width, turned inward all around. And the flesh of the oblation was on the tables.
44 Munthu uja anapita nane mʼkati mwa bwalo ndipo ndinaona zipinda ziwiri. Chimodzi chinali pafupi ndi chipata chakumpoto kuyangʼana kummwera ndi china chinali pafupi ndi chipata chakummwera kuyangʼana kumpoto.
And outside the interior gate, there were storerooms for the cantors, in the inner court, which was beside the gate that looks toward the north. And their face was opposite the way to the south; one was beside the east gate, which looked toward the way of the north.
45 Munthuyo anandiwuza kuti, “Chipinda chimene chikuyangʼana kummwera ndi cha ansembe amene amayangʼanira Nyumba ya Mulungu,
And he said to me: “This is the storeroom that looks toward the south; it shall be for the priests who keep watch for the protection of the temple.
46 ndipo chipinda chimene chikuyangʼana kumpoto ndi cha ansembe amene amayangʼanira guwa lansembe. Amenewa ndiwo ana a Zadoki, ndipo ndi okhawo mwa zidzukulu za Levi amene ayenera kutumikira pamaso pa Yehova mʼNyumba ya Mulungu.”
Moreover, the storeroom that looks toward the north will be for the priests who keep watch over the ministry of the altar. These are the sons of Zadok, those among the sons of Levi who may draw near to the Lord, so that they may minister to him.”
47 Kenaka munthuyo anayeza bwalo; linali lofanana mbali zonse kutalika kwake, mulitali mwake munali mamita 53, ndipo mulifupi mwake munali mamita 53. Ndipo guwa lansembe linali kutsogolo kwa Nyumba ya Mulungu.
And he measured the court to be one hundred cubits in length, and one hundred cubits in width, with four equal sides. And the altar was before the face of the temple.
48 Munthuyo anapita nane pa khonde la Nyumba ya Mulunguyo. Anayeza mphuthu za khondelo ndipo zinali mamita awiri ndi theka mbali zonse. Mulifupi mwa chipatacho munali mamita asanu ndi awiri ndipo mulifupi mwa makoma ake munali mamita awiri mbali zonse.
And he led me into the vestibule of the temple. And he measured the vestibule to be five cubits on one side, and five cubits on the other side. And the width of the gate was three cubits on one side, and three cubits on the other side.
49 Mulitali mwa khonde munali mamita khumi, mulifupi mwake munali mamita asanu ndi limodzi kuchokera kutsogolo mpaka kumbuyo. Panali makwerero khumi, ndipo mbali zonse kunali nsanamira.
Now the length of the vestibule was twenty cubits, and the width was eleven cubits, and there were eight steps to ascend to it. And there were pillars at the front, one on this side and another on that side.

< Ezekieli 40 >