< Ezekieli 4 >

1 Mulungu anati, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga njerwa, uliyike pamaso pako ndipo ujambulepo chithunzi cha mzinda wa Yerusalemu.
»Tudi ti, človeški sin, si vzemi opeko in jo položi pred seboj in na njej upodobi mesto, celó [prestolnico] Jeruzalem,
2 Ndipo uwuzinge mzindawo motere: uwumangire nsanja zowuzinga, uwumbire mitumbira ya nkhondo, uwumangire misasa ya nkhondo ndipo uyike zida zogumulira kuzungulira mzindawo.
in postavi obleganje zoper njo in zgradi utrdbo zoper njo in nasuj nasip zoper njo. Postavi tudi tabor zoper njo in naokoli zoper njo razpostavi oblegovalne ovne.
3 Kenaka utenge chiwaya chachitsulo uchiyike ngati khoma lachitsulo pakati pa iwe ndi mzindawo. Uyangʼanitsitse mzindawo ndipo udzakhala wozingidwa ndi nsanja za nkhondo. Choncho umangire nsanja zankhondo. Chimenechi chidzakhala chizindikiro kwa Aisraeli.
Poleg tega si vzemi železno ponev in jo postavi za železen zid med seboj in mestom, in naravnaj svoj obraz zoper njo in ta bo oblegana, ti pa boš postavil oblegovanje zoper njo. To bo znamenje Izraelovi hiši.
4 “Tsono iwe ugonere kumanzere kwako ndipo ndidzayika pa iwe tchimo la Aisraeli. Iwe udzasenza tchimolo masiku onse amene udzagonere mbali imeneyo.
Lezi tudi na svojo levo stran in nanjo položi krivičnost Izraelove hiše. Glede na število dni, ko boš ležal na tej, boš nosil njihovo krivičnost.
5 Ine ndakuyikira masiku okwana 390 malingana ndi zaka za machimo awo. Umu ndi mmene udzasenzere machimo a Aisraeli.
Kajti nate sem položil leta njihove krivičnosti, glede na število dni, tristo devetdeset dni. Tako boš nosil krivičnost Izraelove hiše.
6 “Utatha zimenezo udzagonerenso mbali ya kudzanja lamanja, ndipo udzasenza machimo a anthu a ku Yuda masiku makumi anayi, tsiku lililonse kuyimira chaka chimodzi.
Ko jih dopolniš, ponovno lezi na svojo desno stran in štirideset dni boš nosil krivičnost Judove hiše. Določil sem ti vsak dan za leto.
7 Tsono udzayangʼanitsitse nsanja za nkhondo zozinga. Dzanja la mkanjo wako utalikwinya ndi dzanja lako utakweza, udzalosere modzudzula Yerusalemu.
Zato boš svoj obraz naravnal proti obleganju [prestolnice] Jeruzalem in tvoj laket bo odkrit in prerokoval boš zoper njo.
8 Ine ndidzakumanga ndi zingwe kotero kuti sudzatha kutembenukira uku ndi uku mpaka utatsiriza masiku akuzingidwa ako.
Glej, nate bom položil vezi in ne boš se obrnil iz ene strani na drugo, dokler ne dokončaš dni svojega obleganja.
9 “Tsono tenga tirigu ndi barele, nyemba ndi mphodza, mapira ndi mchewere; ndipo uyike zonsezi mʼmbale imodzi ndipo upange buledi wako. Uzidya pa masiku 390 amene udzakhala ukugonera mbali imodzi.
K sebi vzemi tudi pšenico, ječmen, fižol, lečo, proso in piro ter jih stresi v eno posodo in iz tega zamesi kruh; glede na število dni, ki jih boš preležal na svoji strani, tristo devetdeset dni boš jedel od tega.
10 Uyeze theka la kilogalamu la chakudyacho kuti uzidya tsiku lililonse kamodzi kokha.
Tvoja hrana, ki jo boš jedel, bo po teži, dvajset šeklov na dan. Od časa do časa jo boš jedel.
11 Uyezenso zikho ziwiri zamadzi ndipo uzimwa tsiku ndi tsiku.
Tudi vodo boš pil po meri, šesti del vrča. Od časa do časa [jo] boš pil.
12 Uzidya chakudya chako ngati momwe amadyera keke ya barele. Uzidzaphika chakudyacho anthu akuona pogwiritsa ntchito ndowe ya munthu ngati nkhuni.”
To boš jedel kakor ječmenove kolače in to boš spekel z iztrebkom, ki prihaja iz človeka, v njihovem pogledu.«
13 Yehova anati, “Chimodzimodzi anthu a Israeli adzadya chakudya chodetsedwa ku mayiko achilendo kumene Ine ndidzawapirikitsira.”
Gospod je rekel: »Celo tako bodo Izraelovi otroci jedli svoj omadeževani kruh med pogani, kamor jih bom pognal.«
14 Koma ine ndinati, “Zisatero, Ambuye Yehova! Ine sindinadziyipitsepo pa zachipembedzo. Kuyambira ubwana wanga mpaka tsopano, sindinadyepo kanthu kalikonse kopezeka katafa kapena kophedwa ndi zirombo za kutchire. Palibe nyama yodetsedwa pa zachipembedzo imene inalowa pakamwa panga.”
Potem sem rekel: »Ah, Gospod Bog! Glej, moja duša ni bila oskrunjena, kajti od svoje mladosti, celo do sedaj, nisem jedel od tega, kar samo umre ali je raztrgano na koščke; niti v moja usta ni prišlo gnusno meso.«
15 Iye anati, “Chabwino, ndidzakulola kuti uphike buledi wako ndi ndowe za ngʼombe mʼmalo mwa ndowe za munthu.”
Potem mi je rekel: »Glej! Dajem ti kravji iztrebek za človeški iztrebek in svoj kruh boš pripravil s tem.«
16 Pambuyo pake anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Yerusalemu ndidzawachepetsera chakudya. Anthuwo adzadya chakudya chochita kuyeza ndipo azidzadya mwa nkhawa. Azidzamwanso madzi ochita kuyeza ndiponso mwa mantha.
Poleg tega mi je rekel: »Človeški sin, glej, zlomil bom oporo kruha v [prestolnici] Jeruzalem. Kruh bodo jedli po teži in s skrbnostjo in vodo bodo pili po meri in z osuplostjo,
17 Ndidzachita zimenezi kuti adzasowe chakudya ndi madzi. Choncho adzachita nkhawa akumapenyana ndipo adzatheratu ndi kuwonda chifukwa cha machimo awo.”
da jim bo lahko primanjkovalo kruha in vode in bodo osupli eden z drugim in shirali zaradi svoje krivičnosti.«

< Ezekieli 4 >