< Ezekieli 4 >
1 Mulungu anati, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga njerwa, uliyike pamaso pako ndipo ujambulepo chithunzi cha mzinda wa Yerusalemu.
Tu pois, ó filho do homem, toma um tijolo, e pôl-o-has diante de ti, e grava n'elle a cidade de Jerusalem.
2 Ndipo uwuzinge mzindawo motere: uwumangire nsanja zowuzinga, uwumbire mitumbira ya nkhondo, uwumangire misasa ya nkhondo ndipo uyike zida zogumulira kuzungulira mzindawo.
E põe contra ella um cerco, e edifica contra ella uma fortificação, e levanta contra ella uma tranqueira, e põe contra ella arraiaes, e põe-lhe vaevens em redor.
3 Kenaka utenge chiwaya chachitsulo uchiyike ngati khoma lachitsulo pakati pa iwe ndi mzindawo. Uyangʼanitsitse mzindawo ndipo udzakhala wozingidwa ndi nsanja za nkhondo. Choncho umangire nsanja zankhondo. Chimenechi chidzakhala chizindikiro kwa Aisraeli.
E tu toma uma sertã de ferro, e põe-n'a por muro de ferro entre ti e entre a cidade; e dirige para ella o teu rosto, e assim será cercada, e a cercarás; isto servirá de signal á casa de Israel.
4 “Tsono iwe ugonere kumanzere kwako ndipo ndidzayika pa iwe tchimo la Aisraeli. Iwe udzasenza tchimolo masiku onse amene udzagonere mbali imeneyo.
Tu tambem deita-te sobre o teu lado esquerdo, e põe a maldade da casa de Israel sobre elle: conforme o numero dos dias que te deitares sobre elle, levarás as suas maldades.
5 Ine ndakuyikira masiku okwana 390 malingana ndi zaka za machimo awo. Umu ndi mmene udzasenzere machimo a Aisraeli.
Porque eu já te tenho dado os annos da sua maldade, conforme o numero dos dias, trezentos e noventa dias; e levarás a maldade da casa de Israel.
6 “Utatha zimenezo udzagonerenso mbali ya kudzanja lamanja, ndipo udzasenza machimo a anthu a ku Yuda masiku makumi anayi, tsiku lililonse kuyimira chaka chimodzi.
E, quando cumprires estes, tornar-te-has a deitar sobre o teu lado direito, e levarás a maldade da casa de Judah quarenta dias: um dia te dei por cada anno.
7 Tsono udzayangʼanitsitse nsanja za nkhondo zozinga. Dzanja la mkanjo wako utalikwinya ndi dzanja lako utakweza, udzalosere modzudzula Yerusalemu.
Dirigirás pois o teu rosto para o cerco de Jerusalem, e o teu braço estará descoberto, e prophetizarás contra ella.
8 Ine ndidzakumanga ndi zingwe kotero kuti sudzatha kutembenukira uku ndi uku mpaka utatsiriza masiku akuzingidwa ako.
E eis que porei sobre ti cordas: assim tu não te voltarás d'um lado para o outro, até que cumpras os dias do teu cerco.
9 “Tsono tenga tirigu ndi barele, nyemba ndi mphodza, mapira ndi mchewere; ndipo uyike zonsezi mʼmbale imodzi ndipo upange buledi wako. Uzidya pa masiku 390 amene udzakhala ukugonera mbali imodzi.
E tu toma trigo, e cevada, e favas, e lentilhas, e milho, e aveia, e mette-os n'um vaso, e faze d'elles pão: conforme o numero dos dias que tu te deitares sobre o teu lado, trezentos e noventa dias, comerás d'isso.
10 Uyeze theka la kilogalamu la chakudyacho kuti uzidya tsiku lililonse kamodzi kokha.
E a tua comida, que has de comer, será do peso de vinte siclos cada dia: de tempo em tempo a comerás.
11 Uyezenso zikho ziwiri zamadzi ndipo uzimwa tsiku ndi tsiku.
Tambem beberás a agua por medida, a saber, a sexta parte d'um hin: de tempo em tempo beberás.
12 Uzidya chakudya chako ngati momwe amadyera keke ya barele. Uzidzaphika chakudyacho anthu akuona pogwiritsa ntchito ndowe ya munthu ngati nkhuni.”
E o comerás como bolos de cevada, e o cozerás com o esterco que sae do homem, diante dos olhos d'elles.
13 Yehova anati, “Chimodzimodzi anthu a Israeli adzadya chakudya chodetsedwa ku mayiko achilendo kumene Ine ndidzawapirikitsira.”
E disse o Senhor: Assim comerão os filhos de Israel o seu pão immundo, entre as nações ás quaes os lançarei.
14 Koma ine ndinati, “Zisatero, Ambuye Yehova! Ine sindinadziyipitsepo pa zachipembedzo. Kuyambira ubwana wanga mpaka tsopano, sindinadyepo kanthu kalikonse kopezeka katafa kapena kophedwa ndi zirombo za kutchire. Palibe nyama yodetsedwa pa zachipembedzo imene inalowa pakamwa panga.”
Então disse eu: Ah! Senhor, Senhor! eis que a minha alma não foi contaminada, porque nunca comi coisa morta, nem despedaçada, desde a minha mocidade até agora: nem carne abominavel entrou na minha bocca.
15 Iye anati, “Chabwino, ndidzakulola kuti uphike buledi wako ndi ndowe za ngʼombe mʼmalo mwa ndowe za munthu.”
E disse-me: Vê, tenho-te dado bosta de vaccas, em logar de esterco de homem; e com ella prepararás o teu pão.
16 Pambuyo pake anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Yerusalemu ndidzawachepetsera chakudya. Anthuwo adzadya chakudya chochita kuyeza ndipo azidzadya mwa nkhawa. Azidzamwanso madzi ochita kuyeza ndiponso mwa mantha.
Então me disse: Filho do homem, eis que eu quebranto o sustento do pão em Jerusalem, e comerão o pão por peso, e com desgosto; e a agua beberão por medida, e com espanto;
17 Ndidzachita zimenezi kuti adzasowe chakudya ndi madzi. Choncho adzachita nkhawa akumapenyana ndipo adzatheratu ndi kuwonda chifukwa cha machimo awo.”
Para que o pão e a agua lhes falte, e se espantem uns com os outros, e se consumam nas suas maldades.