< Ezekieli 4 >
1 Mulungu anati, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga njerwa, uliyike pamaso pako ndipo ujambulepo chithunzi cha mzinda wa Yerusalemu.
Et toi, fils d’un homme, prends une brique, mets-la devant toi, et tu y traceras la cité de Jérusalem.
2 Ndipo uwuzinge mzindawo motere: uwumangire nsanja zowuzinga, uwumbire mitumbira ya nkhondo, uwumangire misasa ya nkhondo ndipo uyike zida zogumulira kuzungulira mzindawo.
Et tu disposeras contre elle un siège, et tu bâtiras des fortifications, tu formeras un rempart, tu établiras contre elle des camps, et tu mettras des béliers autour.
3 Kenaka utenge chiwaya chachitsulo uchiyike ngati khoma lachitsulo pakati pa iwe ndi mzindawo. Uyangʼanitsitse mzindawo ndipo udzakhala wozingidwa ndi nsanja za nkhondo. Choncho umangire nsanja zankhondo. Chimenechi chidzakhala chizindikiro kwa Aisraeli.
Et toi, prends pour toi une poêle de fer, et tu la placeras comme un mur de fer entre toi et entre la cité; tu dirigeras fixement ta face contre elle, et elle sera assiégée, et tu l’entoureras; c’est un signe pour la maison d’Israël.
4 “Tsono iwe ugonere kumanzere kwako ndipo ndidzayika pa iwe tchimo la Aisraeli. Iwe udzasenza tchimolo masiku onse amene udzagonere mbali imeneyo.
Et toi, tu dormiras sur ton côté gauche, et tu mettras sur ce côté là les iniquités de la maison d’Israël, selon le nombre de jours que tu dormiras, et tu prendras sur toi leurs iniquités.
5 Ine ndakuyikira masiku okwana 390 malingana ndi zaka za machimo awo. Umu ndi mmene udzasenzere machimo a Aisraeli.
Pour moi, je t’ai donné les années de leur iniquité, au nombre de trois cent quatre-vingt-dix jours; et tu porteras l’iniquité de la maison d’Israël.
6 “Utatha zimenezo udzagonerenso mbali ya kudzanja lamanja, ndipo udzasenza machimo a anthu a ku Yuda masiku makumi anayi, tsiku lililonse kuyimira chaka chimodzi.
Et, quand tu auras accompli cela, tu dormiras une seconde fois sur ton côté droit, et tu prendras sur toi l’iniquité de la maison de Juda pendant quarante jours; c’est un jour pour une année; un jour, dis-je, pour une année, que je t’ai donné.
7 Tsono udzayangʼanitsitse nsanja za nkhondo zozinga. Dzanja la mkanjo wako utalikwinya ndi dzanja lako utakweza, udzalosere modzudzula Yerusalemu.
Et vers le siège de Jérusalem tu tourneras ta face, et ton bras sera étendu, et tu prophétiseras contre elle.
8 Ine ndidzakumanga ndi zingwe kotero kuti sudzatha kutembenukira uku ndi uku mpaka utatsiriza masiku akuzingidwa ako.
Voilà que je t’ai environné de chaînes, et tu ne te retourneras pas d’un de tes côtés sur l’autre côté, jusqu’à ce que tu aies accompli les jours de ton siège.
9 “Tsono tenga tirigu ndi barele, nyemba ndi mphodza, mapira ndi mchewere; ndipo uyike zonsezi mʼmbale imodzi ndipo upange buledi wako. Uzidya pa masiku 390 amene udzakhala ukugonera mbali imodzi.
Et toi, prends pour toi du froment, de l’orge, des fèves, des lentilles, du millet et de la vesce, et tu les mettras dans un seul vase, et tu t’en feras des pains, selon le nombre de jours que tu dormiras sur ton côté; pendant trois cent quatre-vingt-dix jours, tu mangeras cela.
10 Uyeze theka la kilogalamu la chakudyacho kuti uzidya tsiku lililonse kamodzi kokha.
Or l’aliment dont tu te nourriras sera du poids de vingt statères par jour, et tu en mangeras d’un temps à un temps.
11 Uyezenso zikho ziwiri zamadzi ndipo uzimwa tsiku ndi tsiku.
Et l’eau, tu en boiras par mesure, la sixième partie d’un hin; et tu la boiras d’un temps à un temps.
12 Uzidya chakudya chako ngati momwe amadyera keke ya barele. Uzidzaphika chakudyacho anthu akuona pogwiritsa ntchito ndowe ya munthu ngati nkhuni.”
Et tu le mangeras comme un pain d’orge cuit sous la cendre; et de l’ordure qui sort de l’homme, tu le couvriras à leurs yeux.
13 Yehova anati, “Chimodzimodzi anthu a Israeli adzadya chakudya chodetsedwa ku mayiko achilendo kumene Ine ndidzawapirikitsira.”
Et dit le Seigneur: C’est ainsi que les enfants d’Israël mangeront leur pain souillé parmi les nations vers lesquelles je les chasserai.
14 Koma ine ndinati, “Zisatero, Ambuye Yehova! Ine sindinadziyipitsepo pa zachipembedzo. Kuyambira ubwana wanga mpaka tsopano, sindinadyepo kanthu kalikonse kopezeka katafa kapena kophedwa ndi zirombo za kutchire. Palibe nyama yodetsedwa pa zachipembedzo imene inalowa pakamwa panga.”
Et je dis: Ah! ah! ah! Seigneur Dieu, voilà que mon âme n’a pas été souillée; et je n’ai pas mangé d’animal crevé, ni déchiré par des bêtes, depuis mon enfance jusqu’à maintenant, et il n’est entré dans ma bouche aucune chair immonde.
15 Iye anati, “Chabwino, ndidzakulola kuti uphike buledi wako ndi ndowe za ngʼombe mʼmalo mwa ndowe za munthu.”
Et il me dit: Voilà que je t’ai donné la fiente des bœufs au lieu des excréments humains; et tu feras ton pain avec cette fiente.
16 Pambuyo pake anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Yerusalemu ndidzawachepetsera chakudya. Anthuwo adzadya chakudya chochita kuyeza ndipo azidzadya mwa nkhawa. Azidzamwanso madzi ochita kuyeza ndiponso mwa mantha.
Et il me dit: Fils d’un homme, voilà que moi je briserai le bâton du pain dans Jérusalem; et ils mangeront le pain au poids et dans l’inquiétude, et ils boiront l’eau par mesure et dans l’angoisse;
17 Ndidzachita zimenezi kuti adzasowe chakudya ndi madzi. Choncho adzachita nkhawa akumapenyana ndipo adzatheratu ndi kuwonda chifukwa cha machimo awo.”
Afin que, le pain et l’eau manquant, chacun tombe sur son frère et qu’ils se dessèchent dans leurs iniquités.