< Ezekieli 4 >

1 Mulungu anati, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga njerwa, uliyike pamaso pako ndipo ujambulepo chithunzi cha mzinda wa Yerusalemu.
Et toi, fils de l'homme, prends une brique, mets-la devant toi et y dessine une ville, Jérusalem.
2 Ndipo uwuzinge mzindawo motere: uwumangire nsanja zowuzinga, uwumbire mitumbira ya nkhondo, uwumangire misasa ya nkhondo ndipo uyike zida zogumulira kuzungulira mzindawo.
Établis un siège contre elle, bâtis contre elle des retranchements, élève contre elle des terrasses, environne-la d'un camp, place des béliers tout autour.
3 Kenaka utenge chiwaya chachitsulo uchiyike ngati khoma lachitsulo pakati pa iwe ndi mzindawo. Uyangʼanitsitse mzindawo ndipo udzakhala wozingidwa ndi nsanja za nkhondo. Choncho umangire nsanja zankhondo. Chimenechi chidzakhala chizindikiro kwa Aisraeli.
Prends aussi une plaque de fer, place-la comme une muraille de fer entre la ville et toi; tourne ta face contre elle, en sorte qu'elle soit assiégée, et tu la serreras de près. Ce sera là un signe pour la maison d'Israël.
4 “Tsono iwe ugonere kumanzere kwako ndipo ndidzayika pa iwe tchimo la Aisraeli. Iwe udzasenza tchimolo masiku onse amene udzagonere mbali imeneyo.
Ensuite couche-toi sur ton côté gauche, mets-y l'iniquité d'Israël. Tu porteras leur iniquité autant de jours que tu seras couché sur ce côté.
5 Ine ndakuyikira masiku okwana 390 malingana ndi zaka za machimo awo. Umu ndi mmene udzasenzere machimo a Aisraeli.
Car je te compterai les années de leur iniquité pour un nombre égal de jours, savoir, trois cent quatre-vingt-dix jours, durant lesquels tu porteras l'iniquité de la maison d'Israël.
6 “Utatha zimenezo udzagonerenso mbali ya kudzanja lamanja, ndipo udzasenza machimo a anthu a ku Yuda masiku makumi anayi, tsiku lililonse kuyimira chaka chimodzi.
Quand tu auras accompli ces jours-là, tu te coucheras en second lieu sur ton côté droit, et tu porteras l'iniquité de la maison de Juda pendant quarante jours, un jour pour une année; car je te compte un jour pour la durée d'une année.
7 Tsono udzayangʼanitsitse nsanja za nkhondo zozinga. Dzanja la mkanjo wako utalikwinya ndi dzanja lako utakweza, udzalosere modzudzula Yerusalemu.
Tu tourneras aussi ta face et ton bras retroussé vers Jérusalem assiégée, et tu prophétiseras contre elle.
8 Ine ndidzakumanga ndi zingwe kotero kuti sudzatha kutembenukira uku ndi uku mpaka utatsiriza masiku akuzingidwa ako.
Or voici, je mets sur toi des liens, afin que tu ne te tournes point de l'un de tes côtés sur l'autre, jusqu'à ce que tu aies accompli les jours de ton siège.
9 “Tsono tenga tirigu ndi barele, nyemba ndi mphodza, mapira ndi mchewere; ndipo uyike zonsezi mʼmbale imodzi ndipo upange buledi wako. Uzidya pa masiku 390 amene udzakhala ukugonera mbali imodzi.
Prends aussi du froment, de l'orge, des fèves, des lentilles, du millet et de l'épeautre; mets-les dans un vase, et fais-en du pain pour autant de jours que tu seras couché sur ton côté; tu en mangeras pendant trois cent quatre-vingt-dix jours.
10 Uyeze theka la kilogalamu la chakudyacho kuti uzidya tsiku lililonse kamodzi kokha.
La nourriture que tu mangeras sera du poids de vingt sicles par jour; tu en mangeras de temps à autre.
11 Uyezenso zikho ziwiri zamadzi ndipo uzimwa tsiku ndi tsiku.
Quant à l'eau, tu en boiras par mesure, savoir, la sixième partie d'un hin; tu en boiras de temps à autre.
12 Uzidya chakudya chako ngati momwe amadyera keke ya barele. Uzidzaphika chakudyacho anthu akuona pogwiritsa ntchito ndowe ya munthu ngati nkhuni.”
Tu mangeras des gâteaux d'orge, que tu cuiras sous leurs yeux avec des excréments humains.
13 Yehova anati, “Chimodzimodzi anthu a Israeli adzadya chakudya chodetsedwa ku mayiko achilendo kumene Ine ndidzawapirikitsira.”
Et l'Éernel dit: C'est ainsi que les enfants d'Israël mangeront leur pain souillé parmi les nations au milieu desquelles je les chasserai.
14 Koma ine ndinati, “Zisatero, Ambuye Yehova! Ine sindinadziyipitsepo pa zachipembedzo. Kuyambira ubwana wanga mpaka tsopano, sindinadyepo kanthu kalikonse kopezeka katafa kapena kophedwa ndi zirombo za kutchire. Palibe nyama yodetsedwa pa zachipembedzo imene inalowa pakamwa panga.”
Alors je dis: Ah! Seigneur Éternel, voici, mon âme n'a point été souillée; et depuis ma jeunesse jusqu'à présent, je n'ai mangé d'aucun corps mort, ni d'aucune bête déchirée, et aucune chair impure n'est entrée dans ma bouche.
15 Iye anati, “Chabwino, ndidzakulola kuti uphike buledi wako ndi ndowe za ngʼombe mʼmalo mwa ndowe za munthu.”
Et il me répondit: Voici, je te donne la fiente des bœufs à la place d'excréments humains, et là-dessus tu apprêteras ta nourriture.
16 Pambuyo pake anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Yerusalemu ndidzawachepetsera chakudya. Anthuwo adzadya chakudya chochita kuyeza ndipo azidzadya mwa nkhawa. Azidzamwanso madzi ochita kuyeza ndiponso mwa mantha.
Puis il ajouta: Fils de l'homme, voici, je vais retrancher dans Jérusalem le pain qui soutient; ils mangeront leur pain au poids et dans l'angoisse; ils boiront l'eau à la mesure et dans la stupeur.
17 Ndidzachita zimenezi kuti adzasowe chakudya ndi madzi. Choncho adzachita nkhawa akumapenyana ndipo adzatheratu ndi kuwonda chifukwa cha machimo awo.”
Et parce que le pain et l'eau leur manqueront, ils seront dans la consternation les uns et les autres, et ils se consumeront à cause de leur iniquité.

< Ezekieli 4 >