< Ezekieli 4 >

1 Mulungu anati, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga njerwa, uliyike pamaso pako ndipo ujambulepo chithunzi cha mzinda wa Yerusalemu.
Thou also, son of man, take thee a tile, and lay it before thee, and portray upon it a city, even Jerusalem.
2 Ndipo uwuzinge mzindawo motere: uwumangire nsanja zowuzinga, uwumbire mitumbira ya nkhondo, uwumangire misasa ya nkhondo ndipo uyike zida zogumulira kuzungulira mzindawo.
And lay siege against it, and build forts against it, and cast up a mound against it. Also set camps against it, and plant battering rams against it round about.
3 Kenaka utenge chiwaya chachitsulo uchiyike ngati khoma lachitsulo pakati pa iwe ndi mzindawo. Uyangʼanitsitse mzindawo ndipo udzakhala wozingidwa ndi nsanja za nkhondo. Choncho umangire nsanja zankhondo. Chimenechi chidzakhala chizindikiro kwa Aisraeli.
And take thou to thee an iron pan, and set it for a wall of iron between thee and the city. And set thy face toward it, and it shall be besieged, and thou shall lay siege against it. This shall be a sign to the house of Israel.
4 “Tsono iwe ugonere kumanzere kwako ndipo ndidzayika pa iwe tchimo la Aisraeli. Iwe udzasenza tchimolo masiku onse amene udzagonere mbali imeneyo.
Moreover lie thou upon thy left side, and lay the iniquity of the house of Israel upon it. According to the number of the days that thou shall lie upon it, thou shall bear their iniquity.
5 Ine ndakuyikira masiku okwana 390 malingana ndi zaka za machimo awo. Umu ndi mmene udzasenzere machimo a Aisraeli.
For I have appointed the years of their iniquity to be a number of days to thee, even three hundred and ninety days. So thou shall bear the iniquity of the house of Israel.
6 “Utatha zimenezo udzagonerenso mbali ya kudzanja lamanja, ndipo udzasenza machimo a anthu a ku Yuda masiku makumi anayi, tsiku lililonse kuyimira chaka chimodzi.
And again, when thou have accomplished these, thou shall lie on thy right side, and shall bear the iniquity of the house of Judah forty days, each day for a year. I have appointed it to thee.
7 Tsono udzayangʼanitsitse nsanja za nkhondo zozinga. Dzanja la mkanjo wako utalikwinya ndi dzanja lako utakweza, udzalosere modzudzula Yerusalemu.
And thou shall set thy face toward the siege of Jerusalem, with thine arm uncovered, and thou shall prophesy against it.
8 Ine ndidzakumanga ndi zingwe kotero kuti sudzatha kutembenukira uku ndi uku mpaka utatsiriza masiku akuzingidwa ako.
And, behold, I lay bands upon thee, and thou shall not turn thee from one side to the other, till thou have accomplished the days of thy siege.
9 “Tsono tenga tirigu ndi barele, nyemba ndi mphodza, mapira ndi mchewere; ndipo uyike zonsezi mʼmbale imodzi ndipo upange buledi wako. Uzidya pa masiku 390 amene udzakhala ukugonera mbali imodzi.
Also take thou to thee wheat, and barley, and beans, and lentils, and millet, and spelt, and put them in one vessel, and make thee bread of it, according to the number of the days that thou shall lie upon thy side, even three hundred and ninety days, thou shall eat of it.
10 Uyeze theka la kilogalamu la chakudyacho kuti uzidya tsiku lililonse kamodzi kokha.
And thy food which thou shall eat shall be by weight, twenty shekels a day. Thou shall eat it from time to time.
11 Uyezenso zikho ziwiri zamadzi ndipo uzimwa tsiku ndi tsiku.
And thou shall drink water by measure, the sixth part of a hin. Thou shall drink from time to time.
12 Uzidya chakudya chako ngati momwe amadyera keke ya barele. Uzidzaphika chakudyacho anthu akuona pogwiritsa ntchito ndowe ya munthu ngati nkhuni.”
And thou shall eat it as barley cakes, and thou shall bake it in their sight with dung that comes out of man.
13 Yehova anati, “Chimodzimodzi anthu a Israeli adzadya chakudya chodetsedwa ku mayiko achilendo kumene Ine ndidzawapirikitsira.”
And Jehovah said, Even thus shall the sons of Israel eat their bread unclean among the nations where I will drive them.
14 Koma ine ndinati, “Zisatero, Ambuye Yehova! Ine sindinadziyipitsepo pa zachipembedzo. Kuyambira ubwana wanga mpaka tsopano, sindinadyepo kanthu kalikonse kopezeka katafa kapena kophedwa ndi zirombo za kutchire. Palibe nyama yodetsedwa pa zachipembedzo imene inalowa pakamwa panga.”
Then I said, Ah lord Jehovah! Behold, my soul has not been polluted. For from my youth up even till now I have not eaten of that which dies of itself, or is torn of beasts, neither has abominable flesh come into my mouth.
15 Iye anati, “Chabwino, ndidzakulola kuti uphike buledi wako ndi ndowe za ngʼombe mʼmalo mwa ndowe za munthu.”
Then he said to me, See, I have given thee cow's dung for man's dung, and thou shall prepare thy bread of it.
16 Pambuyo pake anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, anthu a ku Yerusalemu ndidzawachepetsera chakudya. Anthuwo adzadya chakudya chochita kuyeza ndipo azidzadya mwa nkhawa. Azidzamwanso madzi ochita kuyeza ndiponso mwa mantha.
Moreover he said to me, Son of man, behold, I will break the staff of bread in Jerusalem, and they shall eat bread by weight, and with fearfulness, and they shall drink water by measure, and in dismay,
17 Ndidzachita zimenezi kuti adzasowe chakudya ndi madzi. Choncho adzachita nkhawa akumapenyana ndipo adzatheratu ndi kuwonda chifukwa cha machimo awo.”
that they may lack bread and water, and be dismayed one with another, and pine away in their iniquity.

< Ezekieli 4 >