< Ezekieli 39 >
1 “Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
А ти, сину лю́дський, пророкуй на Ґоґа та й скажеш: Так говорить Господь Бог: Ото Я на тебе, кня́же Ро́шу, Мешеху та Тувалу!
2 Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
І верну́ тебе, і попрова́джу тебе, і підійму́ тебе з півні́чних кінці́в, і впрова́джу тебе на Ізраїлеві го́ри.
3 Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
І виб'ю лука твого з твоєї ліви́ці, а твої стрі́ли кину з твоєї прави́ці.
4 Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
Упаде́ш на Ізраїлевих гора́х ти й усі відділи твої та наро́ди, що з тобою; віддам тебе на з'їдження хи́жому пта́ству, усякому крила́тому та польові́й звірині́.
5 Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
На відкритому полі впаде́ш ти, бо це Я говорив, говорить Господь Бог!
6 Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
І пошлю́ Я огонь на Маґоґа та на тих, що безпечно заме́шкують острови́, і пізнають вони, що Я — Господь!
7 “Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
А Своє святе Ім'я́ розголошу́ посеред Мого народу Ізраїля, і більше не дам знева́жити святе Моє Йме́ння, і наро́ди пізнають, що Я — Госпо́дь, Святий Ізраїлів!
8 Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
Ось при́йде і станеться, — говорить Господь Бог, — це той день, що Я говорив.
9 “Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
І повихо́дять ме́шканці Ізраїлевих міст, і накладуть огонь, і палитимуть зброю та щитка́ й щита́, лука та стрі́ли, і ручно́го кия та ра́тище, і будуть ними палити огонь сім років.
10 Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
І не будуть носити дров з поля, і не будуть рубати з лісі́в, бо збро́єю будуть палити огонь, і ві́зьмуть здо́бич із тих, хто брав здо́бич із них, і пограбу́ють тих, хто їх грабував, говорить Господь Бог.
11 “Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
І станеться того дня, дам Я там Ґоґові місце гро́бу в Ізраїлі, Долину Перехо́жих, на схід від моря, і що замикає дорогу перехо́жим. І похова́ють там Ґоґа й усе його многолю́дство, та й назвуть: Долина Многолюдства Ґоґа.
12 “Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
І буде ховати їх Ізраїлів дім, щоб очи́стити землю, сім місяців.
13 Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
І буде ховати ввесь наро́д кра́ю, і він стане для них за пам'ятку, того дня, коли Я просла́влю Себе, говорить Господь Бог.
14 “Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
І відділять людей, які без пере́рви ходи́тимуть по кра́ю й ховатимуть з перехожими позосталих ще на пове́рхні землі, щоб її очи́стити. По семи місяцях вони ще будуть вишу́кувати.
15 Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
І пере́йдуть ті обхідники́ по кра́ю, і коли хто побачить лю́дську кістку, то поставить при ній знака, аж поки не поховають її похоро́нники в Долині Многолю́дства Ґоґа.
16 (Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
А ім'я́ міста — Гамона. І очистять землю.
17 “Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
А ти, сину лю́дський, так говорить Господь Бог: Скажи пта́хові, усякому крилатому, та всій польові́й звірині́: Згромадьтеся й прийдіть, зберіться навколо над жертвою, що Я принесу́ для вас, велика жертва на Ізраїлевих гора́х, і ви будете їсти м'ясо, і будете пити кров.
18 Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
Ви будете їсти тіло ли́царів, а кров князі́в землі будете пити, — барани́, і ві́вці, і козли́, бики́, — ситі баша́нські бики́ всі вони.
19 Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
І будете їсти лій аж до си́тости, і будете пити кров аж до впо́єння з Моєї жертви, яку Я приніс для вас, —
20 Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
і наси́титеся при Моєму столі кі́ньми та верхівця́ми, ли́царями та всякими вояка́ми, говорить Господь Бог!
21 “Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
І дам Свою славу між наро́дами, і побачать усі наро́ди Мій суд, що зроблю́ Я, та Мою руку, що на них покладу́.
22 Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
І пізнає Ізраїлів дім, що Я — Госпо́дь, їхній Бог, від цього дня й далі.
23 Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
І пізнають наро́ди, що Ізраїлів дім пішов на вигна́ння за провини свої, за те, що спроневі́рилися Мені, а Я схова́в був від них лице Своє, і віддав їх у руку їхніх не́приятелів, і всі вони попа́дали від меча.
24 Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
За їхньою нечи́стістю та за їхнє беззако́ння зробив Я це з ними, і сховав від них лице Своє.
25 “Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
Тому́ так говорить Господь Бог: Тепер поверну́ долю Якова, і змилуюся над усім Ізраїлевим домом, і буду ревний за Своє святе Йме́ння.
26 Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
І відчу́ють вони свою га́ньбу та все своє спроневі́рення, яки́м спроневі́рилися Мені, коли сядуть безпечно на своїй землі, і не буде вже ніко́го, хто б їх страши́в,
27 Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
коли поверну́ їх з наро́дів, і позбира́ю їх із країв їхніх ворогів, і покажу Свою святість у них на оча́х числе́нних наро́дів.
28 Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
І пізнають вони, що Я — Госпо́дь, Бог їхній, коли ви́жену їх у поло́н до наро́дів, а пото́му позбираю їх на їхню зе́млю, і більш не позоста́влю там ніко́го з них.
29 Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
І не сховаю вже від них Свого лиця, бо виллю Духа Свого на Ізраїлів дім, говорить Госпо́дь Бог!“