< Ezekieli 39 >

1 “Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
“İnsanoğlu, Gog'a karşı peygamberlik et ve ona de ki, ‘Egemen RAB şöyle diyor: Ey Roş'un, Meşek'in, Tuval'ın önderi Gog, sana karşıyım.
2 Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
Seni geri çevirip sürükleyeceğim. Seni uzak kuzeyden çıkarıp İsrail'in dağlarına getireceğim.
3 Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
Sol elindeki yayını vuracak, sağ elindeki oklarını düşüreceğim.
4 Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
Sen de askerlerinle senden yana olan uluslar da İsrail dağlarına serileceksiniz. Sizi yem olarak her çeşit yırtıcı kuşa, yabanıl hayvana vereceğim.
5 Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Açık kırlarda düşüp öleceksiniz. Çünkü bunu ben söyledim. Egemen RAB böyle diyor.
6 Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
Magog'un ve kıyıda güvenlik içinde yaşayanların üzerine ateş yağdıracağım. O zaman benim RAB olduğumu anlayacaklar.
7 “Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
“‘Halkım İsrail arasında kutsal adımı tanıtacağım. Bundan böyle kutsal adımın aşağılanmasına izin vermeyeceğim. Uluslar benim İsrail'de kutsal olan RAB olduğumu anlayacaklar.
8 Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
O gün yaklaştı! Söylediklerim olacak. Egemen RAB böyle diyor. Budur sözünü ettiğim gün!
9 “Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
“‘O zaman İsrail kentlerinde yaşayanlar dışarı çıkıp topladıkları silahları yakacaklar. Küçük büyük kalkanları, yayları, okları, sopaları, mızrakları ateşe atacaklar. Bunlarla yedi yıl ateş yakacaklar.
10 Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Kırdan odun toplamayacak, ormandan odun kesmeyecekler. Yakmak için silahları kullanacaklar. Mallarını yağmalayanları yağmalayacak, kendilerini soyanları soyacaklar. Egemen RAB böyle diyor.
11 “Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
“‘O gün Lut Gölü'nün doğusunda, Gezginler Deresi'nde Gog'a İsrail'de bilinen bir mezar yeri vereceğim. Gog'la bütün ordusu orada gömülecek. Oraya Hamon-Gog Vadisi adı verilecek. Oradan geçecek gezginlerin önü kesilecek.
12 “Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
İsrail halkı ülkeyi arındırmak için onları gömecek. Bu yedi ay sürecek.
13 Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Onları bütün ülke halkı gömecek. Görkemimi açıkladığım gün onlar için onur olacak. Egemen RAB böyle diyor.
14 “Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
“‘Ülkeyi arındırmak için adamlar görevlendirilecek. Bazıları ülkeyi sürekli dolaşacak, öbürleriyse yerde kalan cesetleri gömecekler. Yedi aylık süre bitince, araştırma işine başlayacaklar.
15 Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
Bu adamlar ülkenin her yanını dolaşacak. Bir insan kemiği görünce, mezarcılar onu Hamon-Gog Vadisi'ne gömünceye dek, yanına bir işaret koyacak.
16 (Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
Orada Hamona adında bir kent olacak. Böylelikle ülke arındırılacak.’
17 “Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
“İnsanoğlu, Egemen RAB şöyle diyor: Her çeşit kuşa ve yabanıl hayvana seslen: ‘Sizin için hazırlayacağım kurbana, İsrail dağları üzerindeki büyük kurbana gelin, her yandan toplanın! Orada et yiyecek, kan içeceksiniz.
18 Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
Başan'ın besili hayvanlarının –koçların, kuzuların, tekelerin, boğaların– etini yiyip kanını içer gibi yiğitlerin etini yiyecek, dünya önderlerinin kanını içeceksiniz.
19 Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
Sizin için hazırlayacağım kurbandan doyana dek yağ yiyeceksiniz, sarhoş oluncaya dek kan içeceksiniz.
20 Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Soframda atlardan, atlılardan, yiğitlerden ve her çeşit askerden bol bol yiyip doyacaksınız.’ Egemen RAB böyle diyor.
21 “Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
“Görkemimi uluslar arasında açıklayacağım. Bütün uluslar kendilerine verdiğim cezayı, üzerlerine koyduğum elimi görecekler.
22 Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
İsrail halkı o günden başlayarak benim Tanrıları RAB olduğumu anlayacak.
23 Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
Uluslar İsrail halkının işlediği suç yüzünden, bana ihanet ettiği için sürgüne gittiğini anlayacaklar. Yüzümü onlardan gizledim, onları düşmanlarının eline teslim ettim, hepsi kılıçtan geçirildi.
24 Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
Onları kirliliklerine, isyanlarına göre cezalandırdım, yüzümü onlardan gizledim.
25 “Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
“Bundan ötürü Egemen RAB şöyle diyor: Yakup'un sürgündeki soyunu geri getirecek, İsrail halkına acıyacağım. Kutsal adımı kıskançlıkla koruyacağım.
26 Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
Ülkelerinde güvenlik içinde yaşayınca, onları korkutan kimse olmayınca, utançlarını, bana ettikleri bütün ihanetleri unutacaklar.
27 Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
Onları uluslar arasından geri getirip düşman ülkelerinden topladığım zaman, onlar aracılığıyla birçok ulusa kutsallığımı göstereceğim.
28 Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
O zaman benim Tanrıları RAB olduğumu anlayacaklar. Onları uluslar arasına sürgüne göndermeme karşın, hiçbirini bırakmadan ülkelerine geri getireceğim.
29 Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
Onlardan bir daha yüzümü gizlemeyeceğim, çünkü İsrail halkı üzerine Ruhum'u dökeceğim.” Egemen RAB böyle diyor.

< Ezekieli 39 >