< Ezekieli 39 >

1 “Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
›Zato, ti, človeški sin, prerokuj zoper Gog in reci: ›Tako govori Gospod Bog: ›Glej, jaz sem zoper tebe, oh Gog, glavni princ Mešeha in Tubála,
2 Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
in obrnil te bom nazaj in pustil samo šesti del tebe in ti povzročil, da prideš gor iz severnih krajev in privedel te bom na Izraelove gore
3 Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
in izbil ti bom lok iz tvoje leve roke in tvojim puščicam povzročil, da izpadejo iz tvoje desnice.
4 Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
Padel boš na Izraelovih gorah, ti in vse tvoje čete in ljudstvo, ki je s teboj. Izročil te bom pticam roparicam vsake vrste in k živalim polja, da boš požrt.
5 Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Padel boš na odprtem polju, kajti jaz sem to govoril, ‹ govori Gospod Bog.
6 Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
›In poslal bom ogenj na Magóg in med tiste, ki brezskrbno prebivajo na otokih. In spoznali bodo, da jaz sem Gospod.
7 “Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
Tako bom svoje sveto ime naredil znano v sredi svojega ljudstva Izraela; in ne bom jim več dopustil, da oskrunijo moje sveto ime. In pogani bodo spoznali, da jaz sem Gospod, Sveti v Izraelu.
8 Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
Glej, prišel je in narejeno je, ‹ govori Gospod Bog; ›to je dan, o katerem sem govoril.
9 “Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
Tisti, ki prebivajo v Izraelovih mestih, bodo šli naprej in bodo zakurili ogenj, sežgali orožje, tako ščite in majhne ščite, loke, puščice, krepelca ter sulice in sedem let jih bodo sežigali z ognjem,
10 Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
tako da ne bodo vzeli nobenega lesa iz polja niti posekali nobenega iz gozdov; kajti orožje bodo sežigali z ognjem in plenili bodo tiste, ki so jih plenili in ropali bodo tiste, ki so jih ropali, ‹ govori Gospod Bog.
11 “Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
›In na tisti dan se bo zgodilo, da bom Gogu dal kraj za grobove v Izraelu, dolino popotnikov na vzhodu morja, in ta bo zamašila nosove popotnikom, in tam bodo sežgali Goga in vso njegovo množico in imenovali jo bodo Dolina Gogove množice.
12 “Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
In sedem mesecev jih bo Izraelova hiša pokopavala, da bodo lahko očistili deželo.
13 Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Da, vse ljudstvo dežele jih bo pokopavalo; in to jim bo ugled na dan, ko bom proslavljen, ‹ govori Gospod Bog.
14 “Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
›In oddvojili bodo može z nenehno zaposlitvijo, ki bodo hodili skozi deželo, da bi s potniki pokopavali tiste, ki ostajajo na obličju zemlje, da jo očistijo; po koncu sedmih mesecev bodo iskali.
15 Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
In potniki, ki gredo skozi deželo, ko kdorkoli zagleda človeško kost, potem bo ob njej postavil znamenje, dokler je grobarji ne pokopljejo v dolini Gogove množice.
16 (Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
In ime mesta bo prav tako Hamóna. Tako bodo očistili deželo.
17 “Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
In ti, človeški sin, ‹ tako govori Gospod Bog: ›Govori vsaki operjeni perjadi in vsaki živali polja: ›Zberite se in pridite; zberite se na vsaki strani k moji klavni daritvi, ki jo darujem za vas, torej veliki klavni daritvi na Izraelovih gorah, da boste lahko jedle meso in pile kri.
18 Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
Jedle boste meso mogočnih in pile kri zemeljskih princev, ovnov, jagnjet in koz, bikcev, vsi izmed njih bašánski pitanci.
19 Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
In jedle boste tolščo, dokler ne boste nasičene in pile kri, dokler ne boste pijane od moje klavne daritve, ki sem jo žrtvoval za vas.
20 Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Tako boste nasičene pri moji mizi s konji in bojnimi vozovi in z mogočnimi možmi in z vsemi bojevniki, ‹ govori Gospod Bog.
21 “Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
›In svojo slavo bom postavil med pogane in vsi pogani bodo videli mojo sodbo, ki sem jo izvršil in mojo roko, ki sem jo položil nanje.
22 Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
Tako bo Izraelova hiša spoznala, da jaz sem Gospod, njihov Bog, od tega dne naprej.
23 Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
In pogani bodo vedeli, da je hiša Izraelova odšla v ujetništvo zaradi svojih krivičnosti, ker so kršili zoper mene, zato sem svoj obraz skril pred njimi in jih izročil v roko njihovih sovražnikov; tako so vsi padli pod mečem.
24 Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
Glede na njihovo nečistost in glede na njihove prestopke sem jim storil in svoj obraz sem skril pred njimi.‹
25 “Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
Zato tako govori Gospod Bog: ›Sedaj bom ponovno privedel Jakobovo ujetništvo in usmiljenje bom imel nad celotno Izraelovo hišo in ljubosumen bom zaradi svojega svetega imena;
26 Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
po tem, ko so nosili svojo sramoto in vse svoje prestopke, s katerimi so kršili zoper mene, ko so varno prebivali v svoji deželi in jih nihče ni strašil.
27 Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
Ko sem jih ponovno privedel izmed ljudstva in jih zbral iz dežel njihovih sovražnikov in sem posvečen v njih pred očmi mnogih narodov;
28 Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
potem bodo spoznali, da jaz sem Gospod, njihov Bog, ki jim je storil, da so bili odvedeni v ujetništvo med pogane, toda zbral sem jih k njihovi lastni deželi in nikogar izmed njih nisem več pustil tam.
29 Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
Niti svojega obraza ne bom več skrival pred njimi, kajti svojega duha sem izlil na Izraelovo hišo, ‹ govori Gospod Bog.‹«

< Ezekieli 39 >