< Ezekieli 39 >
1 “Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
Фиул омулуй, пророчеште акум ымпотрива луй Гог ши спуне: ‘Аша ворбеште Домнул Думнезеу: «Ятэ кэ ам неказ пе тине, Гог, домнул Рошулуй, Мешекулуй ши Тубалулуй!
2 Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
Те вой тыры, те вой адуче, те вой суи дин фундул мязэнопций ши те вой адуче пе мунций луй Исраел.
3 Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
Ыць вой доборы аркул дин мына стынгэ ши вой фаче сэ-ць кадэ сэӂециле дин мына дряптэ.
4 Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
Вей кэдя пе мунций луй Исраел, ту ши тоате оштиле тале ши попоареле каре вор фи ку тине; те вой да де мынкаре пэсэрилор де прадэ, тутурор челор че ау арипь, ши фярелор кымпулуй.
5 Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Вей кэдя пе фаца кымпулуй, кэч Еу ам ворбит», зиче Домнул Думнезеу.
6 Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
«Вой пуне фок Магогулуй ши челор че локуеск лиништиць ын остроаве, ка сэ штие кэ Еу сунт Домнул.
7 “Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
Ымь вой фаче куноскут Нумеле Меу чел сфынт ын мижлокул попорулуй Меу Исраел ши ну-й вой май лэса сэ-Мь пынгэряскэ Нумеле Меу чел сфынт, чи вор шти нямуриле кэ Еу сунт Домнул, Сфынтул луй Исраел!
8 Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
Ятэ кэ лукруриле ачестя вин ши се ынтымплэ», зиче Домнул Думнезеу. «Ачаста есте зиуа деспре каре ам ворбит.
9 “Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
Атунч, локуиторий четэцилор луй Исраел вор еши, вор арде ши вор да прадэ флэкэрилор армеле, павезеле ши скутуриле, аркуриле ши сэӂециле, лэнчиле ши сулицеле; ши шапте ань вор фаче фокул ку еле.
10 Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Ну вор луа лемне де пе кымп ши ну вор тэя лемне дин пэдурь, чи вор фаче фокул ку армеле. Вор жефуи пе чей че й-ау жефуит ши вор прэда пе чей че й-ау прэдат», зиче Домнул Думнезеу.
11 “Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
«Ын зиуа ачея, вой да луй Гог ун лок де ынмормынтаре ын Исраел: Валя Кэлэторилор, ла рэсэритул Мэрий Моарте, ши мормынтул ачеста ва аступа тречеря кэлэторилор. Аколо вор ынгропа пе Гог ку тоатэ мулцимя луй ши вор нуми валя ачаста:
12 “Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
Шапте лунь ый ва ынгропа каса луй Исраел, ка сэ курэцяскэ цара.
13 Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Тот попорул цэрий ый ва ынгропа ши и се ва дуче вестя ын зиуа кынд вой фи прослэвит», зиче Домнул Думнезеу.
14 “Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
«Апой, вор алеӂе ниште оамень каре вор кутреера неынчетат цара ши каре вор ынгропа трупуриле рэмасе пе фаца пэмынтулуй, ка сэ курэцяскэ цара; дупэ шапте лунь, вор ынчепе сэ черчетезе.
15 Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
Чей че вор стрэбате цара о вор кутреера ши, кынд унул дин ей ва ведя оаселе унуй ом, ва пуне ун семн лынгэ ел пынэ ыл вор ынгропа гропарий ын Валя мулцимий луй Гог.
16 (Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
Тот аколо ва май фи ши о четате нумитэ Хамона. Аша вор курэци цара.»’
17 “Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
Фиул омулуй, аша ворбеште Домнул Думнезеу: ‘Спуне пэсэрилор де орьче сой ши тутурор фярелор кымпулуй: «Адунаци-вэ ши вениць! Стрынӂеци-вэ дин тоате пэрциле пентру жертфа Мя пе каре о жунгий пентру вой; жертфэ маре есте пе мунций луй Исраел! Мынкаць карне ши бець сынӂе,
18 Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
мынкаць карня витежилор ши бець сынӂеле воевозилор пэмынтулуй, сынӂе де бербечь, де мей, де цапь, де таурь ынгрэшаць дин Басан!
19 Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
Мынкаць грэсиме пынэ вэ вець сэтура ши бець сынӂе пынэ вэ вець ымбэта дин жертфеле Меле пе каре ле вой ынжунгия пентру вой!
20 Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Сэтураци-вэ ла маса Мя де карня каилор ши а кэлэрецилор, де карня витежилор ши а тутурор оаменилор де рэзбой», зиче Домнул Думнезеу.
21 “Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
«Ымь вой арэта слава ынтре нямурь, ши тоате нямуриле вор ведя жудекэциле пе каре ле вой фаче ши педепселе ку каре ый ва лови мына Мя.
22 Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
Чей дин каса луй Исраел вор шти кэ Еу сунт Домнул Думнезеул лор, дин зиуа ачея ши де атунч ынаинте.
23 Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
Ши нямуриле вор куноаште кэ, дин причина нелеӂюирилор ей, а фост дусэ каса луй Исраел ын робие, дин причина фэрэделеӂилор ей сэвыршите де еа ымпотрива Мя; де ачея ле-ам аскунс Фаца Мя ши й-ам дат ын мыниле врэжмашилор лор, ка сэ пярэ тоць учишь де сабие.
24 Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
Ле-ам фэкут дупэ некурэцииле лор ши дупэ фэрэделеӂиле лор ши ле-ам аскунс Фаца Мя.»’
25 “Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
Де ачея, аша ворбеште Домнул Думнезеу: ‘Акум вой адуче ынапой пе принший де рэзбой ай луй Иаков, вой авя милэ де тоатэ каса луй Исраел ши вой фи ӂелос де Нумеле Меу чел сфынт.
26 Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
Атунч ышь вор уйта окара ши тоате фэрэделеӂиле пе каре ле-ау сэвыршит ымпотрива Мя кынд локуяу лиништиць ын цара лор ши кынд ну-й тулбура нимень.
27 Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
Кынд ый вой адуче ынапой динтре попоаре ши ый вой стрынӂе дин цара врэжмашилор лор, вой фи сфинцит де ей ынаинтя мултор нямурь.
28 Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
Ши вор шти кэ Еу сунт Домнул Думнезеул лор, каре-й лэсасем сэ фие луаць приншь де рэзбой ынтре нямурь ши каре-й стрынг ярэшь ын цара лор; ну вой май лэса пе ничунул дин ей аколо
29 Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
ши ну ле вой май аскунде Фаца Мя, кэч вой турна Духул Меу пентру каса луй Исраел’, зиче Домнул Думнезеу.”