< Ezekieli 39 >

1 “Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
Un tu, cilvēka bērns, sludini pret Gogu un saki: tā saka Tas Kungs Dievs: redzi, Es celšos pret tevi, Gog, tu Roša, Mešeha un Tūbala valdnieks!
2 Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
Un Es tevi griezīšu un vadīšu un tevi atvedīšu no paša ziemeļa gala un tevi vedīšu uz Israēla kalniem.
3 Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
Un Es tavu stopu izsitīšu no tavas kreisās rokas un tavām bultām likšu izkrist no tavas labās rokas.
4 Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
Uz Israēla kalniem tu kritīsi ar visiem saviem karogiem un ļaudīm, kas tev līdz. Visādiem plēsīgiem putniem un lauka zvēriem Es tevi došu par barību.
5 Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Tev būs krist uz lauka; jo Es to esmu runājis, saka Tas Kungs Dievs.
6 Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
Un Es sūtīšu uguni uz Magogu, un starp tiem, kas salās droši dzīvo, un tie samanīs, ka Es esmu Tas Kungs.
7 “Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
Un Savu svēto Vārdu Es darīšu zināmu Saviem Israēla ļaudīm, un vairs neļaušu sagānīt Savu svēto Vārdu, un pagāni samanīs, ka Es esmu Tas Kungs, tas Svētais iekš Israēla.
8 Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
Redzi, tas nāks un notiks, saka Tas Kungs Dievs; šī ir tā diena, par ko Es esmu runājis.
9 “Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
Israēla pilsētu iedzīvotāji izies un iededzinās uguni un sadedzinās tās bruņas un priekšturamās bruņas un krūšu bruņas un stopus un bultas un bozes un šķēpus, un kurs no tiem uguni septiņus gadus,
10 Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Tā ka tiem malka nebūs jānes no lauka nedz jācērt mežos, bet tie kurs uguni no tiem kara rīkiem, un aplaupīs tos, kas viņus bija aplaupījuši, un postīs tos, kas viņus bija postījuši, saka Tas Kungs Dievs.
11 “Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
Un notiks tai dienā, ka Es Gogam došu kapu vietu iekš Israēla, to ieleju, kur no jūras iet pret rīta pusi, tā ka ceļa ļaudīm ceļš būs aiztaisīts; tur apraks Gogu un visu viņa pulku, un to nosauks par Goga pulka ieleju.
12 “Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
Un Israēla nams tos apraks, lai zeme top šķīsta, veselus septiņus mēnešus.
13 Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Un visi zemes ļaudis raks, un tas tiem būs par slavu tai dienā, kad es būšu pagodinājies, saka Tas Kungs Dievs.
14 “Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
Un tie izvēlēs vīrus, kas bez mitēšanās zemi pārstaigā, un kapu racējus tiem līdz, kas staigā apkārt un tos zemes virsū atlikušos aprok, to (zemi) šķīstīt; pēc beigtiem septiņiem mēnešiem tie sāks meklēt.
15 Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
Un tie pārstaigātāji ies pa to zemi, un kas cilvēka kaulu redz, tas liks zīmi pie tā, kamēr tie kapu racēji to apraks Goga pulka ielejā.
16 (Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
Un būs arī vienas pilsētas vārds: Amona (pulks); tā tie to zemi šķīstīs.
17 “Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
Tu tad, cilvēka bērns, tā saka Tas Kungs Dievs: saki uz visiem spārnainiem putniem un uz visiem lauka zvēriem: sapulcējaties un nāciet, sakrājaties no tām apkārtējām vietām pie Mana kaujamā upura, ko Es priekš jums esmu upurējis, pie tā lielā kaujamā upura uz Israēla kalniem, un ēdat gaļu un dzerat asinis.
18 Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
Jums būs ēst gaļu no varoņiem un dzert asinis no valdniekiem virs zemes, no jēriem, no auniem un āžiem un vēršiem, kas visi Bāsanā baroti.
19 Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
Un jums būs ēst taukus, kamēr jūs pieēdaties, un dzert asinis, kamēr jūs piedzeraties no Mana kaujamā upura, ko Es jums esmu kāvis.
20 Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Un jūs tapsiet pie Mana galda pieēdināti no zirgiem un jātniekiem, no varoņiem un visādiem karavīriem, saka Tas Kungs Dievs.
21 “Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
Un Es parādīšu Savu godību pagānu starpā, un visi pagāni redzēs Manu sodu, ko Es esmu turējis, un Manu roku, ko Es pie tiem esmu pielicis.
22 Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
Un Israēla nams samanīs, ka Es esmu Tas Kungs, viņu Dievs, no tās dienas un tā joprojām.
23 Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
Un pagāni samanīs, ka Israēla nams savu noziegumu dēļ aizvests, tāpēc ka tie no Manis bija atkāpušies, un ka Es Savu vaigu no tiem biju apslēpis un tos biju rokā devis viņu pretiniekiem, tā ka tie visi caur zobenu krituši.
24 Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
Pēc viņu nešķīstības un pēc viņu pārkāpšanām Es viņiem esmu darījis un no tiem apslēpis Savu vaigu.
25 “Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
Tāpēc tā saka Tas Kungs Dievs: nu Es Jēkaba cietumniekus atkal atvedīšu un apžēlošos par visu Israēla namu, un Es atriebšos Sava svētā Vārda dēļ.
26 Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
Un tie nesīs savu kaunu un visu savu pārkāpumu, ar ko tie pret Mani apgrēkojušies, kad tie savā zemē droši dzīvos, un nebūs neviena, kas viņus iztrūcina.
27 Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
Kad Es tos būšu atvedis no tautām un tos sapulcinājis no viņu ienaidnieku valstīm, - un Es pie tiem parādīšos svēts priekš daudz pagānu acīm,
28 Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
Tad tie samanīs, ka Es esmu Tas Kungs, viņu Dievs, kas tos esmu licis aizvest pie pagāniem, bet tos atkal sapulcinājis viņu zemē un tur vairs neesmu atstājis neviena no tiem.
29 Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
Un Es no tiem vairs neapslēpšu Savu vaigu, kad Es Savu Garu būšu izlējis pār Israēla namu, saka Tas Kungs Dievs.

< Ezekieli 39 >