< Ezekieli 39 >

1 “Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
And you O son of humankind prophesy on Gog and you will say thus he says [the] Lord Yahweh here I [am] against you O Gog [the] prince of [the] head of Meshech and Tubal.
2 Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
And I will turn around you and I will lead on you and I will bring up you from [the] remotest parts of [the] north and I will bring you on [the] mountains of Israel.
3 Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
And I will strike bow your from [the] hand of left your and arrows your from [the] hand of right your I will make fall.
4 Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
On [the] mountains of Israel you will fall you and all troops your and peoples which [are] with you to bird[s] of prey of bird[s] every wing and [the] animal[s] of the field I will give you for food.
5 Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
On [the] surface of the field you will fall for I I have spoken [the] utterance of [the] Lord Yahweh.
6 Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
And I will send fire on Magog and on [the] inhabitants of the islands to security and they will know that I [am] Yahweh.
7 “Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
And [the] name of holiness my I will make known in among people my Israel and not I will let be profaned [the] name of holiness my again and they will know the nations that I Yahweh [am] holy in Israel.
8 Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
There! [it is] coming and it will occur [the] utterance of [the] Lord Yahweh it [is] the day which I have spoken.
9 “Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
And they will go out [the] inhabitants of - [the] cities of Israel and they will kindle and they will kindle a fire with weapon and shield and body shield with bow and with arrows and with staff of hand and with spear and they will kindle with them fire seven years.
10 Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
And not they will carry wood from the field and not they will cut [it] from the forests for with the weapon they will kindle fire and they will plunder [those who] plundered them and they will take as spoil [those who] took as spoil them [the] utterance of [the] Lord Yahweh.
11 “Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
And it will be on the day that I will give to Gog - a place there a burial site in Israel [the] Valley of the Travellers [the] east of the sea and [will] block [the] way of it those [who] pass through and people will bury there Gog and all (multitude his *Q(K)*) and they will call [it] [the] valley of Hamon-Gog.
12 “Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
And they will bury them [the] house of Israel so as to cleanse the land seven months.
13 Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
And they will bury [them] all [the] people of the land and it will become for them a name [the] day of my glorifying myself [the] utterance of [the] Lord Yahweh.
14 “Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
And people of continuity they will set apart [who] pass in the land [who] bury those [who] pass through those [who] remain on [the] surface of the land to cleanse it from [the] end of seven months they will make a search.
15 Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
And they will pass those [who] pass in the land and they will see a bone of a human and he will build beside it a marker until they have buried it those [who] bury to [the] valley of Hamon-Gog.
16 (Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
And also [the] name of a city [is] Hamonah and they will cleanse the land.
17 “Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
And you O son of humankind thus he says - [the] Lord Yahweh say to bird[s] of every wing and to every - animal of the field assemble and come gather yourselves from round about to sacrifice my which I [am] sacrificing for you a sacrifice great on [the] mountains of Israel and you will eat flesh and you will drink blood.
18 Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
[the] flesh of Warriors you will eat and [the] blood of [the] princes of the land you will drink rams lambs and goats bulls fatlings of Bashan all of them.
19 Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
And you will eat fat to satiety and you will drink blood to drunkenness from sacrifice my which I have sacrificed for you.
20 Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
And you will be satisfied at table my horse and charioteer warrior and every man of war [the] utterance of [the] Lord Yahweh.
21 “Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
And I will set glory my among the nations and they will see all the nations judgment my which I have done and hand my which I have put on them.
22 Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
And they will know [the] house of Israel that I [am] Yahweh God their from the day that and onwards.
23 Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
And they will know the nations that for iniquity their they went into exile [the] house of Israel on that they had acted unfaithfully against me and I hid face my from them and I gave them in [the] hand of opponents their and they fell by the sword all of them.
24 Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
According to uncleanness their and according to transgressions their I have dealt them and I hid face my from them.
25 “Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
Therefore thus he says [the] Lord Yahweh now I will turn back ([the] captivity of *Q(k)*) Jacob and I will have compassion on all [the] house of Israel and I will be zealous for [the] name of holiness my.
26 Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
And they will bear disgrace their and all unfaithfulness their which they acted unfaithfully against me when dwell they on own land their to security and there not [will be one who] disturbs [them].
27 Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
When bring back I them from the peoples and I will gather them from [the] lands of enemies their and I will show myself holy by them to [the] eyes of the nations many.
28 Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
And they will know that I [am] Yahweh God their because sent into exile I them to the nations and I will gather them to own land their and not I will leave behind again any of them there.
29 Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
And not I will hide again face my from them [I] who I have poured out spirit my on [the] house of Israel [the] utterance of [the] Lord Yahweh.

< Ezekieli 39 >