< Ezekieli 39 >
1 “Iwe mwana wa munthu, nenera modzudzula Gogi ndi kumuwuza kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa Mesaki ndi Tubala.
Thou therefore son of man. Prophesy against Gog, and thou shalt say, Thus saith My Lord Yahweh: Behold me! against thee O Gog Prince of Rosh, Meshech and Tubal.
2 Ine ndidzakuzunguza ndi kukupirikitsira kutsogolo. Ndidzakutenga kuchokera kutali kumpoto ndi kukutumiza kuti ukalimbane ndi anthu a ku mapiri a Israeli.
Therefore will I turn thee about and lead thee on, and cause thee to come up out of the remote parts of the North, - And will bring thee in upon the mountains of Israel;
3 Kenaka Ine ndidzathyola uta wa mʼdzanja lako lamanzere ndipo ndidzagwetsa mivi ya mʼdzanja lako lamanja.
And I will smite thy bow out of thy left hand, - And thine arrows—out of thy right hand, will I cause to fall.
4 Udzagwa ku mapiri a ku Israeli, iwe ndi magulu ako onse ankhondo ndiponso mitundu ya anthu imene ili nawe. Ndidzakusandutsa chakudya cha mitundu yonse ya mbalame zodya nyama, ndiponso cha zirombo zakuthengo.
Upon the mountains of Israel, shalt thou fall, Thou and all thy hordes, and the peoples who are with thee, — To birds of prey of every wing. and the wild beast of the field, will I give thee for food:
5 Udzafera pa mtetete kuthengo, pakuti Ine ndayankhula. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Upon the, face of the field, shalt thou fall, - For I, have spoken, Declareth My Lord Yahweh.
6 Ndidzatumiza moto pa Magogi ndi pa onse amene amakhala mwamtendere mʼmbali mwa nyanja. Choncho adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’
And I will send a fire into Magog, And among them who are dwelling in the Coastlands securely, — So shalt thou know that I am Yahweh.
7 “Ndidzachititsa kuti dzina langa loyera lidziwike pakati pa anthu anga Israeli. Sindidzalola kuti dzina langa liyipitsidwenso, ndipo mitundu ya anthu idzadziwa kuti Ine Yehova ndine Woyera mu Israeli.
And my holy Name, will I make known in the midst of my people Israel, And will not suffer my holy Name to be profaned any more, — So shall the nations know that, I am Yahweh, Holy in Israel.
8 Zikubwera! Ndipo zidzachitikadi, ndikutero Ine Ambuye Yehova. Ndiye tsiku limene ndinanena lija.
Lo! it is coming, and shall be brought to pass, Declareth My Lord. Yahweh, -the same, is the day whereof I had spoken.
9 “Pamenepo okhala mʼmizinda ya Israeli adzatuluka ndipo adzasonkhanitsa zida zankhondo kuti zikhale nkhuni ndipo adzazitentha; zishango ndi lihawo, mauta ndi mivi, zibonga za nkhondo ndi mikondo. Adzazisonkhera moto kwa zaka zisanu ndi ziwiri.
Then shall go forth the dwellers of the cities of Israel and shall make fires of the weapons and burn them, Both buckler and shield, bow and arrows, and handstaff and spear, - And shall make fires of them seven years;
10 Iwo sadzatolera nkhuni kuthengo kapena kukadula ku nkhalango, chifukwa adzasonkhera moto zidazo. Ndipo iwo adzafunkha amene anawafunkhawo, ndi kulanda chuma cha amene anawalanda, ndikutero Ine Ambuye Yehova.
And they shall not take wood out of the field Neither shall they cut down out of the forests, - For of the armour, shall they make fires, - So shall they spoil those who spoiled them And prey on those who preyed on them, Declareth My Lord Yahweh.
11 “Pa tsiku limenelo ndidzamupatsa Gogi manda mu Israeli, mʼchigwa cha apaulendo, kummawa kwa Nyanja Yakufa. Mandawo adzatseka njira ya apaulendo, chifukwa Gogi ndi gulu lake lankhondo adzayikidwa kumeneko. Ndipo chigwacho chidzatchedwa chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
And it shall come to pass in that day that I will give to Gog a place of memorial for burial in Israel even the valley of them that pass through east of the sea, And it shall be enough to keep back them who would pass through, - and they shall bury there Gog and all his multitude, and shall call it Ge-hamon-gog. [That is "The valley of the multitude of Gog."]
12 “Nyumba ya Israeli idzakhala ikukwirira mitembo kwa miyezi isanu ndi iwiri ndi cholinga choyeretsa dziko.
So shall the house of Israel bury them (that they may cleanse the land) —seven months;
13 Anthu onse a mʼdzikomo adzakwirira nawo mitembo. Ntchito imeneyo adzatchuka nayo pa tsiku limene ndidzaonetsa ulemerero wanga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Yea all the people of the land, shall bury, and it shall become to them a memorial, —the day that I get myself glory, Declareth My Lord Yahweh.
14 “Patapita miyezi isanu ndi iwiri adzalemba ntchito anthu ena odzayenda mʼdziko lonse kufunafuna mitembo imene inatsalira nʼkumayikwirira. Choncho adzayeretseratu dzikolo.
And, men to keep at it constantly, shall they tell off Men to pass throughout the land, who with the passers-by, shall continue burying, them who have been left on the face of the land to cleanse it, — At the end of seven months, shall they make search.
15 Poyenda mʼdzikomo azidzati akaona fupa la munthu azidzayikapo chizindikiro pambali pake mpaka okumba manda atakalikwirira fupalo ku chigwa cha gulu lankhondo la Gogi.
And when any of the passers-by, in going through the land, shall see a human bone, then shall he set up near it a sign, —until the buriers have buried it, in Ge-hamon-Gog.
16 (Komwekonso kudzakhala mzinda wotchedwa Gulu la nkhondo). Ndipo potero adzayeretsa dziko.
Moreover, the name of a city, shall be Hamonah ["To the multitude"] so shall they cleanse the land.
17 “Tsono iwe mwana wa munthu, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Itana mbalame za mitundu yonse ndi zirombo zonse zakuthengo ndipo uziwuze kuti, ‘Sonkhanani ndipo bwerani kuchokera ku mbali zonse ku nsembe imene ndikukonzerani inu, nsembe yayikulu pa mapiri a Israeli. Kumeneko inu mudzadya mnofu ndi kumwa magazi.
Thou, therefore son of man, Thus, saith My Lord Yahweh, Say to the bird of every wing. And to every wild beast of the field. Assemble yourselves and come Gather yourselves from every side, unto my sacrifice which I am sacrificing for you A great sacrifice on the mountains of Israel, - And ye shall eat flesh and drink blood:
18 Mudzadya mnofu wa anthu ankhondo amphamvu ndi kumwa magazi a akalonga a dziko lapansi. Onsewo anaphedwa ngati nkhosa zazimuna, ana ankhosa onenepa, mbuzi ndiponso ngati ngʼombe zazimuna zonenepa za ku Basani.
The flesh of mighty men, shall ye eat, And the blood of the princes of the earth, shall ye drink.— Rams well-fed lambs and he-goats bullocks, Fatlings of Bashan all of them;
19 Ku phwando lansembe limene ndikukonzera inulo, mudzadya zonona mpaka kukhuta ndi kumwa magazi mpaka kuledzera.
And ye shall eat fat till ye are sated, And drink blood till ye are drunken, Of my sacrifice which I have sacrificed for you;
20 Pa tebulo langa mudzakhuta pakudya akavalo ndi okwerapo ake, anthu amphamvu ndi asilikali amitundumitundu,’ ndikutero Ine Ambuye Yehova.
So shall ye be sated at my table with horse and chariot team, mighty man and every man of war, — Declareth My Lord, Yahweh.
21 “Ine ndidzaonetsa ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina, ndipo adzaona mmene ndidzawalangire ndikadzayika dzanja langa pa iwo.
Thus will I set my glory among the nations, And all the nations, shall see, My judgment which I have executed, —and My hand which I have laid upon them.
22 Kuyambira tsiku limenelo mpaka mʼtsogolo Aisraeli adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo.
So shall the house of Israel know that, I Yahweh, am their God, —from that day and forward;
23 Ndipo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti anthu a Israeli anatengedwa ukapolo chifukwa cha tchimo lawo, chifukwa anali osakhulupirika kwa Ine. Choncho Ine ndinawabisira nkhope yanga ndi kuwapereka kwa adani awo. Motero anaphedwa pa nkhondo.
And the nations shall know That in their iniquity, were the house of Israel exiled because they had committed treachery against me, And so I hid my face from them, — And gave them into the hand of their adversaries, And they fell by the sword all of them.
24 Ndinawachita zimenezi chifukwa cha kunyansa kwawo ndi zolakwa zawo, ndipo ndinawabisira nkhope yanga.
According to their uncleanness and according to their transgressions, dealt I with them, — And so I hid my face from them.
25 “Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Tsopano ndidzakhazikanso pa bwino banja la Yakobo. Ndidzachitira chifundo Aisraeli onse, ndipo ndidzateteza dzina langa loyera.
Therefore— Thus saith My Lord Yahweh, Now, will I bring back them of the captivity of Jacob, And have compassion upon all the house of Israel, - And will be jealous for my holy Name;
26 Anthuwo akadzakhala mwamtendere mʼdziko lawo popanda wina wowaopseza, pamenepo adzayiwala zamanyazi zawo zimene zinawachitikira chifukwa chosandikhulupirira Ine.
And they shall bear their confusion, and the punishment of all their treachery wherewith they have committed treachery against me, - When they dwell upon their own soil securely, with none to make them afraid;
27 Ndidzawabwezeranso kwawo kuchokera pakati pa anthu a mitundu ina ndipo ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mayiko a adani awo. Poteropo ndidzaonetsa pamaso pa anthu a mitundu yambiri kuti ndine Woyera.
When I have brought them back from among the peoples, And gathered them out of the lands of their enemies, - So will I hallow myself in them, before the eyes of the many nations;
28 Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wawo, ngakhale kuti ndinawapereka ku ukapolo pakati pa anthu a mitundu ina. Ine ndidzawasonkhanitsanso ku dziko lawo osasiyako wina mʼmbuyo.
And they shall know that, I Yahweh, am their God, When I have carried them into exile among the nations, And shall then gather them upon their own soil, - And shall no more leave any of them there.
29 Ine sindidzawabisiranso nkhope yanga, pakuti ndidzathira Mzimu wanga pa Aisraeli. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
Neither will I any more hide my face from them, — In that I have poured out my spirit, upon the house of Israel, Declareth My Lord Yahweh.