< Ezekieli 38 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
Et la parole de l'Éternel me fut adressée en ces mots:
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu.
Fils de l'homme, tourne ton visage du côté de Gog, au pays de Magog, prince de Rosch, Mésech et Thubal, et prophétise contre lui
3 Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala.
et dis: Ainsi parle le Seigneur, l'Éternel: J'en veux à toi, Gog, prince de Rosch, Mésech et Thubal.
4 Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola.
Je te détournerai, et mettrai un anneau à tes mâchoires, et t'emmènerai, toi et toute ton armée, chevaux et cavaliers, tous vêtus magnifiquement, foule immense portant le pavois et le bouclier, tous maniant l'épée;
5 Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo.
Perses, Éthiopiens et Libyens, avec eux, ayant tous le bouclier et le casque;
6 Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.
Gomer et tous ses bataillons, la maison de Thogarma venue du fond du nord avec tous ses bataillons, tout autant de peuples qui t'accompagnent.
7 “‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo.
Tiens-toi prêt et t'équipe, toi et toutes les troupes qui sont attroupées autour de toi, et sois leur général!
8 Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere.
Pendant un longtemps tu seras désiré; mais dans la suite des années tu viendras dans le pays, soustrait à l'épée, où ses habitants auront été rassemblés du milieu de peuples nombreux, sur les montagnes d'Israël longtemps désertes, dans le pays où les habitants auront été ramenés du milieu des peuples et dans lequel ils habiteront tous en sécurité.
9 Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.
Et tu arriveras, tu fondras comme un ouragan, pareil à une nuée, pour couvrir le pays, toi et tous tes bataillons, et les peuples nombreux qui sont avec toi.
10 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa.
Ainsi parle le Seigneur, l'Éternel: Dans ce temps-là, des pensées s'élèveront dans ton cœur, et tu formeras de funestes projets
11 Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo.
et tu diras: J'envahirai le pays ouvert, je fondrai sur ces hommes paisibles, vivant tous dans la sécurité, habitant sans murailles, et n'ayant ni verrous ni portes,
12 Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’
pour enlever du butin, et emporter des dépouilles, pour porter ta main sur des ruines de nouveau habitées, sur un peuple recueilli du milieu des peuples, qui s'est remis au soin des troupeaux et au négoce, et habite les hauteurs du pays.
13 Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’”
Séba et Dedan et les marchands de Tarsis, et tous leurs hommes puissants te diront: « Est-ce pour enlever du butin que tu arrives? pour emporter des dépouilles que tu as réuni tes troupes? pour prendre de l'argent et de l'or, des troupeaux et des biens, pour faire un grand butin? »
14 “Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka.
Aussi prophétise, fils de l'homme, et dis à Gog: Ainsi parle le Seigneur, l'Éternel: Voici, en ce jour-là, tandis que mon peuple d'Israël vivra en sécurité, tu l'auras vu,
15 Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu.
et tu viendras de ta demeure, du fond du nord, toi et beaucoup de peuples avec toi, tous montés sur des chevaux, troupe nombreuse, armée immense,
16 Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.
et tu t'avanceras contre mon peuple d'Israël comme une nuée pour couvrir le pays. Dans la suite des temps il arrivera que je t'amènerai contre mon pays, afin que les nations me reconnaissent quand je donnerai sur toi une preuve de ma sainteté sous leurs yeux, ô Gog!
17 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli.
Ainsi parle le Seigneur, l'Éternel: Est-ce toi dont j'ai parlé aux jours d'autrefois par mes serviteurs, les prophètes d'Israël, qui dans ces temps ont prophétisé pendant des années que je t'amènerai contre eux?
18 Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.
Et il arrivera en ce jour-là, au jour que Gog fondra sur la terre d'Israël, dit le Seigneur, l'Éternel, que la colère me montera dans les narines.
19 Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli.
Et je le dis avec indignation et une ardente colère; dans ce jour il y aura un grand tremblement dans le pays d'Israël:
20 Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi.
à ma présence trembleront les poissons de la mer, et les oiseaux des Cieux, et les bêtes des champs, et tous les reptiles qui rampent sur la terre, et tous les hommes qui seront dans le pays; et les montagnes s'ébouleront, et les pics des rochers s'écrouleront, et toutes les murailles s'écrouleront jusqu'en terre;
21 Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga.
et contre lui sur toutes mes montagnes j'appellerai l'épée, dit le Seigneur, l'Éternel; ils croiseront l'épée l'un contre l'autre,
22 Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye.
et j'exécuterai mes jugements sur lui par la peste et le carnage; et d'une pluie d'inondation et des pierres de la grêle, de feu et de soufre, je le couvrirai, lui et tous ses bataillons, et les peuples nombreux qui seront avec lui.
23 Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’”
Et ainsi je manifesterai ma majesté et ma sainteté, et me révélerai aux yeux de beaucoup de nations, afin qu'elles sachent que je suis l'Éternel.

< Ezekieli 38 >