< Ezekieli 38 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
Og Herrens Ord kom til mig saaledes:
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu.
Du Menneskesøn! vend dit Ansigt imod Gog i Magogs Land, Fyrsten over Rosk, Mesek og Tubal, og spaa imod ham!
3 Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala.
Og sig: Saa siger den Herre, Herre: Se, jeg kommer imod dig, Gog, du Fyrste over Rosk, Mesek og Tubal!
4 Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola.
Og jeg vil vende dig om og lægge Kroge i dine Kæver, og jeg vil føre dig ud tillige med al din Hær, Heste og Ryttere, alle sammen klædte i fuld Pragt, en stor Skare med store Skjolde og smaa Skjolde, alle sammen øvede i at bruge Sværd,
5 Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo.
med dem tillige Perser, Morianer og Putæer, alle sammen med Skjold og Hjelm,
6 Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.
Gomer og alle hans Hære, Thogarmas Hus i det yderste Nord og alle dets Hære, ja, mange Folkeslag sammen med dig.
7 “‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo.
Vær beredt og hold dig rede, du og alle dine Skarer, som ere forsamlede om dig! og du skal tage Vare paa dem.
8 Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere.
Efter mange Dage skal du blive hjemsøgt, i de sidste Aar skal du komme til et Land, som er udfriet fra Sværdet og samlet ud fra mange Folkefærd, over Israels Bjerge, som stadigt have været øde; dette er nu udført fra Folkene, og de bo der alle sammen tryggelig.
9 Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.
Og du skal drage op, du skal komme som et Bulder, du skal være som en Sky til at skjule Landet, du og alle dine Hære og de mange Folkeslag, som ere med dig.
10 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa.
Saa siger den Herre, Herre: Og det skal ske paa denne Dag, at der skal opstige Ting i dit Hjerte, og at du skal optænke en ond Tanke;
11 Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo.
og du skal sige: Jeg vil drage op imod et Land med ubefæstede Byer; jeg vil komme over de rolige, som bo tryggelig, alle sammen bo de uden Mur og have hverken Portstænger eller Porte,
12 Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’
for at bytte Bytte og at røve Rov; — for at vende din Haand imod de øde Stæder, som nu ere beboede, og imod et Folk, som er sanket ud fra Hedningerne, og som forhverver sig Fæ og Gods, og som bor over Jordens Navle.
13 Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’”
Seba og Dedan og Købmænd fra Tharsis og alle dets unge Løver skulle sige til dig: Er du kommen for at bytte Bytte? har du samlet din Skare for at røve Rov, for at borttage Sølv og Guld, for at tage Fæ og Gods, for at bytte stort Bytte?
14 “Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka.
Derfor spaa, du Menneskesøn! og sig til Gog: Saa siger den Herre, Herre: Mon du ikke paa den Dag, naar mit Folk Israel bor tryggelig, skal faa det at vide?
15 Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu.
Og du skal komme fra dit Sted, fra det yderste Nord, du og de mange Folk, som ere med dig, alle sammen ridende paa Heste, en stor Skare og en mægtig Hær.
16 Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.
Og du skal drage op imod mit Folk Israel som en Sky til at skjule Landet; det skal ske i de sidste Dage, at jeg vil lade dig komme imod mit Land, paa det Hedningerne skulle kende mig, naar jeg helliggør mig paa dig for deres Øjne, o Gog!
17 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli.
Saa siger den Herre, Herre: Er du den, som jeg talte om i gamle Dage ved mine Tjenere, Profeterne i Israel, som spaaede i hine Dage, Aar efter Aar, at jeg vilde lade dig komme over dem?
18 Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.
Og det skal ske paa den Dag, ja, paa den Dag, da Gog kommer over Israels Land, siger den Herre, Herre, at min Vrede skal stige op i min Næse.
19 Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli.
Ogjeg har talt i min Nidkærhed, i min Vredes Ild: Sandelig, paa denne Dag skal der være en stor Rystelse i Israels Land.
20 Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi.
Og Fiskene i Havet og Fuglene under Himlene og de vilde Dyr paa Marken og alt Krybet, som kryber paa Jorden, og hvert Menneske, som er paa Jorden, skulle bæve for mit Ansigt, og Bjergene skulle omkastes og Taarnene falde, og hver Mur skal falde til Jorden.
21 Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga.
Og jeg vil kalde et Sværd frem imod ham hen over alle mine Bjerge, siger den Herre, Herre; den enes Sværd skal være imod den anden.
22 Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye.
Og jeg vil gaa i Rette med ham ved Pest og ved Blod; og en overskyllende Regn og Hagelstene, Ild og Svovl vil jeg lade regne ned over ham og over hans Hære og over de mange Folk, som ere med ham.
23 Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’”
Og jeg vil bevise mig stor og bevise mig hellig, og jeg vil give mig til Kende for mange Hedningers Øjne; og de skulle fornemme, at jeg er Herren.

< Ezekieli 38 >