< Ezekieli 38 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
I dođe mi riječ Jahvina:
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu.
“Sine čovječji, okreni lice ka Gogu, u zemlji Magogu, velikom knezu Mešeka i Tubala, prorokuj protiv njega.
3 Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala.
Reci: 'Ovako govori Jahve Gospod: Evo me na te, Gože, veliki kneže Mešeka i Tubala!
4 Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola.
Namamit ću te i metnut ću ti žvale u čeljusti, izvest ću tebe i svu tvoju vojsku - konje i konjanike, silno mnoštvo u potpunoj opremi - sve u oklopima i sa štitovima, sve vične maču.
5 Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo.
S njima je i Perzija, Etiopija i Put - svi sa štitovima i pod kacigama;
6 Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.
zatim Gomer i sve čete njegove, Bet Togarma s krajnjega sjevera i sve čete njezine - silan narod s tobom!
7 “‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo.
Dobro se spremi ti i sve mnoštvo što se oko tebe skupilo i stani mu na čelo!
8 Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere.
Poslije mnogo dana dobit ćeš zapovijed; poslije mnogo godina navalit ćeš na zemlju, izbavljenu od mača i skupljenu iz mojih naroda, na gore Izraelove, nekoć zadugo puste: otkako ih izvedoh iz naroda, svi spokojno žive.
9 Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.
Dići ćeš se, doći kao nevrijeme, kao oblak što prekrije zemlju, ti i tvoje čete, a s vama sila naroda!'
10 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa.
Ovako govori Jahve Gospod: 'U onaj će ti se dan misli rojiti u srcu i skovat ćeš zao naum.
11 Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo.
Reći ćeš: 'Hajde da se dignem na zemlju nebranjenu, da navalim na miran narod koji spokojno živi bez zidina i bez prijevornica i bez vrata:
12 Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’
pa da se plijena naplijenim i pljačke napljačkam - da ruku stavim na razvaline opet napučene i na narod iz narÄodÄa sakupljen, koji se bavi stadima i imanjem i živi u središtu zemlje.'
13 Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’”
Šeba, Dedan i trgovci taršiški i svi njihovi lavići pitat će te: 'Zar zato dolaziš plijeniti? I zar si radi pljačke toliku gomilu skupio da odneseš srebro i zlato, da otmeš stoku i imanje i da se plijena velikoga naplijeniš?'
14 “Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka.
Zato prorokuj, sine čovječji, i reci Gogu: 'Ovako govori Jahve Gospod: U onaj dan kad narod moj izraelski bude spokojno živio, ti ćeš se podići!
15 Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu.
Doći ćeš iz svoga sjedišta, s krajnjega sjevera, ti i s tobom mnogo naroda, sve samih konjanika, silno mnoštvo, golema vojska.
16 Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.
Navalit ćeš na Izraela, narod moj, kao oblak kad pokrije zemlju. U posljednje dane dovest ću te na svoju zemlju da me narodi upoznaju, kad na tebi, Gože, njima naočigled, pokažem svetost svoju.'
17 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli.
Ovako govori Jahve Gospod: 'Nisi li ti onaj o kome sam govorio, u davne dane, preko slugu svojih, proroka Izraelovih, koji u ono vrijeme prorokovaše da ću te na njih dovesti?
18 Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.
U onaj dan kad Gog navali na zemlju Izraelovu - riječ je Jahve Gospoda - gnjev će mi iz nosa planuti.
19 Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli.
U ljubomori svojoj i u ognju jarosti svoje odlučih: U onaj dan bit će silan potres u zemlji Izraelovoj.
20 Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi.
I trest će se poda mnom ribe morske i ptice nebeske, poljske zvijeri i gmazovi što gmižu po zemlji i svi ljudi što žive na njoj. Planine će se razvaliti, vrleti popadati i sve se zidine porušiti!
21 Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga.
I po svim svojim gorama pozvat ću na njega mač - riječ je Jahve Gospoda - s mačem će se brat na brata dići!
22 Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye.
Sudit ću mu kugom i krvlju. I spustit ću silan pljusak, i kamenje tÓuče, oganj i sumpor na nj, na njegove čete i na mnogi narod koji bude s njime.
23 Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’”
I uzveličat ću se, posvetiti i objaviti pred svim narodima, i znat će da sam ja Jahve.'

< Ezekieli 38 >