< Ezekieli 38 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
上主的話傳給我說:「
2 “Iwe mwana wa munthu, tembenukira kwa Gogi, wa ku dziko la Magogi, amene ali kalonga wamkulu wa mzinda wa Mesaki ndi Tubala. Umuyimbe mlandu.
人子,你面向哥格和瑪哥格地,即面向默舍克和突巴耳的最高領袖,講預言攻斥他,
3 Umuwuze mawu a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndikudana nawe, iwe Gogi, kalonga wamkulu wa ku Mesaki ndi Tubala.
說:吾主上主這樣說:默舍客和突巴耳的最高領袖,看,我要攻擊你,
4 Ndidzakuzunguza, ndidzakukola ndi mbedza mʼkamwa mwako. Ndidzakutulutsa iweyo pamodzi ndi gulu lako lonse la nkhondo, akavalo ako ndi okwerapo ake. Onse adzakhala atanyamula zida za nkhondo, zishango ndi malihawo ndipo malupanga awo adzakhala osolola.
我要用鉤子鉤住你的牙床,把你拖出來,使你帶領你的大軍、馬隊和騎兵出征,都是全副武裝,戴著盔甲和盾牌的大軍,都手持刀劍。
5 Pamodzi ndi iwowo, padzakhalanso ankhondo a ku Perisiya, ku Kusi, ndi ku Puti. Onsewa adzakhala atanyamula zishango ndi kuvala zipewa zankhondo.
還有波斯、雇士和普特人同他們聯盟,都帶著盾牌和銅盔。
6 Padzakhalanso Gomeri pamodzi ndi ankhondo ake onse ndiponso banja la Togarima ndi gulu lake lonse lankhondo lochokera kutali kumpoto. Padzakhaladi mitundu yambiri ya anthu pamodzi ndi iwe.
哥默爾及其隊伍,極北方的托加爾瑪家族及其隊伍,還有許多人民同你聯合。
7 “‘Konzekani! Mukhaledi okonzeka, iweyo pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo limene lakusonkhanira. Iweyo udzawatsogolera pokamenya nkhondo.
你和同你聯合的各種隊伍都要戒備武裝起來,好為我服務。
8 Pakapita masiku ambiri ndidzakuyitana. Zaka zikubwerazi ndidzakulowetsa mʼdziko limene lapulumuka ku nkhondo. Anthu ake anasonkhanitsidwa kuchokera ku mitundu ya anthu ambiri nʼkukakhazikika pa mapiri a Israeli amene kwa nthawi yayitali anali ngati chipululu. Anthu onsewa tsopano akukhala mwa mtendere.
多日之後,你要奉到命令;到末年,你要去攻擊那脫離兵災已復原的地方,那裏的居民是由各民族聚集起來的;你要去攻擊那久已荒涼的以色列山,那裏的居民是由各民族歸來,已安居在那裏。
9 Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse ndiponso mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe mudzabwera ngati mphepo yamkuntho. Mudzaphimba dziko lonse ngati mitambo.
你和你的大軍,以及同你聯合的各種隊伍都一起上去,有如狂風來臨,有如濃雲遮地。
10 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limenelo mu mtima mwako mudzabwera maganizo ofuna kukonzekera kuchita zoyipa.
吾主上主這樣說:到那一天,你要心起惡念,籌劃一個惡計。
11 Iwe udzanena kuti, ‘Ndikukathira nkhondo dziko la midzi yopanda mipanda; ndikathira nkhondo anthu okhala mwamtendere, anthu amene satchinjirizidwa ndi mipanda, zipata kapena mipiringidzo.
你要想:我要進攻不設防的地方,進攻安居無憂的人民;他們住的地方沒有圍牆,沒有門閂,也沒有門。
12 Ndipita kukalanda chuma chawo ndi kukafunkha zinthu zawo. Ndidzalimbana ndi midzi imene kale inali mabwinja. Ndikathira nkhondo anthu amene anasonkhanitsidwa kuchokera kwa anthu a mitundu ina. Iwowa ali ndi ziweto zambiri, katundu wochuluka ndiponso amakhala pakatikati pa dziko lapansi.’
我要去搶奪劫掠,下手攻擊已為人居住的廢墟,攻擊那由各民族匯集而來,已有牲畜財物,已安居在地中心的人民。
13 Anthu a ku Seba, a ku Dedani ndiponso amalonda a ku Tarisisi pamodzi ndi midzi yake yonse adzakufunsa kuti, ‘Kodi wabwera kudzafunkha? Kodi wasonkhanitsa gulu lako la nkhondo kudzalanda chuma, kudzatenga siliva ndi golide, ziweto ndi katundu kuti zikhale zofunkha zochuluka?’”
舍巴、德丹、塔爾史士的商人和客商都問你說:你來豈不是為了搶奪﹖集合你的聯軍豈不是為了劫掠,奪去金銀,帶走牲畜和財物,拿去大批掠物﹖
14 “Nʼchifukwa chake, iwe mwana wa munthu, nenera ndipo uwuze Gogi kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene anthu anga adzakhala pa mtendere, iwe udzanyamuka.
人子,為此你要講預言,向哥格說:吾主上主這樣說:當我的百姓以色列安居的那一天,你不是就起了身,
15 Udzabwera kuchokera ku dziko lako kutali kumpoto, iwe pamodzi ndi mitundu yambiri ya anthu imene ili nawe, onse okwera akavalo, gulu lankhondo lalikulu ndi lamphamvu.
離開你的住處,由極北之地而來,率領許多民族都騎著馬,實在是一支龐大的聯軍,極強大的隊伍,
16 Udzabwera kudzalimbana ndi anthu anga Aisraeli ngati mtambo wophimba dziko. Masiku amenewo, iwe Gogi, ndidzabwera nawe kuti ulimbane ndi dziko langa, kuti anthu a mitundu ina andidziwe Ine, pamene ndidzaonetsa kuyera kwanga pa zimene ndidzakuchite iweyo.
上來進攻我的百姓以色列,有如密雲遮地一般﹖哥格! 到末日我要領你來攻打我的地方,為的是當我在異民眼前,在你身上顯聖時,叫他們認識我。
17 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi iwe si amene ndinayankhula za iwe masiku amakedzana kudzera mwa atumiki anga aneneri a Israeli? Pa zaka zambiri iwo ankalengeza kuti ndidzawutsa iwe kuti udzalimbane ndi Israeli.
吾主上主這樣說:你就是我昔日藉我的僕人以色列的先知在那些歲月中所預言的:我要領你進攻他們的那一位。
18 Zimene chidzachitika pa tsiku limenelo ndi izi: Gogi akadzathira nkhondo dziko la Israeli, mkwiyo wanga woopsa udzayaka. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.
到哥格進攻以色列的那一天──吾主上主的斷語──我的怒氣要從我的鼻孔發出;
19 Chifukwa cha mkwiyo ndi ukali wanga woyakawo Ine ndikunenetsa kuti pa nthawi imeneyo padzakhala chivomerezi chachikulu mʼdziko la Israeli.
我要在妒忌怒火中說:的確,到那一天,以色列地必要發生大地震;
20 Nsomba za mʼnyanja, mbalame zamumlengalenga, zirombo zakuthengo, cholengedwa chilichonse chimene chimakwawa pansi, ndiponso anthu onse okhala pa dziko lapansi, adzanjenjemera pamaso panga. Mapiri adzangʼambika, malo okwera kwambiri adzagumuka ndipo khoma lililonse lidzagwa pansi.
海裏的魚,空中的飛鳥,田間的走獸,地上所有的爬蟲,地面上所有的人,都要在我面前戰慄;山要崩裂,懸崖要塌陷,所有牆垣要傾倒地上。
21 Ndidzawutsira Gogi nkhondo kuchokera ku mapiri anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova. Anthu a Gogiyo adzaphana okhaokha ndi malupanga.
我要召刀劍到我的各山上來攻擊他──吾主上主的斷語──人們要用刀劍互相殘殺。
22 Ine ndidzamulanga ndi mliri ndi imfa. Ndidzagwetsa mvula yoopsa ya matalala, ndiponso sulufule ndi miyala ya moto pa iye ndi pa asilikali ake ndiponso pa mitundu yambiri ya anthu imene ili naye.
我要以瘟疫和殘殺懲罰他,且要在他和他的軍隊以及同他聯合的眾民身上,降下暴雨、冰雹、火燄和硫磺。
23 Motero ndidzadzionetsa kuti ndine wamphamvu ndi woyera. Ndiponso ndidzadziwika pamaso pa anthu a mitundu ina yambiri. Momwemo adzadziwadi kuti Ine ndine Yehova.’”
如此,我要顯示我的偉大和神聖,且在眾民眼前顯示我自己,使他們承認我是上主。」

< Ezekieli 38 >