< Ezekieli 37 >
1 Dzanja la Yehova linali pa ine, ndipo Mzimu wa Yehova unandinyamula nʼkukandikhazika pakati pa chigwa. Chigwacho chinali chodzaza ndi mafupa.
Була́ надо мною Господня рука, і Дух Госпо́дній ви́провадив мене, і спинив мене серед долини, а вона — повна кісто́к!
2 Yehova anandiyendetsa uku ndi uku pakati pa mafupawo. Mafupawo anali ochuluka kwambiri mʼchigwa monsemo ndipo anali owuma kwambiri.
І Він обвів мене біля них навко́ло, аж ось їх дуже багато на пове́рхні долини, і ось вони стали дуже сухі!
3 Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi mafupa amenewa angakhalenso ndi moyo?” Ndinayankha kuti, “Inu Ambuye Yehova, Inuyo nokha ndiye mukudziwa.”
І сказав Він мені: „Сину лю́дський, чи оживу́ть оці ко́сті?“А я відказав: „Господи Боже, — Ти знаєш!“
4 Pamenepo anandiwuza kuti, “Lengeza kwa mafupa amenewa ndi kuwawuza kuti amve mawu a Ine Yehova!
І сказав Він мені: „Пророку́й про ці кості, та й скажеш до них: Сухі ко́сті, послухайте слова Господнього!
5 Uwawuze kuti zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kwa mafupa ndi izi: Ndidzawuzira mpweya mwa inu, ndipo mudzakhalanso ndi moyo.
Так говорить Господь Бог до цих кісто́к: Ось Я введу́ у вас духа — і ви оживе́те!
6 Ndidzakupatsani mitsempha ndi mnofu. Ndiponso ndidzakukutani ndi khungu. Pambuyo pake ndidzawuzira mpweya mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
І дам на вас жи́ли, і ви́росте на вас тіло, і простягну́ на вас шкіру, і дам у вас духа, — і ви оживе́те. І пізна́єте ви, що Я — Госпо́дь!“
7 Ndipo ndinanenera monga anandilamulira. Ndipo pamene ndinkanenera, ndinamva gobedegobede, ndipo mafupa aja anayamba kulumikizana, fupa ku fupa linzake.
І пророкував я, як наказано. І зня́вся шум, коли я пророкува́в, і ось гу́ркіт, а ко́сті зближа́лися, кістка до кістки своєї.
8 Ine ndinayangʼana, ndipo mitsempha ndi mnofu zinabwera pa mafupawo ndipo khungu linaphimba pamwamba pake, koma munalibe mpweya mwa iwo.
І побачив я, аж ось на них жи́ли, і виросло тіло, і була натя́гнена на них шкіра зве́рху, та духа не було в них.
9 Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Nenera kwa mpweya, nenera iwe mwana wa munthu ndi kuwuza mpweya mawu a Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Bwera kuno iwe mpweya. Bwera kuchokera ku mbali zonse zinayi ndi kudzawuzira anthu ophedwawa kuti akhalenso ndi moyo.’
І сказав Він мені: „Пророкуй до духа, пророкуй, сину лю́дський, та й скажеш до духа: Так говорить Господь Бог: Прилинь, духу, з чотирьох вітрі́в, і дихни́ на цих забитих, — і нехай оживу́ть!“
10 Choncho ndinanenera monga anandilamulira ndipo mpweya unalowa mwa iwo; apo anthu akufawo anakhala ndi moyo, nayimirira ndipo linali gulu lalikulu lankhondo.”
І я пророкував, як Він наказав був мені, — і ввійшов у них дух, і вони ожили́, і постава́ли на ноги свої, — ві́йсько дуже-дуже велике!
11 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, mafupa awa ndi nyumba yonse ya Israeli. Iwo amanena kuti, ‘Mafupa athu awuma ndipo chiyembekezo chathu chatayika, ife tawonongeka!’
І сказав Він мені: „Сину лю́дський, ці кості — вони ввесь Ізраїлів дім. Ось вони кажуть: Повисиха́ли наші кості, і заги́нула наша надія, нам кіне́ць!
12 Nʼchifukwa chake nenera ndi kuwawuza kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu anthu anga, ndidzafukula manda anu, ndipo ndidzakutulutsanimo ndi kukubwezerani ku dziko la Israeli.
Тому́ пророкуй та й скажеш до них: Так говорить Господь Бог: Ось Я повідчиня́ю ваші гроби́, і позво́джу вас із ваших гробі́в, мій наро́де, і введу́ вас до Ізраїлевої землі!
13 Ndipo inu, anthu anga, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzafukula manda anu ndikukutulutsanimo.
І пізнаєте ви, що Я Госпо́дь, коли Я повідчиня́ю ваші гроби́, і коли позво́джу вас із ваших гробі́в, Мій наро́де!
14 Ine ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pambuyo pake ndidzakulowetsani mʼdziko lanulanu. Choncho mudzadziwa kuti Ambuye Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichitadi. Ndikutero Ine Yehova!’”
І дам Я в вас Свого Духа, — і ви оживе́те, і вміщу́ вас на вашій землі, і пізна́єте ви, що Я, Госпо́дь, сказав це й зробив, говорить Госпо́дь!“
15 Yehova anandiyankhula kuti:
І було́ мені слово Господнє таке:
16 “Iwe mwana wa munthu, tenga ndodo ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Yuda ndi Aisraeli oyanjana nawo.’ Utengenso ndodo ina ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Efereimu, ndiye kuti fuko la Yosefe ndi Aisraeli onse oyanjana nawo.’
„А ти, сину лю́дський, візьми́ собі один кусок де́рева, і напиши на ньому: „Юді та синам Ізраїля, його дру́зям“. І візьми ще один кусок дерева, і напиши на ньому: „Йо́сипові дерево Єфрема та всьому домові Ізраїля, дру́зям його“.
17 Ulumikize ndodo ziwirizi kuti zikhale ndodo imodzi mʼdzanja lako.
І зблизь їх собі одне до о́дного на один кусок дерева, — і вони стануть за одне́ в твоїй руці!
18 “Anthu a mtundu wako akadzakufunsa tanthauzo la zimenezi
І як скажуть до тебе сини твого наро́ду, говорячи: Чи не оголо́сиш нам, що́ це в те́бе таке?
19 iwe udzawawuze mawu awa a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndidzatenga ndodo ya Yosefe imene ili mʼdzanja la Efereimu, ndi ya mafuko a Aisraeli oyanjana naye, ndi kuyilumikiza ku ndodo ya Yuda, kuti zikhale ndodo imodzi, ndipo zidzakhaladi ndodo imodzi mʼdzanja langa!’
то скажи їм: Так говорить Госпо́дь Бог: Ось Я візьму́ дерево Йо́сипа, що в Єфремовій руці, та племе́на Ізраїлеві, його дру́зів, і дам на нього дерево Юди, і вчиню́ їх за одне дерево, — і стануть вони одним у Моїй руці!
20 Ndodo ziwiri zimene udzalembepozo zikadzakhala mʼmanja mwako pamaso pa anthu onse,
І будуть ці дере́ва, що напишеш на них, у руці твоїй на їхніх оча́х.
21 udzawawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzawachotsa Aisraeli pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapita ku ukapolo. Ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mbali zonse ndi kubwera nawo ku dziko lawolawo.
І скажи до них: Так говорить Госпо́дь Бог: Ось Я візьму́ Ізраїлевих синів з-посеред наро́дів, куди вони пішли, і позбира́ю їх знавко́ла, і введу́ їх до їхньої землі.
22 Ndidzawasandutsa mtundu umodzi mʼdzikomo, pa mapiri a Israeli. Padzakhala mfumu imodzi yowalamulira, ndipo sadzakhalanso mitundu iwiri kapena kugawikana maufumu awiri.
І зроблю́ їх за один наро́д у краї на Ізраїлевих гора́х, і бу́де для всіх них один цар за царя, і не бу́дуть уже двома́ наро́дами, і не бу́дуть уже більш поді́лені на двоє царств.
23 Sadzadziyipitsanso ndi mafano awo, kapena ndi zinthu zawo zonyansa, kapenanso ndi ntchito zawo zoyipa zilizonse. Ndidzawapulumutsa ku machimo awo onse ndi kuwayeretsa. Choncho adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
І більш не будуть вони занечи́щуватися своїми бовва́нами й гидо́тами своїми та всіма́ своїми пере́ступами, спасу́ їх зо всіх їхніх осе́ль, де вони гріши́ли, й очи́щу їх. І будуть вони мені наро́дом, а Я буду їм Богом!
24 “‘Mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu yawo, motero onsewa adzakhala ndi mʼbusa mmodzi. Iwo adzatsatira malamulo anga ndipo adzasamalira kusunga malangizo anga.
А раб Мій Давид буде царем над ними, і один па́стир буде для всіх них, і постановами Моїми вони будуть ходити, а устави Мої будуть стерегти́ й вико́нувати їх.
25 Iwo adzakhala mʼdziko limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo, dziko limene makolo anu ankakhalamo. Iwo ndi ana awo pamodzi ndi zidzukulu zawo adzakhala kumeneko ndipo Davide adzakhala mfumu yawo kwa muyaya.
І ося́дуть вони на тій землі, яку Я дав був Моєму рабові Яковові, що сиділи на ній їхні батьки́, і ося́дуть на ній вони та їхні сини, та сини синів їхніх аж навіки, а Мій раб Давид буде їм кня́зем навіки!
26 Ndidzachita nawo pangano lamtendere; lidzakhala pangano lamuyaya. Ndidzawakhazikitsa ndi kuwachulukitsa, ndipo ndidzayika malo anga opatulika pakati pawo kwamuyaya.
І складу́ з ними заповіта миру, — це буде вічний запові́т із ними. І зміцню́ їх, і намно́жу їх, і дам Свою святиню серед них на віки!
27 Nyumba yanga yokhalamo idzakhala pakati pawo; Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
І буде місце Мого пробува́ння над ними, і Я буду їм Богом, а вони Мені бу́дуть наро́дом.
28 Pamenepo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti Ine Yehova ndiye amene ndimasandutsa Israeli kukhala woyera, pamene malo anga opatulika adzakhala pakati pawo kwamuyaya!’”
І пізнають ці наро́ди, що Я — Госпо́дь, що освятив Ізраїля, коли буде Моя святиня серед них навіки!“