< Ezekieli 37 >

1 Dzanja la Yehova linali pa ine, ndipo Mzimu wa Yehova unandinyamula nʼkukandikhazika pakati pa chigwa. Chigwacho chinali chodzaza ndi mafupa.
KAU mai la ka lima o Iehova maluna o'u, a lawe ae ia'u iwaho ma ka Uhane o Iehova, a hooku iho ia'u ilalo mawaenakonu o ka papu, ua paapu ia i na iwi.
2 Yehova anandiyendetsa uku ndi uku pakati pa mafupawo. Mafupawo anali ochuluka kwambiri mʼchigwa monsemo ndipo anali owuma kwambiri.
A hoohele ia'u e maalo ma ia mau mea a puni; aia hoi he nui wale o lakou ma ka papu, aia hoi, ua maloo loa lakou.
3 Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi mafupa amenewa angakhalenso ndi moyo?” Ndinayankha kuti, “Inu Ambuye Yehova, Inuyo nokha ndiye mukudziwa.”
A ninau mai la oia ia'u, E ke keiki a ke kanaka, e hiki anei i keia mau iwi ke ola? I aku la hoi au, E Iehova ka Haku, o oe no ka i ike.
4 Pamenepo anandiwuza kuti, “Lengeza kwa mafupa amenewa ndi kuwawuza kuti amve mawu a Ine Yehova!
Olelo hou mai la oia ia'u, E wanaua oe i keia mau iwi, a e olelo aku ia lakou, E na iwi maloo, e hoolohe i ka olelo a Iehova.
5 Uwawuze kuti zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kwa mafupa ndi izi: Ndidzawuzira mpweya mwa inu, ndipo mudzakhalanso ndi moyo.
Ke i mai nei Iehova ka Haku penei i keia mau iwi; Eia hoi, e hookomo au i ke ea iloko o oukou, a e ola na oukou.
6 Ndidzakupatsani mitsempha ndi mnofu. Ndiponso ndidzakukutani ndi khungu. Pambuyo pake ndidzawuzira mpweya mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
A e kau iho au i na olona maluna o oukou, a lawe mai au i ka io maluna o oukou, a e uhi ia oukou i ka ili, a e hookomo ae au i ke ea iloko o oukou, a e ola oukou; a e ike no oukou owau no Iehova ka Haku.
7 Ndipo ndinanenera monga anandilamulira. Ndipo pamene ndinkanenera, ndinamva gobedegobede, ndipo mafupa aja anayamba kulumikizana, fupa ku fupa linzake.
A wanana aku la au e like me au i kauohaia mai ai: a i kuu wanana ana, kawewe ae la, aia hoi, he nauwe ana, a hui ae na iwi, ka iwi me kona iwi.
8 Ine ndinayangʼana, ndipo mitsempha ndi mnofu zinabwera pa mafupawo ndipo khungu linaphimba pamwamba pake, koma munalibe mpweya mwa iwo.
A i ko'u nana ana'ku, aia hoi, pii mai no na olona a me ka io maluna o lakou, a uhi mai ka ili ia lakou maluna; aka, aole ea iloko o lakou.
9 Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Nenera kwa mpweya, nenera iwe mwana wa munthu ndi kuwuza mpweya mawu a Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Bwera kuno iwe mpweya. Bwera kuchokera ku mbali zonse zinayi ndi kudzawuzira anthu ophedwawa kuti akhalenso ndi moyo.’
Alaila olelo mai la oia ia'u, E wanana oe i ka makani, e wanana, e ke keiki a ke kanaka, a e olelo i ka makani, ke i mai nei Iehova ka Haku, E hele mai, e ka makani, mai na makani eha mai, a e ha iho maluna o keia poe make i ka pepehiia, i ola lakou.
10 Choncho ndinanenera monga anandilamulira ndipo mpweya unalowa mwa iwo; apo anthu akufawo anakhala ndi moyo, nayimirira ndipo linali gulu lalikulu lankhondo.”
A wanana aku la au e like me kana i kauoha mai ai ia'u, a komo mai ke ea iloko o lakou, a ola ae la lakou, a ku ae la lakou iluna ma ko lakou mau wawae, he mau koa lehulehu loa.
11 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, mafupa awa ndi nyumba yonse ya Israeli. Iwo amanena kuti, ‘Mafupa athu awuma ndipo chiyembekezo chathu chatayika, ife tawonongeka!’
Alaila olelo mai la oia ia'u, E ke keiki a ke kanaka, o keia poe iwi, o ka ohana a pau ia a Iseraela; aia hoi, ke olelo nei lakou, Uamaloo ko kakou mau iwi, a ua lilo ko kakou mea i manaolana ai; ua oki loa ia'e nei kakou.
12 Nʼchifukwa chake nenera ndi kuwawuza kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu anthu anga, ndidzafukula manda anu, ndipo ndidzakutulutsanimo ndi kukubwezerani ku dziko la Israeli.
Nolaila e wanana aku, a e olelo aku ia lakou, Ke i mai nei Iehova ka Haku, Aia hoi, e ko'u poe kanaka, e huai ae au i ko oukou mau luakupapau, a e hoopii mai au ia oukou mai loko mai o ko oukou mau luakupapau, a e lawe ae ia oukou i ka aina o ka Iseraela.
13 Ndipo inu, anthu anga, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzafukula manda anu ndikukutulutsanimo.
Alaila e ike oukou owau no Iehova, i ka wa i huai ai au i ko oukou mau luakupapau, e ko'u poe kanaka, a lawe mai hoi au ia oukou mai loko mai o ko oukou mau luakupapau;
14 Ine ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pambuyo pake ndidzakulowetsani mʼdziko lanulanu. Choncho mudzadziwa kuti Ambuye Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichitadi. Ndikutero Ine Yehova!’”
A hookomo i kuu Uhane iloko o oukou, a e ola oukou, a e hoonoho au ia oukou ma ko oukou aina; alaila e ike oukou owau no Iehova ka i olelo a e hana aku hoi, wahi a Iehova.
15 Yehova anandiyankhula kuti:
Hiki hou mai la ka olelo a Iehova ia'u, i mai la,
16 “Iwe mwana wa munthu, tenga ndodo ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Yuda ndi Aisraeli oyanjana nawo.’ Utengenso ndodo ina ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Efereimu, ndiye kuti fuko la Yosefe ndi Aisraeli onse oyanjana nawo.’
A o oe, e ke keiki a ke kanaka, e lawe oe i ka laau nou, a e kakau iho maluna iho ona, No Iuda, a no na mamo a Iseraela kona mau hoa; alaila e lawe i kekahi laau, a e kakau iho maluna ona, No Iosepa, ka laau o ka Eperaima, a no ka ohana a pau a Iseraela kona mau hoa.
17 Ulumikize ndodo ziwirizi kuti zikhale ndodo imodzi mʼdzanja lako.
A e hookui ia laua i kekahi i kekahi i laau hookahi; a e lilo laua i hookahi iloko o kou lima.
18 “Anthu a mtundu wako akadzakufunsa tanthauzo la zimenezi
Aia olelo na keiki a kanaka ia oe, e ninau ana, Aole anei oe e hoike mai ia makou i kou ma keia mau mea?
19 iwe udzawawuze mawu awa a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndidzatenga ndodo ya Yosefe imene ili mʼdzanja la Efereimu, ndi ya mafuko a Aisraeli oyanjana naye, ndi kuyilumikiza ku ndodo ya Yuda, kuti zikhale ndodo imodzi, ndipo zidzakhaladi ndodo imodzi mʼdzanja langa!’
E olelo aku oe ia lakou, Ke i mai nei Iehova ka Haku, penei; Aia hoi, e lawe au i ka laau o Iosepa, ka mea iloko o ka lima o Eperaima, a me na ohana a Iseraela kona mau hoa, a e hui aku au ia lakou me ia, me ka laau hoi o Iuda, a e hoolilo au ia lakou i laau hookahi, a lilo lakou i hookahi iloko o ko'u lima.
20 Ndodo ziwiri zimene udzalembepozo zikadzakhala mʼmanja mwako pamaso pa anthu onse,
A e waiho no na laau au e kakau ai iloko o kou lima imua o ko lakou alo.
21 udzawawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzawachotsa Aisraeli pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapita ku ukapolo. Ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mbali zonse ndi kubwera nawo ku dziko lawolawo.
A e olelo aku oe ia lakou, Ke i mai nei Iehova ka Haku, penei; Aia hoi, e lawe mai au i ka poe mamo a Iseraela mai waena mai o na lahuikanaka kahi i hele aku ai lakou, a e houluulu au ia lakou ma kela aoao keia aoao, a e lawe mai ia lakou iloko o ko lakou aina.
22 Ndidzawasandutsa mtundu umodzi mʼdzikomo, pa mapiri a Israeli. Padzakhala mfumu imodzi yowalamulira, ndipo sadzakhalanso mitundu iwiri kapena kugawikana maufumu awiri.
A e hoolilo au ia lakou i lahuikanaka hookahi ma ka aina maluna o na mauna o ka Iseraela; a no lakou a pau he alii hookahi no; aole alua lahuikanaka hou aku lakou, aole loa hoi e mokuahana hou aku i elua aupuni.
23 Sadzadziyipitsanso ndi mafano awo, kapena ndi zinthu zawo zonyansa, kapenanso ndi ntchito zawo zoyipa zilizonse. Ndidzawapulumutsa ku machimo awo onse ndi kuwayeretsa. Choncho adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
Aole hoi e hoohaumia hou aku lakou ia lakou iho me ko lakou mau akuakii, aole hoi me ko lakou mau mea inainaia, aole hoi me kahi o ka lakou lawehala ana: aka, a e hoola au ia lakou mai loko mai o ko lakou mau wahi i noho ai, i hana hewa ai lakou, a e hoomaemae au ia lakou: a e lilo lakou i kanaka no'u, a owau hoi i Akua no lakou.
24 “‘Mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu yawo, motero onsewa adzakhala ndi mʼbusa mmodzi. Iwo adzatsatira malamulo anga ndipo adzasamalira kusunga malangizo anga.
A e lilo ka'u kauwa o Davida i alii maluna o lakou, a no lakou a pau he kahuhipa hookahi; e hele hoi lakou ma ko'u mau kanawai, a malama hoi lakou i ka'u mau kauoha, a e hana hoi malaila.
25 Iwo adzakhala mʼdziko limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo, dziko limene makolo anu ankakhalamo. Iwo ndi ana awo pamodzi ndi zidzukulu zawo adzakhala kumeneko ndipo Davide adzakhala mfumu yawo kwa muyaya.
A e noho lakou ma ka aina a'u i haawi aku ai i kuu kauwa ia Iakoba, kahi i noho ai ko oukou mau makua; a e noho lakou malaila, o lakou, a me ka lakou poe keiki, a me ka poe keiki a ka lakou poe keiki a mau loa aku; a e mau ana no ko ka'u kauwa ko Davida alii ana no lakou.
26 Ndidzachita nawo pangano lamtendere; lidzakhala pangano lamuyaya. Ndidzawakhazikitsa ndi kuwachulukitsa, ndipo ndidzayika malo anga opatulika pakati pawo kwamuyaya.
A e hana au i ka berita hoomalu me lakou, e lilo ia i berita mau loa me lakou; a e hoonoho au ia lakou, a e hoonui au ia lakou, a e hoonoho au i kuu wahi hoano iwaena o lakou a mau loa.
27 Nyumba yanga yokhalamo idzakhala pakati pawo; Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
A o ko'u halelewa kekahi me lakou; a owau auanei ko lakou Akua, a o lakou hoi ko'u poe kanaka.
28 Pamenepo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti Ine Yehova ndiye amene ndimasandutsa Israeli kukhala woyera, pamene malo anga opatulika adzakhala pakati pawo kwamuyaya!’”
A e ike hoi na lahuikanaka, owau o Iehova ka i hoomaemae i ka Iseraela, i ka mau loa ana o ko'u wahi hoano iwaenakonu o lakou.

< Ezekieli 37 >