< Ezekieli 37 >

1 Dzanja la Yehova linali pa ine, ndipo Mzimu wa Yehova unandinyamula nʼkukandikhazika pakati pa chigwa. Chigwacho chinali chodzaza ndi mafupa.
La main de l'Eternel fut sur moi, et l'Eternel me fit sortir en esprit, et me posa au milieu d'une campagne qui était pleine d'os.
2 Yehova anandiyendetsa uku ndi uku pakati pa mafupawo. Mafupawo anali ochuluka kwambiri mʼchigwa monsemo ndipo anali owuma kwambiri.
Et il me fit passer auprès d'eux tout à l'environ, et voici, ils étaient en fort grand nombre sur le dessus de cette campagne, et étaient fort secs.
3 Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi mafupa amenewa angakhalenso ndi moyo?” Ndinayankha kuti, “Inu Ambuye Yehova, Inuyo nokha ndiye mukudziwa.”
Puis il me dit: fils d'homme, ces os pourraient-ils bien revivre? Et je répondis: Seigneur Eternel, tu le sais.
4 Pamenepo anandiwuza kuti, “Lengeza kwa mafupa amenewa ndi kuwawuza kuti amve mawu a Ine Yehova!
Alors il me dit: prophétise sur ces os, et leur dis: os secs, écoutez la parole de l'Eternel.
5 Uwawuze kuti zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kwa mafupa ndi izi: Ndidzawuzira mpweya mwa inu, ndipo mudzakhalanso ndi moyo.
Ainsi a dit le Seigneur l'Eternel à ces os: voici, je m'en vais faire entrer l'esprit en vous, et vous revivrez.
6 Ndidzakupatsani mitsempha ndi mnofu. Ndiponso ndidzakukutani ndi khungu. Pambuyo pake ndidzawuzira mpweya mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
Et je mettrai des nerfs sur vous, et je ferai croître de la chair sur vous, et j'étendrai la peau sur vous; puis je remettrai l'esprit en vous, et vous revivrez; et vous saurez que je suis l'Eternel.
7 Ndipo ndinanenera monga anandilamulira. Ndipo pamene ndinkanenera, ndinamva gobedegobede, ndipo mafupa aja anayamba kulumikizana, fupa ku fupa linzake.
Alors je prophétisai selon qu'il m'avait été commandé, et sitôt que j'eus prophétisé il se fit un son, et voici, il se fit un mouvement, et ces os s'approchèrent l'un de l'autre.
8 Ine ndinayangʼana, ndipo mitsempha ndi mnofu zinabwera pa mafupawo ndipo khungu linaphimba pamwamba pake, koma munalibe mpweya mwa iwo.
Puis je regardai, et voici, il vint des nerfs sur eux, et il y crût de la chair, et la peau y fut étendue par dessus; mais l'esprit n'y était point.
9 Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Nenera kwa mpweya, nenera iwe mwana wa munthu ndi kuwuza mpweya mawu a Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Bwera kuno iwe mpweya. Bwera kuchokera ku mbali zonse zinayi ndi kudzawuzira anthu ophedwawa kuti akhalenso ndi moyo.’
Alors il me dit: prophétise à l'esprit, prophétise, fils d'homme, et dis à l'esprit: ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: esprit, viens des quatre vents, et souffle sur ces morts, et qu'ils revivent.
10 Choncho ndinanenera monga anandilamulira ndipo mpweya unalowa mwa iwo; apo anthu akufawo anakhala ndi moyo, nayimirira ndipo linali gulu lalikulu lankhondo.”
Je prophétisai donc comme il m'avait commandé, et l'esprit entra en eux, et ils revécurent, et se tinrent sur leurs pieds; et ce fut une armée extrêmement grande.
11 Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, mafupa awa ndi nyumba yonse ya Israeli. Iwo amanena kuti, ‘Mafupa athu awuma ndipo chiyembekezo chathu chatayika, ife tawonongeka!’
Alors il me dit: fils d'homme, ces os sont toute la maison d'Israël; voici, ils disent: nos os sont devenus secs, et notre attente est perdue, c'en est fait de nous.
12 Nʼchifukwa chake nenera ndi kuwawuza kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu anthu anga, ndidzafukula manda anu, ndipo ndidzakutulutsanimo ndi kukubwezerani ku dziko la Israeli.
C'est pourquoi prophétise, et leur dis: ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: mon peuple, voici, je m'en vais ouvrir vos sépulcres, et je vous tirerai hors de vos sépulcres, et vous ferai rentrer en la terre d'Israël.
13 Ndipo inu, anthu anga, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzafukula manda anu ndikukutulutsanimo.
Et vous, mon peuple, vous saurez que je suis l'Eternel quand j'aurai ouvert vos sépulcres, et que je vous aurai tirés hors de vos sépulcres.
14 Ine ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pambuyo pake ndidzakulowetsani mʼdziko lanulanu. Choncho mudzadziwa kuti Ambuye Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichitadi. Ndikutero Ine Yehova!’”
Et je mettrai mon esprit en vous, et vous revivrez, et je vous placerai sur votre terre; et vous saurez que moi l'Eternel j'aurai parlé, et que je l'aurai fait, dit l'Eternel.
15 Yehova anandiyankhula kuti:
Puis la parole de l'Eternel me fut [adressée], en disant:
16 “Iwe mwana wa munthu, tenga ndodo ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Yuda ndi Aisraeli oyanjana nawo.’ Utengenso ndodo ina ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Efereimu, ndiye kuti fuko la Yosefe ndi Aisraeli onse oyanjana nawo.’
Et toi, fils d'homme, prends un bois, et écris dessus: pour Juda, et pour les enfants d'Israël ses compagnons; prends encore un autre bois, et écris dessus: le bois d'Ephraïm et de toute la maison d'Israël ses compagnons, pour Joseph.
17 Ulumikize ndodo ziwirizi kuti zikhale ndodo imodzi mʼdzanja lako.
Puis tu les joindras l'un à l'autre pour ne former qu'un même bois, et ils seront unis dans ta main.
18 “Anthu a mtundu wako akadzakufunsa tanthauzo la zimenezi
Et quand les enfants de ton peuple demanderont, en disant: ne nous déclareras-tu pas ce que tu veux dire par ces choses?
19 iwe udzawawuze mawu awa a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndidzatenga ndodo ya Yosefe imene ili mʼdzanja la Efereimu, ndi ya mafuko a Aisraeli oyanjana naye, ndi kuyilumikiza ku ndodo ya Yuda, kuti zikhale ndodo imodzi, ndipo zidzakhaladi ndodo imodzi mʼdzanja langa!’
Dis-leur: ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: voici, je m'en vais prendre le bois de Joseph qui est en la main d'Ephraïm, et des Tribus d'Israël ses compagnons, et je les mettrai sur celui-ci, savoir sur le bois de Juda; et je les ferai être un seul bois; et ils ne seront qu'un seul bois en ma main.
20 Ndodo ziwiri zimene udzalembepozo zikadzakhala mʼmanja mwako pamaso pa anthu onse,
Ainsi les bois sur lesquels tu auras écrit seront en ta main, eux le voyant.
21 udzawawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzawachotsa Aisraeli pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapita ku ukapolo. Ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mbali zonse ndi kubwera nawo ku dziko lawolawo.
Et dis-leur: ainsi a dit le Seigneur l'Eternel: voici, je m'en vais prendre les enfants d'Israël d'entre les nations parmi lesquelles ils sont allés, je les rassemblerai de toutes parts, et je les ferai rentrer en leur terre.
22 Ndidzawasandutsa mtundu umodzi mʼdzikomo, pa mapiri a Israeli. Padzakhala mfumu imodzi yowalamulira, ndipo sadzakhalanso mitundu iwiri kapena kugawikana maufumu awiri.
Et je ferai qu'ils seront une seule nation dans le pays, sur les montagnes d'Israël; ils n'auront tous qu'un Roi pour leur Roi, ils ne seront plus deux nations, et ils ne seront plus divisés en deux Royaumes.
23 Sadzadziyipitsanso ndi mafano awo, kapena ndi zinthu zawo zonyansa, kapenanso ndi ntchito zawo zoyipa zilizonse. Ndidzawapulumutsa ku machimo awo onse ndi kuwayeretsa. Choncho adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
Et ils ne se souilleront plus par leurs idoles, ni par leurs infamies, ni par tous leurs crimes, et je les retirerai de toutes leurs demeures dans lesquelles ils ont péché, et je les purifierai; et ils seront mon peuple, et je serai leur Dieu.
24 “‘Mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu yawo, motero onsewa adzakhala ndi mʼbusa mmodzi. Iwo adzatsatira malamulo anga ndipo adzasamalira kusunga malangizo anga.
Et David mon serviteur sera leur Roi, et ils auront tous un seul Pasteur; et ils marcheront dans mes ordonnances, ils garderont mes statuts, et les feront.
25 Iwo adzakhala mʼdziko limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo, dziko limene makolo anu ankakhalamo. Iwo ndi ana awo pamodzi ndi zidzukulu zawo adzakhala kumeneko ndipo Davide adzakhala mfumu yawo kwa muyaya.
Et ils habiteront au pays que j'ai donné à Jacob mon serviteur, dans lequel vos pères ont habité; ils y habiteront, dis-je, eux, et leurs enfants, et les enfants de leurs enfants, à toujours; et David mon serviteur sera leur Prince à toujours.
26 Ndidzachita nawo pangano lamtendere; lidzakhala pangano lamuyaya. Ndidzawakhazikitsa ndi kuwachulukitsa, ndipo ndidzayika malo anga opatulika pakati pawo kwamuyaya.
Et je traiterai avec eux une alliance de paix, et il y aura une alliance éternelle avec eux, et je les établirai, et les multiplierai, je mettrai mon Sanctuaire au milieu d'eux à toujours.
27 Nyumba yanga yokhalamo idzakhala pakati pawo; Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
Et mon pavillon sera parmi eux; et je serai leur Dieu, et ils seront mon peuple.
28 Pamenepo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti Ine Yehova ndiye amene ndimasandutsa Israeli kukhala woyera, pamene malo anga opatulika adzakhala pakati pawo kwamuyaya!’”
Et les nations sauront que je suis l'Eternel qui sanctifie Israël, quand mon Sanctuaire sera au milieu d'eux à toujours.

< Ezekieli 37 >