< Ezekieli 36 >

1 “Iwe mwana wa munthu, yankhula kwa mapiri a Israeli ndipo unene kuti, ‘Inu mapiri a Israeli, imvani mawu a Yehova.’
and you(m. s.) son: child man to prophesy to(wards) mountain: mount Israel and to say mountain: mount Israel to hear: hear word LORD
2 Ine Ambuye Yehova ndikuti: Mdani wanu ankanena kuti, ‘Aa! Dziko lamapiri lakalekale lija lasanduka lathu.’
thus to say Lord YHWH/God because to say [the] enemy upon you Aha! and high place forever: antiquity to/for possession to be to/for us
3 Choncho nenera ndipo uwawuze kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza anakusakazani ndi kukuponderezani ku mbali zonse motero kuti munakhala mʼmanja mwa anthu a mitundu ina yonse ndipo anthu ankakunenani ndi kukunyozani,
to/for so to prophesy and to say thus to say Lord YHWH/God because in/on/with because be desolate: destroyed and to crush [obj] you from around: side to/for to be you possession to/for remnant [the] nation and to ascend: rise upon lip: words tongue and slander people
4 choncho, inu mapiri a Israeli, imvani zimene Ine Ambuye Yehova ndikuwuza mapiri ndi magomo, zigwembe ndi zigwa, mabwinja ndi mizinda yosiyidwa imene yakhala ikufunkhidwa komanso kunyozedwa ndi anthu a mitundu ina okuzungulirani.
to/for so mountain: mount Israel to hear: hear word Lord YHWH/God thus to say Lord YHWH/God to/for mountain: mount and to/for hill to/for channel and to/for valley and to/for desolation [the] devastated and to/for city [the] to leave: forsake which to be to/for plunder and to/for derision to/for remnant [the] nation which from around
5 Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti: Mu mkwiyo wanga woopsa ndinayankhula kuyimba mlandu mitundu ina yonse ya anthu makamaka a ku Edomu. Iwowa mwa chimwemwe chodzaza tsaya ndi mwa nkhwidzi analanda dziko langa ndi kulisandutsa lawo ndi kutengeratu dziko la msipu kukhala lawo.’
to/for so thus to say Lord YHWH/God if: surely yes not in/on/with fire jealousy my to speak: speak upon remnant [the] nation and upon Edom all her which to give: give [obj] land: country/planet my to/for them to/for possession in/on/with joy all heart in/on/with scorn soul: myself because pasture her to/for plunder
6 Nʼchifukwa chake, lengeza ku dziko la Israeli, ndipo uwuze mapiri ndi magomo, zigwembe ndi zigwa kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikuyankhula ndi mtima wokwiya kwambiri chifukwa inu munalandira chitonzo cha anthu a mitundu ina.’
to/for so to prophesy upon land: soil Israel and to say to/for mountain: mount and to/for hill to/for channel and to/for valley thus to say Lord YHWH/God look! I in/on/with jealousy my and in/on/with rage my to speak: speak because shame nation to lift: bear
7 Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikulumbira nditakweza dzanja langa kuti mitundu ya anthu idzatozedwanso.
to/for so thus to say Lord YHWH/God I to lift: vow [obj] hand: vow my if: surely yes not [the] nation which to/for you from around they(masc.) shame their to lift: vow
8 “Koma Inu mapiri a Israeli mudzaphukanso nthambi ndipo mudzawabalira zipatso anthu anga a Israeli, pakuti ali pafupi kubwerera kwawo.
and you(m. p.) mountain: mount Israel branch your to give: give and fruit your to lift: bear to/for people my Israel for to present: come to/for to come (in): come
9 Taonani, Ine ndili mbali yanu ndipo ndidzakukomerani mtima. Mudzalimidwa ndi kudzalidwa.
for look! I to(wards) you and to turn to(wards) you and to serve: labour and to sow
10 Ndidzachulukitsa chiwerengero cha anthu anu, nyumba yonse ya Israeli. Mʼmizinda mudzakhalanso anthu ndipo mabwinja adzamangidwanso.
and to multiply upon you man all house: household Israel all his and to dwell [the] city and [the] desolation to build
11 Ndidzachulukitsa chiwerengero cha amuna pamodzi ndi ziweto zomwe, ndipo adzachuluka kwambiri ndi kubereka ana ambiri. Ndidzakhazika anthu mʼdzikomo monga analili kale, ndi kukulemeretsani kuposa kale. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
and to multiply upon you man and animal and to multiply and be fruitful and to dwell [obj] you like/as former your and be good from beginning your and to know for I LORD
12 Ndidzachititsa anthu kuyenda pa inu, ndiye kuti inu anthu anga Aisraeli. Iwowo adzakhazikika pa inu, ndipo inu mudzakhala cholowa chawo. Simudzalandanso ana awo.
and to go: walk upon you man [obj] people my Israel and to possess: possess you and to be to/for them to/for inheritance and not to add: again still to/for be bereaved them
13 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza anthu amanena kuti, ndiwe dziko limene limadya anthu ake ‘kulanda ana a mtundu wake,’
thus to say Lord YHWH/God because to say to/for you to eat man (you(f. s.) *Q(K)*) and be bereaved (nation your *Q(K)*) to be
14 nʼchifukwa chake, simudzadyanso anthu kapena kulanda ana a mtundu wako. Ine Ambuye Yehova ndikutero.
to/for so man not to eat still (and nation your *Q(K)*) not (be bereaved *Q(K)*) still utterance Lord YHWH/God
15 Sindidzakulolaninso kumva mnyozo wa anthu a mitundu ina, kapena kupirira kunyogodola kwawo kapenanso kupunthwitsanso anthu a mʼdziko lako. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
and not to hear: hear to(wards) you still shame [the] nation and reproach people not to lift: bear still (and nation your *Q(K)*) not to stumble still utterance Lord YHWH/God
16 Yehova anandiyankhulanso kuti:
and to be word LORD to(wards) me to/for to say
17 “Iwe mwana wa munthu, pamene anthu a Israeli ankakhala mʼdziko lawolawo, analiyipitsa ndi makhalidwe awo ndiponso zochita zawo. Machitidwe awo pamaso panga anali onyansa pa zachipembedzo ngati msambo wa mkazi amene ali pa nthawi yake.
son: child man house: household Israel to dwell upon land: soil their and to defile [obj] her in/on/with way: conduct their and in/on/with wantonness their like/as uncleanness [the] impurity to be way: conduct their to/for face: before my
18 Tsono ndinawalanga chifukwa cha magazi amene anakhetsa mʼdzikomo, ndiponso chifukwa anayipitsa dziko ndi mafano awo.
and to pour: pour rage my upon them upon [the] blood which to pour: kill upon [the] land: country/planet and in/on/with idol their to defile her
19 Ndinawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndipo anabalalikira mʼmayiko onse. Ndinawalanga molingana ndi makhalidwe awo ndi zochita zawo.
and to scatter [obj] them in/on/with nation and to scatter in/on/with land: country/planet like/as way: conduct their and like/as wantonness their to judge them
20 Atafika kwa anthu a mitundu ina, kulikonse kumene anapitako, anayipitsa dzina langa loyera. Zinatero popeza anthu ponena za iwo ankanena kuti, ‘Awa ndi anthu a Yehova, komatu anachotsedwa ku dziko lake.’
and to come (in): come to(wards) [the] nation which to come (in): come there and to profane/begin: profane [obj] name holiness my in/on/with to say to/for them people LORD these and from land: country/planet his to come out: come
21 Koma Ine ndinkadera nkhawa dzina langa loyera, limene Aisraeli analiyipitsa pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapitako.
and to spare upon name holiness my which to profane/begin: profane him house: household Israel in/on/with nation which to come (in): come there [to]
22 “Nʼchifukwa chake awuze Aisraeliwo kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndidzachita zimene ndidzachitezo osati chifukwa cha inuyo Aisraelinu ayi, koma chifukwa cha dzina langa, limene mwaliyipitsa pakati pa anthu a mitundu ina kumene munapitako.
to/for so to say to/for house: household Israel thus to say Lord YHWH/God not because you I to make: do house: household Israel that if: except if: except to/for name holiness my which to profane/begin: profane in/on/with nation which to come (in): come there
23 Ndidzaonetsa chiyero cha dzina langa lotchuka, limene layipitsidwa pakati pawo. Anthu a mitundu inayo atadzazindikira kuti ndaonetsa kudzera mwa inu kuti dzina langa ndi loyera, iwo adzadziwanso kuti Ine ndine Yehova. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
and to consecrate: holiness [obj] name my [the] great: large [the] to profane/begin: profane in/on/with nation which to profane/begin: profane in/on/with midst their and to know [the] nation for I LORD utterance Lord YHWH/God in/on/with to consecrate: holiness I in/on/with you to/for eye their
24 “Pakuti Ine ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina. Ndidzakusonkhanitsani kuchoka ku mayiko onse ndi kukubwezerani ku dziko lanulanu.
and to take: take [obj] you from [the] nation and to gather [obj] you from all [the] land: country/planet and to come (in): bring [obj] you to(wards) land: soil your
25 Ndidzakuwazani madzi oyera, ndipo mudzakhala oyera mtima. Zonse zimene zimakuyipitsani zidzachoka. Ndidzakuyeretsani pochotsa mafano anu onse.
and to scatter upon you water pure and be pure from all uncleanness your and from all idol your be pure [obj] you
26 Ndidzakupatsani mtima watsopano ndi kulowetsa mzimu watsopano mwa inu. Ndidzachotsa mwa inu mtima wanu wowuma ngati mwala ndi kukupatsani mtima wofewa ngati mnofu.
and to give: give to/for you heart new and spirit new to give: put in/on/with entrails: among your and to turn aside: remove [obj] heart [the] stone from flesh your and to give: give to/for you heart flesh
27 Ndipo ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo ndidzakuthandizani kutsatira malangizo anga ndi kukusungitsani mosamala kwambiri malamulo anga.
and [obj] spirit my to give: put in/on/with entrails: among your and to make: do [obj] which in/on/with statute: decree my to go: walk and justice: judgement my to keep: careful and to make: do
28 Mudzakhala mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu. Mudzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
and to dwell in/on/with land: country/planet which to give: give to/for father your and to be to/for me to/for people and I to be to/for you to/for God
29 Ndidzakupulumutsani ku zonse zokuyipitsani. Ndidzakuchulukitsirani tirigu ndipo sindidzakugwetseraninso njala.
and to save [obj] you from all uncleanness your and to call: call to to(wards) [the] grain and to multiply [obj] him and not to give: put upon you famine
30 Ndidzachulukitsa zipatso za mʼmitengo yanu ndi zokolola za mʼmunda mwanu, kotero kuti simudzanyozedwanso pakati pa anthu a mitundu ina chifukwa cha njala.
and to multiply [obj] fruit [the] tree and fruit [the] land: country because which not to take: recieve still reproach famine in/on/with nation
31 Pamenepo mudzakumbukira makhalidwe anu oyipa ndi ntchito zanu zoyipa. Machimo anu ndi ntchito zanu zonyansa zidzakuchititsa nokha manyazi.
and to remember [obj] way: conduct your [the] bad: evil and deed your which not pleasant and to loath in/on/with face of your upon iniquity: crime your and upon abomination your
32 Tsono dziwani kuti Ine sindidzachita zimenezi chifukwa cha inuyo ayi, ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse. Ndiyetu chitani manyazi ndipo mugwetse nkhope zanu, inu Aisraeli chifukwa cha makhalidwe anu!
not because you I to make: do utterance Lord YHWH/God to know to/for you be ashamed and be humiliated from way: journey your house: household Israel
33 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limene ndidzayeretse machimo anu onse, ndidzayikamonso anthu mʼmizinda yanu, ndipo ndidzamanganso nyumba pa mabwinja.
thus to say Lord YHWH/God in/on/with day be pure I [obj] you from all iniquity: crime your and to dwell [obj] [the] city and to build [the] desolation
34 Dziko limene linasanduka chipululu lizidzalimidwanso. Mʼmalo moti aliyense wopitamo alione dzikolo ngati chipululu tsopano adzaliona lolimidwa.
and [the] land: country/planet [the] be desolate: destroyed to serve: labour underneath: instead which to be devastation to/for eye: seeing all to pass
35 Iwo adzati, ‘Dziko ili, limene linali chipululu, lasanduka munda wa Edeni. Mizinda imene inali mabwinja osiyidwa ndi owonongedwa, tsopano ndi yotetezedwa ndi yokhalamo anthu.
and to say [the] land: country/planet this [the] be desolate: destroyed to be like/as garden Eden and [the] city [the] desolate and [the] be desolate: destroyed and [the] to overthrow to gather/restrain/fortify to dwell
36 Ndipo anthu a mitundu ina okhala pafupi nanu amene anatsala adzadziwa kuti Ine Yehova ndine amene ndinamanganso mizinda yowonongeka ndi kudzalanso zinthu zatsopano mʼmalo mʼmene munali chipululu. Ine Yehova ndayankhula ndipo ndidzazichitadi.’
and to know [the] nation which to remain around you for I LORD to build [the] to overthrow to plant [the] be desolate: destroyed I LORD to speak: speak and to make: do
37 “Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzalolanso Aisraeli kuti andipemphe zoti ndiwachitire: Ndidzachulukitsa anthu awo ngati nkhosa.
thus to say Lord YHWH/God still this to seek to/for house: household Israel to/for to make: do to/for them to multiply [obj] them like/as flock man
38 Adzachulukadi ngati nkhosa zomwe ankapereka ngati nsembe ku Yerusalemu pa nthawi za chikondwerero. Choncho mizinda ya mabwinja idzadzaza ndi anthu. Zikadzatero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
like/as flock holiness like/as flock Jerusalem in/on/with meeting: festival her so to be [the] city [the] desolate full flock man and to know for I LORD

< Ezekieli 36 >