< Ezekieli 35 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
I doszło do mnie słowo PANA mówiące:
2 “Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo
Synu człowieczy, zwróć swoją twarz przeciwko górze Seir i prorokuj przeciwko niej.
3 awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu.
Mów do niej: Tak mówi Pan BÓG: Oto jestem przeciwko tobie, góro Seir, wyciągnę moją rękę przeciwko tobie i wydam cię na wielkie spustoszenie.
4 Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Twoje miasta zamienię w ruiny i będziesz spustoszona. I poznasz, że ja jestem PANEM.
5 “Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake.
Ponieważ żywiłaś wieczną nienawiść i wydałaś synów Izraela pod ostrze miecza w czasie ich utrapienia, w czasie wykonywania ich kary;
6 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola.
Dlatego, jak żyję, mówi Pan BÓG, wydam cię na zabicie i krew będzie cię ścigać. Ponieważ nie znienawidziłaś krwi, krew będzie cię ścigać.
7 Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko.
I zamienię górę Seir w wielkie spustoszenie, wygubię z niej każdego, który przechodzi i który wraca.
8 Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse.
Jej góry napełnię jej zabitymi. Na twoich pagórkach, na twoich dolinach i [we] wszystkich twoich strumieniach padną pobici mieczem.
9 Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Zamienię cię w wieczne spustoszenie i twoje miasta nie będą zamieszkałe. I poznacie, że ja jestem PANEM.
10 “Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo.
Ponieważ powiedziałaś: Te dwa narody i te dwa kraje będą moje, weźmiemy je w posiadanie, chociaż PAN tam przebywał;
11 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo.
Jak żyję, mówi Pan BÓG, uczynię według twego gniewu i według twojej zawiści, z jaką postąpiłaś w swej nienawiści względem nich, i dam się poznać wśród nich, gdy cię osądzę.
12 Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’
I poznasz, że ja jestem PANEM i słyszałem wszystkie twoje obelgi, które wypowiedziałaś przeciw górom Izraela, mówiąc: Są spustoszone, zostały nam dane na pożarcie.
13 Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva.
Tak się wynosiliście swoimi ustami przeciwko mnie i mnożyliście swoje słowa przeciwko mnie. Ja [to] słyszałem.
14 Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja.
Tak mówi Pan BÓG: Kiedy cała ziemia będzie się radować, wtedy zamienię cię w pustkowie.
15 Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
Jak ty się radowałaś nad dziedzictwem domu Izraela, że zostało spustoszone, tak uczynię i tobie: będziesz spustoszona, góro Seir i cały Edomie. I poznają, że ja jestem PANEM.

< Ezekieli 35 >