< Ezekieli 35 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
Et la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
2 “Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo
Fils d’un homme, tourne ton visage contre le mont de Séir; prophétise sur lui, et tu lui diras:
3 awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu.
Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Voilà que je viens vers toi, mont de Séir, et j’étendrai ma main sur toi, et je te rendrai désolé et désert.
4 Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Tes villes, je les détruirai et tu seras désert; et tu sauras que je suis le Seigneur.
5 “Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake.
Parce que tu as été un ennemi éternel, et que tu as renfermé les fils d’Israël dans la main du glaive au temps de leur affliction au temps de leur iniquité extrême;
6 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola.
À cause de cela, je vis, moi, dit le Seigneur Dieu; je te livrerai au sang, et le sang te poursuivra; et puisque tu as haï le sang, le sang te poursuivra.
7 Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko.
Et je rendrai le mont de Séir désolé et désert; et j’en retrancherai l’allant et le revenant.
8 Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse.
Et je remplirai ses montagnes de ses morts; sur tes collines, dans tes vallées, et le long de tes torrents, les tués sous le glaive tomberont.
9 Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
Je te réduirai en solitudes éternelles; et tes cités ne seront pas habitées; et vous saurez que je suis le Seigneur Dieu.
10 “Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo.
Parce que tu as dit: Deux nations et deux terres seront à moi, et je les posséderai en héritage, quoique le Seigneur y fût;
11 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo.
À cause de cela, je vis, moi, dit le Seigneur Dieu, j’agirai selon ta colère et selon ta jalousie que tu as exercées, parce que tu les haïssais; et je me ferai connaître par eux, lorsque je t’aurai jugé.
12 Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’
Tu sauras que moi, le Seigneur, j’ai entendu toutes les paroles outrageantes que tu as proférées contre les montagnes d’Israël, en disant: Ce sont des déserts; ils nous ont été donnés pour être dévorés.
13 Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva.
Et vous vous êtes élevés contre moi par votre bouche, et vous avez prononcé dédaigneusement contre moi vos paroles; moi j’ai entendu.
14 Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja.
Voici ce que dit le Seigneur Dieu: Lorsque toute la terre se réjouira, je te réduirai en une solitude.
15 Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
Comme tu t’es réjoui sur l’héritage de la maison d’Israël, de ce qu’elle avait été dévastée, ainsi je te ferai; tu seras dévasté, mont de Séir, et toute l’Idumée; et ils sauront que je suis le Seigneur Dieu.

< Ezekieli 35 >