< Ezekieli 35 >
1 Yehova anandiyankhula kuti:
Then the word of Yahweh came to me, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo
“Son of man, set your face against Mount Seir and prophesy against it.
3 awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu.
Say to it, 'The Lord Yahweh says this: Behold! I am against you, Mount Seir, and I will strike you with my hand and make you a desolation and a waste.
4 Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
I will make your cities ruins, and you yourself will become desolate; then you will know that I am Yahweh.
5 “Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake.
Because you have always been hostile to the people of Israel, and because you poured them out into the hands of the sword at the time of their distress, at the time their punishment was at its greatest.
6 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola.
Therefore, as I live—this is the Lord Yahweh's declaration—I will prepare you for bloodshed, and bloodshed will pursue you! Since you did not hate bloodshed, bloodshed will pursue you.
7 Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko.
I will make Mount Seir a complete desolation when I cut off from it anyone who passes through and returns again.
8 Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse.
I will fill its mountains with those who were killed; on your high hills and valleys and in all your streams those who were killed by the sword will fall.
9 Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
I will make you a perpetual desolation. Your cities will not be inhabited, but you will know that I am Yahweh.
10 “Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo.
You have said, “These two nations and these two lands will become mine, and we will possess them,” even when Yahweh was present with them.
11 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo.
Therefore, as I live—this is the Lord Yahweh's declaration—so I will do according to your anger and according to your jealousy that you had in your hatred of Israel, and I will show myself to them when I judge you.
12 Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’
So you will know that I am Yahweh. I have heard all the insults you spoke against the mountains of Israel, when you said, “They have been destroyed; they have been given over to us to devour.”
13 Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva.
You exalted yourselves against me with what you said, and you multiplied the words you said against me; and I heard it all.
14 Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja.
The Lord Yahweh says this: I will make you a desolation, while the entire earth rejoices.
15 Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
As you rejoiced over the inheritance of the people of Israel because of its desolation, I will do the same to you. You will become a desolation, Mount Seir, and all of Edom—all of it! Then they will know that I am Yahweh.'”