< Ezekieli 35 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
Moreover the word of the LORD came unto me, saying,
2 “Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo
Son of man, set thy face against mount Seir, and prophesy against it,
3 awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu.
and say unto it, Thus saith the Lord GOD: Behold, I am against thee, O mount Seir, and I will stretch out mine hand against thee, and I will make thee a desolation and an astonishment.
4 Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
I will lay thy cities waste, and thou shalt be desolate; and thou shalt know that I am the LORD.
5 “Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake.
Because thou hast had a perpetual enmity, and hast given over the children of Israel to the power of the sword in the time of their calamity, in the time of the iniquity of the end:
6 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola.
therefore, as I live, saith the Lord GOD, I will prepare thee unto blood, and blood shall pursue thee: sith thou hast not hated blood, therefore blood shall pursue thee.
7 Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko.
Thus will I make mount Seir an astonishment and a desolation; and I will cut off from it him that passeth through and him that returneth.
8 Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse.
And I will fill his mountains with his slain: in thy hills and in thy valleys and in all thy watercourses shall they fall that are slain with the sword.
9 Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
I will make thee perpetual desolations, and thy cities shall not be inhabited: and ye shall know that I am the LORD.
10 “Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo.
Because thou hast said, These two nations and these two countries shall be mine, and we will possess it; whereas the LORD was there:
11 Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo.
therefore, as I live, saith the Lord GOD, I will do according to thine anger, and according to thine envy which thou hast shewed out of thy hatred against them; and I will make myself known among them, when I shall judge thee.
12 Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’
And thou shalt know that I the LORD have heard all thy blasphemies which thou hast spoken against the mountains of Israel, saying, They are laid desolate, they are given us to devour.
13 Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva.
And ye have magnified yourselves against me with your mouth, and have multiplied your words against me: I have heard it.
14 Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja.
Thus saith the Lord GOD: When the whole earth rejoiceth, I will make thee desolate.
15 Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
As thou didst rejoice over the inheritance of the house of Israel, because it was desolate, so will I do unto thee: thou shalt be desolate, O mount Seir, and all Edom, even all of it: and they shall know that I am the LORD.

< Ezekieli 35 >