< Ezekieli 34 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
La parole de l’Eternel me fut adressée en ces termes:
2 “Iwe mwana wa munthu, yankhula mawu oyimba mlandu abusa a Israeli. Lengeza ndipo uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Tsoka kwa abusa a Israeli amene mumangodzisamala nokha! Kodi abusa sayenera kusamalira nkhosa?
"Fils de l’homme, prophétise sur les pasteurs d’Israël, prophétise et dis-leur, à ces pasteurs: Ainsi parle le Seigneur Dieu: Malheur aux pasteurs d’Israël, qui se paissaient eux-mêmes! N’Est-ce pas les brebis que doivent paître les pasteurs?
3 Mumadya chambiko, mumadziveka zovala zaubweya, ndi kupha nyama zonenepa, koma simusamalira nkhosazo.
Vous en mangiez la graisse, vous vous vêtiez de leur laine, vous immoliez celle qui était corpulente; les brebis, vous ne les paissiez point!
4 Simunalimbitse nkhosa zofowoka, kapena kuchiritsa zodwala, kapena kumanga mabala a nkhosa zopweteka. Simunabweze zosochera kapena kufunafuna zotayika. Munaziweta mozunza ndi mwankhanza.
Les infirmes, vous ne les souteniez pas; vous n’avez point soigné la malade ni pansé celle qui avait une fracture; celle qui s’écartait, vous ne l’avez pas ramenée, celle qui s’égarait, vous ne l’avez pas cherchée. C’Est avec violence que vous les régentiez et avec dureté.
5 Kotero zinabalalika chifukwa zinalibe mʼbusa, ndipo pamene zinabalalika zinakhala chakudya cha zirombo zonse zakuthengo.
Elles se sont donc dispersées faute de pasteur; elles sont devenues la proie de toutes les bêtes des champs, par leur dispersion.
6 Nkhosa zanga zinayendayenda mʼmapiri onse ndi mʼzitunda zonse zazitali. Zinabalalika pa dziko lonse lapansi, ndipo palibe amene anazilondola kapena kuzifunafuna.
Mes brebis errent par toutes les montagnes et sur toute colline élevée. Sur toute la surface de la terre sont disséminées mes brebis et nul ne s’enquiert d’elles, nul ne se met à leur recherche.
7 “‘Choncho Inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani.
C’Est pourquoi, pasteurs, écoutez la parole de l’Eternel:
8 Pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Wamphamvuzonse, ndithu, nkhosa zanga zinajiwa ndi zirombo zakuthengo, zinasanduka chakudya cha zirombo chifukwa panalibe abusa. Abusa anga sanafunefune nkhosa zanga. Iwo ankangosamala za iwo okha mʼmalo mosamala nkhosa zanga.
Par ma vie, dit le Seigneur Dieu, j’en jure, puisque mes brebis ont été livrées en proie et que mes brebis sont devenues la pâture de toutes les bêtes des champs, faute de pasteur, puisque mes pasteurs n’ont pas pris soin de mes brebis, qu’ils se paissaient eux-mêmes, les pasteurs, sans faire paître mes brebis,
9 Chifukwa chake, inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani.
c’est pourquoi, ô pasteurs, écoutez la parole de l’Eternel:
10 Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndayipidwa nanu, inu abusa. Ndidzakulandani nkhosa zanga ndipo simudzazidyetsanso. Ndidzakuchotsani pa ntchito ya ubusa kuti musamangodzidyetsa nokha. Ndidzalanditsa nkhosa zanga kukamwa kwanu ndipo simudzazidyanso.
Ainsi parle le Seigneur Dieu: Voici, je vais m’en prendre aux pasteurs, je réclamerai mes brebis de leurs mains et je leur enlèverai la conduite de mon troupeau, pour que les pasteurs ne se paissent plus eux-mêmes; je sauverai mes brebis de leur bouche, et elles ne leur serviront plus de pâture.
11 “‘Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, mwini wakene ndidzazifunafuna nkhosa zanga ndi kuzisamalira.
Oui, ainsi parle le Seigneur Dieu, me voici moi-même! J’Aurai soin de mes brebis et je les passerai en revue.
12 Monga mʼbusa amanka nafunafuna nkhosa zake pamene zina zabalalikira kutali, moteronso Ine ndidzafunafuna nkhosa zanga. Ndidzazipulumutsa kuchoka kumalo onse kumene zinabalalikira pa nthawi yankhungu ndi mdima.
Comme un pasteur inspecte son troupeau, le jour où il est au milieu de ses brebis en désarroi, ainsi j’inspecterai mes brebis et les retirerai de tous les lieux où elles se sont dispersées en un jour de nuée et de brume.
13 Ndidzazitulutsa pakati pa mitundu ya anthu ndi kuzisonkhanitsa kuchokera ku mayiko ena, ndipo ndidzazibwezera ku dziko lawo. Ndidzaziwetera ku mapiri a Israeli, mʼmbali mwa mitsinje ndi kumalo kumene kumakhala anthu.
Je les ferai sortir du milieu des nations, je les rassemblerai des différentes contrées et les ramènerai sur leur sol; je les ferai paître sur les montagnes d’Israël, dans les ravins et dans toutes les localités habitables du pays.
14 Ndidzaziwetera kumalo a msipu wabwino. Mapiri okwera a Israeli adzakhala malo azidyetserako. Kumeneko zidzapumula ku abusa abwino a msipu ndipo zizidzadyadi msipu wonenepetsa pa mapiri a Israeli.
C’Est dans un bon pâturage que je les ferai paître, et c’est sur les hautes montagnes d’Israël que sera leur parc; là elles gîteront dans un beau cantonnement et elles se nourriront d’un gras pâturage sur les montagnes d’Israël.
15 Ine mwini wake ndidzaziweta nkhosa zanga ndi kuzilola kuti zipumule. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
C’Est moi qui paîtrai mes brebis, moi qui leur assurerai leur gîte, dit le Seigneur Dieu.
16 Ndidzafunafuna zotayika ndi kubweza zosochera. Ndidzamanga mabala a zopweteka ndi kulimbikitsa zofowoka. Koma zonenepa ndi zamphamvu ndidzaziwononga. Ndidzaweta nkhosazo mwachilungamo.
La brebis égarée, je la rechercherai, celle qui s’est écartée, je la ramènerai; je soignerai celle qui a une fracture, rendrai des forces à celle qui est malade; mais je détruirai celle qui est grasse et vigoureuse. Je les paîtrai toutes avec équité.
17 “‘Kunena za inu, nkhosa zanga, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ndi nkhosa, pakati pa nkhosa zazimuna ndi mbuzi zazimuna.
Quant à vous, mes brebis, ainsi parle le Seigneur Dieu, me voici en train de juger entre brebis et brebis, entre les béliers et les boucs.
18 Kodi sikukukwanirani kudya msipu wabwino kuti muzichita kuponderezanso msipu umene simunadyewo? Kodi simukhutira ndi kumwa madzi abwino kuti muzinka mudetsanso madzi otsalawo ndi mapazi anu?
Est-ce trop peu pour vous de vous repaître d’un excellent pâturage pour que vous fouliez au pied ce qui reste de votre fourrage? De boire d’une eau bien clarifiée pour qu’avec vos pieds vous troubliez ce que vous en laissez?
19 Kodi nkhosa zanga zidye zimene mwazipondaponda ndi kumwa madzi amene mwawadetsa ndi mapazi anu?
Il faut donc que mes brebis se nourrissent de ce que vos pieds ont foulé, qu’elles boivent ce que vos pieds ont troublé?"
20 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Taonani, Ine mwini wake ndidzaweruza pakati pa nkhosa zonenepa ndi nkhosa zowonda.
Eh bien! C’Est de la sorte que le Seigneur parle à leur égard: "Me voici moi-même pour juger entre la brebis grasse et la brebis maigre.
21 Popeza zofowoka mumaziwomba ndi kuzikankhira kumbali, ndipo mumazigunda ndi nyanga zanu nʼkuzimwazira kutali,
Puisque du côté et de l’épaule vous bousculez et, de vos cornes, vous frappez toutes celles qui sont faibles, jusqu’à ce que vous les ayez dispersées et mises dehors,
22 tsono Ine ndidzapulumutsa nkhosa zanga, ndipo sindidzalolanso kuti zijiwe. Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ina ndi nkhosa inanso.
je prêterai secours à mes brebis, pour qu’elles ne soient plus livrées en proie, et je jugerai entre brebis et brebis.
23 Ndidzaziyikira mʼbusa mmodzi, mtumiki wanga Davide. Iyeyo ndiye azidzazisamala. Adzakhala mʼbusa wawo.
J’Établirai sur elles un seul pasteur, qui les paîtra, mon serviteur David c’est lui qui les paîtra, c’est lui qui sera leur pasteur.
24 Ine Yehova ndidzakhala Mulungu wake ndipo mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu pakati pa nkhosazo. Ine Yehova ndayankhula.
Et moi, l’Eternel, je serai leur Dieu, tandis que David, mon serviteur, sera prince au milieu d’elles: moi, l’Eternel, je le dis.
25 “‘Ndidzapangana nazo pangano la mtendere. Ndidzachotsa mʼdzikomo zirombo zolusa. Choncho nkhosa zanga zidzakhala mu mtendere mu chipululu ngakhalenso mʼthengo.
Je contracterai avec elles une alliance de paix, je ferai disparaître les animaux féroces du pays, pour qu’elles puissent demeurer en sécurité dans le désert et dormir dans les forêts.
26 Ndidzakhazika anthu anga pafupi ndi phiri langa loyera ndipo ndidzawadalitsa. Ndidzawagwetsera mvula pa nthawi yake ndipo idzakhala mvula ya madalitso.
Je ferai d’elles et de ce qui avoisine ma colline une bénédiction, je ferai tomber la pluie en son temps: ce seront des pluies riches en bénédictions.
27 Mitengo ya mʼminda idzabereka zipatso zake, ndipo nthaka idzakhala ndi zokolola zake. Anthu adzakhala mwamtendere mʼdziko lawo. Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzathyola magoli awo ndi kuwapulumutsa kuchoka mʼmanja mwa amene anawagwira ukapolo.
L’Arbre des champs donnera son fruit, la terre donnera son produit, ils seront sur leur sol en sécurité, et ils sauront que je suis l’Eternel, quand je briserai les barres de leur joug et les délivrerai de ceux qui les ont asservis.
28 Anthu amitundu ina sadzawafunkhanso ndipo sadzadyedwa ndi zirombo zakuthengo. Adzakhala mwamtendere ndipo palibe amene adzawaopseze.
Ils ne seront plus une proie pour les nations, ni une pâture pour les animaux du pays; ils demeureront en sécurité, sans personne pour les troubler.
29 Ndidzawapatsa zokolola zochuluka motero kuti sadzavutikanso ndi njala. Anthu a mitundu ina sadzawanyozanso.
J’Établirai pour eux une plantation qui sera leur gloire; personne dans le pays ne succombera plus à la faim, et ils n’auront plus à subir l’opprobre des nations.
30 Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wawo ndili nawo pamodzi, ndipo kuti iwo, Aisraeli, ndi anthu anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Ils sauront que moi, l’Eternel, leur Dieu, je suis avec eux, et qu’eux, la maison d’Israël, ils sont mon peuple, dit le Seigneur Dieu.
31 Inu ndinu nkhosa zanga, nkhosa zimene ndimazidyetsa. Ine ndine Mulungu wanu. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.’”
Et vous, mes brebis, brebis que je fais paître, vous êtes des hommes, moi, je suis votre Dieu, dit le Seigneur Dieu"

< Ezekieli 34 >