< Ezekieli 34 >

1 Yehova anandiyankhula kuti:
HERRENS Ord kom til mig saaledes:
2 “Iwe mwana wa munthu, yankhula mawu oyimba mlandu abusa a Israeli. Lengeza ndipo uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Tsoka kwa abusa a Israeli amene mumangodzisamala nokha! Kodi abusa sayenera kusamalira nkhosa?
Menneskesøn, profeter mod Israels Hyrder, profeter og sig til dem: Saa siger den Herre HERREN: Ve Israels Hyrder, som røgtede sig selv! Skal Hyrderne ikke røgte Hjorden?
3 Mumadya chambiko, mumadziveka zovala zaubweya, ndi kupha nyama zonenepa, koma simusamalira nkhosazo.
I fortærede Mælken, med Ulden klædte I eder, de fede Dyr slagtede I, men Hjorden røgtede I ikke;
4 Simunalimbitse nkhosa zofowoka, kapena kuchiritsa zodwala, kapena kumanga mabala a nkhosa zopweteka. Simunabweze zosochera kapena kufunafuna zotayika. Munaziweta mozunza ndi mwankhanza.
de svage Dyr styrkede I ikke, de syge lægte I ikke, de saarede forbandt I ikke, de adsplittede bragte I ikke tilbage, de vildfarende opsøgte I ikke, men I styrede dem med Haardhed og Grumhed.
5 Kotero zinabalalika chifukwa zinalibe mʼbusa, ndipo pamene zinabalalika zinakhala chakudya cha zirombo zonse zakuthengo.
Derfor spredtes de, eftersom der ingen Hyrde var, og blev til Æde for alle Markens vilde Dyr; ja, de spredtes.
6 Nkhosa zanga zinayendayenda mʼmapiri onse ndi mʼzitunda zonse zazitali. Zinabalalika pa dziko lonse lapansi, ndipo palibe amene anazilondola kapena kuzifunafuna.
Min Hjord flakkede om paa alle Bjerge og paa hver en høj Banke, og over hele Jorden spredtes min Hjord, og ingen spurgte eller ledte efter dem.
7 “‘Choncho Inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani.
Derfor, I Hyrder, hør HERRENS Ord!
8 Pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Wamphamvuzonse, ndithu, nkhosa zanga zinajiwa ndi zirombo zakuthengo, zinasanduka chakudya cha zirombo chifukwa panalibe abusa. Abusa anga sanafunefune nkhosa zanga. Iwo ankangosamala za iwo okha mʼmalo mosamala nkhosa zanga.
Saa sandt jeg lever, lyder det fra den Herre HERREN: Fordi min Hjord blev til Rov, fordi min Hjord blev til Æde for alle Markens vilde Dyr, eftersom der ingen Hyrde var, og Hyrderne ikke spurgte efter min Hjord, og fordi Hyrderne røgtede sig selv og ikke min Hjord,
9 Chifukwa chake, inu abusa, tamvani zimene Ine Yehova ndikukuwuzani.
derfor, I Hyrder, hør HERRENS Ord!
10 Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndayipidwa nanu, inu abusa. Ndidzakulandani nkhosa zanga ndipo simudzazidyetsanso. Ndidzakuchotsani pa ntchito ya ubusa kuti musamangodzidyetsa nokha. Ndidzalanditsa nkhosa zanga kukamwa kwanu ndipo simudzazidyanso.
Saa siger den Herre HERREN: Se, jeg, kommer over Hyrderne og kræver min Hjord af deres Haand, og jeg sætter dem fra at vogte min Hjord; Hyrderne skal ikke mere kunne røgte sig selv; jeg redder min Hjord af deres Gab, saa den ikke skal tjene dem til Æde.
11 “‘Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, mwini wakene ndidzazifunafuna nkhosa zanga ndi kuzisamalira.
Thi saa siger den Herre HERREN: Se, jeg vil selv spørge efter min Hjord og tage mig af den.
12 Monga mʼbusa amanka nafunafuna nkhosa zake pamene zina zabalalikira kutali, moteronso Ine ndidzafunafuna nkhosa zanga. Ndidzazipulumutsa kuchoka kumalo onse kumene zinabalalikira pa nthawi yankhungu ndi mdima.
Som en Hyrde tager sig af sin Hjord paa Stormvejrets Dag, saaledes tager jeg mig af min Hjord og redder den fra de Steder, hvorhen de spredtes paa Skyernes og Mulmets Dag;
13 Ndidzazitulutsa pakati pa mitundu ya anthu ndi kuzisonkhanitsa kuchokera ku mayiko ena, ndipo ndidzazibwezera ku dziko lawo. Ndidzaziwetera ku mapiri a Israeli, mʼmbali mwa mitsinje ndi kumalo kumene kumakhala anthu.
jeg fører dem bort fra Folkeslagene, samler dem fra Landene og bringer dem til deres Land, og jeg, røgter dem paa Israels Bjerge, i Kløfterne og paa alle Landets beboede Steder.
14 Ndidzaziwetera kumalo a msipu wabwino. Mapiri okwera a Israeli adzakhala malo azidyetserako. Kumeneko zidzapumula ku abusa abwino a msipu ndipo zizidzadyadi msipu wonenepetsa pa mapiri a Israeli.
Paa gode Græsgange vil jeg vogte dem, og paa Israels Bjerghøjder skal deres Græsmarker være; der skal de lejre sig paa gode Græsmarker, og i fede Græsgange skal de græsse paa Israels Bjerge.
15 Ine mwini wake ndidzaziweta nkhosa zanga ndi kuzilola kuti zipumule. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Jeg vil selv røgte min Hjord og selv lade dem lejre sig, lyder det fra den Herre HERREN.
16 Ndidzafunafuna zotayika ndi kubweza zosochera. Ndidzamanga mabala a zopweteka ndi kulimbikitsa zofowoka. Koma zonenepa ndi zamphamvu ndidzaziwononga. Ndidzaweta nkhosazo mwachilungamo.
De vildfarende Dyr vil jeg opsøge, de adsplittede vil jeg bringe tilbage, de saarede vil jeg forbinde de svage vil jeg styrke, og de fede og kraftige vil jeg vogte; jeg vil røgte dem, som det er ret.
17 “‘Kunena za inu, nkhosa zanga, Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ndi nkhosa, pakati pa nkhosa zazimuna ndi mbuzi zazimuna.
Og I, min Hjord! Saa siger den Herre HERREN: Se, jeg vil skifte. Ret mellem Faar og Faar, mellem Vædre og Bukke.
18 Kodi sikukukwanirani kudya msipu wabwino kuti muzichita kuponderezanso msipu umene simunadyewo? Kodi simukhutira ndi kumwa madzi abwino kuti muzinka mudetsanso madzi otsalawo ndi mapazi anu?
Er det eder ikke nok at græsse paa den bedste Græsgang, siden I nedtramper, hvad der er levnet af eders Græsgange? Er det eder ikke nok at drikke det klare Vand, siden I med eders Fødder plumrer, hvad der er levnet?
19 Kodi nkhosa zanga zidye zimene mwazipondaponda ndi kumwa madzi amene mwawadetsa ndi mapazi anu?
Min Hjord maa græsse, hvad I har nedtrampet, og drikke, hvad I har plumret med eders Fødder!
20 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Taonani, Ine mwini wake ndidzaweruza pakati pa nkhosa zonenepa ndi nkhosa zowonda.
Derfor, saa siger den Herre HERREN: Se, jeg kommer for at skifte Ret mellem de fede og de magre Faar.
21 Popeza zofowoka mumaziwomba ndi kuzikankhira kumbali, ndipo mumazigunda ndi nyanga zanu nʼkuzimwazira kutali,
Fordi I med Side og Skulder skubbede alle de svage Dyr bort og stangede dem med eders Horn, til I fik dem drevet ud,
22 tsono Ine ndidzapulumutsa nkhosa zanga, ndipo sindidzalolanso kuti zijiwe. Ndidzaweruza pakati pa nkhosa ina ndi nkhosa inanso.
derfor vil jeg hjælpe min Hjord, saa den ikke mere skal blive til Rov, og skifte Ret mellem Faar og Faar.
23 Ndidzaziyikira mʼbusa mmodzi, mtumiki wanga Davide. Iyeyo ndiye azidzazisamala. Adzakhala mʼbusa wawo.
Jeg sætter een Hyrde over dem, min Tjener David, og han skal vogte dem; han skal vogte dem, og han skal være deres Hyrde.
24 Ine Yehova ndidzakhala Mulungu wake ndipo mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu pakati pa nkhosazo. Ine Yehova ndayankhula.
Og jeg, HERREN, vil være deres Gud, og min Tjener David skal være Fyrste iblandt dem, saa sandt jeg, HERREN, har talet.
25 “‘Ndidzapangana nazo pangano la mtendere. Ndidzachotsa mʼdzikomo zirombo zolusa. Choncho nkhosa zanga zidzakhala mu mtendere mu chipululu ngakhalenso mʼthengo.
Jeg vil slutte en Fredspagt med dem og udrydde de vilde Dyr at Landet, saa de trygt kan bo i Ørkenen og sove i Skovene.
26 Ndidzakhazika anthu anga pafupi ndi phiri langa loyera ndipo ndidzawadalitsa. Ndidzawagwetsera mvula pa nthawi yake ndipo idzakhala mvula ya madalitso.
Og jeg gør dem og Landet rundt om min Høj til Velsignelse, og jeg sender Regn i rette Tid, mine Byger skal blive til Velsignelse.
27 Mitengo ya mʼminda idzabereka zipatso zake, ndipo nthaka idzakhala ndi zokolola zake. Anthu adzakhala mwamtendere mʼdziko lawo. Iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzathyola magoli awo ndi kuwapulumutsa kuchoka mʼmanja mwa amene anawagwira ukapolo.
Markens Træer skal give deres Frugt og Landet sin Afgrøde; trygt skal de bo paa deres Jord, og de skal kende, at jeg er HERREN, naar jeg bryder Stængerne paa deres Aag og frelser dem af deres Haand, som gjorde dem til Trælle.
28 Anthu amitundu ina sadzawafunkhanso ndipo sadzadyedwa ndi zirombo zakuthengo. Adzakhala mwamtendere ndipo palibe amene adzawaopseze.
Ikke mere skal de blive til Rov for Folkene, og Landets vilde Dyr skal ikke æde dem; trygt skal de bo, uden at nogen skræmmer dem.
29 Ndidzawapatsa zokolola zochuluka motero kuti sadzavutikanso ndi njala. Anthu a mitundu ina sadzawanyozanso.
Jeg lader en Fredens Plantning vokse op for dem, og ingen skal rives bort af Hunger i Landet, og de skal ikke mere bære Folkenes Haan.
30 Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wawo ndili nawo pamodzi, ndipo kuti iwo, Aisraeli, ndi anthu anga. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
De skal kende, at jeg, HERREN deres Gud, er med dem, og at de er mit Folk, Israels Hus, lyder det fra den Herre HERREN.
31 Inu ndinu nkhosa zanga, nkhosa zimene ndimazidyetsa. Ine ndine Mulungu wanu. Ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse.’”
I er min Hjord, I er den Hjord, jeg røgter, og jeg er eders Gud, lyder det fra den Herre HERREN.

< Ezekieli 34 >