< Ezekieli 33 >

1 Yehova anandiyankhula nati:
Ilizwi leNkosi lafika kimi futhi, lisithi:
2 “Iwe mwana wa munthu awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Paja zimati ndikatumiza nkhondo mʼdziko anthu a mʼdzikomo amasankha munthu mmodzi pakati pawo kuti akhale mlonda.
Ndodana yomuntu, khuluma kubantwana babantu bakho, uthi kubo: Ilizwe, lapho ngiletha inkemba phezu kwalo, labantu belizwe bathathe umuntu emingceleni yakibo, bambeke abe ngumlindi wabo,
3 Tsono iyeyo amati akaona nkhondo ikubwera amaliza lipenga kuti achenjeze anthuwo.
lapho ebona inkemba isiza phezu kwelizwe, avuthele uphondo, axwayise abantu,
4 Wina aliyense akamva lipenga koma osasamala, mdani uja akabwera nʼkumupha, ndiye kuti wadziphetsa yekha.
kuzakuthi loba ngubani ozwa umsindo wophondo, kodwa angaxwayi, lapho inkemba ifika, imsuse, igazi lakhe lizakuba phezu kwekhanda lakhe.
5 Iye anamva kulira kwa lipenga koma sanalabadire. Ndiye kuti wadziphetsa yekha. Akanasamala kuchenjeza kwa mlonda akanapulumuka.
Uzwile ukukhala kophondo, kodwa angaxwayi; igazi lakhe lizakuba phezu kwakhe. Kodwa oxwayayo uzawophula umphefumulo wakhe.
6 Koma ngati mlondayo aona lupanga likubwera ndipo osawomba lipengalo kuchenjeza anthu, ndipo lupanga libwera ndi kuchotsa moyo wa mmodzi mwa iwo, munthu ameneyo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma ndidzamuyimba mlandu mlondayo chifukwa cha imfa ya mnzakeyo.’
Kodwa nxa umlindi ebona inkemba isiza, angavutheli uphondo, abantu bengaxwayiswa, aluba inkemba ifika, isuse umuntu phakathi kwabo, yena ususwa esesonweni sakhe, kodwa igazi lakhe ngizalibiza esandleni somlindi.
7 “Tsono iwe mwana wa munthu, ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Choncho imva mawu amene ndikuyankhula ndipo uwachenjeze.
Wena-ke, ndodana yomuntu, ngikubeke waba ngumlindi endlini kaIsrayeli; ngakho uzakuzwa ilizwi elivela emlonyeni wami, ubaxwayise ngokuvela kimi.
8 Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe munthu woyipa, udzafa ndithu,’ ndipo iwe osayankhula kumuchenjeza kuti aleke njira zake, munthu wochimwayo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
Uba ngisithi komubi: Mubi, uzakufa lokufa; uba wena ungakhulumi ukuxwayisa omubi atshiye indlela yakhe, lowo omubi uzafela esonweni sakhe, kodwa igazi lakhe ngizalibiza esandleni sakho.
9 Koma ngati uchenjeza munthu woyipa kuti aleke njira zake, ndipo iye osatero, adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
Kodwa wena uba umxwayisa omubi ngendlela yakhe ukuthi aphenduke kuyo; uba engaphenduki endleleni yakhe, yena uzafela ebubini bakhe, kodwa wena usuwophule umphefumulo wakho.
10 “Iwe mwana wa munthu, akumbutse Aisraeli mawu awo akuti, ‘Ife talemedwa ndi zolakwa zathu ndi machimo athu, ndipo tikuwonda chifukwa cha zimene tachita. Kodi tingakhale ndi moyo bwanji?’”
Ngakho, wena ndodana yomuntu, tshono kuyo indlu kaIsrayeli: Likhuluma ngokunjalo lisithi: Ngoba iziphambeko zethu lezono zethu ziphezu kwethu, thina sicikizeke sikuzo, pho, sizaphila njani?
11 Uwawuze kuti, Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Pali Ine wamoyo, sindikondwera ndi imfa ya munthu woyipa. Ndimakondwera ndikamaona munthu woyipa akuleka zoyipa zake kuti akhale ndi moyo. Tembenukani! Tembenukani, siyani makhalidwe anu oyipa! Muferanji, Inu Aisraeli?
Tshono kubo: Kuphila kwami, itsho iNkosi uJehova, isibili kangithokozi ngokufa komubi, kodwa ngokuthi omubi aphenduke endleleni yakhe aphile. Phendukani, phendukani ezindleleni zenu ezimbi; ngoba lizafelani, lina ndlu kaIsrayeli?
12 “Tsono iwe mwana wa munthu, awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Ngati munthu wolungama achimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwino zija sizidzamupulutsa. Koma wochimwa akaleka ntchito zake zoyipazo, sadzalangidwa konse. Ndithu ngati munthu wolungama ayamba kuchimwa sadzatha kukhala ndi moyo chifukwa cha ntchito zake zabwino zija.’
Wena-ke, ndodana yomuntu, tshono ebantwaneni babantu bakiniuthi: Ukulunga kolungileyo kakuyikumophula ngosuku lwesiphambeko sakhe; mayelana lenkohlakalo yokhohlakeleyo, kayikuwa ngayo ngosuku azaphenduka ngalo enkohlakalweni yakhe; lolungileyo kayikuba lakho ukuphila ngokulunga kwakhe ngosuku ona ngalo.
13 Ngati ndiwuza munthu wolungama kuti adzafa ndithu, koma iyeyo nʼkumadalira ntchito zake zabwino zimene anachita kale ndi kuyamba kuchimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwinozo zidzayiwalika. Iye adzafa chifukwa cha machimo ake.
Lapho ngizakutsho kolungileyo ukuthi uzaphila isibili; uba yena ethembela ekulungeni kwakhe, enze isiphambeko, konke ukulunga kwakhe kakuyikukhunjulwa; kodwa ngenxa yobubi bakhe abenzileyo, uzabufela.
14 Ndipo ngati ndiwuza munthu woyipa kuti, ‘Udzafa ndithu,’ tsono iye nʼkutembenuka kuleka machimo ake ndi kuyamba kuchita zimene Yehova afuna,
Futhi uba ngisitsho kokhohlakeleyo ukuthi: Uzakufa lokufa; uba ephenduka esonweni sakhe, enze isahlulelo lokulungileyo,
15 monga kubweza chimene anatenga ngati chikole cha ngongole, kubweza chimene anaba, kutsatira malamulo omwe amapereka moyo ndi kuleka kuchita zoyipa, iye adzakhala ndithu ndi moyo; sadzafa.
okhohlakeleyo ebuyisela isibambiso, abhadale impango, ahambe ngezimiso zempilo, ukuthi angenzi isiphambeko, uzaphila isibili, kayikufa.
16 Ndidzakhululuka machimo ake onse anachita. Iye wachita zimene ndi zolungama ndi zoyenera ndipo iye adzakhala ndi moyo ndithu.
Kakukho lasinye sezono zakhe azenzileyo esizakhunjulwa kuye; wenzile isahlulelo lokulungileyo; uzaphila isibili.
17 “Komabe anthu a mtundu wako akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, koma makhalidwe awo ndiwo ali osalungama.
Kodwa abantwana babantu bakini bathi: Indlela yeNkosi kayilingani; kanti ngeyabo indlela engalinganiyo.
18 Ngati munthu wolungama atembenuka ndi kuleka ntchito zake zolungama ndi kuyamba kuchita zoyipa, adzafa nazo.
Nxa olungileyo ephenduka ekulungeni kwakhe, enze isiphambeko, uzakufa ngenxa yaso.
19 Ndipo ngati munthu woyipa atembenuka ndi kuleka ntchito zake zoyipa ndi kuyamba kuchita zolungama ndi zoyenera, iye adzakhala ndi moyo pochita zimenezo.
Kodwa uba okhohlakeleyo ephenduka kunkohlakalo yakhe, enze isahlulelo lokulungileyo, yena uzaphila ngakho.
20 Koma Inu Aisraeli, mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, inu Aisraeli, Ine ndidzaweruza aliyense wa inu potsata ntchito zake.”
Kanti lithi: Indlela yeNkosi kayilingani. Wena ndlu kaIsrayeli, ngizalahlulela, ngulowo lalowo njengendlela zakhe.
21 Pa tsiku lachisanu la mwezi wakhumi, chaka chakhumi ndi chiwiri cha ukapolo wathu, munthu wina amene anapulumuka ku Yerusalemu anabwera kudzandiwuza kuti, “Mzinda wagwa!”
Kwasekusithi ngomnyaka wetshumi lambili wokuthunjwa kwethu, ngenyanga yetshumi, ngolwesihlanu lwenyanga, owayephunyukile eJerusalema wafika kimi esithi: Umuzi usutshayiwe.
22 Tsono madzulo ake munthuyo asanafike, dzanja la Yehova linali pa ine. Koma mmawa mwake munthuyo atabwera Yehova anatsekula pakamwa panga, motero kuti sindinakhalenso wosayankhula.
Kwathi isandla seNkosi saba phezu kwami kusihlwa, ophunyukileyo engakafiki, savula umlomo wami, waze wafika kimi ekuseni. Ngokunjalo umlomo wami wavuleka, kangabe ngisaba yisimungulu.
23 Ndipo Yehova anandiyankhula kuti:
Ilizwi leNkosi laselifika kimi, lisithi:
24 “Iwe mwana wa munthu, anthu amene akukhala mʼmizinda ya mabwinja ya dziko la Israeli akunena kuti, ‘Abrahamu anali munthu mmodzi yekha, ndipo anamupatsa dziko lonse. Koma ife tilipo ambiri, motero tsono dzikolo ndi lathu.’
Ndodana yomuntu, abahlali balawomanxiwa elizwe lakoIsrayeli bakhuluma besithi: UAbrahama wayemunye, wadla ilifa lelizwe; kodwa thina sibanengi; ilizwe silinikiwe ukuba yilifa.
25 Choncho iwe uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Inu mumadya nyama ili ndi magazi ake, ndipo mumapembedza mafano ndi kukhetsa magazi, kodi tsono inu nʼkulandira dzikoli?
Ngakho tshono kubo: Itsho njalo iNkosi uJehova: Lidla okulegazi, liphakamisele amehlo enu ezithombeni zenu, lichithe igazi; kambe lizakudla ilifa lelizwe yini?
26 Mumadalira lupanga lanu, mumachita zinthu zonyansa, ndipo aliyense wa inu amachita chigololo ndi mkazi wa mnzake. Kodi inu nʼkulandira dzikoli?’
Lima phezu kwenkemba yenu, lenze isinengiso, lingcolise, ngulowo lalowo umfazi kamakhelwane wakhe; kambe lizakudla ilifa lelizwe yini?
27 “Uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Ndithu pali Ine wamoyo, anthu amene anatsala mʼmizinda ya mabwinja adzaphedwa ndi lupanga, amene ali ku midzi ndidzawapereka kuti adzadyedwe ndi zirombo zakuthengo, ndipo amene ali mʼmalinga ndi mʼmapanga adzafa ndi mliri.
Tshono njalo kubo: Itsho njalo iNkosi uJehova: Kuphila kwami, isibili labo abasemanxiweni bazakuwa ngenkemba; lalowo osegcekeni ngizamnikela ezilweni ukuthi zimudle, lalabo abasezinqabeni labasezimbalwini bazakufa ngomatshayabhuqe wesifo.
28 Ndidzalisandutsa chipululu dzikolo, ndipo mphamvu zake zimene amanyadira zidzatheratu, ndipo mapiri a Yerusalemu adzasanduka chipululu, kotero kuti palibe amene adzatha kudutsako.
Ngoba ngizalenza ilizwe libe lunxiwa lencithakalo, lokuziqhenya kwamandla alo kuzaphela, lezintaba zakoIsrayeli zibe yinkangala, ukuze kungabi khona odlulayo.
29 Ndikadzasandutsa dzikolo chipululu chifukwa cha zonyansa zimene ankachita, pamenepo ndiye adzadziwa kuti ndine Yehova.’
Khona bazakwazi ukuthi ngiyiNkosi, lapho sengenze ilizwe laba yinkangala lesesabiso ngenxa yawo wonke amanyala abo abawenzileyo.
30 “Koma kunena za iwe, mwana wa munthu, anthu a mtundu wako akumayankhula za iwe akakhala pa makoma a mzinda ndi pa makomo a nyumba zawo. Akumawuzana kuti, ‘Tiyeni tikamve uthenga umene wachokera kwa Yehova.’
Wena-ke, ndodana yomuntu, abantwana babantu bakini basakhuluma ngawe ngasemidulwini laseminyango yezindlu, njalo omunye ekhuluma komunye, ngulowo lalowo kumfowabo, besithi: Wozani, ngiyacela, lizwe ukuthi yilizwi bani eliphuma eNkosini.
31 Anthu anga amabwera kwa iwe, monga momwe amachitira nthawi zonse anthu anga, ndipo amakhala pansi pamaso pako kumvetsera mawu ako. Koma zimene akumvazo sazichita. Zokamba zawo zimaonetsa chikondi, koma mitima yawo imakhala pa phindu lawo.
Njalo bayeza kuwe njengokuza kwabantu, bahlale phambi kwakho njengabantu bami, bezwe amazwi akho, kodwa bangawenzi; ngoba ngomlomo wabo babonakalisa uthando olukhulu, kodwa inhliziyo yabo ilandela inzuzo yabo embi.
32 Kunena zoona, kwa iwowo sindiwe kanthu konse, ndiwe munthu wamba chabe womangoyimba nyimbo zachikondi ndi liwu lokoma poyimba zeze. Kumva amamva mawu ako koma sawagwiritsa ntchito.
Khangela-ke, kubo unjengengoma ethandekayo, ilizwi elimnandi, lowazi kuhle ukutshaya ichacho; ngoba besizwa amazwi akho kodwa bengawenzi.
33 “Koma zonsezi zikadzachitika, ndipo zidzachitika ndithu, pamenepo adzadziwa kuti mneneri anali pakati pawo.”
Kodwa ekufikeni kwalokhu (khangela, kuzafika), khona bazakwazi ukuthi bekukhona umprofethi phakathi kwabo.

< Ezekieli 33 >