< Ezekieli 33 >
1 Yehova anandiyankhula nati:
Og Herrens Ord kom til mig saaledes:
2 “Iwe mwana wa munthu awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Paja zimati ndikatumiza nkhondo mʼdziko anthu a mʼdzikomo amasankha munthu mmodzi pakati pawo kuti akhale mlonda.
Du Menneskesøn! tal til dit Folks Børn, og sig til dem: Naar jeg skulde føre Sværd over et Land, og Folk i Landet toge een Mand iblandt sig og gjorde ham til deres Vægter,
3 Tsono iyeyo amati akaona nkhondo ikubwera amaliza lipenga kuti achenjeze anthuwo.
og han saa Sværdet komme over Landet og blæste i Trompeten og advarede Folket;
4 Wina aliyense akamva lipenga koma osasamala, mdani uja akabwera nʼkumupha, ndiye kuti wadziphetsa yekha.
og den, som da hørte Trompetens Lyd, dog ikke vilde lade sig advare, og Sværdet kom og tog ham bort; Saa, skal hans Blod være over hans Hoved.
5 Iye anamva kulira kwa lipenga koma sanalabadire. Ndiye kuti wadziphetsa yekha. Akanasamala kuchenjeza kwa mlonda akanapulumuka.
Han hørte Trompetens Lyd og lod sig ikke advare, hans Blod skal være over ham; men havde han ladet sig advare, vilde han have reddet sit Liv.
6 Koma ngati mlondayo aona lupanga likubwera ndipo osawomba lipengalo kuchenjeza anthu, ndipo lupanga libwera ndi kuchotsa moyo wa mmodzi mwa iwo, munthu ameneyo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma ndidzamuyimba mlandu mlondayo chifukwa cha imfa ya mnzakeyo.’
Men naar Vægteren saa Sværdet komme og ej blæste i Trompeten, og Folket ej advaredes, og Sværdet kom og tog en Sjæl bort af dem: Saa blev han vel borttagen for sin Misgernings Skyld, men hans Blod vil jeg kræve af Vægterens Haand.
7 “Tsono iwe mwana wa munthu, ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Choncho imva mawu amene ndikuyankhula ndipo uwachenjeze.
Og du, Menneskesøn! jeg har sat dig til Vægter for Israels Hus, at, naar du hører et Ord af min Mund, du skal advare dem paa mine Vegne.
8 Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe munthu woyipa, udzafa ndithu,’ ndipo iwe osayankhula kumuchenjeza kuti aleke njira zake, munthu wochimwayo adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
Naar jeg siger til den ugudelige: Du ugudelige skal visselig dø, og du ikke taler for at advare den ugudelige for hans Vej, da skal han, den ugudelige, vel dø for sin Misgerning, men hans Blod vil jeg kræve af din Haand.
9 Koma ngati uchenjeza munthu woyipa kuti aleke njira zake, ndipo iye osatero, adzafa chifukwa cha tchimo lake, koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
Men naar du advarer den ugudelige for hans Vej, at han skal omvende sig derfra, og han, dog ikke omvender sig fra sin Vej, da skal han dø for sin Misgerning, men du skal have din Sjæl frelst.
10 “Iwe mwana wa munthu, akumbutse Aisraeli mawu awo akuti, ‘Ife talemedwa ndi zolakwa zathu ndi machimo athu, ndipo tikuwonda chifukwa cha zimene tachita. Kodi tingakhale ndi moyo bwanji?’”
Og du Menneskesøn! sig til Israels Hus: I sige saaledes: Vore Overtrædelser og vore Synder ere over os, og vi hensvinde under dem; hvorledes kunne vi da leve?
11 Uwawuze kuti, Ine Ambuye Yehova ndikuti: “Pali Ine wamoyo, sindikondwera ndi imfa ya munthu woyipa. Ndimakondwera ndikamaona munthu woyipa akuleka zoyipa zake kuti akhale ndi moyo. Tembenukani! Tembenukani, siyani makhalidwe anu oyipa! Muferanji, Inu Aisraeli?
Sig til dem: Saa sandt jeg lever, siger den Herre, Herre: Jeg har ikke Behag i den ugudeliges Død, men deri, at den ugudelige omvender sig fra sin Vej, at han maa leve; vender om, vender om fra eders onde Veje! hvorfor ville I dog dø, Israels Hus?
12 “Tsono iwe mwana wa munthu, awuze anthu a mtundu wako kuti, ‘Ngati munthu wolungama achimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwino zija sizidzamupulutsa. Koma wochimwa akaleka ntchito zake zoyipazo, sadzalangidwa konse. Ndithu ngati munthu wolungama ayamba kuchimwa sadzatha kukhala ndi moyo chifukwa cha ntchito zake zabwino zija.’
Og du Menneskesøn! sig til dit Folks Børn: Den retfærdiges Retfærdighed skal ikke redde ham paa hans Overtrædelses Dag, og den ugudelige skal ikke falde for sin Ugudelighed paa den Dag, han omvender sig fra sin Ugudelighed, og den retfærdige skal ikke kunne leve derved, paa den Dag han synder.
13 Ngati ndiwuza munthu wolungama kuti adzafa ndithu, koma iyeyo nʼkumadalira ntchito zake zabwino zimene anachita kale ndi kuyamba kuchimwa, ndiye kuti ntchito zake zabwinozo zidzayiwalika. Iye adzafa chifukwa cha machimo ake.
Naar jeg siger om den retfærdige: Han skal visselig leve, og han forlader sig paa sin Retfærdighed og gør Uret, da skal ingen af hans retfærdige Gerninger ihukommes; men han skal dø i sin Uretfærdighed, som han gjorde.
14 Ndipo ngati ndiwuza munthu woyipa kuti, ‘Udzafa ndithu,’ tsono iye nʼkutembenuka kuleka machimo ake ndi kuyamba kuchita zimene Yehova afuna,
Og naar jeg siger til den ugudelige: Du skal visselig dø, og han omvender sig fra sin Synd og gør Ret og Retfærdighed,
15 monga kubweza chimene anatenga ngati chikole cha ngongole, kubweza chimene anaba, kutsatira malamulo omwe amapereka moyo ndi kuleka kuchita zoyipa, iye adzakhala ndithu ndi moyo; sadzafa.
saa at den ugudelige giver Pant tilbage, betaler det, han har røvet, vandrer efter Livets Bud og ikke gør Uret, da skal han visselig leve, han skal ikke dø.
16 Ndidzakhululuka machimo ake onse anachita. Iye wachita zimene ndi zolungama ndi zoyenera ndipo iye adzakhala ndi moyo ndithu.
Ingen af hans Synder, som han har begaaet, skal kommes ham i Hu; han har gjort Ret og Retfærdighed, han skal Visselig leve.
17 “Komabe anthu a mtundu wako akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, koma makhalidwe awo ndiwo ali osalungama.
Dog sige dit Folks Børn: Herrens Vej er ikke rigtig; men det er dem selv, hvis Vej ikke er rigtig.
18 Ngati munthu wolungama atembenuka ndi kuleka ntchito zake zolungama ndi kuyamba kuchita zoyipa, adzafa nazo.
Naar den retfærdige vender om fra sin Retfærdighed og gør Uret, da skal han dø derfor.
19 Ndipo ngati munthu woyipa atembenuka ndi kuleka ntchito zake zoyipa ndi kuyamba kuchita zolungama ndi zoyenera, iye adzakhala ndi moyo pochita zimenezo.
Og naar den ugudelige vender om fra sin Ugudelighed og gør Ret og Retfærdighed, da skal han leve derved.
20 Koma Inu Aisraeli, mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Ayi, inu Aisraeli, Ine ndidzaweruza aliyense wa inu potsata ntchito zake.”
Og dog sige I: Herrens Vej er ikke rigtig; jeg skal dømme eder, Israels Hus! hver efter hans Veje.
21 Pa tsiku lachisanu la mwezi wakhumi, chaka chakhumi ndi chiwiri cha ukapolo wathu, munthu wina amene anapulumuka ku Yerusalemu anabwera kudzandiwuza kuti, “Mzinda wagwa!”
Og det skete i det tolvte Aar, i den tiende Maaned, paa deri femte Dag i Maaneden efter vor Bortførelse, da kom een til mig, som var undkommen fra Jerusalem, og sagde: Staden er indtagen.
22 Tsono madzulo ake munthuyo asanafike, dzanja la Yehova linali pa ine. Koma mmawa mwake munthuyo atabwera Yehova anatsekula pakamwa panga, motero kuti sindinakhalenso wosayankhula.
Og Herrens Haand var kommen over mig om Aftenen, før den undslupne kom, og han oplod min Mund, inden denne kom til mig om Morgenen; saa oplodes min Mund, og jeg var ikke ydermere stum.
23 Ndipo Yehova anandiyankhula kuti:
Og Herrens Ord kom til mig saaledes:
24 “Iwe mwana wa munthu, anthu amene akukhala mʼmizinda ya mabwinja ya dziko la Israeli akunena kuti, ‘Abrahamu anali munthu mmodzi yekha, ndipo anamupatsa dziko lonse. Koma ife tilipo ambiri, motero tsono dzikolo ndi lathu.’
Du Menneskesøn! de, som bo paa disse øde Steder i Israels Land, sige saaledes: Abraham var een og ejede Landet, og vi ere mange, os er Landet givet til Ejendom.
25 Choncho iwe uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Inu mumadya nyama ili ndi magazi ake, ndipo mumapembedza mafano ndi kukhetsa magazi, kodi tsono inu nʼkulandira dzikoli?
Derfor sig til dem: Saa siger den Herre, Herre: I æde Kød tillige med Blod og opløfte eders Øjne til eders Afguder og udøse Blod! og I skulle eje Landet!
26 Mumadalira lupanga lanu, mumachita zinthu zonyansa, ndipo aliyense wa inu amachita chigololo ndi mkazi wa mnzake. Kodi inu nʼkulandira dzikoli?’
I stole paa eders Sværd, I gøre Vederstyggeligheder og vanære hver sin Næstes Hustru; og I skulle eje Landet.
27 “Uwawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti, ‘Ndithu pali Ine wamoyo, anthu amene anatsala mʼmizinda ya mabwinja adzaphedwa ndi lupanga, amene ali ku midzi ndidzawapereka kuti adzadyedwe ndi zirombo zakuthengo, ndipo amene ali mʼmalinga ndi mʼmapanga adzafa ndi mliri.
Saaledes skal du sige til dem: Saa siger den Herre, Herre: Saa sandt jeg lever, de, som ere paa de øde Steder, skulle falde for Sværdet, og den, som er paa Marken, ham har jeg givet til de vilde Dyr, at de skulle æde ham, og de, som ere i Fæstningerne og i Hulerne, skulle dø af Pest.
28 Ndidzalisandutsa chipululu dzikolo, ndipo mphamvu zake zimene amanyadira zidzatheratu, ndipo mapiri a Yerusalemu adzasanduka chipululu, kotero kuti palibe amene adzatha kudutsako.
Og jeg vil gøre Landet til en Ødelæggelse og en Ørk, og dets Magts Stolthed skal ophøre; og Israels Bjerge skulle ligge øde, at ingen skal gaa over dem.
29 Ndikadzasandutsa dzikolo chipululu chifukwa cha zonyansa zimene ankachita, pamenepo ndiye adzadziwa kuti ndine Yehova.’
Saa skulle de fornemme, at jeg er Herren, naar jeg gør Landet til en Ødelæggelse og en Ørk, formedelst alle deres Vederstyggeligheder, som de have gjort.
30 “Koma kunena za iwe, mwana wa munthu, anthu a mtundu wako akumayankhula za iwe akakhala pa makoma a mzinda ndi pa makomo a nyumba zawo. Akumawuzana kuti, ‘Tiyeni tikamve uthenga umene wachokera kwa Yehova.’
Og du Menneskesøn! dit Folks Børn tale indbyrdes om dig ved Væggene og i Husdørene, og den ene taler med den anden, hver med sin Broder, sigende: Kære, kommer og hører, hvad det er for et Ord, som udgaar fra Herren.
31 Anthu anga amabwera kwa iwe, monga momwe amachitira nthawi zonse anthu anga, ndipo amakhala pansi pamaso pako kumvetsera mawu ako. Koma zimene akumvazo sazichita. Zokamba zawo zimaonetsa chikondi, koma mitima yawo imakhala pa phindu lawo.
Og de skulle komme til dig, som et Folk kommer, og sidde for dit Ansigt som mit Folk, og de skulle høre dine Ord og ikke gøre efter dem; men det, der er behageligt i deres Mund, gøre de, og deres Hjerte gaar efter deres egen Fordel.
32 Kunena zoona, kwa iwowo sindiwe kanthu konse, ndiwe munthu wamba chabe womangoyimba nyimbo zachikondi ndi liwu lokoma poyimba zeze. Kumva amamva mawu ako koma sawagwiritsa ntchito.
Og se, du er dem som en behagelig Sanger, der har en dejlig Røst; og som kan spille smukt; derfor skulle de høre dine Ord, men dog ikke gøre efter dem.
33 “Koma zonsezi zikadzachitika, ndipo zidzachitika ndithu, pamenepo adzadziwa kuti mneneri anali pakati pawo.”
Men naar det kommer — se, det kommer! — da skulle de fornemme, at der har været en Profet midt iblandt dem.