< Ezekieli 32 >

1 Pa tsiku loyamba la mwezi wa khumi ndi chiwiri, chaka chakhumi ndi chiwiri, Yehova anandiyankhula kuti:
And it was in two [plus] ten year in two [plus] ten month on [day] one of the month it came [the] word of Yahweh to me saying.
2 “Iwe mwana wa munthu imba nyimbo ya maliro a Farao mfumu ya Igupto ndipo uyiwuze kuti, “Iwe umadziyesa ngati mkango pakati pa mitundu ya anthu. Koma iwe uli ngati ngʼona mʼnyanja. Umakhuvula mʼmitsinje yako, kuvundula madzi ndi mapazi ako ndi kudetsa madzi mʼmitsinje.
O son of humankind take up a lamentation on Pharaoh [the] king of Egypt and you will say to him a young lion of nations you became like and you [were] like sea monster in the seas and you burst forth in rivers your and you made turbid waters with feet your and you fouled rivers their.
3 “Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti, “‘Pogwiritsa ntchito gulu la anthu a mitundu yambiri, ndidzakuponyera khoka langa ndi kukugwira mu ukonde wanga.
Thus he says [the] Lord Yahweh and I will spread over you net my by a company of peoples many and they will bring up you in net my.
4 Ndidzakuponya ku mtunda ndi kukutayira pansi. Ndidzabweretsa mbalame zamumlengalenga kuti zidzatere pa iwe, ndipo zirombo zonse za dziko lapansi zidzakudya.
And I will abandon you on the land on [the] surface of the field I will throw you and I will cause to settle on you every bird of the heavens and I will satisfy from you [the] animal[s] of all the earth.
5 Ndidzayanika mnofu wako pa mapiri ndipo zigwa zidzadzaza ndi zotsalira zako.
And I will put flesh your on the mountains and I will fill the valleys height your.
6 Ndidzanyowetsa dziko ndi magazi ako, mpaka kumapiri komwe, ndipo mitsinje idzadzaza ndi mnofu wako.
And I will make drink [the] land outflow your from blood your to the mountains and ravines they will be filled! from you.
7 Ndikadzakuwononga, ndidzaphimba miyamba ndikudetsa nyenyezi zake. Ndidzaphimba dzuwa ndi mtambo, ndipo mwezi sudzawala.
And I will cover when extinguishing you heavens and I will darken stars their [the] sun with cloud I will cover it and [the] moon not it will give light light its.
8 Zowala zonse zamumlengalenga ndidzazizimitsa; ndidzachititsa mdima pa dziko lako, akutero Ambuye Yehova.
All [the] luminaries of light in the heavens I will darken them over you and I will put darkness over land your [the] utterance of [the] Lord Yahweh.
9 Ndidzasautsa mitima ya anthu a mitundu yambiri pamene ndidzakupititsa ku ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, ku mayiko amene iwe sunawadziwe.
And I will disturb [the] heart of peoples many when bring I breaking your among the nations to lands which not you have known them.
10 Ine ndidzachititsa kuti anthu a mitundu yambiri adabwe nawe, ndipo mafumu awo adzanjenjemera ndi mantha aakulu chifukwa cha iwe pamene ndidzaonetsa lupanga langa pamaso pawo. Pa nthawi ya kugwa kwako, aliyense wa iwo adzanjenjemera moyo wake wonse.
And I will make appalled on you peoples many and kings their they will shudder on you shuddering when brandish I sword my on faces their and they will tremble to moments everyone for life his on [the] day of downfall your.
11 “‘Pakuti ndikunena Ine Ambuye Yehova kuti, “‘Lupanga la mfumu ya ku Babuloni lidzabwera kudzalimbana nawe.
For thus he says [the] Lord Yahweh [the] sword of [the] king of Babylon it will come to you.
12 Ndidzachititsa gulu lako lankhondo kuti ligwe ndi lupanga la anthu amphamvu, anthu ankhanza kwambiri pakati pa mitundu yonse ya anthu. Adzathetsa kunyada kwa Igupto, ndipo gulu lake lonse la nkhondo lidzagonjetsedwa.
By [the] swords of warriors I will make fall multitude your ruthless [ones] of nations all of them and they will devastate [the] pride of Egypt and it will be destroyed all multitude its.
13 Ndidzawononga ziweto zake zonse zokhala mʼmbali mwa madzi ambiri. Ku madziko sikudzaonekanso phazi la munthu kapena kudetsedwa ndi phazi la ziweto.
And I will destroy all livestock its from at waters many and not it will make turbid them a foot of a human again and hooves of livestock not it will make turbid them.
14 Pambuyo pake ndidzayeretsa madzi ake ndipo mitsinje yake idzayenda mokometsera ngati mafuta, akutero Ambuye Yehova.
Then I will make settle waters their and rivers their like oil I will make go [the] utterance of [the] Lord Yahweh.
15 Ndikadzasandutsa dziko la Igupto kukhala bwinja; ndikadzawononga dziko lonse ndi kukantha onse okhala kumeneko, adzadziwa kuti ndine Yehova.’
When make I [the] land of Egypt a desolation and [is] made desolate [the] land from fullness its when strike down I all [the] inhabitants in it and they will know that I [am] Yahweh.
16 “Mawu angawa adzakhala nyimbo ya maliro. Ana a akazi amitundu ya anthu adzayimba, kuyimbira Igupto ndi gulu lake lonse la nkhondo, akutero Ambuye Yehova.”
[is] a lamentation It and people will chant it [the] daughters of the nations they will chant it over Egypt and over all multitude its they will chant it [the] utterance of [the] Lord Yahweh.
17 Pa tsiku la 15 la mwezi woyamba, chaka cha khumi ndi chiwiri, Yehova anayankhula kuti:
And it was in two [plus] ten year on [day] fif-teen of the month it came [the] word of Yahweh to me saying.
18 “Iwe mwana wa munthu, lirira gulu lankhondo la Igupto ndipo uwalowetse pamodzi ndi anthu ena amphamvu a mayiko ena ku dziko la anthu akufa.
O son of humankind wail on [the] multitude of Egypt and bring down it it and [the] daughters of nations mighty to [the] earth of [the] lowest parts with [those who] go down of [the] pit.
19 Ufunse kuti, ‘Ndani amene akukuposa kukongola? Tsikirani ku manda ndi kukhala pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe.’
More than whom? are you lovely go down! and be laid! with uncircumcised [men].
20 Aigupto adzagwa pakati pa amene akuphedwa ndi lupanga. Lupanga ndi losololedwa kale. Iye adzaphedwa pamodzi ndi gulu lake lankhondo.
In among [those] slain of a sword they will fall a sword it has been appointed they have drawn down it and all multitudes its.
21 Mʼkati mwa manda atsogoleri amphamvu pamodzi ndi ogwirizana nawo azidzakambirana za Igupto nʼkumati, ‘Afika kuno anthu osachita mdulidwe aja! Ndi awa agona apawa, ophedwa pa nkhondo.’ (Sheol h7585)
They will speak to him [the] leaders of [the] mighty [ones] from [the] midst of Sheol with helpers his they have come down they have lain down the uncircumcised [men] [those] slain of a sword. (Sheol h7585)
22 “Asiriya ali komweko ndipo ankhondo ake onse ali mʼmanda omuzungulira. Onsewo anaphedwa pa nkhondo.
[is] there Assyria and all company its [are] around it graves its all of them [are] slain those [who] have fallen by the sword.
23 Manda awo ali kumalo ozama a dzenje, ndipo ankhondo ake azungulira manda ake. Onse amene anaopseza dziko la anthu amoyo aphedwa, agwa ndi lupanga.
Which they have been put graves its in [the] remotest parts of [the] pit and it was company its around grave its all of them [are] slain [those who] have fallen by the sword who they had put terror in [the] land of [the] living.
24 “Elamu ali komweko ndipo ankhondo ake ali mʼmanda omuzungulira. Onsewa anaphedwa pa nkhondo, natsikira ku manda ali osachita mdulidwe. Iwowa kale ankaopseza anthu pa dziko lapansi. Tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda.
[is] there Elam and all multitude its around grave its all of them [are] slain those [who] have fallen by the sword who they have gone down uncircumcised - into [the] earth of [the] lowest parts who they had put terror their in [the] land of [the] living and they have borne disgrace their with [those who] go down of [the] pit.
25 Amukonzera pogona pakati pa anthu ophedwa, pamodzi ndi gulu lake lonse la nkhondo litazungulira manda ake. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe ophedwa ndi lupanga. Paja anthuwa ankaopsa mʼdziko la anthu a moyo. Koma tsopano akuchita manyazi pamodzi ndi amene ali mʼmanda. Iwo ayikidwa pakati pa anthu ophedwa.
In among [those] slain people have made a bed for it among all multitude its [are] around it graves its all of them [are] uncircumcised [those] slain of a sword for it was put terror their in [the] land of [the] living and they have borne disgrace their with [those who] go down of [the] pit in among [those] slain it was made.
26 “Mesaki ndi Tubala ali komweko, pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo litazungulira manda awo. Onsewo ndi anthu osachita mdulidwe, ophedwa ndi lupanga. Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo.
[is] there Meshech Tubal and all multitude its [are] around it graves its all of them [are] uncircumcised pierced of [the] sword for they had put terror their in [the] land of [the] living.
27 Iwo sanayikidwe mwaulemu ngati ankhondo amphamvu amakedzana, amene anatsikira ku dziko la anthu akufa ndi zida zawo zomwe za nkhondo. Malupanga awo anawayika ku mitu yawo, ndipo zishango zawo anaphimba mafupa awo. Kale anthu amphamvu amenewa ankaopsa dziko la anthu amoyo. (Sheol h7585)
And not they lie with warriors fallen from uncircumcised [men] who they went down Sheol with [the] weapons of war their and people put swords their under heads their and it was iniquities their on bones their for terror of warriors [was] in [the] land of [the] living. (Sheol h7585)
28 “Iwenso Farao, udzaphwanyidwa ndi kuyikidwa pakati pa anthu osachita mdulidwe, amene anaphedwa ndi lupanga.
And you in among uncircumcised [men] you will be broken and you may lie with [those] slain of a sword.
29 “Edomu ali kumeneko pamodzi ndi mafumu ake ndi akalonga ake onse. Ngakhale anali amphamvu, koma anayikidwa. Ayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi iwo amene akutsikira ku dzenje.
[is] there Edom kings its and all princes its who they have been put in strength their with [those] slain of a sword they with uncircumcised [men] they will lie and with [those who] go down of [the] pit.
30 “Akalonga onse akumpoto pamodzi ndi anthu onse a ku Sidoni ali kumeneko. Anatsikira ku dziko la anthu akufa mwamanyazi ngakhale anali owopsa ndi mphamvu zawo. Iwo akugona osachita mdulidwe pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga ndipo akuchita manyazi pamodzi ndi iwo amene anatsikira kale ku manda.
[are] there Princes of [the] north all of them and all [the] Sidonian[s] who they have gone down with [those] slain in terror their (from strength their *LA(bh)*) being ashamed and they lay uncircumcised with [those] slain of a sword and they have borne disgrace their with [those who] go down of [the] pit.
31 “Farao ndi gulu lake lankhondo akadzawaona iwowa adzathunza mtima pokumbukira kuchuluka kwa gulu lake lankhondo limene linaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
Them he will see Pharaoh and he will be comforted on all (multitude his *Q(K)*) [those] slain of a sword Pharaoh and all army his [the] utterance of [the] Lord Yahweh.
32 Paja ankaopsa mʼdziko la anthu amoyo. Koma Faraoyo pamodzi ndi ankhondo ake onse adzayikidwa pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, pamodzi ndi amene anaphedwa pa nkhondo. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
That I had put (terror my *Q(K)*) in [the] land of [the] living and he will be laid in among uncircumcised [men] with [those] slain of a sword Pharaoh and all (multitude his *Q(K)*) [the] utterance of [the] Lord Yahweh.

< Ezekieli 32 >