< Ezekieli 31 >

1 Pa tsiku loyamba la mwezi wachitatu, chaka cha khumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti:
EIA hoi kekahi, i ka makahiki umikumamakahi, i ka malama kolu, i ka la mua o ka malama; hiki mai la ka olelo a Iehova ia'u, i mai la,
2 “Iwe mwana wa munthu, unene kwa Farao mfumu ya Igupto ndi gulu lake lankhondo. Awawuze kuti, “‘Kodi mu ukulu wanu ndani angafanane ndi inu?
E ke keiki a ke kanaka, e olelo aku oe ia Parao ko Aigupita alii, a me kona lehulehu, Owai la ka mea e like ai me oe i kou nui ana?
3 Taonani, ndidzakufanizirani ndi mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni, wa nthambi zokongola zochititsa mthunzi mʼnkhalango. Unali wautali, msonga zake zooneka pamwamba pa nkhalango.
Aia hoi, o ka Asuria, he laau kedera no Lebanona ia, he nani kona mau lala, he ululaau malumalu, he kino kiekie; aia hoi kona welau iwaena o na lala paapu.
4 Madzi ndiwo ankawukulitsa mkungudzawo, akasupe ozama ankawutalikitsa. Mitsinje yake inkayenda mozungulira malo amene unaliwo ndipo ngalande zake zinkafika ku mitengo yonse ya mʼmunda.
Na na wai i hoonui ia ia, ua hookiekie ka hohonu ia ia me kona mau waikahe e kahe ana a puni kona wahi i kanuia'i, a ua hoopuka ae i kona mau kahawai liilii i na kumu laau a pau.
5 Choncho unatalika kwambiri kupambana mitengo yonse ya mʼmunda. Nthambi zake zinachuluka ndi kutalika kwambiri, chifukwa inkalandira madzi ambiri.
Nolaila i hookiekieia'i kona kiekie, maluna o na laau a pau o ke kula, a ua hoonuiia kona mau lala, a loloa ae la kona mau lala no ka nui o kona mau wai, i kona kupu ana'e.
6 Mbalame zonse zamlengalenga zinkamanga zisa zake mʼnthambi za mtengowo. Nyama zakuthengo zonse zinkaswanirana mʼmunsi mwa nthambi zake. Mitundu yotchuka ya anthu inkakhala mu mthunzi wake.
Maloko o kona mau lala i hana aku ai na manu a pau o ka lewa i ko lakou mau punana, a maloko iho o kona mau lala i hanau ai na holoholona a pau o ke kula i ka lakou mau keiki, a malalo iho o kona mala i noho ai na lahuikanaka nui a pau.
7 Unali wokongola kwambiri, wa nthambi zake zotambalala, chifukwa mizu yake inazama pansi kumene kunali madzi ochuluka.
Nolaila i nani ai ia i kona nui, a me ka loloa ana o kona mau lala; no ka mea, aia kona kumu ma na wai nui.
8 Mʼmunda wa Mulungu munalibe mkungudza wofanana nawo, kapena mitengo ya payini ya nthambi zofanafana ndi nthambi zake. Munalibenso mtengo wa mkuyu nthambi zofanafana ndi zake. Mʼmunda wa Mulungu munalibe mtengo wina uliwonse wofanana ndi iwo kukongola kwake.
Aole i hiki i ke kedera iloko o ka mala a ke Akua, ke hoonalo ia ia; aole like ka laau hukaa me kona mau lala, aole like ka laau pelatano me kona mau lala; aole laau iloko o ka mala a ke Akua i like me ia i kona nani.
9 Ine ndinawupanga wokongola wa nthambi zochuluka. Mitengo yonse ya mu Edeni, mʼmunda wa Mulungu inawuchitira nsanje.
Ua hana aku au ia ia i nani no ka nui loa o kona mau lala, i huahua hoi na laau a pau o Edena iloko o ka mala a ke Akua ia ia.
10 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Chifukwa kuti mtengowo unatalika kwambiri, unatulutsa songa zake mpaka ku thambo, ndipo unadzikweza chifukwa cha msinkhu wake,
No ia mea la, ke olelo mai nei Iehova ka Haku, No kou hookiekie ana ia oe iho i kiekie; a hoopuka aku oia i kona welau iwaena o na lala paapu, a ua hookiekie kona naau i kona kiekie;
11 ndinawupereka mʼdzanja la mfumu ya mitundu ya anthu kuti awulange molingana ndi kuyipa kwake.
Nolaila i haawi aku au ia ia i ka lima o ka mea mana no na lahuikanaka, e hana no oia ia ia; ua kipaku aku au ia ia no kona hewa.
12 Anthu ankhanza kwambiri amitundu ya anthu achilendo adzawudula ndi kuwusiya. Nthambi zake zidzagwera pa mapiri ndi mu zigwa zonse. Nthambi zake zidzathyokera mʼmitsinje ya mʼdzikomo. Motero mitundu yonse ya anthu a dziko lapansi amene ankasangalala mu mthunzi wake idzawusiya.
A o na malihini, na mea weliweli o na lahuikanaka, ua oki aku lakou ia ia, a waiho aku ia ia ma na mauna, a ua haule kona mau lala ma na awawa a pau, a ua hakihaki kona mau lala ma na muliwai o ka honua, a iho iho la na lahuikanaka a pau o ka honua mai kona malu iho, a ua haalele ia ia.
13 Mbalame zonse zamlengalenga zidzakhala pa mtengo wakugwawo, ndipo nyama zakuthengo zonse zidzakhala pa nthambi zake.
A e noho na manu a pau o ka lewa maluna o kona puu opala, a me na holoholona o ke kula maluna o kona mau lala;
14 Zidzakutero kuti pasakhalenso mitengo inanso ya mʼmbali mwa madzi yotalika kwambiri, imene idzatalike kwambiri ndi songa zake kufika mpaka ku mitambo. Komanso kuti pasadzakhalenso mitengo yolandira bwino madzi, imene idzatalika motero. Paja yonseyo kutha kwake ndi kufa, kupita ku dziko lapansi kukhala ndi anthu akufa amene analowa mʼmanda kale.
I mea e hookiekie ole ai kekahi o na laau a pau ma na wai, no ko lakou kiekie, aole hoi e hoopuka i ko lakou welau mawaena o na lala paapu, aole hoi e ku iluna ko lakou mau laau i ko lakou kiekie, o na mea a pau e inu ana i ka wai; no ka mea, ua haawiia lakou a pau i ka make i ko lalo mau wahi o ka honua iwaena o na keiki a kanaka, me na mea e iho ana i ka lua.
15 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene mkungudzawo unatsikira ku manda, ndinawuza nyanja kuti iwulire maliro pakuwuphimba. Ndinawumitsa mitsinje ndipo madzi ambiri anaphwa. Ndinabweretsa mdima pa Lebanoni chifukwa cha mtengowo ndipo mitengo yonse ya mʼdzikomo inawuma. (Sheol h7585)
Ke i mai nei Iehova ka Haku penei; i ka la i iho ai ia i ka luakupapau, hana hoi au e kanikau; ua uhi au i ka hohonu nona, a ua kaohi au i kona mau muliwai, a ua hoopaaia na wai nui; a hana aku au e kanikau o Lebauona nona, a maule ae la na laau a pau o ke kula nona. (Sheol h7585)
16 Mitundu ya anthu inagwedezeka pakumva mkokomo wa kugwa kwake, pamene ndinawutsitsira ku manda pamodzi ndi iwo amene anafa. Pamenepo ku dziko la akufa mitengo yonse ya ku Edeni pamodzi ndi ya ku Lebanoni yosankhidwa bwino inasangalatsidwa chifukwa cha zimenezi. (Sheol h7585)
Ua hoohaalulu au i na lahuikanaka i ka halulu ana o kona haule ana, i kuu wa i hoolei iho ai au ia ia i ka po, me ka poe e iho ana i ka lua; a e oluolu pu na laau a pau i ko lalo wahi o ka honua, na laau a pau o Edena, o na mea i waeia a he maikai o Lebanona, a me na mea a pau e inuwai ana. (Sheol h7585)
17 Amene ankakhala mu mthunzi wake, amene ankayanjana nawo, iwonso anapita nawo pamodzi ku manda, kukakhala pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga pakati pa mitundu ya anthu. (Sheol h7585)
E iho iho la lakou me ia i ka po, i ka poe i pepehiia me ka pahikaua, a o ka poe i lilo i lima nona, a noho iho la malalo iho o kona malu, iwaenakonu o na lahuikanaka. (Sheol h7585)
18 “‘Ndi mitengo iti ya mu Edeni imene ingafanane ndi kukongola kwako ndi ulemerero wako? Komabe iwenso, udzatsikira ku dziko la anthu akufa pamodzi ndi mitengo ya mu Edeni. Udzagona pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, anthu amene anaphedwa pa nkhondo. “‘Mtengowo ndi Farao ndi gulu lake lankhondo, akutero Ambuye Yehova.’”
Owai la kou mea e like ai i ka nani, a me ka nui iwaena o na laau o Edena? aka, e hooiho oe ilalo me na laau o Edena i ko lalo mau wahi o ka honua: a e moe oe iwaena o ka poe okipoepoe ole ia me ka poe i pepehiia me ka pahikaua. Oia hoi, o Parao a me kona lehulehu a pau, wahi a Iehova ka Haku.

< Ezekieli 31 >