< Ezekieli 31 >

1 Pa tsiku loyamba la mwezi wachitatu, chaka cha khumi ndi chimodzi, Yehova anandiyankhula kuti:
II advint, dans la onzième année, le premier jour du troisième mois, que la parole de l’Eternel me fut adressée en ces termes:
2 “Iwe mwana wa munthu, unene kwa Farao mfumu ya Igupto ndi gulu lake lankhondo. Awawuze kuti, “‘Kodi mu ukulu wanu ndani angafanane ndi inu?
"Fils de l’homme, dis à Pharaon, roi d’Egypte, et à sa cohue: A qui es-tu comparable dans ta grandeur?
3 Taonani, ndidzakufanizirani ndi mtengo wa mkungudza wa ku Lebanoni, wa nthambi zokongola zochititsa mthunzi mʼnkhalango. Unali wautali, msonga zake zooneka pamwamba pa nkhalango.
Voici, il était sur le Liban un cèdre superbe, aux belles branches, à la frondaison ombreuse, haut de stature; sa cime perçait les nuages.
4 Madzi ndiwo ankawukulitsa mkungudzawo, akasupe ozama ankawutalikitsa. Mitsinje yake inkayenda mozungulira malo amene unaliwo ndipo ngalande zake zinkafika ku mitengo yonse ya mʼmunda.
Les eaux l’avaient fait croître, la source profonde l’avait développé, en faisant courir ses flots autour de sa plantation et en dirigeant ses canaux vers tous les arbres de la campagne.
5 Choncho unatalika kwambiri kupambana mitengo yonse ya mʼmunda. Nthambi zake zinachuluka ndi kutalika kwambiri, chifukwa inkalandira madzi ambiri.
Aussi, sa taille surpassait celle de tous les arbres de la campagne, ses branches s’étaient multipliées et ses rameaux, grâce à l’abondance des eaux, s’étaient allongés, car il les projetait au loin.
6 Mbalame zonse zamlengalenga zinkamanga zisa zake mʼnthambi za mtengowo. Nyama zakuthengo zonse zinkaswanirana mʼmunsi mwa nthambi zake. Mitundu yotchuka ya anthu inkakhala mu mthunzi wake.
Dans ses branches nichaient tous les oiseaux du ciel, et sous ses rameaux mettaient bas' toutes les bêtes des champs. A son ombre demeuraient toutes les grandes nations.
7 Unali wokongola kwambiri, wa nthambi zake zotambalala, chifukwa mizu yake inazama pansi kumene kunali madzi ochuluka.
Il était beau dans sa grandeur, par la longueur de ses rameaux, car sa racine baignait dans de grandes eaux.
8 Mʼmunda wa Mulungu munalibe mkungudza wofanana nawo, kapena mitengo ya payini ya nthambi zofanafana ndi nthambi zake. Munalibenso mtengo wa mkuyu nthambi zofanafana ndi zake. Mʼmunda wa Mulungu munalibe mtengo wina uliwonse wofanana ndi iwo kukongola kwake.
Les cèdres ne l’avaient pas éclipsé au jardin de Dieu, les cyprès n’étaient pas comparables à ses branches, et les platanes ne rivalisaient pas avec ses rameaux: aucun arbre du jardin de Dieu ne l’égalait en beauté.
9 Ine ndinawupanga wokongola wa nthambi zochuluka. Mitengo yonse ya mu Edeni, mʼmunda wa Mulungu inawuchitira nsanje.
Je l’avais fait beau par la multitude de ses branches, et tous les arbres d’Eden, qui étaient au jardin de Dieu, le jalousaient.
10 “‘Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Chifukwa kuti mtengowo unatalika kwambiri, unatulutsa songa zake mpaka ku thambo, ndipo unadzikweza chifukwa cha msinkhu wake,
Donc, ainsi parle le Seigneur Dieu, puisque tu avais tant monté en hauteur, puisqu’il avait étendu sa cime au milieu des nuages, et que son coeur s’est enorgueilli de sa hauteur,
11 ndinawupereka mʼdzanja la mfumu ya mitundu ya anthu kuti awulange molingana ndi kuyipa kwake.
j’ai voulu le livrer aux mains d’un puissant parmi les nations, pour qu’il lui infligeât le traitement dû à sa méchanceté: je l’ai répudié.
12 Anthu ankhanza kwambiri amitundu ya anthu achilendo adzawudula ndi kuwusiya. Nthambi zake zidzagwera pa mapiri ndi mu zigwa zonse. Nthambi zake zidzathyokera mʼmitsinje ya mʼdzikomo. Motero mitundu yonse ya anthu a dziko lapansi amene ankasangalala mu mthunzi wake idzawusiya.
Ils l’ont coupé, les étrangers, les plus violents des peuples, ils l’ont jeté là. Sur les montagnes et sur toutes les vallées sont tombées ses branches; ses rameaux se sont brisés dans tous les ravins de la terre. Ils se sont retirés de son ombre, tous les peuples de la terre, et ils l’ont abandonné.
13 Mbalame zonse zamlengalenga zidzakhala pa mtengo wakugwawo, ndipo nyama zakuthengo zonse zidzakhala pa nthambi zake.
Sur sa ruine habitent tous les oiseaux du ciel et sur ses rameaux se posent toutes les bêtes des champs,
14 Zidzakutero kuti pasakhalenso mitengo inanso ya mʼmbali mwa madzi yotalika kwambiri, imene idzatalike kwambiri ndi songa zake kufika mpaka ku mitambo. Komanso kuti pasadzakhalenso mitengo yolandira bwino madzi, imene idzatalika motero. Paja yonseyo kutha kwake ndi kufa, kupita ku dziko lapansi kukhala ndi anthu akufa amene analowa mʼmanda kale.
pour qu’aucun des arbres plantés près des eaux ne s’enorgueillisse plus de sa haute taille, et qu’ils ne percent plus les nuages de leur cime et qu’ils ne se dressent plus dans leur hauteur, ces géants, tous ces buveurs d’eau, car tous ont été voués à là mort, précipités dans les régions souterraines, au milieu des fils de l’homme, auprès de ceux qui sont descendus dans la fosse."
15 “‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa nthawi imene mkungudzawo unatsikira ku manda, ndinawuza nyanja kuti iwulire maliro pakuwuphimba. Ndinawumitsa mitsinje ndipo madzi ambiri anaphwa. Ndinabweretsa mdima pa Lebanoni chifukwa cha mtengowo ndipo mitengo yonse ya mʼdzikomo inawuma. (Sheol h7585)
Ainsi parle le Seigneur Dieu: "Le jour où il est descendu dans le Scheol, j’ai fait mener le deuil; à cause de lui j’ai recouvert la source profonde, j’en ai arrêté les fleuves, et les grandes eaux ont été retenues prisonnières; j’ai enténébré pour lui le Liban, et tous les arbres des champs ont été pris de langueur à cause de lui. (Sheol h7585)
16 Mitundu ya anthu inagwedezeka pakumva mkokomo wa kugwa kwake, pamene ndinawutsitsira ku manda pamodzi ndi iwo amene anafa. Pamenepo ku dziko la akufa mitengo yonse ya ku Edeni pamodzi ndi ya ku Lebanoni yosankhidwa bwino inasangalatsidwa chifukwa cha zimenezi. (Sheol h7585)
Au bruit de sa chute, j’ai fait tressaillir les peuples, quand je l’ai fait descendre dans le Scheol avec ceux qui descendent dans la fosse, et ils se sont consolés dans les régions souterraines, tous les arbres de l’Eden, les plus beaux, les meilleurs du Liban, tous les buveurs d’eau. (Sheol h7585)
17 Amene ankakhala mu mthunzi wake, amene ankayanjana nawo, iwonso anapita nawo pamodzi ku manda, kukakhala pamodzi ndi amene anaphedwa ndi lupanga pakati pa mitundu ya anthu. (Sheol h7585)
Eux aussi sont descendus avec lui dans le Scheol auprès des victimes de l’épée; de même ses auxiliaires qui, s’asseyaient à son ombre parmi les nations. (Sheol h7585)
18 “‘Ndi mitengo iti ya mu Edeni imene ingafanane ndi kukongola kwako ndi ulemerero wako? Komabe iwenso, udzatsikira ku dziko la anthu akufa pamodzi ndi mitengo ya mu Edeni. Udzagona pamodzi ndi anthu osachita mdulidwe, anthu amene anaphedwa pa nkhondo. “‘Mtengowo ndi Farao ndi gulu lake lankhondo, akutero Ambuye Yehova.’”
A qui donc pouvais-tu être comparé en gloire et en grandeur parmi les arbres de l’Eden? Et pourtant, tu seras précipité, avec les arbres de l’Eden, dans les régions souterraines, parmi les incirconcis; tu seras couché avec les victimes de l’épée. Voilà ce qu’est Pharaon avec toute sa cohue, dit le Seigneur Dieu."

< Ezekieli 31 >